< 2 Mbiri 16 >

1 Mʼchaka cha 36 cha ufumu wa Asa, Baasa mfumu ya Israeli inapita kukathira nkhondo dziko la Yuda. Anamangira mpanda mzinda wa Rama kuletsa aliyense kutuluka kapena kulowa mʼdziko la Asa mfumu ya Yuda.
In the sixe and thirtieth yeere of the reigne of Asa came Baasha king of Israel vp against Iudah, and built Ramah to let none passe out or goe in to Asa king of Iudah.
2 Ndipo Asa anatenga siliva ndi golide ku malo osungirako a mʼNyumba ya Mulungu ndi ku nyumba yake yaufumu ndi kuzitumiza kwa Beni-Hadadi mfumu ya Aramu imene inkakhala mu Damasiko.
Then Asa brought out siluer and gold out of the treasures of the house of the Lord, and of the Kings house, and sent to Benhadad King of Aram that dwelt at Damascus, saying,
3 Iye anati, “Pakhale pangano pakati pa inu ndi ine, monga zinalili pakati pa abambo anu ndi abambo anga. Taonani, ine ndikutumiza kwa inu siliva ndi golide. Tsopano thetsani mgwirizano wanu ndi Baasa mfumu ya Israeli kuti achoke kwa ine.”
There is a couenant betweene me and thee, and betweene my father and thy father: behold, I haue sent thee siluer and golde: come, breake thy league with Baasha King of Israel that hee may depart from me.
4 Beni-Hadadi anagwirizana ndi mfumu Asa ndipo anatumiza olamulira nkhondo ake kukathira nkhondo mizinda ya Israeli. Iwo anagonjetsa Iyoni, Dani, Abeli-Maimu ndi mizinda yonse yosungira chuma ya Nafutali.
And Benhadad hearkened vnto King Asa, and sent the captaines of the armies which hee had, against the cities of Israel. And they smote Iion, and Dan, and Abel-maim, and all the store cities of Naphtali.
5 Baasa atamva izi, anasiya kumanga Rama ndipo anayimitsa ntchito yakeyo.
And when Baasha heard it, he left building of Ramah, and let his worke cease.
6 Ndipo mfumu Asa anabwera ndi Ayuda onse, ndipo anachotsa miyala ndi matabwa ku Rama amene Baasa amagwiritsa ntchito. Ndi zimenezi Asa ankamangira Geba ndi Mizipa.
Then Asa the King tooke all Iudah, and caryed away the stones of Ramah and the tymber thereof, wherewith Baasha did builde, and he built therewith Geba and Mizpah.
7 Nthawi imeneyi mlosi Hanani anabwera kwa Asa mfumu ya Yuda ndipo anati kwa iye, “Chifukwa chakuti munadalira mfumu ya Aramu osati Yehova Mulungu wanu, gulu la ankhondo la mfumu ya ku Aramu lapulumuka mʼmanja mwanu.
And at that same time Hanani the Seer came to Asa King of Iudah, and saide vnto him, Because thou hast rested vpon the king of Aram, and not rested in the Lord thy God, therefore is the hoste of the King of Aram escaped out of thine hande.
8 Kodi Akusi ndi Alibiya sanali gulu lankhondo lamphamvu lokhala ndi magaleta ochuluka ndi okwera magaleta ake? Koma pamene inu munadalira Yehova, Iye anawapereka mʼdzanja lanu.
The Ethiopians and the Lubims, were they not a great hoste with charets and horsemen, exceeding many? yet because thou diddest rest vpon the Lord, he deliuered them into thine had.
9 Pakuti Yehova amayangʼana uku ndi uku pa dziko lonse lapansi kuti alimbikitse iwo amene mitima yawo ayipereka kwathunthu kwa Iye. Inu mwachita chinthu chopusa ndipo kuyambira lero mudzakhala pa nkhondo.”
For the eyes of the Lord beholde all the earth to shewe him selfe strong with them that are of perfite heart towarde him: thou hast then done foolishly in this: therefore from henceforth thou shalt haue warres.
10 Asa anamupsera mtima mlosi uja chifukwa cha izi mwakuti anakwiya kwambiri namuyika mʼndende. Pa nthawi yomweyonso Asa anazunza mwankhanza anthu ena.
Then Asa was wroth with the Seer, and put him into a prison: for he was displeased with him, because of this thing. And Asa oppressed certaine of the people at the same time.
11 Ntchito zina za mfumu Asa, kuyambira pachiyambi mpaka kumapeto zalembedwa mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
And behold, the actes of Asa first and last, loe, they are written in the booke of the Kings of Iudah and Israel.
12 Mʼchaka cha 39 cha ufumu wake, Asa anayamba kudwala nthenda ya mapazi. Ngakhale nthendayo inali yaululu kwambiri, komabe iye sanafunefune Yehova, koma anafuna thandizo kwa asingʼanga.
And Asa in the nine and thirtieth yeere of his reigne was diseased in his feete, and his disease was extreme: yet he sought not the Lord in his disease, but to the Phisicions.
13 Ndipo mʼchaka cha 41 cha ufumu wake, Asa anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake.
So Asa slept with his fathers, and dyed in the one and fourtieth yeere of his reigne.
14 Iye anayikidwa mʼmanda amene anadzisemera yekha mu Mzinda wa Davide. Anagoneka mtembo wake pa chithatha chimene anayikapo zonunkhira zamitundumitundu, ndipo anasonkha chimoto chachikulu pomuchitira ulemu.
And they buryed him in one of his sepulchres, which he had made for him selfe in the citie of Dauid, and layed him in the bed, which they had filled with sweete odours and diuers kindes of spices made by the arte of the apoticarie: and they burnt odours for him with an exceeding great fire.

< 2 Mbiri 16 >