< 2 Mbiri 17 >

1 Yehosafati mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake ndipo anadzilimbitsa pofuna kulimbana ndi Israeli.
Jehoshaphat son of Asa became king in his place. Jehoshaphat strengthened himself against Israel.
2 Iye anayika magulu a asilikali mʼmizinda yonse yotetezedwa ya Yuda, ndipo anamanga maboma mu Yuda ndi mʼmizinda yonse ya Efereimu imene Asa abambo ake analanda.
He placed forces in all the fortified cities of Judah, and set garrisons in the land of Judah and in the cities of Ephraim, which Asa his father had captured.
3 Yehova anali ndi Yehosafati chifukwa mʼzaka zoyambirira anatsatira makhalidwe a Davide abambo ake. Iye sanafunsire kwa Abaala.
Yahweh was with Jehoshaphat because he walked in the first ways of his father David, and did not seek the Baals.
4 Koma anafunafuna Mulungu wa abambo ake ndipo anatsatira malamulo ake osati zochita za Israeli.
Instead, he relied on the God of his father, and walked in his commandments, not after the behavior of Israel.
5 Yehova anakhazikitsa kolimba ufumuwo mʼmanja mwake ndipo Ayuda onse anabweretsa mphatso kwa Yehosafati, kotero kuti anali ndi chuma ndi ulemu wambiri.
So Yahweh established the rule in his hand; all Judah brought tribute to Jehoshaphat. He had riches and honor in abundance.
6 Mtima wake anawupereka kutsatira Yehova, kuwonjezera apo, anachotsa malo onse achipembedzo ndi mafano a Asera mu Yuda.
His heart was committed to Yahweh's ways. He also removed the high places and the Asherah poles from Judah.
7 Mʼchaka chachitatu cha ufumu wake, iye anatuma akuluakulu ake Beni-Haili, Obadiya, Zekariya, Netaneli ndi Mikaya kukaphunzitsa mʼmizinda ya Yuda.
In the third year of his reign he sent his officials Ben-Hail, Obadiah, Zechariah, Nethanel, and Micaiah, to teach in the cities of Judah.
8 Pamodzi ndi iwo panali Alevi ena: Semaya, Netaniya, Zebadiya, Asaheli, Semiramoti, Yonatani, Adoniya, Tobiya ndi Tobu-Adoniya ndiponso ansembe Elisama ndi Yehoramu.
With them were Levites: Shemaiah, Nethaniah, Zebadiah, Asahel, Shemiramoth, Jehonathan, Adonijah, Tobijah, and Tob-Adonijah; and with them were the priests Elishama and Jehoram.
9 Iwo anaphunzitsa mu Yuda monse atatenga Buku la Malamulo a Yehova iwo anayenda mʼmizinda yonse ya ku Yuda ndipo anaphunzitsa anthu.
They taught in Judah, having the book of the law of Yahweh with them. They went about throughout all the cities of Judah and taught among the people.
10 Kuopsa kwa Yehova kunali pa maufumu onse a mayiko oyandikana ndi Yuda, kotero kuti sanachite nkhondo ndi Yehosafati.
Terror of Yahweh fell on all the kingdoms of the lands that were around Judah, so that they made no war against Jehoshaphat.
11 Afilisti ena anabweretsa kwa Yehosafati mphatso ndi siliva ngati msonkho, ndipo Aarabu anabweretsa ziweto: nkhosa zazimuna 7,700 ndi mbuzi 7,700.
Some of the Philistines brought Jehoshaphat presents, and silver as tribute. Arabians also brought him flocks, 7,700 rams, and 7,700 goats.
12 Mphamvu za Yehosafati zinkakulirakulira. Iye anamanga malo otetezedwa ndi mizinda yosungiramo chuma mu Yuda
Jehoshaphat became very powerful. He built fortresses and store cities in Judah.
13 ndipo anali ndi katundu wambiri mʼmizinda ya Yuda. Iye anayikanso asilikali odziwa bwino nkhondo mu Yerusalemu.
He had many supplies in the cities of Judah, and soldiers—strong, mighty men—in Jerusalem.
14 Chiwerengero chawo potsata mabanja awo chinali chotere: kuchokera ku Yuda, atsogoleri a magulu 1,000; mtsogoleri Adina, anali ndi anthu 300,000 odziwa nkhondo;
These were their divisions listed by the name of their fathers' houses: From Judah, the commanders of thousands; Adnah the commander, and with him 300,000 fighting men;
15 otsatana naye, mtsogoleri Yehohanani, anali ndi anthu 280,000;
next to him Jehohanan the commander, and with him 280,000 men;
16 otsatana naye, Amasiya mwana wa Zikiri amene anadzipereka yekha kutumikira Yehova, anali ndi anthu 200,000.
next to him Amasiah son of Zichri, who willingly offered to serve Yahweh; and with him 200,000 fighting men.
17 Kuchokera ku Benjamini: Eliada, msilikali wolimba mtima, anali ndi anthu 200,000 amene anali ndi mauta ndi zishango;
From Benjamin: Eliada a powerful man of courage, and with him 200,000 armed with bows and shields;
18 otsatana naye, Yehozabadi, anali ndi anthu 180,000 okonzekera nkhondo.
next to him Jehozabad, and with him 180,000 ready prepared for war.
19 Awa ndi anthu amene ankatumikira mfumu osawerengera amene anawayika mʼmizinda yotetezedwa mʼdziko lonse la Yuda.
These were those who served the king, besides those whom the king put in the fortified cities throughout all Judah.

< 2 Mbiri 17 >