< 1 Mafumu 2 >

1 Davide ali pafupi kumwalira, analangiza mwana wake Solomoni kuti:
Then the dayes of Dauid drewe neere that he should die, and hee charged Salomon his sonne, saying,
2 “Ndatsala pangʼono kupita kumene munthu wina aliyense amayenera kupitako. Tsono khala wamphamvu, uvale zilimbe,
I go the way of all the earth: be strong therefore, and shew thy selfe a man,
3 ndipo uzichita zimene Yehova Mulungu wako amafuna, uziyenda mʼnjira zake, uzisunga malangizo ndi malamulo ake monga momwe zinalembedwera mʼMalamulo a Mose, kuti zonse zimene udzachite zidzakuyendere bwino kulikonse kumene udzapite.
And take heede to the charge of the Lord thy God, to walke in his wayes, and keepe his statutes, and his commandements, and his iudgements, and his testimonies, as it is written in the Law of Moses, that thou mayest prosper in all that thou doest, and in euery thing whereunto thou turnest thee,
4 Ndipo Yehova akwaniritse zimene anandilonjeza kuti, ‘Ngati zidzukulu zako zidzakhala mosamala, niziyenda mokhulupirika pamaso panga ndi mtima wawo wonse ndi moyo wawo wonse, sudzasowa munthu wokhala pa mpando waufumu wa Israeli.’
That the Lord may confirme his worde which hee spake vnto me, saying, If thy sonnes take heede to their way, that they walke before me in trueth, with all their hearts, and with all their soules, thou shalt not (sayd he) want one of thy posteritie vpon the throne of Israel.
5 “Tsono iwe ukudziwanso zoyipa zimene Yowabu mwana wa Zeruya anandichitira pakupha atsogoleri awiri a ankhondo a Israeli, Abineri mwana wa Neri ndi Amasa mwana wa Yeteri. Iye anawapha ndi kukhetsa magazi nthawi ya mtendere ngati nthawi ya nkhondo, ndipo anapaka magazi amenewo pa lamba wa mʼchiwuno mwake ndi pa nsapato za ku mapazi ake.
Thou knowest also what Ioab the sonne of Zeruiah did to me, and what he did to the two captaines of the hostes of Israel, vnto Abner the sonne of Ner, and vnto Amasa the sonne of Iether: whome he slewe, and shed blood of battell in peace, and put the blood of warre vpon his girdle that was about his loynes, and in his shooes that were on his feete.
6 Iwe uchite kwa iye molingana ndi nzeru zako, koma usalole kuti afe ndi ukalamba ndi kupita ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
Doe therefore according to thy wisdome, and let thou not his hoare head go downe to the graue in peace. (Sheol h7585)
7 “Koma ana a Barizilai wa ku Giliyadi uwakomere mtima ndipo uwalole kuti akhale mʼgulu la anthu amene azidya pamodzi nawe. Pakuti anandisamalira pamene ndinkathawa mʼbale wako Abisalomu.
But shew kindnes vnto the sonnes of Barzillai the Gileadite, and let them be among them that eate at thy table: for so they came to me when I fled from Absalom thy brother.
8 “Ndipo kumbukira kuti uli ndi Simei mwana wa Gera, wa fuko la Benjamini wochokera ku Bahurimu, amene ananditemberera koopsa tsiku limene ndimapita ku Mahanaimu. Atabwera kudzakumana nane ku Yorodani, ine ndinalumbira mʼdzina la Yehova kuti, ‘Sindidzakupha iwe ndi lupanga.’
And beholde, with thee is Shimei the sonne of Gera, the sonne of Iemini, of Bahurim, which cursed mee with an horrible curse in the day when I went to Mahanaim: but hee came downe to meete me at Iorden, and I sware to him by the Lord, saying, I will not slay thee with the sword.
9 Koma tsopano usamuyese ngati munthu wosalakwa. Iwe ndiwe munthu wanzeru. Udzadziwa choti uchite naye. Ngakhale ndi wokalamba, aphedwe ndithu.” (Sheol h7585)
But thou shalt not count him innocent: for thou art a wise man, and knowest what thou oughtest to doe vnto him: therefore thou shalt cause his hoare head to goe downe to the graue with blood. (Sheol h7585)
10 Tsono Davide anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Mzinda wa Davide.
So Dauid slept with his fathers, and was buried in the citie of Dauid.
11 Iyeyo nʼkuti atalamulira Israeli kwa zaka makumi anayi. Ku Hebroni analamulira zaka zisanu ndi ziwiri ndipo ku Yerusalemu analamulira zaka 33.
And the dayes which Dauid reigned vpon Israel, were fourtie yeeres: seuen yeeres reigned he in Hebron, and thirtie and three yeeres reigned he in Ierusalem.
