< 1 Mafumu 16 >

1 Ndipo Yehova anayankhula kudzera mwa Yehu mwana wa Hanani, mawu odzudzula Baasa kuti,
Alors la parole de l'Eternel fut adressée à Jéhu, fils de Hanani, contre Bahasa, pour lui dire:
2 “Ine ndinakukuza kuchokera pa fumbi ndipo ndinakupanga kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli, koma iwe wakhala ukuyenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchimwitsa anthu anga Aisraeli naputa mkwiyo wanga chifukwa cha machimo awo.
Parce que je t'ai élevé de la poudre, et que je t'ai établi Conducteur de mon peuple d'Israël, et que malgré cela tu as suivi le train de Jéroboam, et as fait pécher mon peuple d'Israël, pour m'irriter par leurs péchés.
3 Taonani, Ine ndatsala pangʼono kuwononga Baasa pamodzi ndi nyumba yake, ndipo ndidzachitira nyumba yake zimene ndinachita pa nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati.
Voici, je m'en vais entièrement exterminer Bahasa, et sa maison, et je mettrai ta maison au même état que j'ai mis la maison de Jéroboam fils de Nébat.
4 Agalu adzadya aliyense wa banja la Baasa amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya iwo amene adzafere kuthengo.”
Celui [de la race] de Bahasa qui mourra dans la ville, les chiens le mangeront; et celui des siens qui mourra aux champs, les oiseaux des cieux le mangeront.
5 Tsono ntchito zina za Baasa ndi zamphamvu zake zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
Le reste des faits de Bahasa, ce qu'il a fait, et sa valeur, n'est-il pas écrit au Livre des Chroniques des Rois d'Israël.
6 Baasa anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Tiriza. Ndipo Ela mwana wake anakhala mfumu mʼmalo mwake.
Ainsi Bahasa s'endormit avec ses pères, et fut enseveli à Tirtsa, et Ela son fils régna en sa place.
7 Komatu Yehova anayankhula kwa Baasa pamodzi ndi banja lake lonse kudzera mwa mneneri Yehu mwana wa Hanani, chifukwa cha zoyipa zonse zimene iye anachita pamaso pa Yehova, kukwiyitsa Yehovayo nakhala ngati nyumba ya Yeroboamu ndiponso chifukwa anawonongeratu banja la Yeroboamu.
La parole de l'Eternel fut aussi [adressée] par le moyen de Jéhu, fils de Hanani le Prophète, contre Bahasa, et contre sa maison, à cause de tout le mal qu'il avait fait devant l'Eternel, en l'irritant par l'œuvre de ses mains, [pour lui dire] qu'il en serait comme de la maison de Jéroboam; même parce qu'il l'avait frappée.
8 Mʼchaka cha 26 cha ufumu wa Asa mfumu ya Yuda, Ela mwana wa Baasa anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira ku Tiriza zaka ziwiri.
L'an vingt et sixième d'Asa Roi de Juda, Ela fils de Bahasa commença à régner sur Israël, et il [régna] deux ans à Tirtsa.
9 Zimuri, mmodzi mwa akuluakulu ake, amene ankalamulira theka la magaleta ake, anamuchitira chiwembu. Nthawi imeneyi Ela anali ku Tiriza, akumwa koledzera nako mʼnyumba ya Ariza, munthu amene ankayangʼanira nyumba yaufumu ku Tiriza.
Et Zimri son serviteur, capitaine de la moitié des chariots, fit une conspiration contre Ela, lorsqu'il était à Tirtsa buvant et s'enivrant dans la maison d'Artsa son maître d'hôtel, à Tirtsa.
10 Zimuri anadzalowa, namukantha ndi kumupha mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda. Ndipo Zimuriyo anakhala mfumu mʼmalo mwake.
Zimri donc vint, et le frappa, et le tua l'an vingt et septième d'Asa Roi de Juda, et régna en sa place.
11 Zimuri atangoyamba kulamulira, anapha banja lonse la Baasa. Sanasiyepo munthu wamwamuna ndi mmodzi yemwe, wachibale kapena bwenzi lake.
