< 2 Mbiri 2 >

1 Solomoni anatsimikiza zoti amange Nyumba ya Dzina la Yehova ndi nyumba yake yaufumu.
And Solomon saith to build a house for the name of Jehovah, and a house for his kingdom,
2 Iye analemba ntchito anthu 70,000 onyamula katundu ndi anthu 80,000 okumba miyala ku mapiri ndiponso akapitawo 3,600 oyangʼanira anthuwo.
and Solomon numbereth seventy thousand men bearing burden, and eighty thousand men hewing in the mountain, and overseers over them — three thousand and six hundred.
3 Solomoni anatumiza uthenga uwu kwa Hiramu mfumu ya ku Turo: “Munditumizire mitengo ya mkungudza monga munachitira ndi abambo anga pamene munawatumizira mitengo ya mkungudza yomangira nyumba yaufumu yokhalamo.
And Solomon sendeth unto Huram king of Tyre, saying, 'When thou hast dealt with David my father, then thou dost send to him cedars to build for him a house to dwell in;
4 Tsono ine ndikufuna kumanga Nyumba ya Yehova Mulungu wanga ndi kuyipereka kwa Iye kuti tiziyikamo buledi wopatulika nthawi zonse ndiponso kuperekeramo nsembe zopsereza mmawa uliwonse ndi madzulo ndi pa masabata ndi pa masiku a chikondwerero cha mwezi watsopano ndiponso pa masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova Mulungu wathu, monga mwa malamulo a Aisraeli mpaka muyaya.
lo, I am building a house to the name of Jehovah my God, to sanctify [it] to Him, to make perfume before Him, perfume of spices, and a continual arrangement, and burnt-offerings at morning and at evening, at sabbaths, and at new moons, and at appointed seasons of Jehovah our God; to the age this [is] on Israel.
5 “Nyumba ya Mulungu imene ndidzamange idzakhala yayikulu, chifukwa Mulungu wathu ndi wamkulu kuposa milungu ina yonse.
'And the house that I am building [is] great, for greater [is] our God than all gods;
6 Koma ndani angathe kumumangira Iye Nyumba, pakuti mlengalenga, ngakhale kumwamba kwenikweni sikungamukwane? Tsono ine ndine yani kuti ndimangire Iyeyo Nyumba, kupatula malo chabe opserezerapo nsembe pamaso pake?
and who doth retain strength to build to Him a house, for the heavens, even the heavens of the heavens, do not contain Him? and who [am] I that I do build to Him a house, except to make perfume before Him?
7 “Tsono tumizireni munthu waluso pa ntchito zagolide ndi siliva, mkuwa ndi chitsulo, nsalu yapepo ndi yofiira ndi yobiriwira ndiponso waluso losema, kuti adzagwire ntchito mu Yuda ndi Yerusalemu pamodzi ndi anthu aluso amene abambo anga Davide anandipatsa.
'And now, send to me a wise man to work in gold, and in silver, and in brass, and in iron, and in purple, and crimson, and blue, and knowing to grave gravings with the wise men who [are] with me in Judah and in Jerusalem, whom David my father prepared;
8 “Munditumizirenso mitengo ya mkungudza, payini ndiponso matabwa a mʼbawa wa ku Lebanoni, pakuti ndikudziwa kuti anthu anu ali ndi luso locheka matabwa kumeneko. Antchito anga adzagwira ntchito pamodzi ndi antchito anu
and send to me cedar-trees, firs, and algums from Lebanon, for I have known that thy servants know to cut down trees of Lebanon, and lo, my servants [are] with thy servants,
9 kuti andipatse matabwa ambiri, chifukwa Nyumba imene ndikumanga iyenera kukhala yayikulu ndi yokongola.
even to prepare for me trees in abundance, for the house that I am building [is] great and wonderful.
10 Ine ndidzalipira antchito anu amene adzacheke matabwa matani 1,000 a tirigu wopunthapuntha, matani 2,000 a barele, malita 440,000 a vinyo, ndiponso malita 440,000 a mafuta a olivi.”
'And lo, to hewers, to those cutting the trees, I have given beaten wheat to thy servants, cors twenty thousand, and barley, cors twenty thousand, and wine, baths twenty thousand, and oil, baths twenty thousand.'
11 Hiramu, mfumu ya ku Turo, anamuyankha Solomoni pomulembera kalata kuti, “Chifukwa Yehova amakonda anthu ake, wayika iwe kukhala mfumu yawo.”
And Huram king of Tyre saith in writing, and sendeth unto Solomon: 'In the love of Jehovah to His people He hath given thee king over them.'
12 Ndipo Hiramu anawonjezera kunena kuti, “Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli, amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi! Iye wamupatsa Davide mwana wanzeru, wodzaza ndi luntha ndi wozindikira, amene adzamanga Nyumba ya Mulungu ndi kudzimangira yekha nyumba yaufumu.
And Huram saith, 'Blessed [is] Jehovah, God of Israel, who made the heavens and the earth, who hath given to David the king a wise son, knowing wisdom and understanding, who doth build a house for Jehovah, and a house for his kingdom.
13 “Ine ndikukutumizira Hiramu Abi, munthu wa luso lalikulu,
'And now, I have sent a wise man having understanding, of Huram my father,
14 amene amayi ake anali wochokera ku Dani ndipo abambo ake anali a ku Turo. Iye anaphunzitsidwa kugwira ntchito zagolide ndi siliva, mkuwa ndi chitsulo, miyala yokongola ndi matabwa, ndiponso nsalu zofewa zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Alinso ndi luso la zosemasema ndipo atha kupanga chilichonse chimene wapatsidwa. Iye adzagwira ntchito ndi amisiri anu ndi a mbuye wanga, Davide abambo anu.
(son of a woman of the daughters of Dan, and his father a man of Tyre), knowing to work in gold, and in silver, in brass, in iron, in stones, and in wood, in purple, in blue, and in fine linen, and in crimson, and to grave any graving, and to devise any device that is given to him, with thy wise men, and the wise men of my lord David thy father.
15 “Tsono mbuye wanga tumizirani antchito anu tirigu ndi barele, mafuta a olivi ndi vinyo zimene mwalonjeza,
'And, now, the wheat, and the barley, the oil, and the wine, as my lord said, let him send to his servants,
16 ndipo ife tidzadula mitengo yonse imene mukuyifuna kuchokera ku Lebanoni ndipo tidzayimanga pamodzi ndi kuyiyadamitsa pa madzi mpaka ku Yopa. Ndipo inu mudzatha kuyitenga mpaka ku Yerusalemu.”
and we — we cut trees out of Lebanon, according to all thy need, and bring them in to thee — floats by sea, to Joppa, and thou dost take them up to Jerusalem.'
17 Solomoni anawerenga alendo onse amene anali mu Israeli, potsatira chiwerengero chimene abambo ake Davide anachita ndipo panapezeka kuti analipo anthu 153,600.
And Solomon numbereth all the men, the sojourners who [are] in the land of Israel, after the numbering with which David his father numbered them, and they are found a hundred and fifty thousand, and three thousand, and six hundred;
18 Iye anayika anthu 70,000 kuti akhale onyamula katundu ndi anthu 80,000 kuti akhale ophwanya miyala mʼmapiri, anthu 3,600 anawayika kukhala akapitawo oyangʼanira anthu pa ntchitoyo.
and he maketh of them seventy thousand burden-bearers, and eighty thousand hewers in the mountain, and three thousand and six hundred overseers, to cause the people to work.

< 2 Mbiri 2 >