< 1 Samueli 30 >

1 Pa tsiku lachitatu, Davide ndi anthu ake anakafika ku Zikilagi. Tsono anapeza Aamaleki atawononga kale dera la Negevi ndi Zikilagi. Anathira nkhondo mzinda wa Zikilagi ndi kuwutentha ndi moto.
Et il se trouva que, lors du retour de David et de son monde à Tsiklag le troisième jour, les Amalécites avaient fait une expédition sur le Midi et sur Tsiklag qu'ils avaient saccagée et incendiée,
2 Anatenga akazi ndi onse amene anali mʼmenemo akuluakulu ndi angʼono omwe kuti akakhale akapolo. Sanaphe aliyense koma anawatenga amoyo napita nawo.
ayant emmené captives les femmes avec ceux qui y restaient, petits et grands: ils n'avaient tué personne; seulement ils avaient emmené leur prise, puis continué leur route.
3 Davide ndi anthu ake atafika ku Zikilagi anapeza kuti mzindawo watenthedwa ndi moto ndipo akazi awo, ana awo, amuna ndi akazi atengedwa ukapolo.
Et au retour de David et de ses hommes à la ville, voilà qu'elle était incendiée et leurs femmes et leurs fils et leurs filles emmenées en captivité.
4 Kotero Davide ndi anthu ake analira mofuwula mpaka analibenso mphamvu zolirira.
Alors David et la troupe qui l'accompagnait laissèrent éclater leur voix et pleurèrent jusqu'à n'avoir plus la force de pleurer.
5 Akazi awiri a Davide, Ahinoamu wa ku Yezireeli ndi Abigayeli mkazi wa Nabala wa ku Karimeli anatengedwanso.
Et les deux femmes de David étaient prisonnières, Ahinoam de Jizréel, et Abigaïl, femme de Nabal, le carmélite.
6 Davide anavutika kwambiri mu mtima mwake chifukwa anthu amakamba zoti amuponye miyala popeza aliyense anali ndi chisoni pokumbukira ana ake aamuna ndi aakazi. Koma Davide anapeza mphamvu mwa Yehova Mulungu wake.
Et David était dans une détresse car la troupe parlait de le lapider parce que l'amertume était dans le cœur de tous, chacun regrettant ses fils et ses filles. Mais David prit sa force dans l'Éternel son Dieu.
7 Kenaka Davide anawuza wansembe Abiatara, mwana wa Ahimeleki kuti, “Ndipatse efodi ija.” Abiatara anabwera nayo efodiyo.
Et David dit à Abiathar, le Prêtre, fils d'Ahimélech: Apporte-moi donc l'éphod! Et Abiathar apporta l'éphod à David.
8 Tsono Davide anapempha nzeru kwa Yehova nati, “Kodi ndilitsatire gulu lankhondoli? Kodi ndidzawapambana?” Yehova anayankha kuti, “Litsatire, iwe udzawapambana ndithu ndipo udzapulumutsa anthu ako.”
Et David interrogea l'Éternel en ces termes: Me mettrai-je à la poursuite de cette horde-là? l'atteindrai-je? Et Il répondit: Poursuis, car tu atteindras et délivreras.
9 Davide pamodzi ndi anthu ake 600 aja ananyamuka nafika ku mtsinje wa Besori. Kumeneko anasiyako anthu ena.
Alors David marcha avec les six cents hommes qui l'accompagnaient, et ils s'avancèrent jusqu'au torrent du Bésor, et les traîneurs firent halte.
10 Davide ndi anthu ake 400 anapitirira kuwalondola Aamaleki aja. Koma anthu ena 200 anatsala popeza anatopa moti sakanatha kuwoloka mtsinje wa Besori uja.
Et David entreprit la poursuite avec quatre cents hommes, deux cents hommes ayant fait halte parce qu'ils étaient trop fatigués pour passer le torrent du Bésor.
