< 1 Mafumu 9 >

1 Solomoni atatsiriza kumanga Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu, ndi kukwaniritsa kuchita zonse zimene ankafuna,
Now it happened that, when Solomon had perfected the building of the house of the Lord, and the king’s house, and all that he had desired and had willed to do,
2 Yehova anamuonekera kachiwiri, monga momwe anamuonekera ku Gibiyoni.
the Lord appeared to him a second time, just as he had appeared to him at Gibeon.
3 Yehova ananena kwa iye kuti: “Ndamva pemphero ndi pembedzero lako pa zimene wapempha pamaso panga. Ndayipatula Nyumba iyi, imene wamanga, poyikamo Dzina langa mpaka muyaya. Maso anga ndi mtima wanga zidzakhala pamenepo nthawi zonse.
And the Lord said to him: “I have heard your prayer and your petition, which you prayed before me. I have sanctified this house, which you have built, so that I may place my name there forever, and so that my eyes and my heart will be there for all days.
4 “Kunena za iwe, ukayenda pamaso panga mokhulupirika, mwangwiro ndi moona mtima monga momwe anachitira abambo ako Davide, ndi kuchita zonse zimene ndakulamula ndi kusamalitsa malangizo ndi malamulo anga,
Also, if you will walk before me, just as your father walked, in simplicity of heart and in equity, and you do all that I have instructed to you, and you keep my laws and my judgments,
5 Ine ndidzakhazikitsa mpando wako waufumu pa Israeli mpaka muyaya, monga ndinalonjezera abambo ako Davide pamene ndinati, ‘Sipadzasowa munthu pa mpando waufumu wa Israeli.’
then I will set the throne of your kingdom over Israel forever, just as I promised your father David, saying: ‘A man from your stock shall not be taken away from the throne of Israel.’
6 “Koma ngati iwe kapena ana ako mudzapatuka ndi kuleka kusunga malamulo ndi mawu anga amene ndakupatsani ndi kupita kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza,
But if you and your sons, wandering, will have turned away, not following me, and not keeping my commandments and my ceremonies, which I have proposed to you, but instead you go away, and you serve strange gods and adore them,
7 pamenepo Ine ndidzazula Aisraeli mʼdziko limene ndinawapatsa ndiponso ndidzayikana Nyumba ino imene ndayipatula chifukwa cha Dzina langa. Pamenepo Aisraeli adzasanduka mwambi ndi chinthu chonyozedwa pakati pa anthu onse.
then I will take away Israel from the face of the land, which I have given to them. And the temple, which I have sanctified to my name, I will cast out from my sight. And Israel will be a proverb and a parable among all the peoples.
8 Ndipo ngakhale kuti tsopano Nyumba ya Mulunguyi ndi yokongola kwambiri, onse amene adzadutsa pano adzadabwa kwambiri ndipo adzatsonya ndipo adzati, ‘Nʼchifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere mʼdziko muno ndi pa Nyumba ya Mulunguyi?’
And this house will become an example: anyone who passes by it will be stupefied, and he will hiss and say, ‘Why has the Lord acted in this way to this land and to this house?’
9 Anthu adzayankha kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti asiya Yehova Mulungu wawo amene anatulutsa makolo awo mʼdziko la Igupto, ndipo akangamira milungu ina ndi kumayipembedza ndi kuyitumikira. Choncho Iye wabweretsa zovuta zonsezi.’”
And they will respond: ‘Because they abandoned the Lord their God, who led their fathers away from the land of Egypt, and they followed strange gods, and they adored them and served them. For this reason, the Lord led all this evil over them.’”
10 Patatha zaka makumi awiri, ndiye nthawi imene Solomoni anamanga nyumba ziwirizi: Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu,
Then, when twenty years were fulfilled, after Solomon had built the two houses, that is, the house of the Lord, and the house of the king,
11 Mfumu Solomoni anapereka mizinda makumi awiri ya ku Galileya kwa Hiramu mfumu ya ku Turo chifukwa Hiramu nʼkuti atapereka mitengo yonse ya mkungudza ndi ya payini ndiponso golide yense zimene Solomoni ankazifuna.
Hiram, the king of Tyre, having supplied Solomon with cedar wood, and spruce wood, and gold, in accord with all that he needed, then Solomon gave Hiram twenty towns in the land of Galilee.
12 Koma Hiramu atabwera kuchokera ku Turo kudzaona mizinda imene Solomoni anamupatsa, sanasangalatsidwe nayo mizindayo.
And Hiram went out of Tyre, so that he might view the towns that Solomon had given to him. And they did not please him.
13 Iye anafunsa kuti, “Mʼbale wanga, kodi iyi nʼkukhala mizinda yondipatsa?” Ndipo iye anayitcha mizindayo Dziko la Kabuli, dzina lomwe amatchedwa mpaka lero lino.
And he said, “Are these the cities that you have given to me, brother?” And he called them the land of Cabul, even to this day.
14 Koma Hiramu anali atatumiza kwa mfumu golide oposa makilogalamu 4,000.
And Hiram sent to king Solomon one hundred twenty talents of gold.