Et comme il entrait en son règne, sitôt qu'il fut assis sur son trône, il frappa toute la maison de Bahasa; il n'en laissa rien depuis l'homme jusqu'à un chien; [il ne lui laissa] ni parent, ni ami.
12 Choncho Zimuri anawononga banja lonse la Baasa, molingana ndi mawu amene Yehova anayankhula motsutsa Baasa kudzera mwa mneneri Yehu,
Ainsi Zimri extermina toute la maison de Bahasa, selon la parole que l'Eternel avait proférée contre Bahasa, par le moyen de Jéhu le Prophète;
13 chifukwa cha machimo onse amene Baasa ndi mwana wake Ela anachita nachimwitsa Israeli, anakwiyitsa Yehova, Mulungu wa Israeli ndi mafano awo osapindulitsa.
A cause de tous les péchés de Bahasa, et des péchés d'Ela son fils, par lesquels ils avaient péché, et avaient fait pécher Israël, irritant l'Eternel le Dieu d'Israël par leurs vanités.
14 Tsono ntchito zina za Ela ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
Le reste des faits d'Ela, et même tout ce qu'il a fait, n'est-il pas écrit au Livre des Chroniques des Rois d'Israël?
15 Mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda, Zimuri analamulira ku Tiriza masiku asanu ndi awiri. Gulu la ankhondo linali litamanga misasa pafupi ndi Gibetoni, mzinda wa Afilisti.
La vingt et septième année d'Asa Roi de Juda, Zimri régna sept jours à Tirtsa; or le peuple était campé contre Guibbethon qui était aux Philistins.
16 Ankhondo amene anali ku misasa atamva kuti Zimuri wachita chiwembu ndi kupha mfumu, tsiku lomwelo ku misasako anasankha Omuri, mkulu wa ankhondo kukhala mfumu ya Israeli.
Et le peuple qui était-là campé, entendit qu'on disait: Zimri a fait une conspiration, et il a même tué le Roi; c'est pourquoi en ce même jour tout Israël établit dans le camp pour Roi Homri, capitaine de l'armée d'Israël.
17 Tsono Omuri ndi Aisraeli onse amene anali naye anachoka ku Gibetoni ndi kukazinga Mzinda wa Tiriza.
Et Homri et tout Israël montèrent de devant Guibbethon, et assiégèrent Tirtsa.
18 Zimuri ataona kuti mzinda walandidwa, anathawira ku nsanja ya nyumba ya mfumu ndipo anatentha nyumbayo iye ali momwemo. Kotero iyeyo anafa,
Mais dès que Zimri eut vu que la ville était prise, il entra au palais de la maison Royale, et brûla sur soi la maison Royale, et il mourut;
19 chifukwa cha machimo amene iye anachita, kuchita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuyenda mʼnjira za Yeroboamu, nachimwitsa nazo Aisraeli.
A cause des péchés par lesquels il avait péché, faisant ce qui déplaît à l'Eternel, en suivant le train de Jéroboam, et son péché, qu'il avait fait pour faire pécher Israël.
20 Tsono ntchito zina za Zimuri ndi chiwembu chake chimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
Le reste des faits de Zimri, et la conspiration qu'il fit, toutes ces choses ne sont-elles pas écrites au Livre des Chroniques des Rois d'Israël?
21 Pambuyo pake Aisraeli anagawikana pakati: theka linatsatira Tibini mwana wa Ginati kuti limulonge ufumu, ndipo theka lina linatsatira Omuri.
Alors le peuple d'Israël se divisa en deux partis; la moitié du peuple suivait Tibni fils de Guinath, pour le faire Roi; et l'autre moitié suivait Homri.
22 Koma anthu otsatira Omuri anali amphamvu kupambana amene ankatsatira Tibini mwana wa Ginati. Choncho Tibini anafa ndipo Omuri anakhala mfumu.
Mais le peuple qui suivait Homri, fut plus fort que le peuple qui suivait Tibni fils de Guinath, et Tibni mourut, et Homri régna.
23 Mʼchaka cha 31 cha Asa mfumu ya Yuda, Omuri anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira zaka 12 ndi miyezi isanu ndi umodzi ku Tiriza.