12 Choncho Solomoni anakhala pa mpando waufumu wa abambo ake Davide, ndipo ufumu wake unakhazikika kwambiri.
Then sate Salomon vpon the throne of Dauid his father, and his kingdome was stablished mightily.
13 Tsono Adoniya, mwana wa Hagiti, anapita kwa Batiseba, amayi ake a Solomoni. Batiseba anamufunsa kuti, “Kodi wabwera mwamtendere?” Iye anayakha kuti, “Eya, ndi zamtendere.”
And Adonijah the sonne of Haggith came to Bath-sheba the mother of Salomon: and she saide, Commest thou peaceably? And hee said, Yea.
14 Ndipo iye anawonjezera kunena kuti, “Ndili ndi mawu oti ndiyankhule nanu.” Batiseba anayankha kuti, “Yankhula.”
He said moreouer, I haue a sute vnto thee. And she sayd, Say on.
15 Tsono Adoniya anati, “Monga inu mukudziwa, ufumu unali wanga. Aisraeli onse ankayembekezera kuti ine ndidzakhala mfumu yawo. Koma zinthu zinasintha ndipo ufumu wapita kwa mʼbale wanga; pakuti wapatsa iye ufumuwu ndi Yehova.
Then he said, Thou knowest that the kingdome was mine, and that all Israel set their faces on me, that I should reigne: howbeit the kingdome is turned away, and is my brothers: for it came to him by the Lord.
16 Tsono ndili ndi pempho limodzi kwa inu. Musandikanize ayi.” Batiseba anati, “Nena.”
Nowe therefore I aske thee one request, refuse me not. And she said vnto him, Say on.
17 Adoniya anapitiriza kunena kuti, “Chonde, inu mupemphe mfumu Solomoni kuti andipatse Abisagi wa ku Sunemu kuti akhale mkazi wanga pakuti mukapempha inu sadzakukanizani.”
And he sayd, Speake, I pray thee, vnto Salomon ye King, (for he will not say thee nay) that he giue me Abishag the Shunammite to wife.
18 Batiseba anayankha kuti, “Chabwino. Ndidzakuyankhulira kwa mfumu.”
And Bath-sheba sayd, Well, I will speake for thee vnto the King.
19 Batiseba atapita kwa Mfumu Solomoni kukayankhula naye mʼmalo mwa Adoniya, mfumu inanyamuka kukumana naye, ndipo inaweramira amayi akewo, kenaka inakhala pa mpando wake waufumu. Iye anayitanitsa mpando wina kuti amayi ake akhalepo ndipo anakhala pansi ku dzanja lake lamanja.
Bath-sheba therefore went vnto King Salomon, to speake vnto him for Adonijah: and the King rose to meete her, and bowed himselfe vnto her, and sate downe on his throne: and he caused a seate to be set for the Kings mother, and she sate at his right hand.
20 Amayi akewo anati, “Ndikufuna ndikupempheni kanthu kakangʼono. Chonde musandikanize.” Mfumu inayankha kuti, “Pemphani amayi, ine sindikukanizani.”
Then she sayd, I desire a small request of thee, say me not nay. Then the King sayde vnto her, Aske on, my mother: for I will not say thee nay.
21 Ndipo amayiwo anati, “Mulole kuti Abisagi wa ku Sunemu akhale mkazi wa mʼbale wanu Adoniya.”
She sayd then, Let Abishag the Shunammite be giuen to Adonijah thy brother to wife.
22 Koma Mfumu Solomoni inayankha amayi ake aja kuti, “Chifukwa chiyani mukupemphera Adoniya Abisagi wa ku Sunemu? Mungathenso kumupemphera ufumu pakuti iyeyu ndi mkulu wanga ndipo mupemphereninso wansembe Abiatara ndi Yowabu mwana wa Zeruya!”
But King Salomon answered and sayd vnto his mother, And why doest thou aske Abishag the Shunammite for Adonijah? aske for him the kingdome also: for he is mine elder brother, and hath for him both Abiathar the Priest, and Ioab the sonne of Zeruiah.
23 Pamenepo Mfumu Solomoni inalumbira mʼdzina la Yehova kuti, “Mulungu andilange ine koopsa ngati Adoniya saphedwa chifukwa cha pempho lakeli!
Then King Salomon sware by the Lord, saying, God doe so to me and more also, if Adoniiah hath not spoken this worde against his owne life.
24 Tsono pali Yehova wamoyo, amene anandikhazikitsa ine pa mpando waufumu wa abambo anga Davide ndi kundipatsa ufumu monga analonjezera, Adoniya aphedwa lero lomwe lino!”
