< 1 Mafumu 12 >

1 Rehobowamu anapita ku Sekemu, pakuti Aisraeli onse nʼkuti atapita kumeneko kukamulonga ufumu.
Rehabám je odšel v Sihem, kajti ves Izrael je prišel v Sihem, da ga postavijo za kralja.
2 Yeroboamu mwana wa Nebati anamva zimenezi. Nthawi imeneyo nʼkuti Yeroboamuyo akukhala ku Igupto, pakuti atathawa Mfumu Solomoni iyeyo anakakhala ku Igupto.
Pripetilo se je, ko je Nebátov sin Jerobeám, ki je bil še v Egiptu, slišal o tem (kajti pobegnil je izpred prisotnosti kralja Salomona in je Jerobeám prebival v Egiptu),
3 Tsono anthu anayitanitsa Yeroboamu, ndipo iye pamodzi ndi gulu lonse la ku Israeli anapita kwa Rehobowamu ndipo anamuwuza kuti,
da so poslali in ga poklicali. Jerobeám in vsa Izraelova skupnost pa je prišla in spregovorila Rehabámu, rekoč:
4 “Abambo anu anatisenzetsa goli lolemetsa kwambiri, koma inu chepetsani ntchito yowawa pa ife ndipo peputsani goli lolemetsa limene anatisenzetsa. Mukatero tidzakutumikirani.”
»Tvoj oče je naš jarem naredil boleč. Sedaj torej olajšaj bolečo službo svojega očeta in njegov težek jarem, ki ga je položil na nas in mi ti bomo služili.«
5 Rehobowamu anayankha kuti, “Pitani, ndipo pakatha masiku atatu, mudzabwerenso.” Choncho anthuwo anapitadi.
Rekel jim je: »Odidite še za tri dni, potem ponovno pridite k meni.« In ljudstvo je odšlo.
6 Ndipo Mfumu Rehobowamu anapempha nzeru kwa akuluakulu amene ankatumikira Solomoni abambo ake pamene anali ndi moyo. Iye anawafunsa kuti, “Kodi mungandilangize zotani kuti ndiwayankhe anthu amenewa?”
Kralj Rehabám se je posvetoval s starci, ki so stali pred njegovim očetom Salomonom, medtem ko je še živel in rekel: »Kako svetujete, da lahko odgovorim temu ljudstvu?«
7 Iwo anayankha kuti, “Ngati lero mudzakhala mtumiki wa anthu amenewa ndi kuwatumikira ndipo mukawayankha bwino, iwowo adzakhala atumiki anu nthawi zonse.”
Odgovorili so mu, rekoč: »Če hočeš biti ta dan služabnik temu ljudstvu in jim hočeš služiti in jim odgovoriti in jim govoriti dobre besede, potem bodo tvoji služabniki na veke.«
8 Koma Rehobowamu anakana malangizo amene akuluakuluwo anamupatsa ndipo anafunsira nzeru kwa anyamata anzake amene anakulira nawo limodzi omwe ankamutumikira.
Toda zapustil je nasvet starcev, ki so mu ga dali in se posvetoval z mladeniči, ki so odrasli z njim in ki so stali pred njim
9 Iye anawafunsa kuti, “Kodi malangizo anu ngotani? Kodi ndiwayankhe chiyani anthu amene akunena kwa ine kuti, ‘Peputsani goli limene abambo anu anatisenzetsa’?”
in jim rekel: »Kakšen nasvet dajete vi, da lahko odgovorimo temu ljudstvu, ki mi je govorilo, rekoč: ›Naredi jarem, ki ga je tvoj oče položil nad nas, lažji?‹«
10 Anyamata anzake amene anakula nawo limodzi aja anamuyankha kuti, “Anthu amene ananena kwa iwe kuti, ‘Abambo anu anatisenzetsa goli lolemetsa, koma inu peputsani goli lathu,’ uwawuze kuti ‘Chala changa chakanise nʼchachikulu kupambana chiwuno cha abambo anga.
Mladeniči, ki so zrasli z njim, so mu govorili, rekoč: »Tako boš govoril temu ljudstvu, ki ti je govorilo, rekoč: ›Tvoj oče je naš jarem naredil težek, toda ti nam ga olajšaj; ‹ tako jim boš rekel: ›Moj mali prst bo debelejši kakor očetova ledja.
11 Abambo anga ankakusenzetsani goli lolemetsa koma ine ndidzachititsa kuti likhale lolemera kwambiri. Abambo anga ankakukwapulani ndi zikoti wamba koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.’”
Kakor vam je moj oče naložil težek jarem, bom sedaj dodal vašemu jarmu. Moj oče vas je kaznoval z biči, toda jaz vas bom kaznoval s škorpijoni.‹«
12 Patapita masiku atatu, Yeroboamu pamodzi ndi anthu onse anabwera kwa Rehobowamu, monga momwe inanenera mfumu kuti, “Mudzabwere pakatha masiku atatu.”
