< 1 Mbiri 7 >

1 Ana a Isakara anali awa: Tola, Puwa, Yasubu ndi Simironi ndipo onse analipo anayi.
And of the sons of Issachar: Tola, and Puah, Jashub, and Shimron, four.
2 Ana a Tola ndi awa: Uzi, Refaya, Yerieli, Yahimai, Ibisamu ndi Samueli. Awa anali atsogoleri a mabanja awo. Pa nthawi ya ulamuliro wa Davide zidzukulu za Tola zomwe zinali anthu odziwa kumenya nkhondo zinalipo 22,600.
And the sons of Tola: Uzzi, and Rephaiah, and Jeriel, and Jahmai, and Ibsam, and Shemuel, heads of their fathers' houses, namely, of Tola, mighty men of valor in their generations. Their number in the days of David was twenty-two thousand and six hundred.
3 Mwana wa Uzi anali Izirahiya. Ana a Izirahiya anali: Mikayeli, Obadiya, Yoweli ndi Isiya. Onse asanu anali atsogoleri a mabanja.
And the sons of Uzzi: Izrahiah. And the sons of Izrahiah: Michael, and Obadiah, and Joel, Isshiah, five; all of them chief men.
4 Monga mwa chiwerengero cha mabanja awo, panali anthu 36,000 odziwa kumenya nkhondo, pakuti iwo anali ndi akazi ndi ana ambiri.
And with them, by their generations, after their fathers' houses, were bands of the army for war, thirty-six thousand, for they had many wives and sons.
5 Abale awo onse a mʼbanja la Isakara amene anali odziwa kumenya nkhondo analipo 87,000, olembedwa potsata mibado yawo.
And their brothers among all the families of Issachar, mighty men of valor, reckoned in all by genealogy, were eighty-seven thousand.
6 Ana atatu a Benjamini anali awa: Bela, Bekeri ndi Yediaeli.
The sons of Benjamin: Bela, and Becher, and Jediael, three.
7 Ana a Bela anali awa: Eziboni, Uzi, Uzieli, Yerimoti ndi Iri. Iwowa anali atsogoleri a mabanja awo ndipo onse pamodzi analipo asanu. Pa mndandanda wa mʼbado wawo panali anthu 22,034 odziwa kumenya nkhondo.
And the sons of Bela: Ezbon, and Uzzi, and Uzziel, and Jerimoth, and Iri, five; heads of fathers' houses, mighty men of valor. And they were reckoned by genealogy twenty-two thousand and thirty-four.
8 Ana a Bekeri anali awa: Zemira, Yowasi, Eliezara, Eliyoenai, Omiri, Yeremoti, Abiya, Anatoti ndi Alemeti. Onsewa anali ana a Bekeri.
And the sons of Becher: Zemirah, and Joash, and Eliezer, and Elioenai, and Omri, and Jeremoth, and Abijah, and Anathoth, and Alemeth. All these were the sons of Becher.
9 Pa mndandanda wa mʼbado wawo panali atsogoleri a mabanja ndi anthu 20,200 odziwa kumenya nkhondo.
And they were reckoned by genealogy, after their generations, heads of their fathers' houses, mighty men of valor, twenty thousand and two hundred.
10 Mwana wa Yediaeli anali Bilihani. Ana a Bilihani anali awa: Yeusi, Benjamini, Ehudi, Kenaana, Zetani, Tarisisi ndi Ahisahara.
And the sons of Jediael: Bilhan. And the sons of Bilhan: Jeush, and Benjamin, and Ehud, and Chenaanah, and Zethan, and Tarshish, and Ahishahar.
11 Ana onsewa a Yediaeli anali atsogoleri a mabanja. Analipo anthu 17,200 amene anali okonzeka kupita ku nkhondo.
All these were sons of Jediael, according to the heads of their fathers, mighty men of valor, seventeen thousand and two hundred, who were able to go forth in the army for war.
12 Asupi ndi Ahupi anali zidzukulu za Iri, ndipo Ahusimu anali zidzukulu za Aheri.
Also the Shuppim, and the Huppim, the sons of Ir, and the Hushim, the sons of Aher.
13 Ana a Nafutali anali awa: Yahazieli, Guni, Yezeri ndi Salumu, zidzukulu za Biliha.
The sons of Naphtali: Jahziel, and Guni, and Jezer, and Shallum, the sons of Bilhah.
14 Ana a Manase anali awa: Asirieli ndi mwana amene anabereka kwa mzikazi wake wa ku Aramu. Mzikazi yemweyo anaberekanso Makiri abambo ake a Giliyadi.
The sons of Manasseh: Asriel, whom his concubine the Aramitess bore. She bore Machir the father of Gilead.
15 Makiri anatenga mkazi wa banja la Ahupi ndi Asupi. Mlongo wake anali Maaka. Mwana wake wina anali Zelofehadi, amene anabereka ana aakazi okhaokha.
And Machir took a wife of Huppim and Shuppim, whose sister's name was Maacah, and the name of the second was Zelophehad. And Zelophehad had daughters.
16 Maaka mkazi wa Makiri anabereka mwana wamwamuna ndipo anamutcha Perezi. Mʼbale wake anamutcha Seresi, ndipo ana ake anali Ulamu ndi Rakemu.
And Maacah the wife of Machir bore a son, and she called his name Peresh. And the name of his brother was Sheresh, and his sons were Ulam and Rakem.
