< 1 Mafumu 2 >

1 Davide ali pafupi kumwalira, analangiza mwana wake Solomoni kuti:
Now the days of David drew near that he should die. And he charged Solomon his son, saying,
2 “Ndatsala pangʼono kupita kumene munthu wina aliyense amayenera kupitako. Tsono khala wamphamvu, uvale zilimbe,
I am going the way of all the earth. Be thou strong therefore, and show thyself a man,
3 ndipo uzichita zimene Yehova Mulungu wako amafuna, uziyenda mʼnjira zake, uzisunga malangizo ndi malamulo ake monga momwe zinalembedwera mʼMalamulo a Mose, kuti zonse zimene udzachite zidzakuyendere bwino kulikonse kumene udzapite.
and keep the charge of Jehovah thy God, to walk in his ways, to keep his statutes, and his commandments, and his ordinances, and his testimonies, according to that which is written in the law of Moses, that thou may prosper in all that thou do, and wherever thou turn thyself.
4 Ndipo Yehova akwaniritse zimene anandilonjeza kuti, ‘Ngati zidzukulu zako zidzakhala mosamala, niziyenda mokhulupirika pamaso panga ndi mtima wawo wonse ndi moyo wawo wonse, sudzasowa munthu wokhala pa mpando waufumu wa Israeli.’
That Jehovah may establish his word which he spoke concerning me, saying, If thy sons take heed to their way, to walk before me in truth with all their heart and with all their soul, there shall not fail thee a man on the throne of Israel.
5 “Tsono iwe ukudziwanso zoyipa zimene Yowabu mwana wa Zeruya anandichitira pakupha atsogoleri awiri a ankhondo a Israeli, Abineri mwana wa Neri ndi Amasa mwana wa Yeteri. Iye anawapha ndi kukhetsa magazi nthawi ya mtendere ngati nthawi ya nkhondo, ndipo anapaka magazi amenewo pa lamba wa mʼchiwuno mwake ndi pa nsapato za ku mapazi ake.
Moreover thou also know what Joab the son of Zeruiah did to me, even what he did to the two captains of the armies of Israel, to Abner the son of Ner, and to Amasa the son of Jether, whom he killed, and shed the blood of war in peace, and put the blood of war upon his belt that was about his loins, and in his shoes that were on his feet.
6 Iwe uchite kwa iye molingana ndi nzeru zako, koma usalole kuti afe ndi ukalamba ndi kupita ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
Do therefore according to thy wisdom, and do not let his hoar head go down to Sheol in peace. (Sheol h7585)
7 “Koma ana a Barizilai wa ku Giliyadi uwakomere mtima ndipo uwalole kuti akhale mʼgulu la anthu amene azidya pamodzi nawe. Pakuti anandisamalira pamene ndinkathawa mʼbale wako Abisalomu.
But show kindness to the sons of Barzillai the Gileadite, and let them be of those who eat at thy table, for so they came to me when I fled from Absalom thy brother.
8 “Ndipo kumbukira kuti uli ndi Simei mwana wa Gera, wa fuko la Benjamini wochokera ku Bahurimu, amene ananditemberera koopsa tsiku limene ndimapita ku Mahanaimu. Atabwera kudzakumana nane ku Yorodani, ine ndinalumbira mʼdzina la Yehova kuti, ‘Sindidzakupha iwe ndi lupanga.’
And, behold, there is with thee Shimei the son of Gera, the Benjamite, of Bahurim, who cursed me with a grievous curse in the day when I went to Mahanaim. But he came down to meet me at the Jordan, and I swore to him by Jehovah, saying, I will not put thee to death with the sword.
9 Koma tsopano usamuyese ngati munthu wosalakwa. Iwe ndiwe munthu wanzeru. Udzadziwa choti uchite naye. Ngakhale ndi wokalamba, aphedwe ndithu.” (Sheol h7585)
Now therefore do not hold him guiltless, for thou are a wise man, and thou will know what thou ought to do to him, and thou shall bring his hoar head down to Sheol with blood. (Sheol h7585)
10 Tsono Davide anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Mzinda wa Davide.
And David slept with his fathers, and was buried in the city of David.
11 Iyeyo nʼkuti atalamulira Israeli kwa zaka makumi anayi. Ku Hebroni analamulira zaka zisanu ndi ziwiri ndipo ku Yerusalemu analamulira zaka 33.
And the days that David reigned over Israel were forty years. He reigned seven years in Hebron, and he reigned thirty-three years in Jerusalem.
