< 1 Mafumu 15 >

1 Mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Nebati, Abiya anakhala mfumu ya Yuda,
I kong Jeroboams, Nebats sønns attende år blev Abiam konge over Juda.
2 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zitatu. Amayi ake anali Maaka, mwana wa Abisalomu.
Han regjerte tre år i Jerusalem. Hans mor hette Ma'aka; hun var datter til Abisalom.
3 Abiya anachita zoyipa zonse zimene abambo ake anazichita. Sanali wangwiro pamaso pa Yehova Mulungu wake, monga linachitira kholo lake Davide.
Han vandret i alle de synder som hans far hadde gjort før ham, og hans hjerte var ikke helt med Herren hans Gud, som hans far Davids hjerte hadde vært;
4 Komabe chifukwa cha Davide, Yehova Mulungu wake anamupatsa nyale mu Yerusalemu pomupatsa mwana wolowa mʼmalo mwake ndi kumukhazikitsa kukhala wamphamvu mu Yerusalemu;
men for Davids skyld lot Herren hans Gud en lampe brenne for ham i Jerusalem, idet han opreiste hans sønn efter ham og lot Jerusalem bli stående,
5 pakuti Davide anachita zolungama pamaso pa Yehova ndipo sanalephere kusunga chilichonse chimene Yehova anamulamula masiku onse a moyo wake kupatula nkhani ija ya Uriya Mhiti.
fordi David gjorde hvad rett var i Herrens øine, og i hele sitt liv ikke vek av fra noget av det han hadde befalt ham, undtagen det som hendte med hetitten Uria.
6 Panali nkhondo pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu masiku onse a moyo wa Abiya.
Mellem Rehabeam og Jeroboam var det krig så lenge han levde.
7 Tsono ntchito zina za Abiya, ndi zina zonse anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? Panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yeroboamu.
Hvad som ellers er å fortelle om Abiam og om alt det han gjorde, er opskrevet i Judas kongers krønike. Mellem Abiam og Jeroboam var det også krig.
8 Ndipo Abiya anamwalira nayikidwa mʼmanda momwe anayikidwa makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Asa, mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Og Abiam la sig til hvile hos sine fedre, og de begravde ham i Davids stad; og hans sønn Asa blev konge i hans sted.
9 Mʼchaka cha makumi awiri cha Yeroboamu mfumu ya Israeli, Asa anakhala mfumu ya Yuda,
I Jeroboams, Israels konges tyvende år blev Asa konge over Juda.
10 ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 41. Agogo ake akazi anali Maaka mwana wa Abisalomu.
Han regjerte en og firti år i Jerusalem. Hans mor hette Ma'aka; hun var datter til Abisalom.
11 Asa anachita zolungama pamaso pa Yehova monga anachitira Davide kholo lake.
Asa gjorde hvad rett var i Herrens øine, likesom hans far David hadde gjort.
12 Iye anachotsa mʼdzikomo amuna onse ochita zadama pochita chipembedzo chawo ndiponso anachotsa mafano onse amene makolo ake anawapanga.
Han drev tempel-bolerne ut av landet og fikk bort alle de motbydelige avguder som hans fedre hadde gjort.
13 Iye anachotsanso gogo wake Maaka pa udindo wake wa amayi a mfumu, chifukwa choti anapanga fano lonyansa la Asera. Asa anagwetsa fanolo nakalitentha ku Chigwa cha Kidroni.
Han avsatte endog sin mor Ma'aka fra hennes verdighet, fordi hun hadde gjort et gruelig avgudsbillede for Astarte; Asa hugg hennes gruelige avgudsbillede ned og brente det i Kidrons dal.
14 Ngakhale sanachotse malo opembedzerapo mafano, mtima wa Asa unali wodzipereka kwathunthu kwa Yehova masiku onse a moyo wake.
Men offerhaugene blev ikke nedlagt; dog var Asas hjerte helt med Herren så lenge han levde.
