< 1 Mafumu 11 >

1 Komatu Mfumu Solomoni anakonda akazi ambiri achilendo ndipo kuwonjezera pa mwana wamkazi wa Farao, analinso ndi akazi a mitundu iyi: Amowabu, Aamoni, Aedomu, Asidoni, ndi Ahiti.
Now king Solomon loved many foreign women, together with the daughter of Pharaoh, women of the Moabites, Ammonites, Edomites, Sidonians, and Hittites,
2 Akazi amenewa anali ochokera ku mitundu ija imene Yehova anawuza Aisraeli kuti, “Simuyenera kudzakwatirana nawo amenewa, chifukwa ndithu, amenewa adzatembenuza mitima yanu kuti mutsatire milungu yawo.” Komabe Solomoni anawakonda kwambiri akazi amenewa.
of the nations concerning which Jehovah said to the sons of Israel, Ye shall not go among them, neither shall they come among you, for surely they will turn away your heart after their gods. Solomon clave to these in love.
3 Iye anali ndi akazi 700 ochokera ku mabanja achifumu ndi azikazi 300 ndipo akaziwo anamusocheretsa.
And he had seven hundred wives, princesses, and three hundred concubines. And his wives turned away his heart.
4 Solomoni atakalamba, akazi akewo anakopa mtima wake kuti atsatire milungu ina, ndipo sanatsatire Yehova Mulungu wake ndi mtima wodzipereka, monga unalili mtima wa Davide abambo ake.
For it came to pass, when Solomon was old, that his wives turned away his heart after other gods. And his heart was not perfect with Jehovah his God as was the heart of David his father.
5 Pakuti iye ankapembedza Asitoreti, mulungu wamkazi wa Asidoni, ndiponso Moleki mulungu wonyansa wa Aamoni.
For Solomon went after Ashtoreth the goddess of the Sidonians, and after Milcom the abomination of the Ammonites.
6 Kotero Solomoni anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Sanatsatire Yehova kwathunthu monga anachitira Davide abambo ake.
And Solomon did that which was evil in the sight of Jehovah, and went not fully after Jehovah as did David his father.
7 Pa phiri la kummawa kwa Yerusalemu, anamanga malo opembedzerapo Kemosi, mulungu wonyansa wa Mowabu, ndiponso malo a Moleki, mulungu wonyansa wa Aamoni.
Then Solomon built a high place for Chemosh the abomination of Moab on the mount that is before Jerusalem, and for Molech the abomination of the sons of Ammon.
8 Iye anamangiranso malo oterewa akazi ake onse achilendo, amene amafukiza lubani ndi kumapereka nsembe kwa milungu yawo.
And so he did for all his foreign wives, who burnt incense and sacrificed to their gods.
9 Choncho Yehova anakwiyira Solomoni chifukwa mtima wake unatembenuka kuchoka kwa Yehova Mulungu wa Israeli, amene anamuonekera kawiri konse.
And Jehovah was angry with Solomon because his heart was turned away from Jehovah, the God of Israel, who had appeared to him twice,
10 Ngakhale kuti Yehova anamuletsa Solomoni kutsatira milungu ina, iyeyo sanamvere lamulo la Yehova.
and had commanded him concerning this thing, that he should not go after other gods. But he did not keep that which Jehovah commanded.
11 Pamenepo Yehova anati kwa Solomoni, “Popeza mtima wako ndi wotere ndipo sunasunge pangano langa ndi malamulo anga amene ndinakuwuza, ndithudi, Ine ndidzawugawa ufumuwu kuwuchotsa kwa iwe ndi kuwupereka kwa mmodzi mwa atumiki ako.
Therefore Jehovah said to Solomon, Forasmuch as this is done by thee, and thou have not kept my covenant and my statutes, which I have commanded thee, I will surely rend the kingdom from thee, and will give it to thy servant.
12 Koma chifukwa cha Davide abambo ako, sindidzachita zimenezi iwe uli moyo. Ndidzawugawa mʼdzanja la mwana wako.
Notwithstanding I will not do it in thy days, for David thy father's sake, but I will rend it out of the hand of thy son.
13 Komabe sindidzamulanda ufumu wonse, koma ndidzamusiyira fuko limodzi chifukwa cha mtumiki wanga Davide ndiponso chifukwa cha Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha.”
However I will not rend away all the kingdom, but I will give one tribe to thy son, for David my servant's sake, and for Jerusalem's sake which I have chosen.
14 Ndipo Yehova anamuutsira Solomoni mdani, Hadadi Mwedomu, wochokera ku banja laufumu ku Edomu.
And Jehovah raised up an adversary to Solomon, Hadad the Edomite. He was of the king's seed in Edom.
15 Kale pamene Davide ankachita nkhondo ndi Aedomu, Yowabu mkulu wa ankhondo, amene anapita kukakwirira Aisraeli akufa, anakantha amuna onse ku Edomu.
