< 1 Mbiri 27 >

1 Uwu ndi mndandanda wa Aisraeli, atsogoleri a mabanja, olamulira asilikali 1,000, olamulira asilikali 100 ndi akuluakulu awo, amene ankatumikira mfumu mʼzonse zokhudza magulu a ankhondo, amene amagwira ntchito mwezi ndi mwezi chaka chonse. Gulu lililonse linali ndi anthu 24,000.
This is a list of the Israeli men who served the king in the army. Some were leaders of families, some were commanders of 100 men, some were commanders of 1,000 men, and some were their officers. There were 24,000 men [DOU] in each group. Each group served one month of each year.
2 Amene amalamulira gulu loyamba pa mwezi woyamba anali Yasobeamu mwana wa Zabidieli. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
Jashobeam, the son of Zabdiel, was in charge of the group that served during the first month [of each year].
3 Iyeyu anali chidzukulu cha Perezi ndipo anali mkulu wa atsogoleri onse a ankhondo mwezi woyamba.
He was a descendant of Perez, and he was the commander of all the army officers during the first month of each year.
4 Amene amalamulira gulu lachiwiri pa mwezi wachiwiri anali Dodai Mwahohi; Mikiloti ndiye anali mtsogoleri wa gulu lake. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
Dodai, from the clan of Ahohi, was the commander of the group that served during the following/second month of each year. Mikloth was his (assistant/chief officer).
5 Wolamulira ankhondo wachitatu, pa mwezi wachitatu anali Benaya, mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anali mtsogoleri ndipo pa gulu lake panali ankhondo 24,000.
Benaiah, the son of Jehoiada the Supreme Priest, was the commander of the group that served during the following/third month.
6 Uyu ndi Benaya uja amene anali wamphamvu pa gulu la anthu makumi atatu ndipo ndiye amatsogolera anthu makumi atatu aja. Mwana wake Amizabadi ndiye amatsogolera gulu lake.
He was the one who was a mighty warrior among David’s thirty greatest soldiers, and he was their leader. His son Ammizabad was his assistant.
7 Wachinayi pa mwezi wachinayi anali Asaheli mʼbale wake wa Yowabu; ndipo mwana wake Zebadiya ndiye analowa mʼmalo mwake. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
Asahel, Joab’s [younger] brother, was [the commander of the group that served] during the following/fourth month. Asahel’s son Zebadiah became the commander after Asahel [was killed].
8 Wachisanu pa mwezi wachisanu anali Samihuti, mdzukulu wa Izira. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
The commander for the following/fifth month was Shamhuth, a descendant of Izrah.
9 Wa 6 pa mwezi wa 6 anali Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
The commander for the following/sixth month was Ira the son of Ikkesh from Tekoa [town].
10 Wa 7 pa mwezi wa 7 anali Helezi Mpeloni wa fuko la Efereimu. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
The commander for the following/seventh month was Helez, a member of the Pelon [clan] from the tribe of Ephraim.
11 Wa 8 pa mwezi wa 8 anali Sibekai Mhusati, wa mbumba ya Zera. Pa gulu lake panali asilikali 24,000
The commander for the following/eighth month was Sibbecai, a descendant of Zerah from Hushah [town].
12 Wa 9 pa mwezi wa 9 anali Abiezeri wa banja la Anatoti, wa fuko la Benjamini. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
The commander for the following/ninth month was Abiezer from Anathoth [city] in the tribe of Benjamin.
13 Wa khumi pa mwezi wa khumi anali Mahazayi wa ku Netofa, wa mbumba ya Zera. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
The commander for the following/tenth month was Maharai, a descendant of Zerah from Netophath [town].
14 Mtsogoleri wa 11, pa mwezi wa 11 anali Benaya wa ku Piratoni, wa fuko la Efereimu. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
The commander for the following/eleventh month was Benaiah from Pirathon [town] in the tribe of Ephraim.
15 Mtsogoleri wa 12, pa mwezi wa 12 anali Helidai Mnetofa, wa banja la Otanieli. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
The commander for the last month [of each year] was Heldai, a descendant of Othniel from Netophath [town].
16 Akuluakulu amene amatsogolera mafuko a Israeli ndi awa: Mtsogoleri wa fuko la Rubeni: Eliezara mwana wa Zikiri; mtsogoleri wa fuko la Simeoni: Sefatiya mwana wa Maaka;
This is a list of the administrators of the [twelve] tribes [DOU] of Israel: Eliezer, the son of Zicri, was the administrator of the tribe of Reuben. Shephatiah, the son of Maacah, was the administrator of the tribe of Simeon.
17 mtsogoleri wa fuko la Levi: Hasabiya mwana wa Kemueli, mtsogoleri wa banja la Aaroni: Zadoki;
Hashabiah, the son of Kemuel, was the administrator of the tribe of Levi. Zadok was the administrator of the tribe of Aaron.
18 mtsogoleri wa fuko la Yuda: Elihu, mʼbale wake wa Davide; mtsogoleri wa fuko la Isakara: Omuri mwana wa Mikayeli;
Elihu, David’s [older] brother, was the administrator of the tribe of Judah. Omri, the son of Michael, was the administrator of the tribe of Issachar.
