< 1 Mbiri 22 >

1 Ndipo Davide anati, “Nyumba ya Yehova Mulungu idzakhala pano, ndiponso guwa lansembe zopsereza za Israeli.”
Then David said, This is the house of Jehovah God, and this is the altar of burnt offering for Israel.
2 Choncho Davide analamula kuti asonkhanitse alendo onse amene amakhala mu Israeli ndipo kuchokera pakati pawo anasankha amisiri a miyala kuti aseme miyala yomangira nyumba ya Mulungu.
And David commanded to gather together the sojourners that were in the land of Israel. And he set masons to hew wrought stones to build the house of God.
3 Ndipo anapereka zitsulo zambiri zopangira misomali ya zitseko za pa zipata ndi zolumikiza zake. Anaperekanso mkuwa wochuluka wokanika kuwuyeza.
And David prepared iron in abundance for the nails for the doors of the gates, and for the couplings, and brass in abundance without weight,
4 Iye anaperekanso mitengo yambiri ya mkungudza, yosawerengeka, pakuti anthu a ku Sidoni ndi a ku Turo anabweretsa yambiri kwa Davide.
and cedar trees without number. For the Sidonians and those of Tyre brought cedar trees in abundance to David.
5 Davide anati, “Mwana wanga Solomoni ndi wamngʼono ndipo sadziwa zambiri. Koma nyumba yomwe timangire Yehova iyenera kukhala yaulemerero, yotchuka ndi yokongola pamaso pa anthu a mitundu yonse. Choncho ndikonzekeratu zambiri.” Motero Davide anayikonzekera kwambiri asanamwalire.
And David said, Solomon my son is young and tender, and the house that is to be built for Jehovah must be exceedingly magnificent, of fame and of glory throughout all countries. I will therefore make preparation for it. So David prepared abundantly before his death.
6 Tsono iye anayitana Solomoni mwana wake ndipo anamulamula kuti adzamangire nyumba Yehova Mulungu wa Israeli.
Then he called for Solomon his son, and charged him to build a house for Jehovah, the God of Israel.
7 Davide anati kwa Solomoni, “Mwana wanga, ine ndinali ndi maganizo oti ndimangire nyumba Dzina la Yehova Mulungu wanga.
And David said to Solomon his son, As for me, it was in my heart to build a house to the name of Jehovah my God.
8 Koma Yehova anandiyankhula kuti, ‘Iwe wapha anthu ambiri ndiponso wachita nkhondo zambiri. Sumangira dzina langa nyumba chifukwa wapha anthu ambiri pa dziko lapansi pamaso panga.
But the word of Jehovah came to me, saying, Thou have shed blood abundantly, and have made great wars. Thou shall not build a house to my name because thou have shed much blood upon the earth in my sight.
9 Koma udzabala mwana wamwamuna amene adzakhala munthu wamtendere ndi wabata ndipo ndidzamupatsa mpumulo kuchokera kwa adani ake onse a mbali zonse. Dzina lake adzatchedwa Solomoni ndipo Ine ndidzapereka mtendere ndi bata kwa Israeli pa nthawi ya ulamuliro wake.
Behold, a son shall be born to thee, who shall be a man of rest. And I will give him rest from all his enemies round about, for his name shall be Solomon. And I will give peace and quietness to Israel in his days.
10 Iye ndiye adzandimangire nyumba. Adzakhala mwana wanga ndipo Ine ndidzakhala abambo ake. Ndipo ndidzakhazikitsa mpando wake waufumu mʼdziko la Israeli mpaka muyaya.’”
He shall build a house for my name. And he shall be my son, and I will be his father, and I will establish the throne of his kingdom over Israel forever.
11 “Tsopano mwana wanga, Yehova akhale nawe ndipo upambane ndi kumanga Nyumba ya Yehova Mulungu wako, monga momwe Iye ananenera kuti udzatero.
Now, my son, Jehovah be with thee, and prosper thou, and build the house of Jehovah thy God as he has spoken concerning thee.
12 Yehova akupatse nzeru ndi kumvetsetsa pamene Iye adzakuyika kukhala wolamulira Israeli, kuti udzasunge malamulo a Yehova Mulungu wako.
Only Jehovah give thee discretion and understanding, and give thee charge concerning Israel, so that thou may keep the law of Jehovah thy God.
13 Ndipo udzapambana ngati udzamvera mosamala malangizo ndi malamulo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli kudzera mwa Mose. Khala wamphamvu ndi wolimba mtima. Usachite mantha kapena kutaya mtima.
Then thou shall prosper, if thou observe to do the statutes and the ordinances which Jehovah charged Moses with concerning Israel. Be strong, and of good courage. Fear not, neither be dismayed.
14 “Ine movutikira kwambiri ndapereka ku Nyumba ya Mulungu matani 3,400 agolide, matani 34,000 asiliva, ndiponso mkuwa ndi chitsulo, matabwa ndi miyala. Ndipo iwe utha kuwonjezerapo pa zimenezi.
Now, behold, in my affliction I have prepared for the house of Jehovah a hundred thousand talents of gold, and a million talents of silver, and of brass and iron without weight, for it is in abundance. Also I have prepared timber and stone, and thou may add thereto.
15 Iwe uli ndi antchito ambiri: osema miyala, amisiri a miyala, ndi amisiri a matabwa, komanso anthu ambiri aluso la ntchito zosiyanasiyana,
Moreover there are workmen with thee in abundance, hewers and workers of stone and timber, and all men who are skilful in every manner of work.
16 zagolide ndi zasiliva, zamkuwa, zazitsulo, amisiri osawerengeka. Tsopano yamba ntchito, ndipo Yehova akhale nawe.”
Of the gold, the silver, and the brass, and the iron, there is no number. Arise and be doing, and Jehovah be with thee.
17 Tsono Davide analamula atsogoleri onse a Israeli kuti athandize Solomoni mwana wake.
David also commanded all the rulers of Israel to help Solomon his son, saying,
18 Iye anawawuza kuti, “Kodi Yehova Mulungu, sali nanu? Ndipo Iye siwakupatsani mpumulo mbali zonse? Pakuti Iyeyo wapereka eni nthaka kwa inu ndipo dziko lili pa ulamuliro wa Yehova ndi anthu ake.
Is not Jehovah your God with you? And has he not given you rest on every side? For he has delivered the inhabitants of the land into my hand, and the land is subdued before Jehovah, and before his people.
19 Tsono perekani mtima wanu ndi moyo wanu kufunafuna Yehova Mulungu wanu. Yambani kumanga malo opatulika a Yehova Mulungu, kuti mubweretse Bokosi la Chipangano la Yehova ndi zinthu zopatulika za Mulungu mʼNyumba ya Mulungu imene idzamangidwa chifukwa cha dzina la Yehova.”
Now set your heart and your soul to seek after Jehovah your God. Arise therefore, and build ye the sanctuary of Jehovah God, to bring the ark of the covenant of Jehovah, and the holy vessels of God, into the house that is to be built to the name of Jehovah.

< 1 Mbiri 22 >