Tako je Jerobeám in vse ljudstvo tretji dan prišlo k Rehabámu, kakor je kralj določil, rekoč: »Ponovno pridite k meni tretji dan.«
13 Mfumuyo inawayankha anthuwo mwankhanza. Kukana malangizo amene akuluakulu anayipatsa.
Kralj je ljudstvu surovo odgovoril in zapustil nasvet starcev, ki so mu ga dali.
14 Anatsatira malangizo amene anyamata anzake anamupatsa ndipo anati “Abambo anga ankakusenzetsani goli lolemetsa. Ine ndidzachititsa kuti likhale lolemera kwambiri. Abambo anga ankakukwapulani ndi zikoti wamba koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.”
Spregovoril jim je glede na nasvet mladeničev, rekoč: »Moj oče je vaš jarem naredil težek, jaz pa bom vašemu jarmu dodal. Moj oče vas je kaznoval tudi z biči, toda jaz vas bom kaznoval s škorpijoni.«
15 Choncho mfumu sinamvere pempho la anthuwo, pakuti zinthu izi zinali zochokera kwa Yehova, kukwaniritsa mawu amene Yehova anayankhula kwa Yeroboamu mwana wa Nebati kudzera mwa Ahiya wa ku Silo.
Zatorej kralj ni prisluhnil ljudstvu, kajti stvar je bila od Gospoda, da je lahko izpolnil svojo besedo, ki jo je Gospod po Šilčanu Ahíju govoril Nebátovemu sinu Jerobeámu.
16 Aisraeli onse ataona kuti mfumu yakana kumva zopempha zawo, iwo anayankha mfumu kuti, “Kodi ife tili ndi gawo lanji mwa Davide, ndi gawo lanjinso mwa mwana wa Yese? Inu Aisraeli, bwererani ku matenti anu! Ziyangʼanira nyumba yako, Iwe Davide!” Kotero Aisraeli anachoka napita ku nyumba zawo.
Torej ko je ves Izrael videl, da jim kralj ni prisluhnil, je ljudstvo odgovorilo kralju, rekoč: »Kakšen delež imamo v Davidu? Niti nimamo dediščine v Jesejevem sinu. K svojim šotorom, oh Izrael. Sedaj poglej k svoji lastni hiši, David.« Tako je Izrael odšel v svoje šotore.
17 Koma Aisraeli amene ankakhala mʼmizinda ya Yuda ankalamuliridwa ndi Rehobowamu.
Toda kar se tiče Izraelovih otrok, ki so prebivali v Judovih mestih, je nad njimi kraljeval Rehabám.
18 Mfumu Rehobowamu anatuma Adoramu amene ankayangʼanira ntchito yathangata, koma Aisraeli onse anamugeda ndi miyala mpaka kumupha. Koma Mfumu Rehobowamu anakwera msangamsanga galeta wake nathawira ku Yerusalemu.
Potem je kralj Rehabám poslal Adoráma, ki je bil nad davkom in ves Izrael ga je kamnal s kamni, da je umrl. Zato je kralj Rehabám pohitel, da se spravi k svojemu bojnemu vozu, da pobegne v Jeruzalem.
19 Choncho Aisraeli akhala akuwukira nyumba ya Davide mpaka lero lino.
Tako se je Izrael uprl zoper Davidovo hišo do današnjega dne.
20 Aisraeli onse atamva kuti Yeroboamu wabwerera kuchokera ku Igupto, anatumiza mawu okamuyitana kuti abwere ku msonkhano ndipo anamuyika kukhala mfumu ya Aisraeli onse. Fuko la Yuda lokha ndi lomwe linkatsatira nyumba ya Davide.
Pripetilo se je, ko je ves Izrael slišal, da je Jerobeám ponovno prišel, da so poslali in ga poklicali k skupnosti in ga postavili za kralja nad vsem Izraelom. Tam ni bilo nikogar, ki je sledil Davidovi hiši, razen samo Judovega rodu.
21 Rehobowamu atafika ku Yerusalemu, anasonkhanitsa nyumba yonse ya Yuda ndi fuko la Benjamini, nasankha ankhondo okwanira 180,000, kuti akamenyane ndi nyumba ya Israeli kuti amubwezere Rehobowamu mwana wa Solomoni ufumu wake.
Ko je Rehabám prišel v Jeruzalem, je zbral vso Judovo hišo, z Benjaminovim rodom, sto osemdeset tisoč izbranih mož, ki so bili bojevniki, da se bojujejo zoper Izraelovo hišo, da kraljestvo ponovno privedejo k Salomonovemu sinu Rehabámu.
