< 2 Mbiri 17 >

1 Yehosafati mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake ndipo anadzilimbitsa pofuna kulimbana ndi Israeli.
Namesto njega je zakraljeval njegov sin Józafat in se okrepil zoper Izraela.
2 Iye anayika magulu a asilikali mʼmizinda yonse yotetezedwa ya Yuda, ndipo anamanga maboma mu Yuda ndi mʼmizinda yonse ya Efereimu imene Asa abambo ake analanda.
Namestil je sile v vsa utrjena Judova mesta in postavil garnizije v Judovi deželi in v Efrájimovih mestih, ki jih je zavzel njegov oče Asá.
3 Yehova anali ndi Yehosafati chifukwa mʼzaka zoyambirira anatsatira makhalidwe a Davide abambo ake. Iye sanafunsire kwa Abaala.
Gospod je bil z Józafatom, ker je hodil po prvih poteh svojega očeta Davida in ni iskal Báalov,
4 Koma anafunafuna Mulungu wa abambo ake ndipo anatsatira malamulo ake osati zochita za Israeli.
temveč je sledil Gospodu, Bogu svojega očeta in hodil po njegovih zapovedih in ne po Izraelovih ravnanjih.
5 Yehova anakhazikitsa kolimba ufumuwo mʼmanja mwake ndipo Ayuda onse anabweretsa mphatso kwa Yehosafati, kotero kuti anali ndi chuma ndi ulemu wambiri.
Zato je Gospod utrdil kraljestvo v njegovi roki. Ves Juda je Józafatu prinesel darila in imel je bogastva, čast in obilje.
6 Mtima wake anawupereka kutsatira Yehova, kuwonjezera apo, anachotsa malo onse achipembedzo ndi mafano a Asera mu Yuda.
Njegovo srce je bilo vzdignjeno na Gospodovih poteh. Poleg tega je iz Juda odstranil visoke kraje in ašere.
7 Mʼchaka chachitatu cha ufumu wake, iye anatuma akuluakulu ake Beni-Haili, Obadiya, Zekariya, Netaneli ndi Mikaya kukaphunzitsa mʼmizinda ya Yuda.
Tudi v tretjem letu svojega kraljevanja je poslal k svojim princem, torej k Ben Hajilu, k Obadjáju, k Zeharjáju, k Netanélu in k Mihajáju, da bi učili po Judovih mestih.
8 Pamodzi ndi iwo panali Alevi ena: Semaya, Netaniya, Zebadiya, Asaheli, Semiramoti, Yonatani, Adoniya, Tobiya ndi Tobu-Adoniya ndiponso ansembe Elisama ndi Yehoramu.
Z njimi je poslal Lévijevce, torej Šemajája, Netanjája, Zebadjája, Asaéla, Šemiramóta, Jehonatana, Adoníja, Tobija, Tob Adoníja, Lévijevce in z njimi duhovnika Elišamája in Jehoráma.
9 Iwo anaphunzitsa mu Yuda monse atatenga Buku la Malamulo a Yehova iwo anayenda mʼmizinda yonse ya ku Yuda ndipo anaphunzitsa anthu.
Učili so v Judu in s seboj so imeli knjigo Gospodove postave in šli so naokoli po vseh Judovih mestih in učili ljudstvo.
10 Kuopsa kwa Yehova kunali pa maufumu onse a mayiko oyandikana ndi Yuda, kotero kuti sanachite nkhondo ndi Yehosafati.
Gospodov strah je padel na vsa kraljestva dežel, ki so bile naokoli Juda, tako da zoper Józafata niso bojevali nobene vojne.
11 Afilisti ena anabweretsa kwa Yehosafati mphatso ndi siliva ngati msonkho, ndipo Aarabu anabweretsa ziweto: nkhosa zazimuna 7,700 ndi mbuzi 7,700.
Tudi nekateri izmed Filistejcev so Józafatu prinesli darila in davek srebra. Arabci so mu privedli trope, sedem tisoč sedemsto ovnov in sedem tisoč sedemsto kozlov.
12 Mphamvu za Yehosafati zinkakulirakulira. Iye anamanga malo otetezedwa ndi mizinda yosungiramo chuma mu Yuda
Józafat je postal silno velik in v Judu je zgradil gradove in skladiščna mesta.
13 ndipo anali ndi katundu wambiri mʼmizinda ya Yuda. Iye anayikanso asilikali odziwa bwino nkhondo mu Yerusalemu.
Po Judovih mestih je imel mnogo posla. In v Jeruzalemu so bili bojevniki, močni junaški možje.
14 Chiwerengero chawo potsata mabanja awo chinali chotere: kuchokera ku Yuda, atsogoleri a magulu 1,000; mtsogoleri Adina, anali ndi anthu 300,000 odziwa nkhondo;
To so njihova števila glede na hišo njihovih očetov. Iz Juda poveljniki nad tisočimi: vodja Adnáh in z njim tristo tisoč močnih junaških mož.
15 otsatana naye, mtsogoleri Yehohanani, anali ndi anthu 280,000;
Poleg njega je bil poveljnik Johanán in z njim dvesto osemdeset tisoč.
16 otsatana naye, Amasiya mwana wa Zikiri amene anadzipereka yekha kutumikira Yehova, anali ndi anthu 200,000.
Poleg njega je bil Zihríjev sin Amasjá, ki se je voljno daroval Gospodu in z njim dvesto tisoč močnih junaških mož.
17 Kuchokera ku Benjamini: Eliada, msilikali wolimba mtima, anali ndi anthu 200,000 amene anali ndi mauta ndi zishango;
Od Benjamina Eljadá, mogočen hraber mož in z njim dvesto tisoč z lokom in ščitom oboroženih mož.
18 otsatana naye, Yehozabadi, anali ndi anthu 180,000 okonzekera nkhondo.
Poleg njega je bil Jozabád in z njim sto osemdeset tisoč pripravljenih za vojno.
19 Awa ndi anthu amene ankatumikira mfumu osawerengera amene anawayika mʼmizinda yotetezedwa mʼdziko lonse la Yuda.
Ti so čakali na kralja, poleg tistih, ki jih je kralj namestil v utrjenih mestih po vsem Judu.

< 2 Mbiri 17 >