< 1 Mbiri 2 >

1 Ana a Israeli anali awa: Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, Zebuloni,
These are the sons of Israel: Reuben, Simeon, Levi, Judah, Issachar, Zebulun,
2 Dani, Yosefe, Benjamini, Nafutali, Gadi ndi Aseri.
Dan, Joseph, Benjamin, Naphtali, Gad, and Asher.
3 Ana a Yuda anali awa: Eri, Onani ndi Sela. Ana atatu awa anabereka ndi mkazi wa Chikanaani, Batisuwa. Eri, mwana woyamba wa Yuda anali woyipa kwambiri pamaso pa Yehova, kotero Yehova anamupha.
The sons of Judah: Er, Onan, and Shelah, which three were born to him of Shua’s daughter the Canaanitess. Er, Judah’s firstborn, was wicked in Yahweh’s sight; and he killed him.
4 Mpongozi wake Tamara anamuberekera Perezi ndi Zera. Ana onse a Yuda analipo asanu.
Tamar his daughter-in-law bore him Perez and Zerah. All the sons of Judah were five.
5 Ana a Perezi anali awa: Hezironi ndi Hamuli.
The sons of Perez: Hezron and Hamul.
6 Ana a Zera anali awa: Zimuri, Etani, Hemani, Kalikoli ndi Dara. Onse analipo asanu.
The sons of Zerah: Zimri, Ethan, Heman, Calcol, and Dara—five of them in all.
7 Mwana wa Karimi anali Akani, amene anabweretsa mavuto pakati pa Israeli pamene anatenga zinthu zoyenera kuwonongedwa.
The son of Carmi: Achar, the troubler of Israel, who committed a trespass in the devoted thing.
8 Mwana wa Etani anali Azariya.
The son of Ethan: Azariah.
9 Ana amene anabadwa kwa Hezironi anali: Yerahimeeli, Ramu ndi Kelubai.
The sons also of Hezron, who were born to him: Jerahmeel, Ram, and Chelubai.
10 Ramu anabereka Aminadabu ndipo Aminadabu anali abambo ake a Naasoni, mtsogoleri wa fuko la Yuda.
Ram became the father of Amminadab, and Amminadab became the father of Nahshon, prince of the children of Judah;
11 Naasoni anabereka Salima, Salima anabereka Bowazi,
and Nahshon became the father of Salma, and Salma became the father of Boaz,
12 Bowazi anabereka Obedi ndipo Obedi anabereka Yese.
and Boaz became the father of Obed, and Obed became the father of Jesse;
13 Yese anabereka Eliabu mwana wake woyamba, wachiwiri Abinadabu, wachitatu Simea,
and Jesse became the father of his firstborn Eliab, Abinadab the second, Shimea the third,
14 wachinayi Netaneli, wachisanu Radai,
Nethanel the fourth, Raddai the fifth,
15 wachisanu ndi chimodzi Ozemu ndi wachisanu ndi chiwiri Davide.
Ozem the sixth, and David the seventh;
16 Alongo awo anali Zeruya ndi Abigayeli. Ana atatu a Zeruya anali Abisai Yowabu ndi Asaheli.
and their sisters were Zeruiah and Abigail. The sons of Zeruiah: Abishai, Joab, and Asahel, three.
17 Abigayeli anali amayi ake a Amasa amene abambo ake anali Yeteri wa fuko la Ismaeli.
Abigail bore Amasa; and the father of Amasa was Jether the Ishmaelite.
18 Kalebe mwana wa Hezironi anabereka ana mwa Azuba mkazi wake (ndi mwa Yerioti). Ana a mkaziyo anali awa: Yeseri, Sobabu ndi Aridoni.
Caleb the son of Hezron became the father of children by Azubah his wife, and by Jerioth; and these were her sons: Jesher, Shobab, and Ardon.
19 Azuba atamwalira, Kalebe anakwatira Efurata, amene anamuberekera Huri.
Azubah died, and Caleb married Ephrath, who bore him Hur.
20 Huri anabereka Uri ndipo Uri anabereka Bezaleli.
Hur became the father of Uri, and Uri became the father of Bezalel.
