< 1 Mbiri 9 >

1 Aisraeli onse analembedwa potsata mibado yawo mʼbuku la mafumu a Aisraeli. Anthu a ku Yuda anatengedwa kunka ku ukapolo ku Babuloni chifukwa cha kusakhulupirika kwawo.
So all Israel were reckoned by genealogies. And, behold, they are written in the book of the kings of Israel. And Judah was carried away captive to Babylon for their transgression.
2 Tsono anthu oyamba kukhala mʼmadera awo anali Aisraeli wamba, ansembe, Alevi ndi otumikira ku Nyumba ya Yehova.
Now the first inhabitants who dwelt in their possessions in their cities were Israelites, the priests, the Levites, and the Nethinim.
3 Anthu a ku Yuda, Benjamini ndi Efereimu ndiponso Manase amene anakhala mu Yerusalemu anali awa:
And in Jerusalem dwelt of the sons of Judah, and of the sons of Benjamin, and of the sons of Ephraim and Manasseh:
4 Utai mwana wa Amihudi, mwana wa Omuri, mwana wa Imuri, mwana wa Bani, chidzukulu cha Perezi mwana wa Yuda.
Uthai the son of Ammihud, the son of Omri, the son of Imri, the son of Bani, of the sons of Perez the son of Judah.
5 A banja la Siloni: Asaya mwana wake woyamba pamodzi ndi ana ake.
And of the Shilonites: Asaiah the firstborn, and his sons.
6 A banja la Zera: Yeueli. Anthu ochokera ku Yuda analipo 690.
And of the sons of Zerah: Jeuel, and their brothers, six hundred and ninety.
7 A fuko la Benjamini: Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Hodaviya, mwana wa Hasenuya;
And of the sons of Benjamin: Sallu the son of Meshullam, the son of Hodaviah, the son of Hassenuah,
8 Ibineya mwana wa Yerohamu; Ela mwana wa Uzi, mwana wa Mikiri; ndi Mesulamu mwana wa Sefatiya, mwana wa Reueli mwana wa Ibiniya.
and Ibneiah the son of Jeroham, and Elah the son of Uzzi, the son of Michri, and Meshullam the son of Shephatiah, the son of Reuel, the son of Ibnijah,
9 Anthu ochokera ku Benjamini monga analembedwera mwa mibado yawo, analipo 956. Anthu onsewa anali atsogoleri a mabanja awo.
and their brothers, according to their generations, nine hundred and fifty-six. All these men were heads of fathers by their fathers' houses.
10 Ansembe: Yedaya, Yehoyaribu; Yakini;
And of the priests: Jedaiah, and Jehoiarib, Jachin,
11 Azariya mwana wa Hilikiya, mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki mwana wa Merayoti, mwana wa Ahitubi, wamkulu woyangʼanira Nyumba ya Mulungu;
and Azariah the son of Hilkiah, the son of Meshullam, the son of Zadok, the son of Meraioth, the son of Ahitub, the ruler of the house of God,
12 Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pasi-Huri, mwana wa Malikiya; ndi Maasai mwana wa Adieli, mwana wa Yahizera, mwana wa Mesulamu, mwana wa Mesilemoti, mwana wa Imeri.
and Adaiah the son of Jeroham, the son of Pashhur, the son of Malchijah, and Maasai the son of Adiel, the son of Jahzerah, the son of Meshullam, the son of Meshillemith, the son of Immer,
13 Ansembe amene anali atsogoleri a mabanja awo analipo 1,760. Anali anthu amphamvu ndi odziwa kutumikira mʼnyumba ya Mulungu.
and their brothers, heads of their fathers' houses, a thousand and seven hundred and sixty, very able men for the work of the service of the house of God.