15 Asa anabweretsa ku Nyumba ya Yehova zinthu zimene abambo ake anazipereka, ndiponso zinthu zimene iye mwini anazipereka: zagolide, siliva ndi ziwiya zotengera.
Han lot de ting hans far hadde helliget, og dem han selv hadde helliget, føre inn i Herrens hus, både sølv og gull og andre ting.
16 Panali nkhondo pakati pa Asa ndi Baasa mfumu ya Israeli nthawi yonse ya ulamuliro wawo.
Mellem Asa og Baesa, Israels konge, var det krig så lenge de levde.
17 Baasa mfumu ya Israeli anapita kukathira nkhondo dziko la Yuda, ndipo anamangira linga mzinda wa Rama kuletsa kuti wina aliyense asatuluke kapena kulowa mʼdziko la Asa, mfumu ya Yuda.
Baesa, Israels konge, drog op mot Juda og bygget festningsverker i Rama for å hindre enhver fra å dra fra eller til Asa, Judas konge.
18 Tsono Asa anatenga siliva yense pamodzi ndi golide zimene zinatsala ku malo osungira chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso ku nyumba yake yaufumu. Anazipereka kwa atumiki ake, nawatuma kupita nazo kwa Beni-Hadadi mwana wa Tabirimoni, mwana wa Heziyoni, mfumu ya Aramu, amene ankakhala ku Damasiko ndipo anakamuwuza kuti,
Da tok Asa alt det sølv og gull som var tilbake i skattkammerne i Herrens hus, og likeså skattene i kongens hus og overgav dem til sine tjenere; så sendte kong Asa dem til Benhadad, kongen i Syria, som bodde i Damaskus og var sønn til Tabrimmon, Hesjons sønn, med de ord:
19 “Tiyeni tigwirizane inu ndi ine, monga panali mgwirizano pakati pa abambo anu ndi abambo anga. Onani, ndikukutumizirani mphatso za siliva ndi golide. Tsopano kathetseni mgwirizano wanu ndi Baasa mfumu ya Israeli kuti andisiye.”
Mellem mig og dig er det jo et forbund, som det var mellem min far og din far. Her sender jeg dig en gave av sølv og gull; bryt nu ditt forbund med Baesa, Israels konge, så han må dra bort fra mig!
20 Choncho Beni-Hadadi anamvera zimene ananena mfumu Asa ndipo anatumiza olamulira magulu ake ankhondo ku mizinda ya Israeli. Ndipo iye anagonjetsa Iyoni, Dani, Abeli-Beti-Maaka ndi dera lonse la Kinereti kuphatikiza dziko lonse la Nafutali.
Benhadad lød kong Asa og sendte sine hærførere mot Israels byer og inntok Ijon og Dan og Abel-Bet-Ma'aka og hele Kinneret med hele Naftalis land.
21 Baasa atamva zimenezi, anasiya kumangira linga Rama ndipo anakakhala ku Tiriza.
Da Baesa hørte det, holdt han op med å bygge festningsverker i Rama og gav sig til i Tirsa.
22 Pamenepo Mfumu Asa analamula anthu onse a ku Yuda osasiya ndi mmodzi yemwe, ndipo anachotsa ku Rama miyala ndi matabwa amene Baasa ankamangira kumeneko. Zipangizo zimenezi Mfumu Asa inamangira linga la Geba ku Benjamini ndi la ku Mizipa.
Men kong Asa opbød hele Juda - ingen var fritatt - og de førte bort stenene og tømmeret som Baesa hadde brukt til festningsarbeidet i Rama; med det bygget kong Asa festningsverker i Geba i Benjamin og i Mispa.
23 Tsono ntchito zina za Asa, za mphamvu zake ndi mizinda imene anayimanga ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? Koma pa nthawi ya ukalamba wake anadwala nthenda ya mapazi.