11 Anthu amene anali ndi Davide anapeza Mwigupto mʼmunda wina ndipo anabwera naye kwa Davide. Iwo anamupatsa madzi kuti amwe ndi chakudya kuti adye.
Et ils trouvèrent un Egyptien dans la campagne et ils l'amenèrent à David, et ils lui servirent des aliments et il mangea, et ils lui donnèrent de l'eau à boire;
12 Anamupatsanso chidutswa cha keke yankhuyu ndi makeke awiri a mphesa zowumika kuti adye. Atadya anapezanso mphamvu popeza anakhala masiku atatu wosadya kapena kumwa kanthu kalikonse.
ils lui donnèrent aussi un quartier de bol de figues et deux gâteaux de raisins secs, et il mangea, et fut ranimé, car il n'avait ni mangé, ni bu, ni pain, ni eau, trois jours et trois nuits.
13 Davide anafunsa kuti, “Kodi ndiwe yani, ndipo ukuchokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine Mwigupto, kapolo wa Mwamaleki. Mbuye wanga anandisiya nditayamba kudwala masiku atatu apitawo.
Et David lui dit: A qui es-tu? et d'où es-tu? Et il répondit: Je suis un jeune Egyptien, au service d'un Amalécite, et mon maître m'a laissé parce que je suis malade voici trois jours.
14 Ife tinathira nkhondo dera la kummwera kwa mayiko a Akereti, dera la Yuda, ndi dera la kummwera kwa mayiko a Kalebe. Mzinda wa Zikilagi tinawutentha ndi moto.”
Nous avons fait une incursion dans le Midi des Chrétites et dans les dépendances de Juda et dans le Midi de Caleb et nous avons livré Tsiklag aux flammes.
15 Davide anamupempha kuti, “Kodi unganditsogolere kumene kuli gulu lankhondoli?” Iye anayankha kuti, “Mukandilonjeza molumbira kuti simudzandipha kapena kundipereka kwa mbuye wanga, ine ndikulondolerani kumene kuli gululo.”
Et David lui dit: Veux-tu être mon guide jusqu'à cette horde-là? Et il dit: Jure-moi devant Dieu que tu ne me feras pas mourir et ne me livreras pas à mon maître, et je te conduirai à cette horde.
16 Mwigupto uja anaperekeza Davide. Tsono Aamaleki anali atamwazikana ponseponse. Iwo ankadya, kumwa ndi kuvina chifukwa cha zofunkha zambiri zimene anatenga ku dziko la Afilisti ndi ku dziko la Ayuda.
Et il fut leur guide. Et voilà que les Amalécites étaient épars dans toute la campagne mangeant et buvant et faisant fête pour tout le grand butin qu'ils avaient enlevé du pays des Philistins et du pays de Juda.
17 Tsono Davide anawakantha kuyambira madzulo atsikulo mpaka madzulo a tsiku linalo. Palibe anapulumuka kupatula anyamata 400 amene anakwera pa ngamira nʼkuthawa.
Et depuis l'aube jusqu'au soir qui ouvrait le lendemain il en fit un tel carnage que pas un homme n'échappa sauf quatre cents jeunes gens qui montèrent sur des chameaux et s'enfuirent.
18 Choncho Davide analanditsa zinthu zonse zimene Aamaleki aja anatenga. Anapulumutsanso akazi ake awiri aja.
Et ainsi, David recouvra tout ce qu'avaient enlevé les Amalécites, et délivra aussi ses deux femmes.
19 Palibe chimene chinasowa anthu onse, kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, mnyamata mpaka mtsikana anapulumutsidwa. Davide anapulumutsa chilichonse chimene anafunkha Aamaleki aja.
Et ils n'eurent à regretter personne, ni petit ni grand, ni fils ni fille, ni aucun objet du butin qui leur avait été pris; David fit tout rentrer.
20 Anapulumutsanso nkhosa ndi ngʼombe zonse. Tsono anthu ankakusa ziwetozo namati, “Izi ndizo zofunkha za Davide.”
Et David prit tout le menu et le gros bétail; et ceux qui étaient en tête du troupeau disaient en le conduisant: C'est la capture de David.