15 Izi ndi zimene anachita Mfumu Solomoni: Analamula anthu kuti agwire ntchito yathangata pomanga Nyumba ya Yehova, nyumba yake, malo achitetezo a Milo, mpanda wa Yerusalemu, Hazori, Megido ndi Gezeri.
This is the sum of the expenses that king Solomon offered for the building of the house of the Lord, and his own house, and for Millo, and the wall of Jerusalem, and Hazor, and Megiddo, and Gezer.
16 (Farao mfumu ya ku Igupto inali itathira nkhondo ndi kulanda Gezeri. Iye anatentha mzindawo. Anapha Akanaani amene ankakhala mʼmenemo ndipo kenaka anawupereka ngati mphatso yaukwati kwa mwana wake wamkazi amene anakwatiwa ndi Solomoni.
Pharaoh, the king of Egypt, ascended and seized Gezer, and he burned it with fire. And he put to death the Canaanite who was living in the city, and he gave it as a dowry for his daughter, the wife of Solomon.
17 Ndipo Solomoni anamanganso Gezeri.) Iye anamanga Beti-Horoni Wakumunsi,
Therefore, Solomon built up Gezer, and lower Beth-horon,
18 Baalati ndi Tadimori ku chipululu, mʼdziko lake lomwelo,
and Baalath, and Palmira in the land of the wilderness.
19 pamodzinso ndi mizinda yake yosungira chuma ndiponso mizinda yosungiramo magaleta ndi akavalo ake. Anamanganso chilichonse chimene anafuna kumanga ku Yerusalemu, ku Lebanoni ndi ku madera onse amene iye ankalamulira.
And all the towns which belonged to him, and which were without walls, he walled, along with the cities of the chariots, and the cities of the horsemen, and whatever was pleasing to him that he might build in Jerusalem, and in Lebanon, and in the entire land of his dominion.
20 Panali anthu amene anatsala pakati pa mitundu ya Aamori, Ahiti, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi (anthu awa sanali Aisraeli).
All the people who had remained of the Amorites, and the Hittites, and the Perizzites, and the Hivites, and the Jebusites, who were not of the sons of Israel,
21 Zimenezi ndiye zinali zidzukulu zawo zotsalira mʼdzikoli, anthu amene Aisraeli sanathe kuwawononga kotheratu. Solomoni anawatenga ndi kukhala akapolo ake ogwira ntchito yathangata, monga zilili mpaka lero lino.
their sons, who had remained in the land, namely, those whom the sons of Israel had not been able to destroy, Solomon made tributary, even to this day.
22 Koma Solomoni sanagwiritse ntchito ya ukapolo Mwisraeli aliyense; iwo anali anthu ake ankhondo, nduna zake, atsogoleri a ankhondo, akapitawo ake, olamulira magaleta ndi oyendetsa magaleta ake.
But from the sons of Israel, Solomon did not appoint anyone at all to serve, except the men of war, and his ministers, and leaders, and commanders, and the overseers of the chariots and the horses.
23 Amenewa ndiwo anali akuluakulu oyangʼanira ntchito za Solomoni. Anthu okwana 550 ndiwo ankayangʼanira anthu amene ankagwira ntchitowo.
Now there were five hundred fifty leaders in the first place over all the works of Solomon, and they had people subject to them, and these were given orders for the appointed works.
24 Mwana wamkazi wa Farao atachoka mu Mzinda wa Davide, kupita ku nyumba ya mfumu imene Solomoni anamumangira, Solomoni anamanga malo achitetezo a Milo.
And the daughter of Pharaoh went up from the city of David to her house, which Solomon had built for her. Then he built up Millo.
25 Katatu pa chaka Solomoni ankapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pa guwa lansembe limene anamangira Yehova ndiponso ankafukiza lubani pamaso pa Yehova. Potero ankakwaniritsa zoyenera kuchitika mu Nyumba ya Yehova.
Also, three times each year, Solomon offered holocausts and victims of peace offerings, upon the altar that he had built to the Lord, and he burned incense before the Lord. And the temple was perfected.
26 Mfumu Solomoni anapanganso sitima zapamadzi ku Ezioni Geberi, malo amene ali pafupi ndi Eloti ku Edomu, mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.
And king Solomon made a navy at Ezion Geber, which is beside Eloth, on the shores of the Red Sea, in the land of Idumea.
27 Ndipo Hiramu anatumiza anthu ake oyendetsa sitima zapamadzi amene ankadziwa za pa nyanja kuti aziyendetsa pamodzi ndi anthu a Solomoni.
And Hiram sent his servants to that navy, the sailors and those knowledgeable about the sea, with the servants of Solomon.
28 Iwo anapita ku Ofiri ndipo anakatenga golide okwana makilogalamu 14,000, amene anamupereka kwa Mfumu Solomoni.
And when they had gone to Ophir, taking from there four hundred twenty talents of gold, they brought it to king Solomon.

< 1 Mafumu 9 >