Now therefore as ye Lord liueth, who hath established me, and set me on the throne of Dauid my father, who also hath made me an house, as he promised, Adoniiah shall surely die this day.
25 Choncho Mfumu Solomoni inalamula Benaya mwana wa Yehoyada ndipo anakantha Adoniyayo, nafa.
And King Salomon sent by the hand of Benaiah the sonne of Iehoiada, and hee smote him that he dyed.
26 Ndipo mfumu inati kwa Abiatara wansembe, “Pita ku Anatoti ku minda yako chifukwa ndiwe woyenera kufa, koma sindikupha tsopano, chifukwa unkanyamula Bokosi la Chipangano la Ambuye Yehova pamaso pa abambo anga Davide ndipo unazunzika limodzi ndi abambo angawo.”
Then the King sayd vnto Abiathar the Priest, Go to Anathoth vnto thine owne fieldes: for thou art worthy of death: but I will not this day kill thee, because thou barest the Arke of the Lord God before Dauid my father, and because thou hast suffered in all, wherein my father hath bene afflicted.
27 Kotero Solomoni anachotsa Abiatara pa udindo wokhala wansembe wa Yehova, kukwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula za nyumba ya Eli ku Silo.
So Salomon cast out Abiathar from being Priest vnto the Lord, that he might fulfill the wordes of the Lord, which he spake against the house of Eli in Shiloh.
28 Yowabu atamva zimenezi anathawira ku tenti ya Yehova ndipo anakagwira msonga za guwa lansembe, popeza Yowabu ndiye anathandiza Adoniya kuwukira koma sanathandize Abisalomu.
Then tidings came to Ioab: (for Ioab had turned after Adoniiah, but he turned not after Absalom) and Ioab fled vnto the Tabernacle of the Lord, and caught hold on the hornes of the altar.
29 Mfumu Solomoni inawuzidwa kuti Yowabu wathawira ku tenti ya Yehova ndipo ali pambali pa guwa lansembe. Tsono Solomoni analamula Benaya mwana wa Yehoyada kuti, “Pita, kamukanthe!”
And it was tolde king Salomon, that Ioab was fled vnto the Tabernacle of the Lord, and beholde, he is by the altar. Then Salomon sent Benaiah the sonne of Iehoiada, saying, Goe, fall vpon him.
30 Choncho Benaya analowa mʼtenti ya Yehova ndipo anati kwa Yowabu, “Mfumu ikuti ‘Tuluka!’” Koma iye anayankha kuti, “Ayi, ine ndifera muno.” Benaya anakafotokozera mfumu kuti, “Umu ndi mmene Yowabu wandiyankhira.”
And Benaiah came to the Tabernacle of the Lord, and sayd vnto him, Thus sayth the King, Come out. And he sayde, Nay, but I will die here. Then Benaiah brought the King worde againe, saying, Thus sayd Ioab, and thus he answered me.
31 Pamenepo mfumu inalamula Benaya kuti, “Kachite monga iye wanenera. Ukamukanthe ndi kumuyika mʼmanda. Ukatero udzandichotsera ine pamodzi ndi nyumba ya abambo anga mlandu wa anthu osalakwa amene Yowabu anawapha.
And the King sayde vnto him, Doe as he hath sayd, and smite him, and bury him, that thou mayest take away the blood, which Ioab shed causelesse, from me and from the house of my father.
32 Yehova adzamubwezera zomwe anachita pokhetsa magazi, chifukwa iye anakantha ndi lupanga anthu awiri abwino ndi olungama kuposa iye, nawapha, abambo anga Davide osadziwa. Anthu awiriwo ndi Abineri mwana wa Neri, wolamulira gulu lankhondo la Israeli ndi Amasa mwana wa Yeteri, wolamulira gulu lankhondo la Yuda.
And the Lord shall bring his blood vpon his owne head: for he smote two men more righteous and better then he, and slew them with the sword, and my father Dauid knew not: to wit, Abner the sonne of Ner, captaine of the hoste of Israel, and Amasa the sonne of Iether captaine of the hoste of Iudah.
33 Magazi amene Yowabu anakhetsa akhale pamutu pake ndi pa zidzukulu zake kwamuyaya. Koma pa Davide ndi zidzukulu zake, nyumba yake ndi mpando wake waufumu pakhale mtendere wochokera kwa Yehova kwamuyaya.”
Their blood shall therefore returne vpon the head of Ioab, and on the head of his seede for euer: but vpon Dauid, and vpon his seede, and vpon his house, and vpon his throne shall there be peace for euer from the Lord.
34 Choncho Benaya mwana wa Yehoyada anapita kukakantha Yowabu nʼkumupha ndipo anayikidwa mʼmanda mʼnyumba yakeyake ya ku chipululu.
