< 1 Timoteyo 2 >

1 Tsono choyamba ndikukupemphani kuti mupempherere anthu onse. Mapemphero anu akhale opemba, opempha, opempherera ena ndi oyamika.
Avant tout, j'exhorte donc à faire des prières, des supplications, des intercessions, des actions de grâces pour tous les hommes,
2 Mupempherere mafumu ndi onse aulamuliro, kuti tikhale moyo wamtendere ndi bata, woopa Mulungu ndi oyera mtima.
pour les rois et pour ceux qui sont constitués en dignité, afin que nous passions une vie paisible et tranquille, en toute piété et honnêteté.
3 Izi ndi zabwino ndipo zimakondweretsa Mulungu Mpulumutsi wathu,
Cela est bon et agréable aux yeux de Dieu notre Sauveur,
4 amene amafuna kuti anthu onse apulumutsidwe ndipo kuti adziwe choonadi.
qui veut que tous les hommes soient sauvés et parviennent à la connaissance de la vérité.
5 Pakuti pali Mulungu mmodzi yekha ndi Mʼkhalapakati mmodzi yekha pakati pa Mulungu ndi anthu, munthu uja Khristu Yesu.
Car il y a un seul Dieu; et aussi un seul médiateur entre Dieu et les hommes, le Christ Jésus fait homme,
6 Iyeyu anadzipereka kukhala dipo lowombolera anthu onse. Umenewu ndi umboni umene waperekedwa mu nthawi yake yoyenera.
qui s'est donné lui-même en rançon pour tous: c'est là un fait attesté en son temps,
7 Nʼchifukwa chake anandisankha kukhala mlaliki ndiponso mtumwi wophunzitsa anthu a mitundu ina mawu achikhulupiriro choona. Sindikunama ayi, ndikunena zoona.
et c'est pour en témoigner, que j'ai été établi prédicateur et apôtre, — je dis la vérité, je ne mens pas, — docteur des nations dans la foi et la vérité.
8 Choncho ndikufuna kuti paliponse popemphera, amuna azikweza manja awo kwa Mulungu mopanda mkwiyo kapena kukangana.
Je veux donc que les hommes prient en tout lieu, levant au ciel des mains pures, sans colère ni agitation de pensées;
9 Ndikufunanso kuti amayi azivala mwaulemu, modzilemekeza ndi moyenera. Adzikongoletse koma osati ndi tsitsi loluka mowonjeza muyeso kapena zokongoletsa zagolide kapena mikanda yamtengowapatali kapena ndi zovala zamtengowapatali.
de même que les femmes soient en vêtements décents, se parant avec pudeur et simplicité, sans tresses, or, perles où habits somptueux;
10 Koma adzikongoletse ndi ntchito zabwino zoyenera mayi wopembedza Mulungu.
mais de bonnes œuvres, comme il convient à des femmes qui font profession de servir Dieu.
11 Amayi azikhala chete pophunzitsidwa ndi mtima ogonjera kwathunthu.
Que la femme reçoive l'instruction en silence, avec une entière soumission.
12 Ine sindikulola kuti amayi aziphunzitsa kapena kulamulira amuna; koma akhale chete.
Je ne permets pas à la femme d'enseigner, ni de prendre autorité sur l'homme; mais elle doit se tenir dans le silence.
13 Pakuti Adamu ndiye anayamba kupangidwa kenaka Hava.
Car Adam a été formé le premier, Eve ensuite;
14 Ndipo Adamu si amene ananyengedwa koma mkazi ndiye amene ananyengedwa nachimwa.
et ce n'est pas Adam qui a été séduit: c'est la femme qui, séduite, est tombée dans la transgression.
15 Ndipo mkazi adzapulumutsidwa pobereka mwana ngati apitiriza kukhala mʼchikhulupiriro, mʼchikondi ndi mʼkuyera mtima pamodzi ndi kudzichepetsa konse.
Néanmoins, elle sera sauvée en devenant mère, pourvu qu'elle persévère dans la foi, dans la charité et dans la sainteté, unies à la modestie.

< 1 Timoteyo 2 >