21 Davide anafika ku malo kumene kunali anthu 200 otopa kwambiri aja amene sanathe kutsagana naye koma anangokhala ku mtsinje wa Besori. Tsono ananyamuka kuti akumane ndi Davide pamodzi ndi anthu amene anali naye. Davide anawayandikira nawalonjera.
Et David ayant rejoint les deux cents hommes trop fatigués pour suivre David, qu'il avait laissés faire halte au torrent du Bésor, ils vinrent au devant de David et de la troupe qui l'accompagnait, et David les aborda en s'informant d'eux amicalement.
22 Tsono anthu ena oyipa mtima achabechabe mwa amene anatsagana ndi Davide aja anati, “Popeza awa sanapite nafe, sitiwapatsako zofunkha zimene tapulumutsazi, kupatula kuti aliyense atenge mkazi wake ndi ana ake azipita.”
Et tous les hommes mauvais et de bas aloi, parmi les compagnons de David, prirent la parole et dirent: Puisqu'ils n'ont pas marché avec nous, nous ne voulons leur donner aucune part au butin que nous avons reconquis, sinon à chacun sa femme et qu'il les emmène et parte.
23 Koma Davide anawayankha kuti, “Ayi, abale anga, musachite zimenezi ndi zinthu zimene Yehova watipatsa. Iye watisunga ndi kupereka mʼmanja mwathu gulu la ankhondo limene linabwera kudzalimbana nafe.
Mais David dit: N'en usez pas ainsi, mes frères, avec ce que l'Éternel nous a donné, d'autant qu'Il nous a eus en sa garde et a livré entre nos mains la horde de nos envahisseurs.
24 Ndani angakumvereni zimene mukunenazi? Gawo la munthu amene anapita kukamenya nkhondo likhale lofanana ndi la munthu amene anatsala pano kuyangʼanira katundu wathu. Pasakhale kusiyana kulikonse.”
Et qui vous écoutera dans ce que vous prononcez là… car telle la part de ceux qui sont descendus sur le champ de bataille, telle doit être la part de ceux qui sont restés auprès des bagages: ensemble ils partageront.
25 Choncho Davide anakhazikitsa ngati lamulo mʼchitidwe woterewu pakati pa Aisraeli kuyambira tsiku limenelo mpaka lero.
Et c'est ce qui à partir de ce jour eut lieu postérieurement et dont on fit une règle et une pratique pour Israël jusqu'aujourd'hui.
26 Davide atafika ku Zikilagi, anatumiza zina mwa zofunkhazo kwa akuluakulu a Yuda, amene anali abwenzi ake. Anati, “Nayi mphatso yanu yochokera pa zofunkha za adani a Yehova.”
Et revenu à Tsiklag, David envoya du butin aux Anciens de Juda, à ses amis, avec ces paroles: Voici pour vous un don sur le butin des ennemis de l'Éternel!
27 Iye anatumiza mphatsozo kwa anthu a ku Beteli, Ramoti-Negavi, Yatiri,
[il l'envoya] à ceux de Béthel et à ceux de Ramoth-Negeb, et à ceux de Jathir,
28 Aroeri, Sifimoti, Esitemowa
et à ceux d'Aroër, et à ceux de Siphmoth, et à ceux d'Esthmoha,
29 Rakala, mizinda ya fuko la Ayerahimeeli, mizinda ya fuko la Akeni,
et à ceux de Rachal, et à ceux des villes de Jehraméel, et à ceux des villes des Kénites,
30 a ku Horima, Borasani, Ataki,
et à ceux de Horma, et à ceux de Chor-Asan, et à ceux d'Athach,
31 Hebroni pamodzi ndi onse a kumalo kumene Davide ndi anthu ake anakhala akuyendayendako.
et à ceux de Hébron et dans tous les lieux où David avait erré lui et ses hommes.

< 1 Samueli 30 >