< 1 Timoteyo 2 >

1 Tsono choyamba ndikukupemphani kuti mupempherere anthu onse. Mapemphero anu akhale opemba, opempha, opempherera ena ndi oyamika.
Obsecro igitur primum omnium fieri obsecrationes, orationes, postulationes, gratiarum actiones pro omnibus hominibus:
2 Mupempherere mafumu ndi onse aulamuliro, kuti tikhale moyo wamtendere ndi bata, woopa Mulungu ndi oyera mtima.
pro regibus, et omnibus, qui in sublimitate sunt, ut quietam et tranquillam vitam agamus in omni pietate, et castitate.
3 Izi ndi zabwino ndipo zimakondweretsa Mulungu Mpulumutsi wathu,
hoc enim bonum est, et acceptum coram Salvatore nostro Deo,
4 amene amafuna kuti anthu onse apulumutsidwe ndipo kuti adziwe choonadi.
qui omnes homines vult salvos fieri, et ad agnitionem veritatis venire.
5 Pakuti pali Mulungu mmodzi yekha ndi Mʼkhalapakati mmodzi yekha pakati pa Mulungu ndi anthu, munthu uja Khristu Yesu.
Unus enim Deus, unus et mediator Dei et hominum homo Christus Iesus:
6 Iyeyu anadzipereka kukhala dipo lowombolera anthu onse. Umenewu ndi umboni umene waperekedwa mu nthawi yake yoyenera.
qui dedit redemptionem semetipsum pro omnibus, testimonium temporibus suis:
7 Nʼchifukwa chake anandisankha kukhala mlaliki ndiponso mtumwi wophunzitsa anthu a mitundu ina mawu achikhulupiriro choona. Sindikunama ayi, ndikunena zoona.
in quo positus sum ego prædicator, et Apostolus (veritatem dico, non mentior) doctor Gentium in fide, et veritate.
8 Choncho ndikufuna kuti paliponse popemphera, amuna azikweza manja awo kwa Mulungu mopanda mkwiyo kapena kukangana.
Volo ergo viros orare in omni loco, levantes puras manus sine ira, et disceptatione.
9 Ndikufunanso kuti amayi azivala mwaulemu, modzilemekeza ndi moyenera. Adzikongoletse koma osati ndi tsitsi loluka mowonjeza muyeso kapena zokongoletsa zagolide kapena mikanda yamtengowapatali kapena ndi zovala zamtengowapatali.
Similiter et mulieres in habitu ornato, cum verecundia, et sobrietate ornantes se, et non in tortis crinibus, aut auro, aut margaritas, vel veste pretiosa:
10 Koma adzikongoletse ndi ntchito zabwino zoyenera mayi wopembedza Mulungu.
sed quod decet mulieres, promittentes pietatem per opera bona.
11 Amayi azikhala chete pophunzitsidwa ndi mtima ogonjera kwathunthu.
Mulier in silentio discat cum omni subiectione.
12 Ine sindikulola kuti amayi aziphunzitsa kapena kulamulira amuna; koma akhale chete.
Docere autem mulieri non permitto, neque dominari in virum: sed esse in silentio.
13 Pakuti Adamu ndiye anayamba kupangidwa kenaka Hava.
Adam enim primus formatus est: deinde Heva.
14 Ndipo Adamu si amene ananyengedwa koma mkazi ndiye amene ananyengedwa nachimwa.
et Adam non est seductus: mulier autem seducta in prævaricatione fuit.
15 Ndipo mkazi adzapulumutsidwa pobereka mwana ngati apitiriza kukhala mʼchikhulupiriro, mʼchikondi ndi mʼkuyera mtima pamodzi ndi kudzichepetsa konse.
Salvabitur autem per filiorum generationem, si permanserit in fide, et dilectione, et sanctificatione cum sobrietate.

< 1 Timoteyo 2 >