< 1 Samueli 27 >

1 Davide anaganiza mu mtima mwake nati, “Tsiku lina ine ndidzaphedwa ndi Sauli. Palibe chabwino ndingachite, koma kuthawira ku dziko la Afilisti. Kotero Sauli adzasiya kundifunafuna mʼdziko lonse la Israeli, ndipo ndidzapulumuka.”
And David said in his heart, I shall now perish one day by the hand of Saul. There is nothing better for me than that I should escape into the land of the Philistines, and Saul will despair of me, to seek me any more in all the borders of Israel, so I shall escape out of his hand.
2 Choncho Davide ndi anthu 600 amene anali nawo anachoka napita kwa Akisi mwana wa Maoki mfumu ya ku Gati.
And David arose, and passed over, he and the six hundred men who were with him, to Achish the son of Maoch, king of Gath.
3 Davide anakhala ndi Akisi ku Gati pamodzi ndi ankhondo ake, aliyense ndi banja lake. Davide ali ndi akazi ake awiri, Ahinoamu wa ku Yezireeli ndi Abigayeli wa ku Karimeli, mkazi wamasiye wa Nabala.
And David dwelt with Achish at Gath, he and his men, every man with his household, even David with his two wives, Ahinoam the Jezreelitess, and Abigail the Carmelitess, Nabal's wife.
4 Sauli anamva kuti Davide wathawira ku Gati, ndipo sanamufunefunenso.
And it was told Saul that David was fled to Gath, and he sought no more again for him.
5 Kenaka Davide anawuza Akisi kuti, “Ngati ndapeza kuyanja pamaso panu mundipatse malo dera limodzi la dziko lanu kuti ndizikhala kumeneko. Mtumiki wanu adzakhala mu mzinda waufumu chifukwa chiyani?”
And David said to Achish, If now I have found favor in thine eyes, let them give me a place in one of the cities in the country that I may dwell there, for why should thy servant dwell in the royal city with thee?
6 Choncho tsiku limenelo Akisi anamupatsa Zikilagi ndipo mzindawo wakhala wa mafumu a Yuda mpaka lero.
Then Achish gave him Ziklag that day. Therefore Ziklag pertains to the kings of Judah to this day.
7 Davide anakhala mʼdziko la Afilisti kwa chaka chimodzi ndi miyezi inayi.
And the number of the days that David dwelt in the country of the Philistines was a full year and four months.
8 Tsono Davide ndi anthu ake ankapita kukathira nkhondo Agesuri, Agirizi ndi Aamaleki. (Mitundu ya anthu imeneyi kuyambira kale inkakhala mʼdziko la pakati pa Suri ndi Igupto).
And David and his men went up, and made a raid upon the Geshurites, and the Girzites, and the Amalekites, for those nations were the inhabitants of the land, who were of old as thou go to Shur, even to the land of Egypt.
9 Davide ankati akathira nkhondo dera lina, sankasiya munthu wamoyo, mwamuna kapena mkazi, koma ankatenga nkhosa, ngʼombe, abulu, ngamira ndi zovala, pambuyo pake nʼkubwerera kwa Akisi.
And David smote the land, and saved neither man nor woman alive, and took away the sheep, and the oxen, and the donkeys, and the camels, and the apparel, and he returned, and came to Achish.
10 Akisi akafunsa kuti, “Kodi lero unapita kukathira nkhondo kuti?” Davide ankayankha kuti, “Ndinapita kukathira nkhondo kummwera kwa Yuda,” mwinanso ankanena kuti, “Ndinapita ku dziko la Ayerahimeeli” kapenanso ankanena kuti, “Ndinapita ku dziko la Akeni.”
And Achish said, Against whom have ye made a raid today? And David said, Against the South of Judah, and against the South of the Jerahmeelites, and against the South of the Kenites.
11 Davide sankasiya mwamuna kapena mkazi wamoyo kuti akafotokozere anthu a ku Gati zochitikazo kuopa kuti opulumukawo akhoza kudzanena kuti “Davide watichita zakutizakuti.” Tsono izi ndi zimene Davide ankachita pamene ankakhala mʼdziko la Afilisti.
And David saved neither man nor woman alive to bring them to Gath, saying, Lest they should tell of us, saying, So did David, and so has been his manner all the while he has dwelt in the country of the Philistines.
12 Akisi ankamukhulupirira Davide ndipo ankati mu mtima mwake, “Davide wadzisandutsa munthu woyipa kwambiri pakati pa anthu ake omwe, Aisraeli. Tsono adzakhala mtumiki wanga mpaka kalekale.”
And Achish believed David, saying, He has made his people Israel utterly to abhor him. Therefore he shall be my servant forever.

< 1 Samueli 27 >