< 1 Samueli 2 >

1 Ndipo Hana anapemphera nati, “Moyo wanga ukukondwera mwa Yehova; Ndiyenda mwa tukumutukumu chifukwa cha Yehova. Pakamwa panga pakula ndi kuseka adani anga mowanyogodola. Ndikukondwa chifukwa mwandipulumutsa.
Tad Anna pielūdza un sacīja: “Mana sirds lec no prieka iekš Tā Kunga, mans rags ir paaugstināts iekš Tā Kunga; mana mute ir atvērta pret maniem ienaidniekiem, jo es priecājos par Tavu pestīšanu.
2 “Palibe wina woyera ngati Yehova, palibe wina koma inu nokha, palibe thanthwe lofanana ndi Mulungu wathu.
Neviens nav svēts, kā Tas Kungs, neviens, kā Tu vien, un nekāds patvērums nav, kā mūsu Dievs.
3 “Musandiyankhulenso modzitama, pakamwa panu pasatuluke zonyada, pakuti Yehova ndi Mulungu wanzeru, ndipo ndiye amene amayesa ntchito za anthu onse.
Nedaudzinājiet runu augsti jo augsti, blēņas lai paliek nost no jūsu mutes; jo Tas Kungs ir Dievs, tas visu zinātājs, Viņš sver tos darbus.
4 “Mauta a anthu ankhondo athyoka koma anthu ofowoka avala dzilimbe.
Vareniem stops ir salauzts, un vājie ir apjozti ar stiprumu;
5 Amene kale anali okhuta tsopano akukagula chakudya, koma iwo amene anali ndi njala sakumvanso njala. Amene anali wosabereka, wabereka ana aamuna asanu ndi awiri, koma iye wobereka ana ambiri watsala yekha.
Paēdušie sader par maizi, un izsalkušie vairs nav izsalkuši. Pati neauglīgā dzemdē septiņus, kam bija daudz bērnu, tā savīst.
6 “Yehova amabweretsa imfa ndipo amaperekanso moyo, amatsitsira ku manda ndipo amawatulutsakonso. (Sheol h7585)
Tas Kungs nokauj un dara dzīvu, Viņš noved ellē un atkal uzved augšā. (Sheol h7585)
7 Yehova amasaukitsa ndipo amalemeretsa, amatsitsa ndipo amakweza.
Tas Kungs dara nabagu un dara bagātu, Viņš pazemo un paaugstina.
8 Iye amakweza osauka kuwachotsa pa fumbi, ndipo amachotsa anthu osowa pa dzala. Iye amawakhazika pamodzi ndi ana a mafumu, amawapatsa mpando waulemu. “Pakuti nsanamira za dziko lapansi ndi za Yehova, anakhazika dziko lapansi pa nsanamirazo.
Viņš uzceļ nabagu no pīšļiem, un bēdīgo Viņš paaugstina no dubļiem, ka Viņš tos sēdina starp lieliem kungiem un tiem liek iemantot goda krēslu; jo zemes pamati pieder Tam Kungam, un Viņš uz tiem pasauli licis.
9 Iye adzateteza moyo wa anthu okhulupirika koma anthu oyipa adzawonongedwa mu mdima. “Pakuti munthu sapambana ndi mphamvu zake.
Savu svēto kājas Viņš pasargā; bet tie bezdievīgie tumsībā iet bojā: jo neviens nav varens caur (savu) spēku.
10 Yehova adzaphwanya omutsutsa. Adzawaopsa ndi bingu kuchokera kumwamba; Yehova adzaweruza mathero a dziko lapansi. “Koma adzapereka mphamvu kwa mfumu yake, adzakuza mphamvu za odzozedwa wake.”
Tas Kungs - Viņa pretinieki top iztrūcināti, debesīs pār tiem Viņš liek pērkoniem rūkt. Tas Kungs tiesās zemes galus un dos Savam ķēniņam spēku un paaugstinās Sava svaidītā ragu.”
11 Tsono Elikana anapita ku mudzi kwawo ku Rama, koma mnyamatayo amatumikira Yehova pansi pa ulamuliro wa wansembe Eli.
Un Elkanus nogāja uz Rāmatu savā namā, bet tas zēns kalpoja Tam Kungam priestera Elus priekšā.
12 Ana a Eli anali ana achabechabe pakuti samasamala za Yehova.
Bet Elus dēli bija netikli, tie neatzina To Kungu.
13 Ndipo chizolowezi cha ansembe pakati pa anthu chinali motere kuti pamene munthu aliyense ankapereka nsembe ndipo nyama ija ikuwira pa moto, mtumiki wa wansembe ankabwera ndi chifoloko cha mano atatu mʼdzanja lake.
Un priesteru ieradums ar ļaudīm bija: kad kāds upuri upurēja, tad priestera puisis nāca, kamēr tā gaļa vārījās, - un tam dakšas ar trim zariem bija rokā, -
14 Iye ankachipisa mu mʼphikamo, ndipo wansembeyo amatenga chilichonse chimene folokoyo yabaya. Umu ndi mmene ansembewo amachitira ndi Aisraeli onse amene amabwera ku Silo.
