< 1 Samueli 10 >

1 Ndipo Samueli anatenga botolo la mafuta nathira mafutawo pa mutu wa Sauli ndipo anapsompsona nati, “Yehova wakudzoza kuti ukhale mtsogoleri wa anthu ake, Aisraeli. Iwe udzalamulira anthu a Yehova ndiponso udzawapulumutsa mʼmanja mwa adani awo owazungulira. Chizindikiro chakuti Yehova wakudzoza kuti ukhale mtsogoleri wa anthu ake ndi ichi:
Then took Samuel a flask of oil, and poured out upon his head, and kissed him, —and said—Is it not, that Yahweh hath anointed thee over his inheritance, as leader?
2 Ukachoka pano lero lino, udzakumana ndi amuna awiri kufupi ndi manda a Rakele ku Zeliza mʼmalire mwa dziko la Benjamini ndipo adzakuwuza kuti, ‘Abulu amene munkafunafuna aja apezeka. Ndipo tsopano abambo ako asiya kuganiza za abulu ndipo akudera nkhawa za iwe.’ Iwo akufunsa kuti, ‘Kodi ndidzachita chiyani mmene mwana wanga sakuoneka?’”
When thou departest, to-day, from me, then shalt thou find two men by the grave of Rachel, within the boundary of Benjamin, in Zelzah, —and they will say unto thee, The asses are found, which thou wentest to seek, and lo! thy father hath abandoned caring for the asses, and is concerned for you, saying, What shall I do for my son?
3 “Ndipo udzapyola pamenepo ndi kufika ku mtengo wa thundu wa ku Tabori. Kumeneko udzakumana ndi anthu atatu akupita kukapereka nsembe ku Nyumba ya Mulungu ku Beteli. Mmodzi adzakhala atanyamula ana ambuzi atatu, wina atanyamula malofu atatu a buledi, ndi winayo atanyamula thumba la vinyo.
Then shalt thou pass on quickly from thence onwards, and come as far as the oak of Tabor, and there shall find thee there, three men going up unto God, at Bethel, —one, carrying three kids, and, another, carrying three cakes of bread, and, another, carrying a skin of wine;
4 Adzakupatsa moni ndi kukupatsa malofu awiri a buledi. Iwe udzalandire bulediyo.
then will they ask thee, of thy welfare, —and give thee two cakes of bread, which thou shalt receive at their hand.
5 “Pambuyo pake, udzafike ku Gibeyati-Elohimu, kumene kuli gulu la ankhondo la Afilisti. Pamene ukuyandikira mzindawo, udzakumana ndi gulu la aneneri akutsika kuchokera ku phiri, akuyimba zeze, ngʼoma, zitoliro ndi pangwe, ndiponso akulosera.
After that, shalt thou come unto the hill of God, where is the garrison of the Philistines, —and it shall be, as thou comest in thither into the city, thou shalt light upon a band of prophets, coming down from the high place, and, before them, a harp, and a timbrel, and a flute, and a lyre, they having been moved to prophesy.
6 Kenaka Mzimu wa Yehova udzabwera pa iwe ndi mphamvu, ndipo udzayamba kulosera nawo pamodzi. Ndipo udzasinthika kukhala munthu wina.
Then will come suddenly upon thee, the Spirit of Yahweh, and thou shalt be moved to prophesy with them, —and shalt be changed into another man.
7 Zizindikiro izi zikakachitika, dzachite chilichonse manja ako angathe kuchita, pakuti Mulungu ali nawe.
And it shall be, when these signs shall come unto thee, then act thou for thyself, as thou shalt find occasion, for, God, is with thee.
8 “Tsono tsogola kupita ku Giligala. Ine ndidzabwera ndithu kudzapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Koma ukandidikire masiku asanu ndi awiri mpaka ine nditabwera kuti ndidzakuwuze zomwe udzachite.”
And thou shalt go down before me to Gilgal, for lo! I am coming down unto thee, to offer up ascending-offerings, to sacrifice peace-offerings, —seven days, shalt thou tarry, until I come unto thee, then will I let thee know what thou shalt do.
9 Sauli akutembenuka kusiyana ndi Samueli, Mulungu anasintha mtima wa Sauli, ndipo zinthu zonsezi zinakwaniritsidwa tsiku lomwelo.
And so it was, that, when he turned away to depart from Samuel, God gave him another heart, —and all these signs came to pass that day.
10 Atafika ku Gibeya, anakumana ndi gulu la aneneri. Mzimu wa Mulungu unabwera pa iye mwamphamvu, nayamba kulosa nawo.
And, when they came thither to the hill, lo! a band of prophets coming to meet him, —then came suddenly upon him, the Spirit of God, and he was moved to prophesy in their midst.
11 Pamene onse amene ankamudziwa kale anamuona akulosera pamodzi ndi aneneri, anafunsana wina ndi mnzake. “Kodi nʼchiyani chachitika ndi mwana wa Kisi? Kodi Sauli alinso mʼgulu la aneneri?”
And it came to pass, that, all who knew him aforetime, looked, and lo! with the prophets, he did prophesy. So the people said, one to another—What, now, hath befallen the son of Kish? Is, even Saul, among the prophets?
12 Munthu wina wa kumeneko anayankha kuti, “Nanga enawa abambo awo ndani?” Kotero kunayambika mwambi wakuti, “Kodi Saulinso ali mʼgulu la aneneri?”
