< 2 Mbiri 25 >

1 Amaziya anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 29. Dzina la amayi ake linali Yehoyadini wa ku Yerusalemu.
Amaziah was twenty-five years old when he began to reign, and he reigned twenty-nine years in Jerusalem. And his mother's name was Jehoaddan, of Jerusalem.
2 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, koma osati ndi mtima wonse.
And he did that which was right in the eyes of Jehovah, but not with a perfect heart.
3 Pamene mphamvu zonse zaufumu zinali mʼmanja mwake, iye anapha akuluakulu amene anapha abambo ake, mfumu ija.
Now it came to pass, when the kingdom was established to him, that he killed his servants who had killed the king his father.
4 Komabe iye sanaphe ana awo koma anatsatira zolembedwa mʼbuku la Mose, mʼmene Yehova analamula kuti, “Makolo sadzaphedwa chifukwa cha ana awo kapena ana kuphedwa chifukwa cha makolo awo. Aliyense adzafera machimo ake.”
But he did not put their sons to death, but did according to that which is written in the law in the book of Moses, as Jehovah commanded, saying, The fathers shall not die for the sons, neither shall the sons die for the fathers, but every man shall die for his own sin.
5 Amaziya anasonkhanitsa anthu a ku Yuda ndipo anawapatsa zochita molingana ndi mabanja awo kukhala anthu olamulira 1,000, ndi olamulira 100 pa Ayuda onse ndi Benjamini. Ndipo iye anawerenga amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo napeza kuti analipo amuna 300,000 okonzeka kugwira ntchito ya usilikali, okhoza kugwiritsa ntchito mkondo ndi chishango.
Moreover Amaziah gathered Judah together, and appointed them according to their fathers' houses, for heads of thousands and heads of hundreds, even all Judah and Benjamin. And he numbered them from twenty years old and upward, and found them three hundred thousand chosen men, able to go forth to war, who could handle spear and shield.
6 Iye analembanso ntchito anthu odziwa nkhondo 100,000 ochokera ku Israeli pa mtengo wa makilogalamu 3,400 a siliva.
He also hired a hundred thousand mighty men of valor out of Israel for a hundred talents of silver.
7 Koma munthu wa Mulungu anabwera kwa iye ndipo anati, “Inu mfumu, asilikali awa ochokera ku Israeli asapite ndi inu, pakuti Yehova sali ndi Israeli kapena ndi aliyense wa anthu a Efereimu.
But there came a man of God to him, saying, O king, let not the army of Israel go with thee. For Jehovah is not with Israel, namely, with all the sons of Ephraim.
8 Ngakhale mupite ndi kuchita nkhondo molimba mtima, Mulungu adzakugonjetsani pamaso pa adani anu, pakuti Mulungu ali ndi mphamvu yothandiza kapena kugonjetsa.”
But if thou are going, do it. Be strong for the battle, because God will cast thee down before the enemy, for God has power to help, and to cast down.
9 Amaziya anafunsa munthu wa Mulungu kuti, “Koma nanga za makilogalamu aja a siliva amene ndapereka kwa asilikali a Israeli?” Munthu wa Mulungu anayankha kuti, “Yehova atha kukupatsani zambiri kuposa zimenezo.”
And Amaziah said to the man of God, But what shall we do for the hundred talents which I have given to the army of Israel? And the man of God answered, Jehovah is able to give thee much more than this.
10 Choncho Amaziya anachotsa asilikali amene anabwera kwa iye kuchokera ku Efereimu ndipo anawatumiza kwawo. Iwo anakwiyira anthu a ku Yuda ndipo anapita kwawo atapsa mtima kwambiri.
Then Amaziah separated them, namely, the army that came to him out of Ephraim, to go home again. Therefore their anger was greatly kindled against Judah, and they returned home in fierce anger.
11 Ndipo Amaziya analimba mtima ndipo anatsogolera gulu lake lankhondo ku Chigwa cha Mchere, kumene anapha anthu 10,000 a ku Seiri.
And Amaziah took courage, and led forth his people, and went to the Valley of Salt, and smote ten thousand of the sons of Seir.
12 Gulu la ankhondo la Yuda linagwiranso anthu amoyo 10,000, napita nawo pamwamba pa thanthwe ndipo anawaponya pansi kotero kuti onse ananyenyeka.
And the sons of Judah carried away ten thousand alive, and brought them to the top of the rock, and cast them down from the top of the rock, so that they all were broken in pieces.
13 Pa nthawi imeneyi asilikali amene Amaziya anawabweza ndipo sanawalole kuti achite nawo nkhondo, anakathira nkhondo mizinda ya Yuda kuyambira ku Samariya mpaka ku Beti-Horoni. Iwo anapha anthu 3,000 ndipo anafunkha katundu wambiri.
But the men of the army whom Amaziah sent back, that they should not go with him to battle, fell upon the cities of Judah, from Samaria even to Beth-horon, and smote three thousand of them, and took much spoil.
14 Amaziya atabwerera kuja anakapha Aedomu, anabweretsa milungu ya anthu a ku Seiri. Ndipo anayika kuti ikhale milungu yake, ankayipembedza ndi kupereka nsembe zopsereza.
Now it came to pass, after Amaziah came from the slaughter of the Edomites, that he brought the gods of the sons of Seir, and set them up to be his gods, and bowed down himself before them, and burned incense to them.
15 Yehova anakwiyira Amaziya, ndipo anamutumizira mneneri amene anati, “Nʼchifukwa chiyani mukupembedza milungu ya anthu awa, imene sinathe kupulumutsa anthu ake mʼdzanja lanu?”