Un bakstīja grāpī vai katlā vai pannā vai podā. Ko nu tās dakšas uzvilka, to priesteris ņēma priekš sevis. Tā tie darīja visiem Israēla ļaudīm, kas tur nāca uz Šīlo.
15 Ndipo ngakhale mafuta asanatenthedwe, mtumiki wansembe amabwera ndi kunena kwa munthu amene akupereka nsembeyo kuti, “Ndipatse nyama kuti ndiwotche, pakuti Yehova salandira nyama yophika koma yayiwisi.”
Un pirms tie tos taukus iededzināja, priestera puisis nāca un sacīja uz to vīru, kas upurēja: dod gaļas priesterim priekš cepeša, jo viņš no tevis negrib vārītu gaļu, bet jēlu.
16 Ngati munthuyo anena kuti, “Apseretu mafuta poyamba, ndipo kenaka mutenge mmene mufunira,” mtumikiyo amayankha kuti, “Ayi ndipatse tsopano lino. Ngati sutero, ine nditenga molanda.”
Ja kas uz to sacīja: pašu laiku(vispirms) tos taukus iededzinās, tad ņem priekš sevis, kā tava sirds kāro, - tad šis uz to sacīja: nupat tev būs dot, un ja ne, tad es ņemšu ar varu.
17 Tchimo la ana a Eli linali lalikulu kwambiri pamaso pa Yehova pakuti iwo amanyoza nsembe za Yehova.
Tā šo puišu grēki bija ļoti lieli Tā Kunga priekšā, jo šie vīri nicināja Tā Kunga ēdamo upuri. -
18 Koma Samueli amatumikira pamaso pa Yehova atavala efodi ya nsalu yofewa yosalala.
Bet Samuēls kalpoja Tā Kunga priekšā, puisis būdams, apjozts ar nātnu efodu.
19 Chaka chilichonse amayi ake ankamusokera kamkanjo ndi kukamupatsa akamapita ndi mwamuna wake kukapereka nsembe za pa chaka.
Un māte viņam taisīja mazus svārciņus un tos viņam nesa ik gadus, kad ar savu vīru nāca, gadskārtējo upuri upurēt.
20 Tsono Eli amadalitsa Elikana ndi mkazi wake ndi mawu akuti “Yehova akupatseni ana mwa mkazi uyu kulowa mʼmalo mwa amene anapempha ndi kumupereka kwa Yehova.”
Un Elus svētīja Elkanu un viņa sievu un sacīja: lai Tas Kungs tev dod dzimumu no šās sievas, par to izlūgto, ko viņa no Tā Kunga ir izlūgusi. Un tie gāja uz savu māju.
21 Ndipo Yehova anamukomera mtima Hana. Anakhala ndi pathupi ndi kubereka ana aamuna atatu ndi ana aakazi awiri. Ndipo Samueli ankakula pamaso pa Yehova.
Un Tas Kungs piemeklēja Annu un tā tapa grūta un dzemdēja trīs dēlus un divas meitas. Bet tas puisītis Samuēls uzauga pie Tā Kunga.
22 Tsono Eli anakalamba kwambiri. Iye ankamva zonse zimene ana ake aamuna ankachitira Aisraeli onse, ndiponso kuti ankagona ndi akazi pa chipata cha tenti ya msonkhano.
Un Elus bija ļoti vecs un dzirdēja visu, ko viņa dēli visam Israēlim darīja, un ka tie gulēja pie tām sievām, kas sapulcējās priekš saiešanas telts durvīm.
23 Choncho anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukuchita zinthu zotere? Ine ndikumva kuchokera kwa anthu onse za zoyipa zanuzo.
Un viņš uz tiem sacīja: kāpēc jūs darāt tādas lietas? Kā es par jums tādu neslavu dzirdu no visiem šiem ļaudīm?
24 Ayi, ana anga si mbiri yabwino imene ndikumva anthu a Mulungu akufalitsa.
Nē, mani bērni, tā nav laba slava, ko es dzirdu, jo jūs darāt Tā Kunga ļaudis pārkāpjam.
25 Ngati munthu alakwira munthu mnzake, mwina Mulungu adzamupepesera, koma ngati munthu achimwira Yehova adzamupepesera ndani?” Koma ana ake sanamvere kudzudzula kwa abambo awo, pakuti chinali cholinga cha Yehova kuti awaphe.
Kad cilvēks pret cilvēku grēko, tad tiesas kungi to izlīdzina, bet kad cilvēks pret To Kungu grēko, kas priekš tāda var aizlūgt? Bet tie neklausīja sava tēva balsi, jo Tas Kungs tos gribēja nokaut.
26 Ndipo mnyamata Samueli anapitirira kukula mu msinkhu, ndipo ankapeza kuyanja pamaso pa Yehova ndi anthu.
Un tas puisis Samuēls augdams auga un patika gan Tam Kungam, gan tiem ļaudīm.
