< 1 Samueli 31 >

1 Tsono Afilisti anachitanso nkhondo ndi Aisraeli ndipo Aisraeli anathawa Afilistiwo, kotero kuti ambiri anaphedwa pa phiri la Gilibowa.
Now the Philistines fought against Israel. And the men of Israel fled from before the Philistines, and fell down slain in mount Gilboa.
2 Afilisti anapanikiza kwambiri Sauli ndi ana ake, ndipo anapha Yonatani, Abinadabu ndi Maliki-Suwa.
And the Philistines followed hard upon Saul and upon his sons, and the Philistines killed Jonathan, and Abinadab, and Malchishua, the sons of Saul.
3 Nkhondo inakula kwambiri mozungulira Sauli ndipo pamene anthu amauta anamupeza, anamuvulaza kwambiri.
And the battle went severely against Saul, and the archers overtook him, and he was greatly distressed because of the archers.
4 Tsono Sauli anawuza mnyamata wake wonyamula zida zake kuti, “Solola lupanga lako undiphe kuopa kuti anthu osachita mdulidwewa angabwere kudzandizunza ine.” Koma mnyamata wonyamula zida uja anachita mantha kwambiri ndipo sanathe kutero. Choncho Sauli anatenga lupanga lake lomwe nagwerapo.
Then Saul said to his armor bearer, Draw thy sword, and thrust me through with it, lest these uncircumcised come and thrust me through, and abuse me. But his armor bearer would not, for he was very afraid. Therefore Saul took his sword, and fell upon it.
5 Mnyamata wonyamula zida zake uja ataona kuti Sauli wafa, nayenso anadzigwetsera pa lupanga lake nafa naye limodzi.
And when his armor bearer saw that Saul was dead, he likewise fell upon his sword, and died with him.
6 Motero Sauli ndi ana ake atatu, wonyamula zida zake pamodzi ndi anthu ake onse anafera limodzi pa tsikulo.
So Saul died, and his three sons, and his armor bearer, and all his men, that same day together.
7 Pamene Aisraeli amene anali tsidya lina la chigwa ndi amene anali tsidya la chigwa cha Yorodani anaona kuti gulu la ankhondo la Aisraeli lathawa komanso kuti Sauli ndi ana ake aphedwa, nawonso anathawa kusiya mizinda yawo. Ndipo Afilisti anabwera kudzakhalamo.
And when the men of Israel who were on the other side of the valley, and those who were beyond the Jordan, saw that the men of Israel fled, and that Saul and his sons were dead, they forsook the cities, and fled. And the Philistines came and dwelt in them.
8 Mmawa mwake, Afilisti atabwera kudzatenga zinthu za anthu ophedwa anapeza Sauli ndi ana ake atatu atafa pa phiri la Gilibowa.
And it came to pass on the morrow, when the Philistines came to strip the slain, that they found Saul and his three sons fallen in mount Gilboa.
9 Iwo anadula mutu wake ndi kumuvula zida zake zankhondo. Ndipo anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Afilisti kukafalitsa nkhani yabwinoyi kwa mafano awo ndi kwa anthu awo.
And they cut off his head, and stripped off his armor, and sent into the land of the Philistines round about to carry the news to the house of their idols, and to the people.
10 Iwo anayika zida zake zankhondo mʼnyumba yopembedzera Asitoreti, ndipo thupi lake analikhomera pa khoma la mzinda wa Beti-Sani.
And they put his armor in the house of the Ashtaroth, and they fastened his body to the wall of Beth-shan.
11 Pamene anthu a ku Yabesi Giliyadi anamva zimene Afilisti anachitira Sauli,
And when the inhabitants of Jabesh-gilead heard concerning him, that which the Philistines had done to Saul,
12 anthu awo onse olimba mtima anayenda usiku wonse kupita ku Beti-Sani. Anakachotsa mtembo wa Sauli ndi mitembo ya ana ake pa khoma la mzinda wa Beti-Sani, ndipo anabwera nayo ku Yabesi kumene anayitentha ndi moto.
all the valiant men arose, and went all night, and took the body of Saul and the bodies of his sons from the wall of Beth-shan, and they came to Jabesh, and burnt them there.
13 Pambuyo pake anatenga mafupa awo ndi kuwakwirira pansi pa mtengo wabwemba ku Yabesi, ndipo anasala kudya masiku asanu ndi awiri.
And they took their bones, and buried them under the tamarisk tree in Jabesh, and fasted seven days.

< 1 Samueli 31 >