For it came to pass, when David was in Edom, and Joab the captain of the army was gone up to bury the slain, and had smitten every male in Edom
16 Yowabu ndi Aisraeli onse anakhala kumeneko miyezi isanu ndi umodzi mpaka anawononga amuna onse a ku Edomu.
(for Joab and all Israel remained there six months until he had cut off every male in Edom),
17 Koma Hadadi akanali mwana anathawira ku Igupto pamodzi ndi akuluakulu ena a ku Edomu amene ankatumikira abambo ake.
that Hadad fled, he and certain Edomites of his father's servants with him, to go into Egypt, Hadad being yet a little child.
18 Iwo ananyamuka ku Midiya ndi kupita ku Parani. Ndipo anatenga amuna ena ku Paraniko, napita nawo ku Igupto, kwa Farao mfumu ya Igupto, amene anamupatsa nyumba, malo ndiponso chakudya.
And they arose out of Midian, and came to Paran. And they took men with them out of Paran, and they came to Egypt, to Pharaoh king of Egypt, who gave him a house, and appointed him provisions, and gave him land.
19 Farao anamukomera mtima Hadadi ndipo anamupatsa mkazi amene anali mngʼono wake wa Mfumukazi Tahipenesi.
And Hadad found great favor in the sight of Pharaoh, so that he gave him to wife the sister of his own wife, the sister of Tahpenes the queen.
20 Mngʼono wake wa Tahipenesi anabereka mwana wamwamuna ndipo anamutcha Genubati, amene analeredwa mʼnyumba yaufumu ndi Tahipenesi. Genubatiyo ankakhala limodzi ndi ana a Farao.
And the sister of Tahpenes bore him Genubath his son, whom Tahpenes weaned in Pharaoh's house. And Genubath was in Pharaoh's house among the sons of Pharaoh.
21 Ali ku Iguptoko, Hadadi anamva kuti Davide ndi Yowabu anamwalira. Pamenepo Hadadi anati kwa Farao, “Loleni ndichoke kuti ndibwerere ku dziko la kwathu.”
And when Hadad heard in Egypt that David slept with his fathers, and that Joab the captain of the army was dead, Hadad said to Pharaoh, Let me depart that I may go to my own country.
22 Farao anafunsa kuti, “Kodi ukusowa chiyani kuno kuti ufune kubwerera ku dziko la kwanu?” Hadadi anayankha kuti, “Palibe chimene ndikusowa, koma loleni kuti ndichoke!”
Then Pharaoh said to him, But what have thou lacked with me, that, behold, thou seek to go to thine own country? And he answered, Nothing, however only let me depart.
23 Ndipo Mulungu anawutsira Solomoni mdani wina, Rezoni mwana wa Eliada, amene anali atathawa mbuye wake, Hadadezeri mfumu ya ku Zoba.
And God raised up another adversary to him, Rezon the son of Eliada, who had fled from his lord Hadadezer king of Zobah.
24 Iye anasonkhanitsa anthu ndipo anali mtsogoleri wa anthu owukira pamene Davide anapha ankhondo a ku Zoba. Anthu owukirawa anapita ku Damasiko, nakakhala kumeneko ndi kuyamba kulamulira.
And he gathered men to him, and became captain over a troop when David killed them of Zobah. And they went to Damascus, and dwelt therein, and reigned in Damascus.
25 Rezoni anali mdani wa Israeli pa masiku onse a Solomoni, kuwonjezera pa mavuto amene ankabweretsa Hadadi. Kotero Rezoni ankalamulira ku Aramu ndipo ankadana ndi Israeli.
And he was an adversary to Israel all the days of Solomon, besides the mischief that Hadad did. And he abhorred Israel, and reigned over Syria.
26 Yeroboamu, mwana wa Nebati anawukiranso mfumu. Iye anali mmodzi mwa akuluakulu a Solomoni wa fuko la Efereimu, wa ku Zeredi, ndipo amayi ake anali Zeruya, mkazi wamasiye.
And Jeroboam the son of Nebat, an Ephraimite of Zeredah, a servant of Solomon whose mother's name was Zeruah, a widow, he also lifted up his hand against the king.
27 Nkhani ya kuwukira kwa Yeroboamu inali yotere: Solomoni anamanga malo a chitetezo a Milo ndipo anakonza khoma logumuka la mzinda wa Davide, abambo ake.
And this was the reason why he lifted up his hand against the king: Solomon built Millo, and repaired the breach of the city of David his father.
28 Tsono Yeroboamu anali munthu wamphamvu kwambiri ndipo Solomoni ataona kuti mnyamatayo amadziwa kugwira ntchito bwino, anamuyika kukhala woyangʼanira anthu a ntchito onse a nyumba ya Yosefe.
And the man Jeroboam was a mighty man of valor. And Solomon saw the young man that he was industrious, and he gave him charge over all the labor of the house of Joseph.
29 Tsiku lina Yeroboamu ali pa ulendo kuchokera ku Yerusalemu, anakumana ndi mneneri Ahiya pa msewu, ndipo Ahiyayo anali atavala mwinjiro watsopano. Awiriwo anali okha kuthengoko,
And it came to pass at that time, when Jeroboam went out of Jerusalem, that the prophet Ahijah the Shilonite found him in the way. Now Ahijah had clad himself with a new garment, and the two were alone in the field.
