< 1 Samueli 8 >

1 Samueli atakalamba anasankha ana ake kuti akhale oweruza Aisraeli.
Kad je Samuel ostario, postavio je svoje sinove za suce u Izraelu.
2 Mwana wake woyamba anali Yoweli, wachiwiri anali Abiya, ndipo ankaweruza ku Beeriseba.
Njegov prvorođenac zvao se Joel, a drugi sin Abija; oni su bili suci u Beer Šebi.
3 Koma ana akewo sanatengere makhalidwe ake abwino. Iwo ankapotokera ku zoyipa namatsata phindu mwachinyengo. Ankalandira ziphuphu ndi kumaweruza mwachinyengo.
Ali sinovi nisu išli stopama očevim: gledali su na svoj dobitak, primali mito i izvrtali pravicu.
4 Tsono akuluakulu onse a Israeli anasonkhana pamodzi ndipo anabwera kwa Samueli ku Rama.
Tada se skupiše sve starješine izraelske i dođoše k Samuelu u Ramu.
5 Iwo anati kwa iye “Taonani, inu mwakula tsopano ndipo ana anu sakutsata makhalidwe anu abwino. Tsono mutipatse mfumu kuti izitilamulira, monga momwe ikuchitira mitundu ina yonseyi.”
I rekoše mu: “Eto, ti si ostario, a tvoji sinovi ne idu tvojim stopama. Postavi nam, dakle, kralja da nam vlada, kao što je to kod svih naroda.”
6 Koma mawu oti, “Mutipatse mfumu kuti izitilamulira,” sanakondweretse Samueli. Choncho anapemphera kwa Yehova.
Ali Samuelu nije bilo drago što su rekli: “Daj nam kralja da nam vlada!” Zato se Samuel pomoli Jahvi.
7 Yehova anamuyankha nati, “Mvera zonse zimene anthuwa akukuwuza. Si ndiwe amene akumukana, koma akukana Ine kuti ndikhale mfumu yawo.
A Jahve reče Samuelu: “Poslušaj glas naroda u svemu što od tebe traži, jer nisu odbacili tebe, nego su odbacili mene, ne želeći da ja kraljujem nad njima.
8 Kuyambira tsiku limene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto mpaka lero zochita zawo zakhala zondikana Ine nʼkumatumikira milungu ina. Tsopano akukukananso iwe.
Sve što su činili meni od onoga dana kad sam ih izveo iz Egipta pa do današnjega dana - ostavili su mene i služili tuđim bogovima - tako oni čine i tebi.
9 Tsono amvere zimene akunena, koma uwachenjeze kwambiri ndipo uwawuzitse za khalidwe la mfumu imene idzawalamulire.”
Sada, dakle, poslušaj njihov zahtjev, ali ih svečano opomeni i pouči o pravima kralja koji će vladati nad njima.”
10 Samueli anawawuza anthu amene amamupempha mfumu aja mawu onse a Yehova.
Samuel ponovi sve Jahvine riječi narodu koji je od njega tražio kralja.
11 Iye anati, “Zimene mfumu imene idzakulamulireniyo idzachite ndi izi: Izidzatenga ana anu aamuna kuti akhale ankhondo ake; ena pa magaleta ake, ena pa akavalo ake ndipo ena othamanga patsogolo pa magaleta akewo.
I reče: “Ovo će biti pravo kralja koji će kraljevati nad vama: uzimat će vaše sinove da mu služe kod bojnih kola i kod konja i oni će trčati pred njegovim bojnim kolima.
12 Ena adzawayika kukhala olamulira asilikali 1,000, ena olamulira asilikali makumi asanu, ndi ena otipula minda yake, ndi kukolola ndiponso ena adzakhala osula zida zankhondo ndi zida za magaleta ake.
Postavljat će ih za tisućnike i pedesetnike; orat će oni njegovu zemlju, žeti njegovu žetvu, izrađivati mu bojno oružje i opremu za njegova bojna kola.
13 Iyo idzatenga ana anu akazi kuti akhale oyenga mafuta onunkhira, ophika chakudya ndi kupanga buledi.
Uzimat će kralj vaše kćeri da mu priređuju mirisne pomasti, da mu kuhaju i peku.
14 Idzatenga minda yanu yabwino ya mpesa ndi ya mitengo ya olivi ndipo adzayipereka kwa antchito ake.
Uzimat će najbolja vaša polja, vaše vinograde i vaše maslinike i poklanjat će ih svojim dvoranima.
15 Idzatenga gawo lakhumi la tirigu wanu ndi mphesa zanu ndi kupereka kwa nduna zake ndi akapitawo ake.
Uzimat će desetinu od vaših usjeva i vaših vinograda i davat će je svojim dvoranima i svojim službenicima.
16 Mfumuyo idzatenga antchito anu aamuna ndi aakazi. Idzatenganso ngʼombe zanu zabwino ndi abulu anu nʼkumazingwiritsa ntchito.
Uzimat će vaše sluge i vaše sluškinje, vaše najljepše volove i magarce i upotrebljavat će ih za svoj posao.
17 Iyo idzatenga gawo lakhumi la zoweta zanu, ndipo inu eni mudzakhala akapolo ake.
Uzimat će desetinu od vaše sitne stoke, a vi sami postat ćete mu robovi.
18 Nthawi imeneyo ikadzafika inu mudzalira momvetsa chisoni chifukwa cha mfumu imene mwadzisankhira, koma Yehova sadzakuyankhani.”
I kad jednoga dana budete vapili za pomoć zbog kralja koga ste sami izabrali, Jahve vas neće uslišati u onaj dan!”
19 Koma anthu anakana kumumvera Samueli. Iwo anati, “Ayi! Ife tikufuna mfumu yotilamulira.
Narod nije htio poslušati Samuelova glasa nego reče: “Ne! Hoćemo da kralj vlada nad nama!
20 Kotero ifenso tidzakhala ngati mayiko ena. Mfumu yathu idzatiweruza ndiponso idzatuluka nafe kutitsogolera kukamenya nkhondo.”
Tako ćemo i mi biti kao svi narodi: sudit će nam naš kralj, bit će nam vođa i vodit će naše ratove.”
21 Samueli atamva zonse zimene anthuwo ananena, iye anakazifotokozanso kwa Yehova.
Kad je Samuel čuo što narod govori, kaza sve Jahvi.
22 Yehova anamuyankha nati, “Amvere zimene akunena ndipo apatse mfumu.” Ndipo Samueli anati kwa Aisraeli aja, “Bwererani aliyense kwawo.”
A Jahve reče Samuelu: “Poslušaj njihovu želju i postavi im kralja!” Tada Samuel reče Izraelcima: “Vratite se svaki u svoj grad!”

< 1 Samueli 8 >