12 Choncho Solomoni anakhala pa mpando waufumu wa abambo ake Davide, ndipo ufumu wake unakhazikika kwambiri.
And Solomon sat upon the throne of David his father, and his kingdom was established greatly.
13 Tsono Adoniya, mwana wa Hagiti, anapita kwa Batiseba, amayi ake a Solomoni. Batiseba anamufunsa kuti, “Kodi wabwera mwamtendere?” Iye anayakha kuti, “Eya, ndi zamtendere.”
Then Adonijah the son of Haggith came to Bathsheba the mother of Solomon. And she said, Do thou come peaceably? And he said, Peaceably.
14 Ndipo iye anawonjezera kunena kuti, “Ndili ndi mawu oti ndiyankhule nanu.” Batiseba anayankha kuti, “Yankhula.”
He said moreover, I have something to say to thee. And she said, Say on.
15 Tsono Adoniya anati, “Monga inu mukudziwa, ufumu unali wanga. Aisraeli onse ankayembekezera kuti ine ndidzakhala mfumu yawo. Koma zinthu zinasintha ndipo ufumu wapita kwa mʼbale wanga; pakuti wapatsa iye ufumuwu ndi Yehova.
And he said, Thou know that the kingdom was mine, and that all Israel set their faces on me, that I should reign. However the kingdom is turned about, and has become my brother's, for it was his from Jehovah.
16 Tsono ndili ndi pempho limodzi kwa inu. Musandikanize ayi.” Batiseba anati, “Nena.”
And now I ask one petition of thee; do not deny me. And she said to him, Say on.
17 Adoniya anapitiriza kunena kuti, “Chonde, inu mupemphe mfumu Solomoni kuti andipatse Abisagi wa ku Sunemu kuti akhale mkazi wanga pakuti mukapempha inu sadzakukanizani.”
And he said, Speak, I pray thee, to Solomon the king (for he will not say no thee), that he give me Abishag the Shunammite to wife.
18 Batiseba anayankha kuti, “Chabwino. Ndidzakuyankhulira kwa mfumu.”
And Bathsheba said, Well, I will speak for thee to the king.
19 Batiseba atapita kwa Mfumu Solomoni kukayankhula naye mʼmalo mwa Adoniya, mfumu inanyamuka kukumana naye, ndipo inaweramira amayi akewo, kenaka inakhala pa mpando wake waufumu. Iye anayitanitsa mpando wina kuti amayi ake akhalepo ndipo anakhala pansi ku dzanja lake lamanja.
Bathsheba therefore went to king Solomon to speak to him for Adonijah. And the king rose up to meet her, and bowed himself to her, and sat down on his throne, and caused a throne to be set for the king's mother. And she sat on his right hand.
20 Amayi akewo anati, “Ndikufuna ndikupempheni kanthu kakangʼono. Chonde musandikanize.” Mfumu inayankha kuti, “Pemphani amayi, ine sindikukanizani.”
Then she said, I ask one small petition of thee; do not deny me. And the king said to her, Ask on, my mother, for I will not deny thee.
21 Ndipo amayiwo anati, “Mulole kuti Abisagi wa ku Sunemu akhale mkazi wa mʼbale wanu Adoniya.”
And she said, Let Abishag the Shunammite be given to Adonijah thy brother to wife.
22 Koma Mfumu Solomoni inayankha amayi ake aja kuti, “Chifukwa chiyani mukupemphera Adoniya Abisagi wa ku Sunemu? Mungathenso kumupemphera ufumu pakuti iyeyu ndi mkulu wanga ndipo mupemphereninso wansembe Abiatara ndi Yowabu mwana wa Zeruya!”
And king Solomon answered and said to his mother, And why do thou ask Abishag the Shunammite for Adonijah? Ask for him the kingdom also, for he is my elder brother, even for him, and for Abiathar the priest, and for Joab the son of Zeruiah.
23 Pamenepo Mfumu Solomoni inalumbira mʼdzina la Yehova kuti, “Mulungu andilange ine koopsa ngati Adoniya saphedwa chifukwa cha pempho lakeli!
Then king Solomon swore by Jehovah, saying, God do so to me, and more also, if Adonijah has not spoken this word against his own life.
24 Tsono pali Yehova wamoyo, amene anandikhazikitsa ine pa mpando waufumu wa abambo anga Davide ndi kundipatsa ufumu monga analonjezera, Adoniya aphedwa lero lomwe lino!”