21 Patapita nthawi, Hezironi anagona ndi mwana wamkazi wa Makiri abambo ake a Giliyadi (iye anamukwatira ali ndi zaka 60) ndipo anamuberekera Segubu.
Afterward Hezron went in to the daughter of Machir the father of Gilead, whom he took as wife when he was sixty years old; and she bore him Segub.
22 Segubu anabereka Yairi, amene anali ndi mizinda 23 ku Giliyadi.
Segub became the father of Jair, who had twenty-three cities in the land of Gilead.
23 (Koma Gesuri ndi Aramu analanda Havoti Yairi komanso Kenati ndi madera ake onse ozungulira, mizinda makumi asanu ndi umodzi). Onsewa anali adzukulu, a Makiri abambo ake a Giliyadi.
Geshur and Aram took the towns of Jair from them, with Kenath, and its villages, even sixty cities. All these were the sons of Machir the father of Gilead.
24 Atamwalira Hezironi ku Kalebe Efurata, Abiya mkazi wa Hezironi anamuberekera Asihuri abambo a Tekowa.
After Hezron died in Caleb Ephrathah, Abijah, Hezron’s wife, bore him Ashhur the father of Tekoa.
25 Ana a Yerahimeeli, mwana woyamba wa Hezironi anali: Ramu, mwana wake woyamba, Buna, Oreni, Ozemu ndi Ahiya.
The sons of Jerahmeel the firstborn of Hezron were Ram the firstborn, Bunah, Oren, Ozem, and Ahijah.
26 Yerahimeeli anali ndi mkazi wina amene dzina lake linali Atara, amene anali amayi a Onamu.
Jerahmeel had another wife, whose name was Atarah. She was the mother of Onam.
27 Ana a Ramu, mwana woyamba wa Yerahimeeli, anali awa: Maazi, Yamini ndi Ekeri.
The sons of Ram the firstborn of Jerahmeel were Maaz, Jamin, and Eker.
28 Ana a Onamu anali awa: Shamai ndi Yada. Ana a Shamai anali awa: Nadabu ndi Abisuri.
The sons of Onam were Shammai and Jada. The sons of Shammai: Nadab and Abishur.
29 Mkazi wa Abisuri anali Abihaili, amene anamuberekera Ahibani ndi Molidi.
The name of the wife of Abishur was Abihail; and she bore him Ahban and Molid.
30 Ana a Nadabu anali awa: Seledi ndi Apaimu. Koma Seledi anamwalira wopanda ana.
The sons of Nadab: Seled and Appaim; but Seled died without children.
31 Ana a Apaimu anali awa: Isi, amene anabereka Sesani. Sesani anabereka Ahilai.
The son of Appaim: Ishi. The son of Ishi: Sheshan. The son of Sheshan: Ahlai.
32 Ana a Yada, mʼbale wa Samai, anali awa: Yereri ndi Yonatani. Koma Yeteri anamwalira wopanda ana.
The sons of Jada the brother of Shammai: Jether and Jonathan; and Jether died without children.
33 Ana a Yonatani anali awa: Peleti ndi Zaza. Amenewa anali adzukulu a Yerahimeeli.
The sons of Jonathan: Peleth and Zaza. These were the sons of Jerahmeel.
34 Sesani sanabereke ana aamuna koma aakazi okhaokha. Iye anali ndi wantchito wa ku Igupto, dzina lake Yariha.
Now Sheshan had no sons, but only daughters. Sheshan had a servant, an Egyptian, whose name was Jarha.
35 Sesani anapereka mwana wake wamkazi kwa Yariha wantchito wake kuti amukwatire ndipo anamuberekera Atayi.
Sheshan gave his daughter to Jarha his servant as wife; and she bore him Attai.
