< 2 Mbiri 14 >

1 Tsono Abiya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide. Asa mwana wake anakhala mfumu mʼmalo mwake ndipo pa masiku ake, dziko linakhala pa mtendere kwa zaka khumi.
So Abijah slept with his fathers, and they buried him in the city of David. And Asa his son reigned in his stead. In his days the land was quiet ten years.
2 Asa anachita zabwino ndi zolungama pamaso pa Yehova Mulungu wake.
And Asa did that which was good and right in the eyes of Jehovah his God.
3 Iye anachotsa maguwa achilendo ndi malo opembedzerapo mafano, anaphwanya zipilala za miyala yachipembedzo ndi kugwetsa mafano a Asera.
For he took away the foreign altars, and the high places, and broke down the pillars, and hewed down the Asherim,
4 Asa analamula Yuda kuti afunefune Yehova Mulungu wa makolo awo ndi kumvera malamulo ndi zolamulira zake.
and commanded Judah to seek Jehovah, the God of their fathers, and to do the law and the commandment.
5 Iye anachotsa malo opembedzera mafano ndi maguwa ofukizira lubani mu mzinda uliwonse wa mu Yuda, ndipo mu ufumu wake munali mtendere pa nthawi ya ulamuliro wake.
Also he took away out of all the cities of Judah the high places and the sun-images. And the kingdom was quiet before him.
6 Asa anamanga mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda pakuti dziko linali pa mtendere. Panalibe amene anachita naye nkhondo mʼzaka zimenezo, pakuti Yehova anamupatsa mpumulo.
And he built fortified cities in Judah. For the land was quiet, and he had no war in those years, because Jehovah had given him rest.
7 Iye anati kwa Yuda “Tiyeni timange mizinda iyi ndipo timange makoma ndi nsanja, zitseko ndi zotchinga. Dzikoli likanali lathu chifukwa tafuna Yehova Mulungu wathu; tinamufuna Iye ndipo watipatsa mpumulo mbali zonse.” Kotero iwo anamanga ndi kukhala pa ulemerero.
For he said to Judah, Let us build these cities, and make about them walls, and towers, gates, and bars. The land is yet before us, because we have sought Jehovah our God. We have sought him, and he has given us rest on every side. So they built and prospered.
8 Asa anali ndi ankhondo 300,000 ochokera ku Yuda, okhala ndi zishango zikuluzikulu ndi mikondo, ndiponso ankhondo 280,000 ochokera ku Benjamini, okhala ndi zishango ndi mauta. Onsewa anali ankhondo amphamvu ndi olimba mtima.
And Asa had an army that bore bucklers and spears, out of Judah three hundred thousand, and out of Benjamin, that bore shields and drew bows, two hundred and eighty thousand. All these were mighty men of valor.
9 Zera wa ku Kusi anapita kukamenyana nawo ali ndi gulu lalikulu kwambiri la asilikali ndi magaleta 300 ndipo anafika mpaka ku Maresa.
And there came out against them Zerah the Ethiopian with an army of a million, and three hundred chariots. And he came to Mareshah.
10 Asa anapita kukakumana naye ndipo anakhala pa mizere yawo ya nkhondo mʼchigwa cha Zefata pafupi ndi Maresa.
Then Asa went out to meet him, and they set the battle in array in the valley of Zephathah at Mareshah.
11 Kenaka Asa anafuwulira Yehova Mulungu wake ndipo anati “Yehova palibe wina wofanana nanu kuti angathandize anthu opanda mphamvu pakati pa amphamvu. Tithandizeni Inu Yehova Mulungu wathu pakuti ife timadalira Inu ndipo mʼdzina lanu ife tabwera kudzalimbana ndi gulu la ankhondo lalikulu kwambiri ngati ili. Inu Yehova ndinu Mulungu wathu, musalole kuti munthu akupambaneni.”
And Asa cried to Jehovah his God, and said, Jehovah, there is none besides thee to help, between the mighty and him who has no strength. Help us, O Jehovah our God. For we rely on thee, and in thy name we come against this multitude. O Jehovah, thou are our God. Let not man prevail against thee.
12 Yehova anakantha Akusi pamaso pa Asa ndi Ayuda. Akusi anathawa,
So Jehovah smote the Ethiopians before Asa, and before Judah. And the Ethiopians fled.
13 ndipo Asa ndi ankhondo ake anawathamangitsa mpaka ku Gerari. Gulu lonse lalikulu lija la Akusi linaphedwa. Sanapezeke mmodzi wamoyo pakati pawo. Iwo anakanthidwa pamaso pa Yehova ndi asilikali ake. Anthu a ku Yuda anatenga katundu wambiri olanda ku nkhondo.
And Asa and the people who were with him pursued them to Gerar. And there fell of the Ethiopians so many that they could not recover themselves. For they were destroyed before Jehovah, and before his army. And they carried away very much booty.
14 Iwo anawononga midzi yonse yozungulira Gerari pakuti mantha aakulu wochokera kwa Yehova anagwera anthuwo. Analanda katundu wa midzi yonse, popeza kunali katundu wambiri kumeneko.
And they smote all the cities round about Gerar. For the fear of Jehovah came upon them. And they despoiled all the cities. For there was much spoil in them.
15 Anakathiranso nkhondo misasa ya anthu oweta ziweto ndipo anatenga nkhosa zambiri, mbuzi ndi ngamira. Atatero anabwerera ku Yerusalemu.
They also smote the tents of cattle, and carried away sheep in abundance, and camels, and returned to Jerusalem.

< 2 Mbiri 14 >