Now therefore as Jehovah lives, who has established me, and set me on the throne of David my father, and who has made me a house as he promised, surely Adonijah shall be put to death this day.
25 Choncho Mfumu Solomoni inalamula Benaya mwana wa Yehoyada ndipo anakantha Adoniyayo, nafa.
And king Solomon sent by Benaiah the son of Jehoiada, and he fell upon him so that he died.
26 Ndipo mfumu inati kwa Abiatara wansembe, “Pita ku Anatoti ku minda yako chifukwa ndiwe woyenera kufa, koma sindikupha tsopano, chifukwa unkanyamula Bokosi la Chipangano la Ambuye Yehova pamaso pa abambo anga Davide ndipo unazunzika limodzi ndi abambo angawo.”
And the king said to Abiathar the priest, Get thee to Anathoth, to thine own fields, for thou are worthy of death. But I will not at this time put thee to death, because thou bore the ark of the lord Jehovah before David my father, and because thou were afflicted in all wherein my father was afflicted.
27 Kotero Solomoni anachotsa Abiatara pa udindo wokhala wansembe wa Yehova, kukwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula za nyumba ya Eli ku Silo.
So Solomon thrust out Abiathar from being priest to Jehovah, that he might fulfill the word of Jehovah, which he spoke concerning the house of Eli in Shiloh.
28 Yowabu atamva zimenezi anathawira ku tenti ya Yehova ndipo anakagwira msonga za guwa lansembe, popeza Yowabu ndiye anathandiza Adoniya kuwukira koma sanathandize Abisalomu.
And the news came to Joab, for Joab had turned after Adonijah, though he did not turn after Absalom. And Joab fled to the tent of Jehovah, and caught hold on the horns of the altar.
29 Mfumu Solomoni inawuzidwa kuti Yowabu wathawira ku tenti ya Yehova ndipo ali pambali pa guwa lansembe. Tsono Solomoni analamula Benaya mwana wa Yehoyada kuti, “Pita, kamukanthe!”
And it was told king Solomon, Joab has fled to the tent of Jehovah, and, behold, he is by the altar. Then Solomon sent Benaiah the son of Jehoiada, saying, Go, fall upon him.
30 Choncho Benaya analowa mʼtenti ya Yehova ndipo anati kwa Yowabu, “Mfumu ikuti ‘Tuluka!’” Koma iye anayankha kuti, “Ayi, ine ndifera muno.” Benaya anakafotokozera mfumu kuti, “Umu ndi mmene Yowabu wandiyankhira.”
And Benaiah came to the tent of Jehovah, and said to him, Thus says the king, Come forth. And he said, No, but I will die here. And Benaiah brought the king word again, saying, Thus said Joab, and thus he answered me.
31 Pamenepo mfumu inalamula Benaya kuti, “Kachite monga iye wanenera. Ukamukanthe ndi kumuyika mʼmanda. Ukatero udzandichotsera ine pamodzi ndi nyumba ya abambo anga mlandu wa anthu osalakwa amene Yowabu anawapha.
And the king said to him, Do as he has said, and fall upon him, and bury him, that thou may take away the blood, which Joab shed without cause, from me and from my father's house.
32 Yehova adzamubwezera zomwe anachita pokhetsa magazi, chifukwa iye anakantha ndi lupanga anthu awiri abwino ndi olungama kuposa iye, nawapha, abambo anga Davide osadziwa. Anthu awiriwo ndi Abineri mwana wa Neri, wolamulira gulu lankhondo la Israeli ndi Amasa mwana wa Yeteri, wolamulira gulu lankhondo la Yuda.
And Jehovah will return his blood upon his own head, because he fell upon two men more righteous and better than he, and killed them with the sword, and my father David did not know it, namely, Abner the son of Ner, captain of the army of Israel, and Amasa the son of Jether, captain of the army of Judah.
33 Magazi amene Yowabu anakhetsa akhale pamutu pake ndi pa zidzukulu zake kwamuyaya. Koma pa Davide ndi zidzukulu zake, nyumba yake ndi mpando wake waufumu pakhale mtendere wochokera kwa Yehova kwamuyaya.”
So shall their blood return upon the head of Joab, and upon the head of his seed forever. But to David, and to his seed, and to his house, and to his throne, there shall be peace forever from Jehovah.
34 Choncho Benaya mwana wa Yehoyada anapita kukakantha Yowabu nʼkumupha ndipo anayikidwa mʼmanda mʼnyumba yakeyake ya ku chipululu.
Then Benaiah the son of Jehoiada went up, and fell upon him, and killed him. And he was buried in his own house in the wilderness.
