< 2 Mbiri 16 >

1 Mʼchaka cha 36 cha ufumu wa Asa, Baasa mfumu ya Israeli inapita kukathira nkhondo dziko la Yuda. Anamangira mpanda mzinda wa Rama kuletsa aliyense kutuluka kapena kulowa mʼdziko la Asa mfumu ya Yuda.
In the thirty-sixth year of the reign of Asa, Baasha king of Israel went up against Judah, and built Ramah, that he might not allow anyone to go out or come in to Asa king of Judah.
2 Ndipo Asa anatenga siliva ndi golide ku malo osungirako a mʼNyumba ya Mulungu ndi ku nyumba yake yaufumu ndi kuzitumiza kwa Beni-Hadadi mfumu ya Aramu imene inkakhala mu Damasiko.
Then Asa brought out silver and gold out of the treasures of the house of Jehovah and of the king's house, and sent to Ben-hadad king of Syria, who dwelt at Damascus, saying,
3 Iye anati, “Pakhale pangano pakati pa inu ndi ine, monga zinalili pakati pa abambo anu ndi abambo anga. Taonani, ine ndikutumiza kwa inu siliva ndi golide. Tsopano thetsani mgwirizano wanu ndi Baasa mfumu ya Israeli kuti achoke kwa ine.”
There is a league between me and thee, as between my father and thy father. Behold, I have sent thee silver and gold. Go, break thy league with Baasha king of Israel that he may depart from me.
4 Beni-Hadadi anagwirizana ndi mfumu Asa ndipo anatumiza olamulira nkhondo ake kukathira nkhondo mizinda ya Israeli. Iwo anagonjetsa Iyoni, Dani, Abeli-Maimu ndi mizinda yonse yosungira chuma ya Nafutali.
And Ben-hadad hearkened to king Asa, and sent the captains of his armies against the cities of Israel. And they smote Ijon, and Dan, and Abel-maim, and all the store-cities of Naphtali.
5 Baasa atamva izi, anasiya kumanga Rama ndipo anayimitsa ntchito yakeyo.
And it came to pass, when Baasha heard of it, that he left off building Ramah, and let his work cease.
6 Ndipo mfumu Asa anabwera ndi Ayuda onse, ndipo anachotsa miyala ndi matabwa ku Rama amene Baasa amagwiritsa ntchito. Ndi zimenezi Asa ankamangira Geba ndi Mizipa.
Then Asa the king took all Judah, and they carried away the stones of Ramah, and the timber of it, with which Baasha had built. And he built Geba and Mizpah with it.
7 Nthawi imeneyi mlosi Hanani anabwera kwa Asa mfumu ya Yuda ndipo anati kwa iye, “Chifukwa chakuti munadalira mfumu ya Aramu osati Yehova Mulungu wanu, gulu la ankhondo la mfumu ya ku Aramu lapulumuka mʼmanja mwanu.
And at that time Hanani the seer came to Asa king of Judah, and said to him, Because thou have relied on the king of Syria, and have not relied on Jehovah thy God, therefore the army of the king of Syria has escaped out of thy hand.
8 Kodi Akusi ndi Alibiya sanali gulu lankhondo lamphamvu lokhala ndi magaleta ochuluka ndi okwera magaleta ake? Koma pamene inu munadalira Yehova, Iye anawapereka mʼdzanja lanu.
Were not the Ethiopians and the Lubim a huge army, with chariots and horsemen exceedingly many? Yet, because thou relied on Jehovah, he delivered them into thy hand.
9 Pakuti Yehova amayangʼana uku ndi uku pa dziko lonse lapansi kuti alimbikitse iwo amene mitima yawo ayipereka kwathunthu kwa Iye. Inu mwachita chinthu chopusa ndipo kuyambira lero mudzakhala pa nkhondo.”
For the eyes of Jehovah run to and fro throughout the whole earth, to show himself strong on behalf of those whose heart is perfect toward him. In this thou have done foolishly, for from henceforth thou shall have wars.
10 Asa anamupsera mtima mlosi uja chifukwa cha izi mwakuti anakwiya kwambiri namuyika mʼndende. Pa nthawi yomweyonso Asa anazunza mwankhanza anthu ena.
Then Asa was angry with the seer, and put him in the prison-house. For he was in a rage with him because of this thing. And Asa oppressed some of the people at the same time.
11 Ntchito zina za mfumu Asa, kuyambira pachiyambi mpaka kumapeto zalembedwa mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
And, behold, the acts of Asa, first and last, lo, they are written in the book of the kings of Judah and Israel.
12 Mʼchaka cha 39 cha ufumu wake, Asa anayamba kudwala nthenda ya mapazi. Ngakhale nthendayo inali yaululu kwambiri, komabe iye sanafunefune Yehova, koma anafuna thandizo kwa asingʼanga.
And in the thirty-ninth year of his reign Asa was diseased in his feet. His disease was exceedingly great, yet in his disease he did not seek for Jehovah, but to the physicians.
13 Ndipo mʼchaka cha 41 cha ufumu wake, Asa anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake.
And Asa slept with his fathers, and died in the forty-first year of his reign.
14 Iye anayikidwa mʼmanda amene anadzisemera yekha mu Mzinda wa Davide. Anagoneka mtembo wake pa chithatha chimene anayikapo zonunkhira zamitundumitundu, ndipo anasonkha chimoto chachikulu pomuchitira ulemu.
And they buried him in his own sepulchers, which he had hewn out for himself in the city of David, and laid him in the bed which was filled with sweet odors and various kinds of spices prepared by the perfumers' art. And they made a very great burning for him.

< 2 Mbiri 16 >