Therefore the anger of Jehovah was kindled against Amaziah. And he sent a prophet to him, who said to him, Why have thou sought after the gods of the people, which have not delivered their own people out of thy hand?
16 Iye ali kuyankhula, mfumu inati, “Kodi ife takusankha iwe kuti ukhale mlangizi wa mfumu? Khala chete! Ufuna kuphedweranji?” Choncho mneneriyo analeka koma anati, “Ine ndikudziwa kuti Mulungu watsimikiza kukuwonongani chifukwa mwachita izi ndipo simunamvere uphungu wanga.”
And it came to pass, as he talked with him, that the king said to him, Have we made thee of the king's counsel? Cease. Why should thou be smitten? Then the prophet ceased, and said, I know that God has determined to destroy thee, because thou have done this, and have not hearkened to my counsel.
17 Amaziya mfumu ya ku Yuda, atafunsa alangizi ake, anatumiza mawu awa kwa Yowasi mwana wa Yehowahazi mwana wa Yehu, mfumu ya Israeli: “Bwera udzakumane nane maso ndi maso.”
Then Amaziah king of Judah took advice, and sent to Joash, the son of Jehoahaz the son of Jehu, king of Israel, saying, Come, let us look each other in the face.
18 Koma Yowasi mfumu ya Israeli inayankha Amaziya mfumu ya Yuda kuti, “Nthawi ina kamtengo kaminga ka ku Lebanoni kanatumiza mawu kwa mkungudza wa ku Lebanoni kuti, ‘Pereka mwana wako wamkazi kwa mwana wanga kuti amukwatire!’ Koma chirombo cha ku Lebanoni chinabwera ndi kupondaponda mtengo wa minga uja.
And Joash king of Israel sent to Amaziah king of Judah, saying, The thistle that was in Lebanon sent to the cedar that was in Lebanon, saying, Give thy daughter to my son to wife. And there passed by a wild beast that was in Lebanon, and trampled down the thistle.
19 Iwe ukuti wagonjetsa Edomu, ndipo tsopano ukudzikuza ndi kudzitamandira, koma khala kwanu komweko! Nʼchifukwa chiyani ukufuna mavuto ndi kudzichititsa kuti ugwe pamodzinso ndi Yuda?”
Thou say, Lo, I have smitten Edom. And thy heart lifts thee up to boast. Remain now at home. Why should thou meddle to thy hurt, that thou should fall, even thou, and Judah with thee?
20 Komabe Amaziya sanamvere pakuti ndi Mulungu amene anakonzeratu kuti awapereke kwa Yehowasi, chifukwa iwo amapembedza milungu ya ku Edomu.
But Amaziah would not hear, for it was of God, that he might deliver them into the hand of their enemies, because they had sought after the gods of Edom.
21 Kotero Yowasi mfumu ya Israeli inakamuthira nkhondo. Iye ndi Amaziya anayangʼanana maso ndi maso ku Beti-Semesi ku Yuda.
So Joash king of Israel went up. And he and Amaziah king of Judah looked each other in the face at Beth-shemesh, which belongs to Judah.
22 Yuda anagonjetsedwa ndi Israeli ndipo munthu aliyense anathawira kwawo.
And Judah was put to the worse before Israel, and they fled every man to his tent.
23 Yehowahazi mfumu ya Israeli inagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yowasi, mwana wa Ahaziya ku Beti-Semesi. Yehowasi anabwera naye ku Yerusalemu ndipo anagwetsa khoma la Yerusalemu kuyambira pa Chipata cha Efereimu mpaka ku Chipata Chapangodya, khoma lotalika mamita 180.
And Joash king of Israel took Amaziah king of Judah, the son of Joash the son of Jehoahaz, at Beth-shemesh, and brought him to Jerusalem, and broke down the wall of Jerusalem from the gate of Ephraim to the corner gate, four hundred cubits.
24 Iye anatenga golide ndi siliva yense ndi zida zonse zimene zimapezeka mʼNyumba ya Mulungu zimene ankazisamalira Obedi-Edomu, pamodzinso ndi chuma cha mʼnyumba yaufumu ndipo anatenga anthu ngati chikole.
And he took all the gold and silver, and all the vessels that were found in the house of God with Obed-edom, and the treasures of the king's house, also the hostages, and returned to Samaria.
25 Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anakhala ndi moyo kwa zaka khumi ndi zisanu atamwalira Yehowasi mwana wa Yehowahazi mfumu ya Israeli.
And Amaziah the son of Joash king of Judah lived fifteen years after the death of Joash son of Jehoahaz king of Israel.
26 Ntchito zina za mfumu Amaziya, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli?
Now the rest of the acts of Amaziah, first and last, behold, are they not written in the book of the kings of Judah and Israel?
27 Kuyambira nthawi imene Amaziya analeka kutsatira Yehova anthu anamukonzera chiwembu mu Yerusalemu ndipo anathawira ku Lakisi, koma adaniwo anatumiza anthu ku Lakisiko ndipo anamupha komweko.
Now from the time that Amaziah turned away from following Jehovah they made a conspiracy against him in Jerusalem, and he fled to Lachish. But they sent after him to Lachish, and killed him there.
28 Iwo anabwera naye ali pa kavalo ndipo anayikidwa mʼmanda ndi makolo ake mu mzinda wa Yuda.
And they brought him upon horses, and buried him with his fathers in the city of Judah.

< 2 Mbiri 25 >