< 1 Mbiri 7 >

1 Ana a Isakara anali awa: Tola, Puwa, Yasubu ndi Simironi ndipo onse analipo anayi.
Now the sons of Issachar [were], Tola, and Puah, Jashub, and Shimron, four.
2 Ana a Tola ndi awa: Uzi, Refaya, Yerieli, Yahimai, Ibisamu ndi Samueli. Awa anali atsogoleri a mabanja awo. Pa nthawi ya ulamuliro wa Davide zidzukulu za Tola zomwe zinali anthu odziwa kumenya nkhondo zinalipo 22,600.
And the sons of Tola; Uzzi, and Rephaiah, and Jeriel, and Jahmai, and Jibsam, and Shemuel, heads of their father’s house, [to wit], of Tola: [they were] valiant men of might in their generations; whose number [was] in the days of David two and twenty thousand and six hundred.
3 Mwana wa Uzi anali Izirahiya. Ana a Izirahiya anali: Mikayeli, Obadiya, Yoweli ndi Isiya. Onse asanu anali atsogoleri a mabanja.
And the sons of Uzzi; Izrahiah: and the sons of Izrahiah; Michael, and Obadiah, and Joel, Ishiah, five: all of them chief men.
4 Monga mwa chiwerengero cha mabanja awo, panali anthu 36,000 odziwa kumenya nkhondo, pakuti iwo anali ndi akazi ndi ana ambiri.
And with them, by their generations, after the house of their fathers, [were] bands of soldiers for war, six and thirty thousand [men: ] for they had many wives and sons.
5 Abale awo onse a mʼbanja la Isakara amene anali odziwa kumenya nkhondo analipo 87,000, olembedwa potsata mibado yawo.
And their brethren among all the families of Issachar [were] valiant men of might, reckoned in all by their genealogies fourscore and seven thousand.
6 Ana atatu a Benjamini anali awa: Bela, Bekeri ndi Yediaeli.
[The sons] of Benjamin; Bela, and Becher, and Jediael, three.
7 Ana a Bela anali awa: Eziboni, Uzi, Uzieli, Yerimoti ndi Iri. Iwowa anali atsogoleri a mabanja awo ndipo onse pamodzi analipo asanu. Pa mndandanda wa mʼbado wawo panali anthu 22,034 odziwa kumenya nkhondo.
And the sons of Bela; Ezbon, and Uzzi, and Uzziel, and Jerimoth, and Iri, five; heads of the house of [their] fathers, mighty men of valour; and were reckoned by their genealogies twenty and two thousand and thirty and four.
8 Ana a Bekeri anali awa: Zemira, Yowasi, Eliezara, Eliyoenai, Omiri, Yeremoti, Abiya, Anatoti ndi Alemeti. Onsewa anali ana a Bekeri.
And the sons of Becher; Zemira, and Joash, and Eliezer, and Elioenai, and Omri, and Jerimoth, and Abiah, and Anathoth, and Alameth. All these [are] the sons of Becher.
9 Pa mndandanda wa mʼbado wawo panali atsogoleri a mabanja ndi anthu 20,200 odziwa kumenya nkhondo.
And the number of them, after their genealogy by their generations, heads of the house of their fathers, mighty men of valour, [was] twenty thousand and two hundred.
10 Mwana wa Yediaeli anali Bilihani. Ana a Bilihani anali awa: Yeusi, Benjamini, Ehudi, Kenaana, Zetani, Tarisisi ndi Ahisahara.
The sons also of Jediael; Bilhan: and the sons of Bilhan; Jeush, and Benjamin, and Ehud, and Chenaanah, and Zethan, and Tharshish, and Ahishahar.
11 Ana onsewa a Yediaeli anali atsogoleri a mabanja. Analipo anthu 17,200 amene anali okonzeka kupita ku nkhondo.
All these the sons of Jediael, by the heads of their fathers, mighty men of valour, [were] seventeen thousand and two hundred [soldiers], fit to go out for war [and] battle.
12 Asupi ndi Ahupi anali zidzukulu za Iri, ndipo Ahusimu anali zidzukulu za Aheri.
Shuppim also, and Huppim, the children of Ir, [and] Hushim, the sons of Aher.
13 Ana a Nafutali anali awa: Yahazieli, Guni, Yezeri ndi Salumu, zidzukulu za Biliha.
The sons of Naphtali; Jahziel, and Guni, and Jezer, and Shallum, the sons of Bilhah.
14 Ana a Manase anali awa: Asirieli ndi mwana amene anabereka kwa mzikazi wake wa ku Aramu. Mzikazi yemweyo anaberekanso Makiri abambo ake a Giliyadi.
The sons of Manasseh; Ashriel, whom she bare: ([but] his concubine the Aramitess bare Machir the father of Gilead:
15 Makiri anatenga mkazi wa banja la Ahupi ndi Asupi. Mlongo wake anali Maaka. Mwana wake wina anali Zelofehadi, amene anabereka ana aakazi okhaokha.
And Machir took to wife [the sister] of Huppim and Shuppim, whose sister’s name [was] Maachah; ) and the name of the second [was] Zelophehad: and Zelophehad had daughters.
16 Maaka mkazi wa Makiri anabereka mwana wamwamuna ndipo anamutcha Perezi. Mʼbale wake anamutcha Seresi, ndipo ana ake anali Ulamu ndi Rakemu.
And Maachah the wife of Machir bare a son, and she called his name Peresh; and the name of his brother [was] Sheresh; and his sons [were] Ulam and Rakem.