19 mtsogoleri wa fuko la Zebuloni: Isimaiya mwana wa Obadiya; mtsogoleri wa fuko la Nafutali: Yerimoti mwana wa Azirieli;
Ishmaiah, the son of Obadiah, was the administrator of the tribe of Zebulun. Jerimoth, the son of Azriel, was the administrator of the tribe of Naphtali.
20 mtsogoleri wa fuko la Efereimu: Hoseya mwana wa Azaziya; mtsogoleri wa fuko la theka la Manase: Yoweli mwana wa Pedaya;
Hoshea, the son of Azaziah, was the administrator of the tribe of Ephraim. Joel, the son of Pedaiah, was the administrator of the tribe of the [western] half of the tribe of Manasseh.
21 mtsogoleri wa fuko la theka la Manase limene linali ku Giliyadi: Ido mwana wa Zekariya; mtsogoleri wa fuko la Benjamini: Yaasieli mwana wa Abineri;
Iddo, the son of Zechariah, was the administrator of the [eastern] half of the tribe of Manasseh, in [the] Gilead [region]. Jaasiel, the son of Abner, was the administrator of the tribe of Benjamin.
22 mtsogoleri wa fuko la Dani: Azareli mwana wa Yerohamu. Awa anali akuluakulu a mafuko a Israeli.
Azarel, the son of Jeroham, was the administrator of the tribe of Dan. Those were the leaders over the tribes of Israel.
23 Davide sanawerenge amuna amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kucheperapo, chifukwa Yehova analonjeza kuti adzachulukitsa Aisraeli ngati nyenyezi zamumlengalenga.
[When] David [told Joab to count the men of Israel, he] did not [tell him to] count the men who were less then 20 years old, because Yahweh had promised [many years previously] that there would be as many [people] in Israel as there are stars in the sky.
24 Yowabu mwana wa Zeruya anayamba kuwerenga amuna koma sanamalize. Mkwiyo unagwera Aisraeli chifukwa cha zimenezi ndipo chiwerengerochi sanachilowetse mʼbuku la mbiri ya mfumu Davide.
Joab [and his helpers] started to count the men of Israel, but they did not finish counting them [because Joab knew that Yahweh was angry about their being counted]. Yahweh punished [MTY] the people of Israel because of this counting, and as a result the total number of Israeli men [able to serve in the army] was not written on the scroll about King David’s [rule].
25 Azimaveti mwana wa Adieli ankayangʼanira nyumba zosungiramo katundu wa mfumu. Yonatani mwana wa Uziya ankayangʼanira nyumba zosungiramo katundu wa maboma ozungulira, mizinda, midzi ndi malo olondera.
Azmaveth, the son of Adiel, was in charge of the king’s storehouses. Jonathan, the son of Uzziah, was is charge of the storehouses in various towns and villages in Israel, and also in charge of the watchtowers.
26 Eziri mwana wa Kelubi ankayangʼanira anthu ogwira ntchito yolima ku munda.
Ezri the son of Kelub was in charge of the workers who farmed the land [that belonged to the king].
27 Simei wa ku Rama ankayangʼanira minda ya mpesa. Zabidi wa ku Sifamu ankayangʼanira mphesa ndi mosungiramo mwake.
Shimei from Ramath [town] was in charge of the king’s vineyards. Zabdi from Shepham [town] was in charge of storing the wine from the [grapes produced in] vineyards.
28 Baala-Hanani wa ku Gederi ankayangʼanira mitengo ya olivi ndi ya mikuyu ya ku Sefela. Yowasi ankayangʼanira mafuta a Olivi.
Baal-Hanan from Geder [city] was in charge of storing the olive oil.
29 Sitirayi wa ku Saroni ankayangʼanira ziweto zimene amaweta ku Saroni. Safati mwana wa Adilayi ankayangʼanira ngʼombe zakuzigwa.
Shitrai from the Sharon Plain was in charge of the herds of cattle that (grazed/ate grass) there. Shaphat the son of Adlai was in charge of the cattle in the valleys.
30 Obili Mwismaeli ankayangʼanira ngamira. Yehideya Mmerenoti ankayangʼanira abulu.
Obil, a descendant of Ishmael, was in charge of the camels. Jehdeiah from Meronoth [town] was in charge of the donkeys.
31 Yazizi Mhagiri akayangʼanira nkhosa ndi mbuzi. Onsewa anali akuluakulu oyangʼanira chuma cha mfumu Davide.
Jaziz, a descendant of Hagar, was in charge of the [king’s] flocks of sheep. All of those officials were in charge of the things that belonged to King David.
32 Yonatani, malume wake wa Davide, anali phungu wake ndipo anali munthu wanzeru komanso analinso mlembi. Yehieli mwana wa Hakimoni ankasamalira ana a mfumu.
David’s uncle Jonathan was a wise counselor for him. Jehiel, the son of Hacmoni, taught the king’s sons.
33 Ahitofele anali phungu wa mfumu. Husai Mwariki anali bwenzi la mfumu.
Ahithophel was the king’s official counselor.
34 Ahitofele atamwalira mʼmalo mwake munalowa Yehoyada mwana wa Benaya ndi Abiatara. Yowabu anali mtsogoleri wa gulu lankhondo la mfumu.
Hushai from the Ark people-group was the king’s special friend. Benaiah’s son Jehoiada became the king’s advisor after Ahithophel died, and later Abiathar became his advisor. Joab was the chief commander of the army.

< 1 Mbiri 27 >