< 1 Samueli 29 >

1 Afilisti anasonkhanitsa asilikali awo onse ku Afeki, ndipo Israeli anamanga misasa yawo pa chitsime cha Yezireeli.
Now the Philistines gathered together all their hosts, towards Aphek, —and, the Israelites, were encamping by the fountain, that is in Jezreel.
2 Pamene atsogoleri a Afilisti ankatsogolera magulu awo ankhondo a miyandamiyanda, Davide ndi ankhondo ake ankayenda pambuyo pamodzi ndi Akisi.
And, the lords of the Philistines, were passing on by hundreds, and by thousands, —but, David and his men, were passing on in the rear, with Achish.
3 Tsono atsogoleri a Afilisti aja anafunsa kuti, “Kodi Ahebri awa akufuna chiyani?” Akisi anayankha kuti, “Uyu ndi Davide, mtumiki wa Sauli mfumu ya Israeli. Iye wakhala ndi ine kwa masiku ndithu, kapena titi zaka ndipo kuyambira tsiku limene anachoka kwa Sauli mpaka lero, ine sindinapeze cholakwa mwa iye.”
Then said the princes of the Philistines, What are these Hebrews [doing]? And Achish said unto the princes of the Philistines—Is not this David, servant of Saul king of Israel, who hath been with me this year, or two, and I have found in him nothing, from the day of his coming over unto me unto this day?
4 Koma atsogoleri a ankhondo a Afilisti anamukwiyira Akisi kwambiri ndipo anati, “Mubweze munthuyu kuti abwerere ku malo amene unamupatsa. Iye asapite nafe ku nkhondo kuopa kuti angadzasanduke mdani wathu. Kodi iyeyu adzadziyanjanitsa bwanji ndi mbuye wake? Iyeyutu adzadziyanjanitsa ndi mbuye wake pakupha anthu ali panowa?
But the princes of the Philistines raged against him, and the princes of the Philistines said unto him—Let the man go back, that he may return unto the place which thou didst appoint him, and let him not go down with us, into battle, so shall he not become to us a traitor, in the battle, —for, wherewith, should this fellow gain favour with his lord? Would it not be with the heads of those men?
5 Paja ameneyu ndi Davide yemwe ankamuvinira namuyimbira kuti, “‘Sauli wapha anthu 1,000 koma Davide wapha miyandamiyanda?’”
Is not this David, of whom they made responses in the dances, saying, —Saul, hath smitten, his thousands, But, David, his, tens of thousands?
6 Kotero Akisi anayitana Davide ndipo anamuwuza kuti, “Pali Yehova wamoyo, iwe wakhala wodalirika ndipo chikanakhala chinthu chabwino kuti uzimenya nkhondo pamodzi nane popeza chibwerere iwe kuno ine sindinapeze cholakwa chilichonse ndi iwe. Koma atsogoleri enawa ndiwo sakukufuna.
So Achish called for David, and said unto him—By the life of Yahweh, surely, upright, thou art, and, pleasing in mine eyes, have been thy going out and thy coming in with me, in the host, for I have found in thee no wrong, from the day of thy coming in unto me, until this day, —but, in the eyes of the lords, displeasing, thou art.
7 Tsono bwerera. Upite mu mtendere kuopa kuti ungachite kanthu kena koyipira atsogoleri a Afilistiwa.”
Now, therefore, return, and go in peace, —so shalt thou not do wrong in the eyes of the lords of the Philistines.
8 Davide anafunsa Akisi kuti, “Kodi ndachita chiyani? Kodi mwapeza cholakwa chotani mwa ine mtumiki wanu chiyambire kukutumikirani mpaka lero? Tsono chifukwa chiyani sindingapite kukamenya nkhondo ndi adani a mbuye wanga mfumu?”
Then said David unto Achish—But what have I done? and what hast thou found in thy servant, from the day that I came before thee, unto this day, —that I may not go in and fight, with the enemies of my lord the king.
9 Akisi anayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti ndiwe wangwiro ngati mngelo wa Mulungu. Komabe atsogoleri a ankhondo a Afilisti akuti, ‘Davide asapite nafe ku nkhondo.’
Then answered Achish, and said unto David, I acknowledge that, pleasing, thou art in mine eyes, as a messenger of God, —notwithstanding, the princes of the Philistines, have said, He shall not go up with us, into the battle.
10 Tsono udzuke mmamawa, pamodzi ndi ankhondo ako amene unabwera nawo, ndipo unyamuke kukangocha.”
Now, therefore, rise up early in the morning, thou and the servants of thy lord who have come with thee, —yea, as soon as ye have risen early in the morning, and have light, then depart.
11 Choncho Davide ndi anthu ake anadzuka mmamawa kubwerera ku dziko la Afilisti. Koma Afilistiwo anapita ku Yezireeli.
So David rose up early, he and his men, to depart in the morning, to return into the land of the Philistines, —but, the Philistines, went up to Jezreel.

< 1 Samueli 29 >