Hvad som ellers er å fortelle om Asa, om alle hans store gjerninger og alt det han gjorde, og om de byer han bygget, det er opskrevet i Judas kongers krønike. Men i sin alderdom fikk han en sykdom i føttene.
24 Ndipo Asa anamwalira nayikidwa mʼmanda momwe anayikidwa makolo ake mu mzinda wa Davide kholo lake. Ndipo Yehosafati mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Og Asa la sig til hvile hos sine fedre og blev begravet hos sine fedre i sin far Davids stad, og hans sønn Josafat blev konge i hans sted.
25 Nadabu, mwana wa Yeroboamu anakhala mfumu ya Israeli mʼchaka chachiwiri cha Asa mfumu ya Yuda, ndipo analamulira Israeli zaka ziwiri.
Nadab, Jeroboams sønn, blev konge over Israel i Asas, Judas konges annet år, og han regjerte over Israel i to år.
26 Nadabu anachita zoyipa pamaso pa Yehova, anayenda mʼnjira za abambo ake ndi mu uchimo womwe anachimwitsa nawo Israeli.
Han gjorde hvad ondt var i Herrens øine, og vandret på sin fars vei og i hans synd, den som han hadde fått Israel til å gjøre.
27 Baasa mwana wa Ahiya, wa banja la Isakara anakonzera Nadabuyo chiwembu, ndipo anamukantha ku Gibetoni, mzinda wa Afilisti, pamene Nadabu ndi anthu onse a ku Israeli anali atawuzungulira.
Men Baesa, Akias sønn, av Issakars hus, fikk i stand en sammensvergelse mot ham; og Baesa slo ham ihjel ved Gibbeton, som tilhørte filistrene, mens Nadab og hele Israel holdt Gibbeton kringsatt.
28 Baasa anapha Nadabu mʼchaka chachitatu cha Asa, mfumu ya ku Yuda ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
Baesa drepte ham i Asas, Judas konges tredje år og blev så konge i hans sted.
29 Iye atangoyamba kulamulira, anapha anthu onse a banja la Yeroboamu. Sanasiye ndi mmodzi yemwe wamoyo pa banjapo, koma anawononga anthu onse, molingana ndi mawu a Yehova amene anayankhula mwa mtumiki wake Ahiya wa ku Silo
Og da han var blitt konge, slo han hele Jeroboams hus ihjel; han lot ikke en levende sjel bli tilbake av Jeroboams hus, men utryddet det efter det ord som Herren hadde talt ved sin tjener Akia fra Silo;
30 chifukwa cha machimo amene Yeroboamu anachita, ndiponso kuchimwitsa anthu a ku Israeli, naputa mkwiyo wa Yehova Mulungu wa Israeli.
dette skjedde for de synders skyld som Jeroboam hadde gjort, og som han hadde fått Israel til å gjøre, og fordi han hadde vakt Herrens, Israels Guds harme.
31 Tsono ntchito za Nadabu ndi zina zonse zimene anazichita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
Hvad som ellers er å fortelle om Nadab og om alt det han gjorde, er opskrevet i Israels kongers krønike.
32 Panali nkhondo pakati pa Asa ndi Baasa mfumu ya Israeli pa nthawi yonse ya ulamuliro wawo.
Mellem Asa og Israels konge Baesa var det krig så lenge de levde.
33 Chaka chachitatu cha Asa mfumu ya Yuda, Baasa mwana wa Ahiya anakhala mfumu ya Aisraeli onse ku Tiriza, ndipo analamulira zaka 24.
I Asas, Judas konges tredje år blev Baesa, Akias sønn, konge over hele Israel i Tirsa, og han var konge i fire og tyve år.
34 Anachita zoyipa pamaso pa Yehova, nayenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchita tchimo lake limene linachimwitsa anthu a ku Israeli.
Han gjorde hvad ondt var i Herrens øine, og vandret på Jeroboams vei og i hans synd, den som han hadde fått Israel til å gjøre.

< 1 Mafumu 15 >