22 Koma Mulungu anayankhula ndi Semaya, munthu wa Mulungu kuti,
Toda beseda od Boga je prišla k Šemajáju, Božjemu možu, rekoč:
23 “Nena kwa Rehobowamu mwana wa Solomoni mfumu ya Yuda, kwa nyumba yonse ya Yuda ndi Benjamini, ndiponso kwa anthu ena onse kuti,
»Govori Salomonovemu sinu Rehabámu, Judovemu kralju in vsej Judovi in Benjaminovi hiši in preostanku ljudstva, rekoč:
24 ‘Yehova akuti: Musapite kukamenyana ndi abale anu Aisraeli. Aliyense wa inu abwerere kwawo, pakuti zimenezi ndachita ndine.’” Choncho anthuwo anamvera mawu a Yehova ndi kubwerera kwawo, monga analamulira Yehova.
›Tako govori Gospod: ›Ne boste šli gor niti se ne boste borili zoper vaše brate, Izraelove otroke. Vsak mož naj se vrne k svoji hiši, kajti ta stvar je od mene.‹« Prisluhnili so torej Gospodovi besedi in se vrnili, da odidejo, glede na Gospodovo besedo.
25 Tsono Yeroboamu anamanga mzinda wa Sekemu mʼdziko la mapiri la Efereimu ndipo anakhala kumeneko. Kuchokera kumeneko anapita kukamanga mzinda wa Penueli.
Potem je Jerobeám na gori Efrájim zgradil Sihem in tam prebival in odšel od tam ter zgradil Penuél.
26 Yeroboamu anaganiza mu mtima mwake kuti, “Ndithu, ufumuwu udzabwereranso ku nyumba ya Davide.
Jerobeám je v svojem srcu rekel: »Sedaj se bo kraljestvo vrnilo k Davidovi hiši.
27 Ngati anthuwa azipitabe kukapereka nsembe ku Nyumba ya Yehova ku Yerusalemu, adzayambanso kutsatira mbuye wawo Rehobowamu, mfumu ya Yuda. Adzandipha ndi kubwerera kwa Mfumu Rehobowamu.”
Če gre to ljudstvo gor, da opravi klavno daritev v Gospodovi hiši, v Jeruzalemu, potem se bo srce tega ljudstva ponovno obrnilo k njihovemu gospodu, k Judovemu kralju Rehabámu, mene pa bodo ubili in ponovno odšli k Judovemu kralju Rehabámu.«
28 Itapempha nzeru, mfumuyo inapanga mafano awiri a ana angʼombe. Mfumuyo inati kwa anthuwo, “Mwakhala mukupita ku Yerusalemu nthawi yayitali. Iwe Israeli, nayi milungu yako imene inakutulutsa mʼdziko la Igupto.”
Nakar se je kralj posvetoval in naredil dve teleti iz zlata ter jim rekel: »To je za vas preveč, da greste gor v Jeruzalem. Poglejte svoje bogove, oh Izrael, ki so te privedli gor iz egiptovske dežele.«
29 Fano lina analiyika ku Beteli ndipo lina analiyika ku Dani.
Eno je postavil v Betelu, drugo pa v Danu.
30 Ndipo zimenezi zinachimwitsa anthu pakuti anthu ankapita mpaka ku Dani kukapembedza fano limene linali kumeneko.
Ta stvar je postala greh, kajti ljudstvo je odšlo, da bi oboževalo pred enim, celó k Danu.
31 Yeroboamu anamanga Nyumba za Mulungu pa malo azipembedzo nasankha ansembe kuchokera pakati pa anthu wamba, ngakhale sanali Alevi.
Naredil je hišo visokih krajev in iz najnižjih izmed ljudstva naredil duhovnike, ki niso bili izmed Lévijevih sinov.
32 Iye anakhazikitsa chikondwerero pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chitatu, lofanana ndi tsiku la chikondwerero cha ku Yuda, ndipo ankapereka nsembe pa guwa. Izi ankachita ku Beteli, kupereka nsembe kwa ana angʼombe amene anapanga. Ndipo ku Beteliko anayikako ansembe pa malo achipembedzo amene anamanga.
Jerobeám je odredil praznovanje v osmem mesecu, na petnajsti dan meseca, podobno prazniku, ki je v Judu in daroval na oltarju. Tako je storil v Betelu, žrtvoval je teletoma, ki ju je naredil in v Betelu je postavil duhovnike visokih krajev, ki jih je naredil.
33 Tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chitatu, mwezi umene anawusankha yekha, anapereka nsembe pa guwa limene analimanga ku Beteli. Motero anakhazikitsa chikondwerero cha Aisraeli ndipo iye ankapita kukapereka nsembe yofukiza lubani pa guwa.
Tako je daroval na oltarju, ki ga je naredil v Betelu, na petnajsti dan osmega meseca, celó v mesecu, ki ga je zasnoval iz svojega lastnega srca in odredil praznovanje Izraelovim otrokom in daroval na oltarju in zažgal kadilo.

< 1 Mafumu 12 >