Then responded one of that place, and said, But who is, their father? For this cause, it became a proverb, Is, even Saul, among the prophets?
13 Sauli atasiya kuloserako, anapita ku kachisi ku phiri.
And, when he had made an end of prophesying, he came to the high place.
14 Tsono amalume ake a Sauli anamufunsa ndi mnyamata wake kuti, “Munapita kuti?” Iye anayakha, “Timakafunafuna abulu koma titaona kuti sakupezeka, tinapita kwa Samueli.”
Then said Saul’s uncle unto him, and unto his young man—Whither have ye been? And he said, To seek the asses, and, when they were nowhere, to be seen, we came unto Samuel.
15 Amalume ake a Sauli anati, “Chonde, ndifotokozereniko zimene Samueli wakuwuzani.”
And Saul’s uncle said, —Do tell me, I pray thee, what Samuel said to you.
16 Sauli anati, “Iye anatitsimikizira kuti abulu anapezeka.” Koma sanawawuze amalume akewo za nkhani ija ya ufumu imene Samueli anamuwuza.
And Saul said unto his uncle, He, told, us that the asses were found, —but, as to the matter of the kingdom, he told him not what Samuel had said.
17 Samueli anayitana Aisraeli onse kuti asonkhane pamaso pa Yehova ku Mizipa.
Then Samuel called out the people, unto Yahweh, at Mizpah,
18 Ndipo anawuza Aisraeli onse kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi kukupulumutsani mʼdzanja la Igupto ndi mʼdzanja la mafumu onse amene ankakuzunzani.’
and said unto the sons of Israel—Thus, saith Yahweh, God of Israel: I myself, brought up Israel, out of Egypt, —and rescued you out of the hand of the Egyptians, and out of the hand of all the kingdoms that distressed you.
19 Koma lero mwamukana Mulungu wanu amene amakupulumutsani mʼmavuto anu onse ndi mʼzowawa zanu. Ndipo mukuti, ‘Ayi, koma mutipatse mfumu yotilamulira.’ Tsopanotu sonkhanani pamaso pa Yehova mwa mafuko ndi mabanja anu.”
Yet, ye, to-day, have rejected your God, who, himself, hath been giving you salvation from all your calamities and your distresses, and ye have said to him: A king, shalt thou set over us, —Now, therefore, present yourselves before Yahweh, by your tribes, and by your thousands.
20 Samueli atasonkhanitsa mafuko onse a Israeli, fuko la Benjamini linasankhidwa.
And, when Samuel had brought near all the tribes of Israel, then was taken the tribe of Benjamin.
21 Anasonkhanitsa fuko la Benjamini banja ndi banja. Pomaliza anasonkhanitsa banja la Matiri mmodzimmodzi ndipo Sauli mwana wa Kisi anasankhidwa. Koma atamufunafuna, sanamupeze.
And, when he had brought near the tribe of Benjamin, by their families, then was taken the family of Matri, —and, when he had brought near the family of Matri, man by man, then was taken Saul the son of Kish; so they sought him, but he was not to be found.
22 Tsono anthu anafunsanso kwa Yehova kuti, “Kodi munthuyu wabwera kale kuno?” Ndipo Yehova anayankha kuti, “Inde wabisala pakati pa katundu.”
Then asked they again of Yahweh, Hath there yet to come in hither a man? And Yahweh said, Lo! he, hath hid himself among the stores.
23 Iwo anathamanga ndi kukamutenga kumeneko. Atayimirira pakati pa anthu anapezeka kuti anali wamtali kuposa anthu ena mwakuti ankamulekeza mʼmapewa.
So they ran, and fetched him thence, and, when he presented himself in the midst of the people, then was he [seen to be] taller than any of the people, from his shoulders and upwards.
24 Samueli anafunsa anthu onse kuti, “Kodi mukumuona munthu amene Yehova wasankha? Palibe wofanana naye pakati pa anthu onse.” Kenaka anthu onse anafuwula kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wautali!”
And Samuel said unto all the people—Have ye seen him whom Yahweh hath chosen, that there is none like him, among all the people? And all the people shouted, and said—Let the king live!
25 Samueli anafotokozera anthu ntchito ndi udindo wa mfumu. Pambuyo pake analemba mʼbuku zonse zokhudza ntchito ndi udindo wa mfumu, ndipo bukulo analiyika pamaso pa Yehova. Kenaka Samueli analola aliyense kuti abwerere kupita kwawo.
Then Samuel declared unto the people the manner of the kingdom, and wrote it in a scroll, and laid it up before Yahweh. And Samuel sent away all the people, every man to his own house.
26 Sauli anapitanso ku mudzi kwawo ku Gibeya, pamodzi ndi anthu amphamvu amene Mulungu anawafewetsa mitima.
Yea, even Saul, went to his own house, at Gibeah, —and the valiant men whose heart God had moved went with him.
27 Koma anthu ena achabechabe anati, “Kodi munthu uyu angathe bwanji kutipulumutsa?” Iwo anayamba kumunyoza Sauliyo, ndipo sankamupatsa ngakhale mphatso. Koma iye sanalabadireko.
But, abandoned men, said—How can this one save us? So they treated him with contempt, and brought him no present, —but he was as one that was deaf.

< 1 Samueli 10 >