35 Mfumu inayika Benaya mwana wa Yehoyada kuti akhale woyangʼanira gulu lankhondo mʼmalo mwa Yowabu ndipo inayika Zadoki kuti akhale wansembe mʼmalo mwa Abiatara.
And the king put Benaiah the son of Jehoiada in his room over the army. And the king put Zadok the priest in the place of Abiathar.
36 Kenaka mfumu inatuma anthu kukayitana Simei ndipo inamuwuza kuti, “Udzimangire nyumba mu Yerusalemu ndipo uzikhala kumeneko, koma usatuluke mu mzinda kupita kwina kulikonse.
And the king sent and called for Shimei, and said to him, Build for thee a house in Jerusalem, and dwell there, and go not forth from there anywhere.
37 Tsiku lomwe udzatulukemo ndi kuwoloka Chigwa cha Kidroni, udziwiretu kuti udzafa ndipo magazi ako adzakhala pamutu pako.”
For on the day thou go out, and pass over the brook Kidron, know thou for certain that thou shall surely die; thy blood shall be upon thine own head.
38 Simei anayankha mfumu kuti, “Zimene mwanenazi nʼzabwino. Kapolo wanu adzachita monga mbuye wanga mfumu mwanenera.” Choncho Simei anakhala mu Yerusalemu nthawi yayitali.
And Shimei said to the king, The saying is good. As my lord the king has said, so will thy servant do. And Shimei dwelt in Jerusalem many days.
39 Koma patatha zaka zitatu, akapolo awiri a Simei anathawira kwa Akisi mwana wa Maaka, mfumu ya ku Gati, ndipo Simei anawuzidwa kuti, “Akapolo anu ali ku Gati.”
And it came to pass at the end of three years, that two of the servants of Shimei ran away to Achish, son of Maacah, king of Gath. And they told Shimei, saying, Behold, thy servants are in Gath.
40 Atamva zimenezi, anakwera bulu wake ndipo anapita kwa Akisi ku Gati kukafunafuna akapolo ake. Choncho Simei anapita ndi kukatenga akapolo ake ku Gati ndipo anabwera nawo.
And Shimei arose, and saddled his donkey, and went to Gath to Achish to seek his servants. And Shimei went, and brought his servants from Gath.
41 Solomoni atawuzidwa kuti Simei anatuluka mu Yerusalemu ndi kupita ku Gati ndipo kuti wabwerako,
And it was told Solomon that Shimei had gone from Jerusalem to Gath, and was come again.
42 mfumu inamuyitanitsa Simei ndipo inamufunsa kuti, “Kodi sindinakulumbiritse mʼdzina la Yehova ndi kukuchenjeza kuti, ‘Tsiku limene udzatuluka kupita kwina kulikonse, udziwe kuti udzafa’? Nthawi imeneyo iwe unandiwuza kuti, ‘Zimene mwanena nʼzabwino. Ine ndidzamvera.’
And the king sent and called for Shimei, and said to him, Did I not adjure thee by Jehovah, and protest to thee, saying, Know for certain, that on the day thou go out, and walk abroad anywhere, thou shall surely die? And thou said to me, The saying that I have heard is good.
43 Chifukwa chiyani tsono sunasunge lumbiro lako kwa Yehova? Bwanji nanga sunamvere lamulo limene ndinakuwuza?”
Why then have thou not kept the oath of Jehovah, and the commandment that I have charged thee with?
44 Mfumuyo inawuzanso Simei kuti, “Ukudziwa mu mtima mwakomo zoyipa zonse zimene unachitira abambo anga Davide. Tsopano Yehova akubwezera zoyipa zakozo.
The king said moreover to Shimei, Thou know all the iniquity which thy heart is privy to, what thou did to David my father. Therefore Jehovah shall return thy iniquity upon thine own head.
45 Koma Mfumu Solomoni idzadalitsidwa ndipo mpando waufumu wa Davide udzakhazikika pamaso pa Yehova kwamuyaya.”
But king Solomon shall be blessed, and the throne of David shall be established before Jehovah forever.
46 Pamenepo mfumu inalamula Benaya mwana wa Yehoyada ndipo iye anapita kukakantha Simei ndi kumupha. Tsono ufumu unakhazikika mʼdzanja la Solomoni.
So the king commanded Benaiah the son of Jehoiada. And he went out, and fell upon him so that he died. And the kingdom was established in the hand of Solomon.

< 1 Mafumu 2 >