14 Alevi: Semaya mwana wa Hasubu, mwana wa Azirikamu, mwana wa Hasabiya, wa mʼbanja la Merari;
And of the Levites: Shemaiah the son of Hasshub, the son of Azrikam, the son of Hashabiah, of the sons of Merari,
15 Bakibakara, Heresi, Galali ndi Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zikiri, mwana wa Asafu;
and Bakbakkar, Heresh, and Galal, and Mattaniah the son of Mica, the son of Zichri, the son of Asaph,
16 Obadiya mwana wa Semaya mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni ndi Berekiya mwana wa Asa, mwana wa Elikana, amene ankakhala ku midzi ya Anetofati.
and Obadiah the son of Shemaiah, the son of Galal, the son of Jeduthun, and Berechiah the son of Asa, the son of Elkanah, who dwelt in the villages of the Netophathites.
17 Alonda a pa makomo: Salumu, Akubu, Talimoni, Ahimani ndi abale awo. Mtsogoleri wawo anali Salumu.
And the porters: Shallum, and Akkub, and Talmon, and Ahiman, and their brothers (Shallum was the chief),
18 Amenewa amakhala pa chipata cha mfumu kummawa mpaka lero lino. Alonda a gulu la Alevi anali awa:
who formerly served in the king's gate eastward. They were the porters for the camp of the sons of Levi.
19 Salumu mwana wa Kore, mwana wa Ebiyasafu, mwana wa Kora, pamodzi ndi abale ake a ku banja la makolo ake, Akora aja ankanyangʼanira khomo la Tenti monga ankachitira abambo awo polondera khomo la malo okhalapo Yehova.
And Shallum the son of Kore, the son of Ebiasaph, the son of Korah, and his brothers, of his father's house, the Korahites, were over the work of the service, keepers of the thresholds of the tent. And their fathers had been over the camp of Jehovah, keepers of the entry.
20 Masiku oyamba Finehasi mwana wa Eliezara anali woyangʼanira alonda apakhomo ndipo Yehova anali naye.
And Phinehas the son of Eleazar was ruler over them in time past, and Jehovah was with him.
21 Zekariya mwana wa Meselemiya anali mlonda woyangʼanira pa chipata cha tenti ya msonkhano.
Zechariah the son of Meshelemiah was porter of the door of the tent of meeting.
22 Onse amene anasankhidwa kukhala alonda pa khonde analipo 212. Iwo analembedwa mwa mibado yawo ku midzi yawo. Davide ndi mneneri Samueli ndiwo anawayika mʼmalo awo antchito chifukwa cha kukhulupirika kwawo.
All these who were chosen to be porters in the thresholds were two hundred and twelve. These were reckoned by genealogy in their villages, whom David and Samuel the seer ordained in their office of trust.
23 Iwo ndi zidzukulu zawo anali oyangʼanira zipata za nyumba ya Yehova imene imatchedwa Tenti.
So they and their sons had the oversight of the gates of the house of Jehovah, even the house of the tent, by wards.
24 Alonda apakhomowa anali mbali zonse zinayi: kummawa, kumadzulo, kumpoto ndi kummwera.
On the four sides were the porters, toward the east, west, north, and south.
25 Abale awo a ku midzi yawo amabwera nthawi ndi nthawi kudzagwira ntchito yawo kwa masiku asanu ndi awiri.
And their brothers, in their villages, were to come in every seven days from time to time to be with them;
26 Koma atsogoleri akuluakulu anayi a alonda, amene anali Alevi, anapatsidwa udindo woyangʼanira zipinda ndi chuma cha nyumba ya Mulungu.
for the four chief porters, who were Levites, were in an office of trust, and were over the chambers and over the treasuries in the house of God.
27 Iwo amakhala usiku wonse atayima mozungulira Nyumba ya Mulungu, chifukwa anayenera kuyilondera. Ndipo anali ndi kiyi wotsekulira mmawa uliwonse.
And they lodged round about the house of God, because the charge of it was upon them, and to them pertained the opening of it morning by morning.
28 Ena amayangʼanira zipangizo zimene amagwiritsa ntchito pa ntchito mʼNyumba ya Mulungu. Iwo amaziwerenga zikamalowetsedwa ndi potulutsidwa.
And certain of them had charge of the vessels of service, for by count were these brought in, and by count were these taken out.