17 Mwana wa Ulamu anali Bedani. Awa anali ana a Giliyadi mwana wa Makiri, mwana wa Manase.
And the son of Ulam: Bedan. These were the sons of Gilead the son of Machir, the son of Manasseh.
18 Mlongo wake Hamoleketi anabereka Isihodi, Abiezeri ndi Mahila.
And his sister Hammolecheth bore Ishhod, and Abiezer, and Mahlah.
19 Ana a Semida anali: Ahiyani, Sekemu, Likihi ndi Aniyamu.
And the sons of Shemida were Ahian, and Shechem, and Likhi, and Aniam.
20 Ana a Efereimu anali awa: Sutela, Beredi, Tahati, Eliada, Tahati,
And the sons of Ephraim: Shuthelah, and Bered his son, and Tahath his son, and Eleadah his son, and Tahath his son,
21 Zabadi, Sutela. Ezeri ndi Eladi anaphedwa ndi anthu a ku Gati, pamene anabwera kudzalanda zoweta zawo.
and Zabad his son, and Shuthelah his son, and Ezer, and Elead, whom the men of Gath that were born in the land killed, because they came down to take away their cattle.
22 Efereimu, abambo awo, anawalira masiku ambiri, ndipo abale ake anabwera kudzamutonthoza.
And Ephraim their father mourned many days, and his brothers came to comfort him.
23 Kenaka anagona ndi mkazi wake, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Anamutcha dzina lake Beriya, chifukwa tsoka linagwera banja lake.
And he went in to his wife, and she conceived, and bore a son, and he called his name Beriah, because it went evil with his house.
24 Mwana wake wamkazi anali Seera, amene anamanga mzinda wa Beti-Horoni Wakumunsi, Wakumtunda kudzanso Uzeni-Seera.
And his daughter was Sheerah, who built Beth-horon the lower and the upper, and Uzzen-sheerah.
25 Mwana wina wa Efereimu anali Refa amene zidzukulu zake zinali Resefu, Tela, Tahani,
And Rephah was his son, and Resheph, and Telah his son, and Tahan his son,
26 Ladani, Amihudi, Elisama,
Ladan his son, Ammihud his son, Elishama his son,
27 Nuni ndi Yoswa.
Nun his son, Joshua his son.
28 Malo amene ankakhala anali Beteli ndi midzi yozungulira, cha kummawa kunali Naarani, Gezeri ndi midzi yake ya kumadzulo ndi Sekemu ndi midzi yake mpaka ku Aya ndi midzi yake.
And their possessions and habitations were Bethel and the towns of it, and eastward Naaran, and westward Gezer, with the towns of it, also Shechem and the towns of it, to Azzah and the towns of it,
29 Mʼmbali mwa malire a Manase munali Beti-Seani, Taanaki, Megido ndi Dori, pamodzi ndi midzi yake. Zidzukulu za Yosefe mwana wa Israeli zimakhala mʼmizinda imeneyi.
and by the borders of the sons of Manasseh, Beth-shean and its towns, Taanach and its towns, Megiddo and its towns, Dor and its towns. In these dwelt the sons of Joseph the son of Israel.
30 Ana a Aseri anali awa: Imuna, Isiva, Isivi ndi Beriya. Mlongo wawo anali Sera.
The sons of Asher: Imnah, and Ishvah, and Ishvi, and Beriah, and Serah their sister.
31 Ana a Beriya anali awa: Heberi ndi Malikieli amene anabereka Birizaiti.
And the sons of Beriah: Heber, and Malchiel, who was the father of Birzaith.
32 Heberi anabereka Yafuleti, Someri, Hotamu ndi Suwa, mlongo wawo.
And Heber begot Japhlet, and Shomer, and Hotham, and Shua their sister.
33 Ana a Yafuleti anali awa: Pasaki, Bimuhali ndi Asivati. Awa anali ana a Yafuleti.
And the sons of Japhlet: Pasach, and Bimhal, and Ashvath. These are the sons of Japhlet.
34 Ana a Someri anali awa: Ahi, Rohiga, Yehuba ndi Aramu.
And the sons of Shemer: Ahi, and Rohgah, Jehubbah, and Aram.
35 Ana a mʼbale wake Helemu anali awa: Zofa, Imuna, Selesi ndi Amali.
And the sons of Helem his brother: Zophah, and Imna, and Shelesh, and Amal.
36 Ana a Zofa anali awa: Suwa, Harineferi, Suwali, Beri, Imula,
The sons of Zophah: Suah, and Harnepher, and Shual, and Beri, and Imrah,
37 Bezeri, Hodi, Sama, Silisa, Itirani ndi Bera.
Bezer, and Hod, and Shamma, and Shilshah, and Ithran, and Beera.
38 Ana a Yeteri anali awa: Yefune, Pisipa ndi Ara.
And the sons of Jether: Jephunneh, and Pispa, and Ara.
39 Ana a Ula anali awa: Ara, Hanieli ndi Riziya.
And the sons of Ulla: Arah, and Hanniel, and Rizia.
40 Onsewa anali zidzukulu za Aseri, atsogoleri a mabanja, anthu omveka, ankhondo olimba mtima, ndi akuluakulu pakati pa atsogoleri anzawo. Chiwerengero cha anthu odziwa kumenya nkhondo chomwe chinalembedwa chinali 26,000.
All these were the sons of Asher, heads of the fathers' houses, choice and mighty men of valor, chief of the rulers. And the number of them reckoned by genealogy for service in war was twenty-six thousand men.

< 1 Mbiri 7 >