< 1 Samueli 13 >

1 Sauli analowa ufumu ali ndi zaka makumi atatu, ndipo analamulira Israeli kwa zaka 42.
Saul was … years old when he began to reign. And when he had reigned two years over Israel,
2 Nthawi ina Sauli anasankha Aisraeli 3,000. Mwa iwowa, 2,000 anali ndi Sauliyo ku Mikimasi ndi ku dziko la mapiri ku Beteli, ndipo 1,000 anali ndi Yonatani ku Gibeya ku Benjamini. Anthu ena onse otsala anawabweza kwawo.
Saul chose for him three thousand men of Israel, of which two thousand were with Saul in Michmash, and on the mount of Bethel, and a thousand were with Jonathan in Gibeah of Benjamin, and the rest of the people he sent every man to his tent.
3 Yonatani anakantha mkulu wa ankhondo wa Afilisti ku Geba, ndipo Afilisti anamva kuti Aheberi awukira. Tsono Sauli anawuza amithenga kuti alize lipenga mʼdziko lonse la Israeli.
And Jonathan smote the garrison of the Philistines that was in Geba, and the Philistines heard of it. And Saul blew the trumpet throughout all the land, saying, Let the Hebrews hear.
4 Choncho Aisraeli onse anamva kuti Sauli wakantha mkulu wa ankhondo Wachifilisiti ndi kuti Afilisti anayipidwa nawo Aisraeli. Ndiye anthu anayitanidwa kuti abwere kwa Sauli ku Giligala.
And all Israel heard say that Saul had smitten the garrison of the Philistines, and also that Israel was had in abomination with the Philistines. And the people were gathered together after Saul to Gilgal.
5 Tsono Afilisti anasonkhana kuti amenyane ndi Aisraeli. Iwo anali ndi magaleta 3,000, okwera pa akavalo 2,000 ndiponso asilikali kuchuluka kwake ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja. Iwo anapita ndi kukamanga misasa yawo ku Mikimasi, kummawa kwa Beti-Aveni.
And the Philistines assembled themselves together to fight with Israel: thirty thousand chariots, and six thousand horsemen, and people as the sand which is on the sea-shore in multitude. And they came up, and encamped in Michmash, eastward of Beth-aven.
6 Pamene Aisraeli anaona kuti anali pamavuto akulu, poti anali atapanikizidwa kwambiri, anabisala mʼmapanga, mʼmaenje, mʼmatanthwe, mʼmakwalala ndi mʼzitsime.
When the men of Israel saw that they were in a strait (for the people were distressed), then the people hid themselves in caves, and in thickets, and in rocks, and in coverts, and in pits.
7 Ahebri ena anawoloka Yorodani mpaka kukafika ku dziko la Gadi ndi ku Giliyadi. Koma Sauli anakhalabe ku Giligala ndipo ankhondo onse amene anali naye anali njenjenje ndi mantha.
Now some of the Hebrews had gone over the Jordan to the land of Gad and Gilead, but as for Saul, he was yet in Gilgal, and all the people followed him trembling.
8 Saulo anadikirira masiku asanu ndi awiri, monga mwa nthawi imene ananena Samueli. Koma Samueli sanabwere ku Giligala, ndipo anthu anayamba kumuthawa Sauli uja.
And he tarried seven days, according to the set time that Samuel had appointed, but Samuel did not come to Gilgal, and the people were scattered from him.
9 Kotero iye anati, “Bwera nayoni nsembe yopsereza ndi nsembe ya chiyanjano.” Ndipo Sauli anapereka nsembe yopsereza.
And Saul said, Bring here the burnt offering to me, and the peace offerings. And he offered the burnt offering.
10 Atangomaliza kupereka nsembe, anangoona Samueli watulukira ndipo Sauli anapita kukamulonjera.
And it came to pass that, as soon as he had made an end of offering the burnt offering, behold, Samuel came, and Saul went out to meet him, that he might salute him.