30 ndipo Ahiya anagwira mwinjiro watsopano umene anavala ndi kuwungʼamba zidutswa 12.
And Ahijah laid hold of the new garment that was on him, and tore it in twelve pieces.
31 Tsono iye anati kwa Yeroboamu, “Tenga zidutswa khumi, pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Taona, Ine ndidzachotsa ufumu mʼdzanja la Solomoni ndipo ndidzakupatsa iwe mafuko khumi.
And he said to Jeroboam, Take thee ten pieces, for thus says Jehovah, the God of Israel, Behold, I will rend the kingdom out of the hand of Solomon, and will give ten tribes to thee
32 Koma chifukwa cha mtumiki wanga Davide ndiponso mzinda wa Yerusalemu, umene ndinawusankha pakati pa mafuko a Israeli, iye adzakhala ndi fuko limodzi lokha.
(but he shall have one tribe, for my servant David's sake and for Jerusalem's sake, the city which I have chosen out of all the tribes of Israel),
33 Ndidzachita zimenezi chifukwa wandisiya Ine ndi kupembedza Asitoreti mulungu wamkazi wa Asidoni, Kemosi mulungu wa Amowabu ndiponso Moleki mulungu wa Aamoni, ndipo sanayende mʼnjira yanga, kapena kusunga mawu anga ndi malamulo anga monga anachitira Davide abambo ake.
because that they have forsaken me, and have worshiped Ashtoreth the goddess of the Sidonians, Chemosh the god of Moab, and Milcom the god of the sons of Ammon. And they have not walked in my ways, to do that which is right in my eyes, and to keep my statutes and my ordinances as David his father did.
34 “‘Koma sindidzalanda ufumu wonse mʼdzanja la Solomoni. Ine ndamuyika kukhala wolamulira masiku onse a moyo wake chifukwa cha mtumiki wanga Davide, amene ndinamusankha ndiponso amene anamvera malamulo anga ndi mawu anga.
However I will not take the whole kingdom out of his hand, but I will make him prince all the days of his life, for David my servant's sake whom I chose, who kept my commandments and my statutes.
35 Ndidzalanda ufumu mʼdzanja la mwana wake ndipo ndidzakupatsa iwe mafuko khumi.
But I will take the kingdom out of his son's hand, and will give it to thee, even ten tribes.
36 Ndidzapereka fuko limodzi kwa mwana wake ndi cholinga choti Davide mtumiki wanga adzakhale nyale nthawi zonse pamaso panga mu Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha kuyikamo Dzina langa.
And I will give one tribe to his son, that David my servant may have a lamp always before me in Jerusalem, the city which I have chosen for me to put my name there.
37 Koma kunena za iwe, ndidzakutenga ndipo udzalamulira chilichonse chimene mtima wako ukukhumba; udzakhala mfumu ya Israeli.
And I will take thee, and thou shall reign according to all that thy soul desires, and shall be king over Israel.
38 Ngati udzamvera zonse zimene ndidzakulamula ndi kuyenda mʼnjira yanga ndi kuchita zabwino pamaso panga, posunga malamulo anga ndi mawu anga monga anachitira Davide mtumiki wanga, Ine ndidzakhala nawe. Ndidzakupatsa ufumu umene udzakhala wokhazikika monga ndinamupatsira Davide, ndipo Ine ndidzakupatsa Israeli.
And it shall be, if thou will hearken to all that I command thee, and will walk in my ways, and do that which is right in my eyes, to keep my statutes and my commandments, as David my servant did. That I will be with thee, and will build thee a sure house as I built for David, and will give Israel to thee.
39 Ine ndidzalanga zidzukulu za Davide chifukwa cha zimenezi, koma osati kwamuyaya.’”
And for this I will afflict the seed of David, but not forever.
40 Solomoni anafunitsitsa kupha Yeroboamu, koma Yeroboamu anathawira ku Igupto, kwa Sisaki mfumu ya Igupto ndipo anakhala kumeneko mpaka Solomoni atamwalira.
Solomon therefore sought to kill Jeroboam. But Jeroboam arose, and fled into Egypt, to Shishak king of Egypt, and was in Egypt until the death of Solomon.
41 Ntchito zina za Solomoni, zonse zomwe anachita komanso za nzeru zake, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya Solomoni?
Now the rest of the acts of Solomon, and all that he did, and his wisdom, are they not written in the book of the acts of Solomon?
42 Solomoni analamulira Aisraeli onse mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi.
And the time that Solomon reigned in Jerusalem over all Israel was forty years.
43 Ndipo anagona ndi makolo ake nayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide abambo ake. Ndipo Rehobowamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo ake.
And Solomon slept with his fathers, and was buried in the city of David his father. And Rehoboam his son reigned in his stead.

< 1 Mafumu 11 >