La trente et unième année d'Asa Roi de Juda, Homri commença à régner sur Israël, [et il régna] douze ans; il régna six ans à Tirtsa.
24 Iye anagula phiri la Samariya kwa Semeri pa mtengo wa ndalama 6,000 za siliva ndipo pa phiripo anamangapo mzinda, nawutcha Samariya, potsata dzina la Semeri, dzina la mwini wakale wa phirilo.
Puis il acheta de Sémer la montagne de Samarie, deux talents d'argent; et il bâtit [une ville] sur cette montagne, et il nomma la ville qu'il bâtit, du nom de Sémer, Seigneur de la montagne de Samarie.
25 Koma Omuri anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo anachimwa kuposa mafumu ena onse amene analipo iye asanakhale mfumu.
Et Homri fit ce qui déplaît à l'Eternel; il fit même pis que tous ceux qui avaient été avant lui.
26 Pakuti iye anayenda mʼnjira zonse za Yeroboamu mwana wa Nebati, ndipo tchimo lake anachimwitsa nalo Aisraeli, nakwiyitsa Yehova Mulungu wa Israeli ndi mafano awo opandapake.
Car il suivit tout le train de Jéroboam fils de Nébat, et son péché, par lequel il avait fait pécher Israël, afin qu'ils irritassent l'Eternel le Dieu d'Israël par leurs vanités.
27 Tsono ntchito zina za Omuri ndi zamphamvu zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
Le reste des faits de Homri, tout ce qu'il a fait, et les exploits qu'il fit, ne sont-ils pas écrits aux Livre des Chroniques des Rois d'Israël?
28 Choncho Omuri anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Samariya. Ndipo Ahabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Ainsi Homri s'endormit avec ses pères, et fut enseveli à Samarie, et Achab son fils régna en sa place.
29 Mʼchaka cha 38 cha ufumu wa Asa, mfumu ya Yuda, Ahabu mwana wa Omuri anakhala mfumu ya Israeli nalamulira Israeli ku Samariya zaka 22.
Achab fils de Homri commença à régner sur Israël la trente-huitième année d'Asa Roi de Juda; et Achab fils de Homri régna sur Israël à Samarie vingt et deux ans.
30 Ahabu mwana wa Omuri anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova kupambana mafumu onse akale.
Et Achab fils de Homri fit ce qui déplaît à l'Eternel, plus que tous ceux qui avaient été avant lui.
31 Iye sanachiyese ngati chinthu chochepa chabe kuchita machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, koma anakwatiranso Yezebeli, mwana wa Etibaala mfumu ya Asidoni, nayamba kutumikira Baala ndi kumupembedza.
Et il arriva que, comme si ce lui eût été peu de chose de marcher dans les péchés de Jéroboam fils de Nébat, il prit pour femme Izebel, fille d'Eth-bahal, Roi des Sidoniens, puis il alla, et servit Bahal, et se prosterna devant lui.
32 Iye anapangira Baala guwa lansembe mʼnyumba ya Baala imene anamanga ku Samariya.
Et il dressa un autel à Bahal, en la maison de Bahal, qu'il bâtit à Samarie.
33 Ahabu anapanganso fano la Asera ndi kukwiyitsa kwambiri Yehova Mulungu wa Israeli, kupambana mafumu onse a Israeli amene analipo iye asanakhale mfumu.
Et Achab fit un bocage; de sorte qu'Achab fit encore pis que tous les Rois d'Israël qui avaient été avant lui, pour irriter l'Eternel le Dieu d'Israël.
34 Pa nthawi ya Ahabu, Hiyeli wa ku Beteli anamanganso mzinda wa Yeriko. Pa nthawi yomanga maziko ake, mwana wake woyamba wa mwamuna, Abiramu anamwalira, ndipo pa nthawi yomanga zipata zake, mwana wa mngʼono wa mwamuna Segubu, anamwaliranso. Izi zinachitika monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa Yoswa mwana wa Nuni.
En son temps Hiel de Bethel bâtit Jérico, laquelle il fonda sur Abiram son premier-né, et posa ses portes sur Ségub son puîné, selon la parole que l'Eternel avait proférée par le moyen de Josué, fils de Nun.

< 1 Mafumu 16 >