11 Samueli anafunsa kuti, “Nʼchiyani chimene wachita?” Sauli anayankha kuti, “Nditaona kuti anthu ayamba kundithawa, ndi kuti inu simunabwere pa nthawi munanena ija, ndiponso kuti Afilisti akusonkhana ku Mikimasi,
And Samuel said, What have thou done? And Saul said, Because I saw that the people were scattered from me, and that thou did not come within the days appointed, and that the Philistines assembled themselves together at Michmash,
12 ndinati, ‘Tsopano Afilisti abwera kudzandithira nkhondo ku Giligala kuno, chonsecho sindinapemphe Yehova kuti andikomere mtima.’ Motero ndinakakamizika kupereka nsembe yopsereza.”
therefore I said, Now the Philistines will come down upon me to Gilgal, and I have not entreated the favor of Jehovah. I forced myself therefore, and offered the burnt offering.
13 Samueli anati, “Mwachita zopusa. Simunatsate zimene Yehova Mulungu wanu anakulamulani kuti muchite. Mukanazitsata, Yehova akanawukhazikitsa ufumu wanu mu Israeli mpaka kalekale.
And Samuel said to Saul, Thou have done foolishly. Thou have not kept the commandment of Jehovah thy God, which he commanded thee. For now Jehovah would have established thy kingdom upon Israel forever,
14 Koma tsopano ufumu wanu sudzakhalitsa. Yehova wapeza munthu wapamtima pake ndipo wamusankha kukhala mtsogoleri wa anthu ake chifukwa inu simunasunge malamulo a Yehova.”
but now thy kingdom shall not continue. Jehovah has sought for him a man after his own heart, and Jehovah has appointed him to be prince over his people, because thou have not kept that which Jehovah commanded thee.
15 Kenaka Samueli anachoka ku Giligala ndi kupita ku Gibeyati ku dziko la Benjamini. Saulo anawerenga anthu amene anali naye ndipo analipo 600.
And Samuel arose, and got up from Gilgal to Gibeah of Benjamin. And Saul numbered the people who were present with him, about six hundred men.
16 Sauli ndi mwana wake Yonatani pamodzi ndi asilikali amene anali naye aja amakhala ku Geba ku dziko la Benjamini. Koma Afilisti anamanga misasa yawo ku Mikimasi.
And Saul, and Jonathan his son, and the people that were present with them, abode in Geba of Benjamin, but the Philistines encamped in Michmash.
17 Ankhondo a Afilisti anatuluka mʼmisasa yawo mʼmagulu atatu. Gulu lina linapita ku Ofiri ku dziko la Suwala.
And the spoilers came out of the camp of the Philistines in three companies. One company turned to the way that leads to Ophrah, to the land of Shual,
18 Gulu lina linalunjika ku Beti-Horoni, ndipo gulu lachitatu linalunjika ku malire oyangʼanana ndi chigwa cha Zeboimu cha ku chipululu.
and another company turned the way to Beth-horon, and another company turned the way of the border that looks down upon the valley of Zeboim toward the wilderness.
19 Nthawi imeneyo nʼkuti mulibe osula zitsulo mʼdziko lonse la Israeli, pakuti Afilisti anati, “Tisawalole Aheberi kudzipangira okha malupanga kapena mikondo!”
Now there was no blacksmith found throughout all the land of Israel, for the Philistines said, Lest the Hebrews make for them swords or spears,
20 Kotero Aisraeli onse amapita kwa Afilisti kukanoletsa mapulawo, makasu, nkhwangwa ndi zikwakwa zawo.
but all the Israelites went down to the Philistines to sharpen every man his share, and his coulter, and his axe, and his mattock.
21 Mtengo wonolera mapulawo ndi makasu unali zigawo ziwiri za sekeli, mtengo wonolera zisonga ndi nkhwangwa unali gawo limodzi la Sekeli.
Yet they had a file for the mattocks, and for the coulters, and for the forks, and for the axes, and to set the goads.
22 Motero tsiku la nkhondolo panalibe lupanga kapena mkondo mʼdzanja la aliyense amene anatsatira Saulo ndi Yonatani. Koma Saulo ndi Yonatani, iwo okha ndiwo anali ndi zida.
So it came to pass in the day of battle, that there was neither sword nor spear found in the hand of any of the people who were with Saul and Jonathan. But with Saul and with Jonathan his son there was found.
23 Tsono gulu lina lankhondo la Chifilisti linapita kukalonda mpata wa Mikimasi.
And the garrison of the Philistines went out to the pass of Michmash.

< 1 Samueli 13 >