36 Atayi anali abambo ake a Natani, Natani anali abambo ake a Zabadi,
Attai became the father of Nathan, and Nathan became the father of Zabad,
37 Zabadi anali abambo a Efilali, Efilali anali abambo a Obedi,
and Zabad became the father of Ephlal, and Ephlal became the father of Obed,
38 Obedi anali abambo a Yehu, Yehu anali abambo a Azariya,
and Obed became the father of Jehu, and Jehu became the father of Azariah,
39 Azariya anali abambo a Helezi, Helezi anali abambo a Eleasa,
and Azariah became the father of Helez, and Helez became the father of Eleasah,
40 Eleasa anali abambo ake a Sisimai, Sisimai anali abambo a Salumu,
and Eleasah became the father of Sismai, and Sismai became the father of Shallum,
41 Salumu anali abambo a Yekamiya, Yekamiya anali abambo a Elisama.
and Shallum became the father of Jekamiah, and Jekamiah became the father of Elishama.
42 Ana a Kalebe mʼbale wa Yerahimeeli anali awa: Mesa mwana wachisamba, anali abambo a Zifi, ndipo mwana wake Maresa anali abambo a Hebroni.
The sons of Caleb the brother of Jerahmeel were Mesha his firstborn, who was the father of Ziph, and the sons of Mareshah the father of Hebron.
43 Ana a Hebroni anali awa: Kora, Tapuwa, Rekemu ndi Sema.
The sons of Hebron: Korah, Tappuah, Rekem, and Shema.
44 Sema anali abambo ake Rahamu ndipo Rahamu anali abambo a Yorikeamu. Rekemu anali abambo a Samai.
Shema became the father of Raham, the father of Jorkeam; and Rekem became the father of Shammai.
45 Mwana wa Samai anali Maoni, ndipo Maoni anali abambo a Beti Zuri.
The son of Shammai was Maon; and Maon was the father of Beth Zur.
46 Efai, mzikazi wa Kalebe, anali amayi a Harani, Moza ndi Gazezi. Harani anali abambo a Gazezi.
Ephah, Caleb’s concubine, bore Haran, Moza, and Gazez; and Haran became the father of Gazez.
47 Ana a Yahidai anali awa: Regemu, Yotamu, Gesani, Peleti, Efai ndi Saafi.
The sons of Jahdai: Regem, Jothan, Geshan, Pelet, Ephah, and Shaaph.
48 Maaka mzikazi wa Kalebe anali mayi Seberi ndi Tirihana.
Maacah, Caleb’s concubine, bore Sheber and Tirhanah.
49 Iye anaberekanso Saafi abambo a Madimena ndi Seva abambo a Makibena ndi Gibeya. Mwana wamkazi wa Kalebe anali Akisa.
She bore also Shaaph the father of Madmannah, Sheva the father of Machbena and the father of Gibea; and the daughter of Caleb was Achsah.
50 Izi zinali zidzukulu za Kalebe. Ana a Huri mwana wachisamba wa Efurata anali awa: Sobala abambo a Kiriati Yearimu,
These were the sons of Caleb, the son of Hur, the firstborn of Ephrathah: Shobal the father of Kiriath Jearim,
51 Salima abambo a Betelehemu ndi Harefu abambo ake a Beti-Gadera.
Salma the father of Bethlehem, and Hareph the father of Beth Gader.
52 Zidzukulu za Sobala abambo a Kiriati Yearimu zinali izi: Harowe, theka la banja la Manahati,
Shobal the father of Kiriath Jearim had sons: Haroeh, half of the Menuhoth.
53 ndipo mabanja a Kiriati-Yeyarimu anali awa: Aitiri, Aputi, Asumati ndi Amisirai. Azorati ndi Aesitaoli anachokera kwa amenewa.
The families of Kiriath Jearim: the Ithrites, the Puthites, the Shumathites, and the Mishraites; from them came the Zorathites and the Eshtaolites.
54 Zidzukulu za Salima zinali izi: Betelehemu, Anetofati, Atiroti-Beti-Yowabu, theka la banja la Manahati, Azori,
The sons of Salma: Bethlehem, the Netophathites, Atroth Beth Joab, and half of the Manahathites, the Zorites.
55 ndiponso mabanja a alembi amene amakhala ku Yabesi: Atiroti, Asimeati ndiponso Asukati. Awa ndi Akeni amene anachokera kwa Hamati, kholo la Arekabu.
The families of scribes who lived at Jabez: the Tirathites, the Shimeathites, and the Sucathites. These are the Kenites who came from Hammath, the father of the house of Rechab.

< 1 Mbiri 2 >