29 Ena anapatsidwa udindo wosamalira zipangizo ndi zinthu zina zonse za ku malo opatulika, pamodzi ndi ufa, vinyo, mafuta, lubani ndi zonunkhira.
Some of them were also appointed over the furniture, and over all the vessels of the sanctuary, and over the fine flour, and the wine, and the oil, and the frankincense, and the spices.
30 Koma ansembe ena amasakaniza zonunkhirazo.
And some of the sons of the priests prepared the confection of the spices.
31 Mlevi wotchedwa Matitiya mwana woyamba wa Salumu wa mʼbanja la Kora, anapatsidwa udindo woyangʼanira zophikidwa mʼziwaya.
And Mattithiah, one of the Levites, who was the firstborn of Shallum the Korahite, had the office of trust over the things that were baked in pans.
32 Abale ake ena a mʼbanja la Akohati amaphika buledi wa pa Sabata lililonse amene amayikidwa pa tebulo.
And some of their brothers, of the sons of the Kohathites, were over the showbread to prepare it every sabbath.
33 Atsogoleri a mabanja a Alevi, amene anali ndi luso loyimba, amakhala mʼzipinda za Nyumba ya Mulungu ndipo samagwira ntchito zina chifukwa ankatumikira usana ndi usiku.
And these are the singers, heads of fathers of the Levites, who dwelt in the chambers and were free from other service, for they were employed in their work day and night.
34 Onsewa anali atsogoleri a mabanja a Alevi, akuluakulu monga analembedwera pa mibado yawo, ndipo ankakhala mu Yerusalemu.
These were heads of fathers of the Levites, throughout their generations, chief men; these dwelt at Jerusalem.
35 Yeiyeli abambo a Gibiyoni ankakhala ku Gibiyoni. Dzina la akazi awo linali Maaka,
And in Gibeon there dwelt the father of Gibeon, Jeiel, whose wife's name was Maacah,
36 ndipo mwana wawo woyamba kubadwa anali Abidoni, motsatana ndi Zuri, Kisi, Baala, Neri, Nadabu,
and his firstborn son Abdon, and Zur, and Kish, and Baal, and Ner, and Nadab,
37 Gedori, Ahiyo, Zekariya ndi Mikiloti.
and Gedor, and Ahio, and Zechariah, and Mikloth.
38 Mikiloti anabereka Simeamu. Iwonso ankakhala ndi abale awo ku Yerusalemu.
And Mikloth begot Shimeam. And they also dwelt with their brothers in Jerusalem, opposite their brothers.
39 Neri anabereka Kisi, Kisi anabereka Sauli, ndipo Sauli anabereka Yonatani, Maliki-Suwa, Abinadabu ndi Esibaala.
And Ner begot Kish, and Kish begot Saul, and Saul begot Jonathan, and Malchi-shua, and Abinadab, and Eshbaal.
40 Mwana wa Yonatani anali Meri-Baala, amene anabereka Mika.
And the son of Jonathan was Merib-baal, and Merib-baal begot Micah.
41 Ana a Mika anali: Pitoni, Meleki, Tahireya ndi Ahazi.
And the sons of Micah: Pithon, and Melech, and Tahrea, and Ahaz.
42 Ahazi anabereka Yara, Yara anabereka Alemeti, Azimaveti ndi Zimuri, ndipo Zimiri anabereka Moza.
And Ahaz begot Jarah, and Jarah begot Alemeth, and Azmaveth, and Zimri; and Zimri begot Moza,
43 Moza anabereka Bineya. Ana ake anali Refaya, Eleasa ndi Azeli.
and Moza begot Binea, and Rephaiah his son, Eleasah his son, Azel his son.
44 Azeli anali ndi ana asanu ndi mmodzi ndipo mayina awo anali awa: Azirikamu, Bokeru, Ismaeli, Seariya, Obadiya ndi Hanani. Awa anali ana a Azeli.
And Azel had six sons, whose names are these: Azrikam, Bocheru, and Ishmael, and Sheariah, and Obadiah, and Hanan; these were the sons of Azel.

< 1 Mbiri 9 >