17 Mwana wa Ulamu anali Bedani. Awa anali ana a Giliyadi mwana wa Makiri, mwana wa Manase.
And the sons of Ulam; Bedan. These [were] the sons of Gilead, the son of Machir, the son of Manasseh.
18 Mlongo wake Hamoleketi anabereka Isihodi, Abiezeri ndi Mahila.
And his sister Hammoleketh bare Ishod, and Abiezer, and Mahalah.
19 Ana a Semida anali: Ahiyani, Sekemu, Likihi ndi Aniyamu.
And the sons of Shemida were, Ahian, and Shechem, and Likhi, and Aniam.
20 Ana a Efereimu anali awa: Sutela, Beredi, Tahati, Eliada, Tahati,
And the sons of Ephraim; Shuthelah, and Bered his son, and Tahath his son, and Eladah his son, and Tahath his son,
21 Zabadi, Sutela. Ezeri ndi Eladi anaphedwa ndi anthu a ku Gati, pamene anabwera kudzalanda zoweta zawo.
And Zabad his son, and Shuthelah his son, and Ezer, and Elead, whom the men of Gath [that were] born in [that] land slew, because they came down to take away their cattle.
22 Efereimu, abambo awo, anawalira masiku ambiri, ndipo abale ake anabwera kudzamutonthoza.
And Ephraim their father mourned many days, and his brethren came to comfort him.
23 Kenaka anagona ndi mkazi wake, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Anamutcha dzina lake Beriya, chifukwa tsoka linagwera banja lake.
And when he went in to his wife, she conceived, and bare a son, and he called his name Beriah, because it went evil with his house.
24 Mwana wake wamkazi anali Seera, amene anamanga mzinda wa Beti-Horoni Wakumunsi, Wakumtunda kudzanso Uzeni-Seera.
(And his daughter [was] Sherah, who built Beth-horon the nether, and the upper, and Uzzen-sherah.)
25 Mwana wina wa Efereimu anali Refa amene zidzukulu zake zinali Resefu, Tela, Tahani,
And Rephah [was] his son, also Resheph, and Telah his son, and Tahan his son,
26 Ladani, Amihudi, Elisama,
Laadan his son, Ammihud his son, Elishama his son,
27 Nuni ndi Yoswa.
Non his son, Jehoshua his son.
28 Malo amene ankakhala anali Beteli ndi midzi yozungulira, cha kummawa kunali Naarani, Gezeri ndi midzi yake ya kumadzulo ndi Sekemu ndi midzi yake mpaka ku Aya ndi midzi yake.
And their possessions and habitations [were], Beth-el and the towns thereof, and eastward Naaran, and westward Gezer, with the towns thereof; Shechem also and the towns thereof, unto Gaza and the towns thereof:
29 Mʼmbali mwa malire a Manase munali Beti-Seani, Taanaki, Megido ndi Dori, pamodzi ndi midzi yake. Zidzukulu za Yosefe mwana wa Israeli zimakhala mʼmizinda imeneyi.
And by the borders of the children of Manasseh, Beth-shean and her towns, Taanach and her towns, Megiddo and her towns, Dor and her towns. In these dwelt the children of Joseph the son of Israel.
30 Ana a Aseri anali awa: Imuna, Isiva, Isivi ndi Beriya. Mlongo wawo anali Sera.
The sons of Asher; Imnah, and Isuah, and Ishuai, and Beriah, and Serah their sister.
31 Ana a Beriya anali awa: Heberi ndi Malikieli amene anabereka Birizaiti.
And the sons of Beriah; Heber, and Malchiel, who [is] the father of Birzavith.
32 Heberi anabereka Yafuleti, Someri, Hotamu ndi Suwa, mlongo wawo.
And Heber begat Japhlet, and Shomer, and Hotham, and Shua their sister.
33 Ana a Yafuleti anali awa: Pasaki, Bimuhali ndi Asivati. Awa anali ana a Yafuleti.
And the sons of Japhlet; Pasach, and Bimhal, and Ashvath. These [are] the children of Japhlet.
34 Ana a Someri anali awa: Ahi, Rohiga, Yehuba ndi Aramu.
And the sons of Shamer; Ahi, and Rohgah, Jehubbah, and Aram.
35 Ana a mʼbale wake Helemu anali awa: Zofa, Imuna, Selesi ndi Amali.
And the sons of his brother Helem; Zophah, and Imna, and Shelesh, and Amal.
36 Ana a Zofa anali awa: Suwa, Harineferi, Suwali, Beri, Imula,
The sons of Zophah; Suah, and Harnepher, and Shual, and Beri, and Imrah,
37 Bezeri, Hodi, Sama, Silisa, Itirani ndi Bera.
Bezer, and Hod, and Shamma, and Shilshah, and Ithran, and Beera.
38 Ana a Yeteri anali awa: Yefune, Pisipa ndi Ara.
And the sons of Jether; Jephunneh, and Pispah, and Ara.
39 Ana a Ula anali awa: Ara, Hanieli ndi Riziya.
And the sons of Ulla; Arah, and Haniel, and Rezia.
40 Onsewa anali zidzukulu za Aseri, atsogoleri a mabanja, anthu omveka, ankhondo olimba mtima, ndi akuluakulu pakati pa atsogoleri anzawo. Chiwerengero cha anthu odziwa kumenya nkhondo chomwe chinalembedwa chinali 26,000.
All these [were] the children of Asher, heads of [their] father’s house, choice [and] mighty men of valour, chief of the princes. And the number throughout the genealogy of them that were apt to the war [and] to battle [was] twenty and six thousand men.

< 1 Mbiri 7 >