< 2 Mbiri 10 >

1 Rehobowamu anapita ku Sekemu, pakuti Aisraeli onse anapita kumeneko kuti akamulonge ufumu.
Forsothe Roboam yede forth in to Sichem; for al Israel came togidere thidur to make hym kyng.
2 Yeroboamu mwana wa Nebati atamva zimenezi (Iye anali ku Igupto, kumene anapita pothawa mfumu Solomoni) anabwerako kuchokera ku Igupto.
And whanne Jeroboam, the sone of Nabath, that was in Egipt, `for he fledde thidur bifor Salomon, hadde herd this, he turnyde ayen anoon.
3 Kotero anthu anakayitana Yeroboamu ndipo iye ndi Aisraeli onse anapita kwa Rehobowamu ndi kumuwuza kuti,
And thei clepiden hym, and he cam with al Israel, and thei spaken to Roboam, and seiden,
4 “Abambo anu anatisenzetsa goli lolemetsa koma tsopano mutipeputsire ntchito yolemetsayi ndi goli lolemerali limene analiyika pa ife ndipo ifeyo tidzakutumikirani.”
Thi fadir oppresside vs with ful hard yok; comaunde thou liytere thingis than thi fader, that settide on vs a greuouse seruage; and releese thou a litil of `the birthun, that we serue thee. And he seide,
5 Rehobowamu anayankha kuti, “Mukabwerenso pakapita masiku atatu.” Choncho anthuwo anachoka.
After thre daies turne ye ayen to me. And whanne the puple was goon, he took counsel with elde men,
6 Kenaka mfumu Rehobowamu anafunsira nzeru kwa akuluakulu amene ankatumikira abambo ake, Solomoni, pamene anali moyo. Iye anafunsa kuti, “Kodi inu mungandilangize zotani kuti ndiwayankhe anthu awa?”
that stoden bifor his fadir Salomon, while he lyuyde yit, and seide, What counsel yyuen ye, that Y answere to the puple?
7 Iwo anayankha kuti, “Ngati inu muwakomera mtima anthu awa ndi kuwasangalatsa ndiponso kuwayankha mawu abwino, iwo adzakutumikirani nthawi zonse.”
And thei seiden to hym, If thou plesist this puple, and makist hem softe bi meke wordis, thei schulen serue thee in al tyme.
8 Koma Rehobowamu anakana malangizo amene akuluakulu anamupatsa ndipo anakafunsira nzeru kwa anyamata amene anakula naye pamodzi komanso amamutumikira.
And he forsook the counsel of elde men, and bigan to trete with yonge men, that weren nurischid with hym, and weren in his cumpenye.
9 Iye anawafunsa kuti, “Kodi malangizo anu ndi otani? Kodi tiwayankhe chiyani anthu amene akunena kuti, ‘Peputsani goli limene abambo anu anayika pa ife?’”
And he seide to hem, What semeth to you? ether what owe Y answere to this puple, that seide to me, Releese thou the yok, which thi fadir puttide on vs?
10 Anyamata amene anakula pamodzi naye anamuyankha kuti, “Anthu amene anena kwa inu kuti, ‘Abambo anu anatisenzetsa goli lolemetsa koma inu mupeputse goli lathu,’ muwawuze kuti, ‘Chala changa chachingʼono ndi chachikulu kuposa chiwuno cha abambo anga.
And thei answeriden, as yonge men and nurschyd with hym in delicis, and seiden, Thus thou schalt speke to the puple that seide to thee, Thi fadir made greuouse oure yok, releese thou; and thus thou schalt answere to hem, My leeste fyngur is gretter than the leendis of my fader;
11 Abambo anga anakusenzetsani goli lolemetsa koma ine ndidzalichititsa kukhala lolemetsa kwambiri. Abambo anga anakukwapulani ndi zikoti wamba koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.’”
my fadir puttide on you a greuouse yok, and Y schal leie to a gretter birthun; my fadir beet you with scourgis, forsothe Y schal bete you with `scorpiouns, that is, hard knottid roopis.
12 Tsiku lachitatu Yeroboamu ndi anthu onse anabwerera kwa Rehobowamu monga ananenera mfumu kuti, “Mukabwerenso kwa ine pakapita masiku atatu.”
Therfor Jeroboam and al the puple cam to Roboam in the thridde dai, as he hadde comaundid to hem.
13 Mfumu inawayankha mwankhanza, pokana malangizo a akuluakulu aja.
And `the kyng answeride harde thingis, after that he hadde forsake the counsel of the eldere men,
14 Iye anatsatira malangizo a anyamata ndipo anati, “Abambo anga anakusenzetsani goli lolemetsa koma ine ndidzalichititsa kukhala lolemetsa kwambiri. Abambo anga anakukwapulani ndi zikoti wamba koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.”
and he spak bi the wille of the yonge men, My fadir puttide on you a greuouse yok, which Y schal make greuousere; my fadir beet you with scourgis, sotheli Y schal bete you with scorpiouns.
15 Kotero mfumu sinamvere anthuwo, pakuti zinthu izi zinali zochokera kwa Mulungu, kukwaniritsa mawu amene Yehova ananena kwa Yeroboamu mwana wa Nebati kudzera mwa Ahiya wa ku Silo.
And he assentide not to the preieris of the puple; for it was the wille of God, that his word schulde be fillid, which he hadde spoke bi the hond of Ahie of Silo to Jeroboam, sone of Nabath.
16 Aisraeli onse ataona kuti mfumu yakana kuwamvera, iwo anayankha mfumu kuti, “Kodi ife tili ndi gawo lanji mwa Davide, gawo lanji mwa mwana wa Yese? Inu Aisraeli! Pitani kwanu. Iwe Davide! Yangʼana banja lako.” Kotero Aisraeli onse anapita kwawo.
Sotheli whanne the kyng seide hardere thingis, al the puple spak thus to hym, No part is to vs in Dauid, nether eritage in the sone of Isai; Israel, turne thou ayen in to thi tabernaclis, sotheli thou, Dauid, feede thin hows. And Israel yede in to hise tabernaclis.
17 Koma Rehobowamu anakhala akulamulirabe Aisraeli amene amakhala mʼmizinda ya Yuda.
Forsothe Roboam regnede on the sones of Israel, that dwelliden in the citees of Juda.
18 Mfumu Rehobowamu inatuma Hadoramu amene ankayangʼanira ntchito yathangata, koma Aisraeli anamugenda miyala ndi kumupha. Koma mfumu Rehobowamu anakwera galeta lake ndi kuthawira ku Yerusalemu.
And kyng Roboam sente Adhuram, that was souereyn ouer the tributis; and the sones of Israel stonyden hym, and he was deed. Certis kyng Roboam hastide to stie in to the chare, and fledde in to Jerusalem.
19 Motero Israeli wakhala akuwukira banja la Davide mpaka lero lino.
And Israel yede awei fro the hows of Dauid `til to this dai. Forsothe it was doon, whanne al Israel hadde herd, that Jeroboam turnede ayen, thei senten, and clepiden hym, whanne the cumpeny was gaderid, and thei ordeyneden him king on al Israel; and no man, outakun the lynage of Juda aloone, suede `the hows of Dauid.

< 2 Mbiri 10 >