So Benaiah the sonne of Iehoiada went vp, and smote him, and slewe him, and he was buryed in his owne house in the wildernesse.
35 Mfumu inayika Benaya mwana wa Yehoyada kuti akhale woyangʼanira gulu lankhondo mʼmalo mwa Yowabu ndipo inayika Zadoki kuti akhale wansembe mʼmalo mwa Abiatara.
And the King put Benaiah the sonne of Iehoiada in his roume ouer the hoste: and the King set Zadok the Priest in the roume of Abiathar.
36 Kenaka mfumu inatuma anthu kukayitana Simei ndipo inamuwuza kuti, “Udzimangire nyumba mu Yerusalemu ndipo uzikhala kumeneko, koma usatuluke mu mzinda kupita kwina kulikonse.
Afterwarde the King sent, and called Shimei, and sayde vnto him, Buylde thee an house in Ierusalem, and dwell there, and depart not thence any whither.
37 Tsiku lomwe udzatulukemo ndi kuwoloka Chigwa cha Kidroni, udziwiretu kuti udzafa ndipo magazi ako adzakhala pamutu pako.”
For that day that thou goest out, and passest ouer the riuer of Kidron, knowe assuredly, that thou shalt dye the death: thy blood shall be vpon thine owne head.
38 Simei anayankha mfumu kuti, “Zimene mwanenazi nʼzabwino. Kapolo wanu adzachita monga mbuye wanga mfumu mwanenera.” Choncho Simei anakhala mu Yerusalemu nthawi yayitali.
And Shimei sayd vnto the King, The thing is good: as my lord the King hath sayd, so wil thy seruant doe. So Shimei dwelt in Ierusalem many dayes.
39 Koma patatha zaka zitatu, akapolo awiri a Simei anathawira kwa Akisi mwana wa Maaka, mfumu ya ku Gati, ndipo Simei anawuzidwa kuti, “Akapolo anu ali ku Gati.”
And after three yeres two of the seruants of Shimei fled away vnto Achish sonne of Maachah King of Gath: and they tolde Shimei, saying, Behold, thy seruants be in Gath.
40 Atamva zimenezi, anakwera bulu wake ndipo anapita kwa Akisi ku Gati kukafunafuna akapolo ake. Choncho Simei anapita ndi kukatenga akapolo ake ku Gati ndipo anabwera nawo.
And Shimei arose, and sadled his asse, and went to Gath to Achish, to seeke his seruantes: and Shimei went, and brought his seruants from Gath.
41 Solomoni atawuzidwa kuti Simei anatuluka mu Yerusalemu ndi kupita ku Gati ndipo kuti wabwerako,
And it was tolde Salomon, that Shimei had gone from Ierusalem to Gath, and was come againe.
42 mfumu inamuyitanitsa Simei ndipo inamufunsa kuti, “Kodi sindinakulumbiritse mʼdzina la Yehova ndi kukuchenjeza kuti, ‘Tsiku limene udzatuluka kupita kwina kulikonse, udziwe kuti udzafa’? Nthawi imeneyo iwe unandiwuza kuti, ‘Zimene mwanena nʼzabwino. Ine ndidzamvera.’
And the King sent and called Shimei, and sayde vnto him, Did I not make thee to sweare by the Lord, and protested vnto thee, saying, That day that thou goest out, and walkest any whither, knowe assuredly that thou shalt dye the death? And thou saydest vnto mee, The thing is good, that I haue heard.
43 Chifukwa chiyani tsono sunasunge lumbiro lako kwa Yehova? Bwanji nanga sunamvere lamulo limene ndinakuwuza?”
Why then hast thou not kept the othe of the Lord, and the commandement wherewith I charged thee?
44 Mfumuyo inawuzanso Simei kuti, “Ukudziwa mu mtima mwakomo zoyipa zonse zimene unachitira abambo anga Davide. Tsopano Yehova akubwezera zoyipa zakozo.
The King sayde also to Shimei, Thou knowest all the wickednes whereunto thine heart is priuie, that thou diddest to Dauid my father: the Lord therefore shall bring thy wickednesse vpon thine owne head.
45 Koma Mfumu Solomoni idzadalitsidwa ndipo mpando waufumu wa Davide udzakhazikika pamaso pa Yehova kwamuyaya.”
And let King Salomon be blessed, and the throne of Dauid stablished before the Lord for euer.
46 Pamenepo mfumu inalamula Benaya mwana wa Yehoyada ndipo iye anapita kukakantha Simei ndi kumupha. Tsono ufumu unakhazikika mʼdzanja la Solomoni.
So the King comanded Benaiah the sonne of Iehoiada: who went out and smote him that he dyed. And the kingdome was established in the hand of Salomon.

< 1 Mafumu 2 >