27 Tsiku lina munthu wa Mulungu anabwera kwa Eli ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti, ‘Kodi Ine sindinadziwulule ndekha kwa banja la kholo lako pamene iwo anali akapolo a Farao ku Igupto?
Un viens Dieva vīrs nāca pie Elus un uz to sacīja: tā saka Tas Kungs: vai Es neesmu skaidri parādījies tava tēva namam, kad tie bija Ēģiptes zemē Faraona namā,
28 Ndipo ndinamusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti akhale wansembe wanga ndi kuti azipita pa guwa langa la nsembe, kufukiza Lubani ndi kuvala efodi pamaso panga. Ndinapatsa banja la abambo ako gawo la nsembe zonse zopsereza zimene Aisraeli amapereka.
Un to no visām Israēla ciltīm Sev esmu licis par priesteri, upurēt uz Mana altāra, kvēpināmās zāles iededzināt un to plecu apsegu nest Manā priekšā, un Es tava tēva namam esmu devis visus Israēla bērnu uguns upurus.
29 Nʼchifukwa chiyani ukunyoza nsembe ndi zopereka zanga zimene ndinalamula? Nʼchifukwa chiyani ukupereka ulemu kwa ana ako kuposa Ine podzinenepetsa nokha ndi zopereka zabwino kwambiri za nsembe zimene Aisraeli amapereka?’”
Kāpēc tad jūs kājām minat Manu upuri un Manu ēdamo upuri, ko Es esmu pavēlējis (nest Manā) dzīvoklī? Un tu godā savus dēlus vairāk nekā Mani, ka jūs barojaties no visu Manu Israēla ļaužu upuru pirmajiem.
30 “Paja Ine Yehova Mulungu wa Israeli ‘Ndinalonjeza kuti anthu a pa banja lako ndi a pa banja la abambo ako azidzanditumikira nthawi zonse.’ Koma tsopano ndikuti, ‘Zonsezi zithe!’ Tsopano anthu amene amandilemekeza Inenso ndidzawalemekeza koma iwo amene amandinyoza Ine ndidzawanyoza.
Tādēļ Tas Kungs, Israēla Dievs, saka: gan Es biju skaidri sacījis: tavam namam un tava tēva namam bija Manā priekšā staigāt mūžīgi. Bet nu Tas Kungs saka: nemūžam nē, bet kas Mani godā, tos Es godāju, un kas Mani nicina, tie paliek kaunā.
31 Nthawi ikubwera imene ndidzachotsa anyamata ako ndi anyamata a pa banja la abambo ako, kotero kuti sipadzakhala munthu wokalamba pa banja lako.
Redzi, nāk dienas, tad Es nocirtīšu tavu elkoni un tava tēva nama elkoni, tā ka neviena veca vairs nebūs tavā namā.
32 Pa mavuto ako udzayangʼana ndi maso ansanje zabwino zimene ndidzachitira Aisraeli ena. Mʼbanja lako simudzapezeka munthu wokalamba.
Un tu redzēsi (Dieva) dzīvokļa bēdas pie visa, ko Viņš Israēlim labu darīs, un veca nebūs tavā namā nemūžam.
33 Komabe pa banja lako mmodzi yekha ndidzamuleka wosamuchotsa kuti azidzanditumikira. Iyeyu azidzakuliritsa ndi kukumvetsa chisoni. Koma ena onse pa banja lako adzafa akanali aangʼono.”
Tomēr visus Es tev neizdeldēšu no Mana altāra, ka tavām acīm būs īgt un tavai dvēselei iztvīkt, bet viss tava nama dzimums mirs vīra gados.
34 “‘Ndipo chimene chidzachitike kwa ana ako awiriwa, Hofini ndi Finehasi, chidzakhala chizindikiro kwa iwe. Onse awiri adzafa pa tsiku limodzi.
Šī nu būs tā zīme, kas nāks pār taviem abiem dēliem, par Hofnu un Pinehasu: vienā dienā abi mirs.
35 Pambuyo pake ndidzasankha wansembe wokhulupirika, amene adzachita zimene zili mu mtima ndi mʼmaganizo mwanga. Ndidzakhazikitsa banja lako kolimba ndipo adzatumikira pamaso pa wodzozedwa wanga nthawi zonse.
Un Es Sev celšu uzticīgu priesteri; tas darīs pēc Manas sirds un dvēseles, tam Es uztaisīšu pastāvīgu namu, un tas staigās priekš Mana svaidītā vienmēr.
36 Ndipo aliyense wotsala wa banja lako adzabwera ndi kugwada pamaso pake kupempha ndalama kapena chakudya.’ Adzati, ‘Chonde ndiloleni kuti ndizithandizako pa ntchito iliyonse ya unsembe kuti ndipeze chakudya.’”
Un kas vēl atliks no tava nama, nāks un klanīsies priekš viņa par naudas artavu un par maizes riecienu un sacīs: pieņem mani lūdzams kādā priestera amatā, ka dabūju maizes kumosu, ko ēst.

< 1 Samueli 2 >