< 1 Mbiri 12 >

1 Nawa anthu amene anabwera kwa Davide ali ku Zikilagi pamene iye anathamangitsidwa ndi Sauli mwana wa Kisi (iwowo anali mʼgulu la asilikali amene ankamuthandiza pa nkhondo.
Now these are they that came to David to Ziklag, while he was yet shut up because of Saul the son of Kish; and they were among the mighty men, his helpers in war.
2 Iwo anali ndi mauta ndipo amadziwa kuponya mivi komanso miyala, ndipo amatha kuponyera dzanja lamanja kapena lamanzere. Iwo anali abale ake a Sauli ochokera ku fuko la Benjamini.
They were armed with bows, and could use both the right hand and the left in slinging stones and in shooting arrows from the bow; they were of Saul's brethren of Benjamin.
3 Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri ndi Yowasi ana a Semaya wa ku Gibeya; Yezieli ndi Peleti ana a Azimaveti; Beraka, Yehu wa ku Anatoti,
The chief was Ahiezer, then Joash, the sons of Shemaah the Gibeathite; and Jeziel, and Pelet, the sons of Azmaveth; and Beracah, and Jehu the Anathothite;
4 ndi Isimaiya wa ku Gibiyoni, munthu wamphamvu mʼgulu la anthu makumi atatu aja, yemwenso anali mtsogoleri wawo; Yeremiya, Yahazieli, Yohanani, Yozabadi wa ku Gederi,
and Ishmaiah the Gibeonite, a mighty man among the thirty, and over the thirty; and Jeremiah, and Jahaziel, and Johanan, and Jozabad the Gederathite;
5 Eluzai, Yerimoti, Bealiya, Semariya ndi Sefatiya Mharufi;
Eluzai, and Jerimoth, and Bealiah, and Shemariah, and Shephatiah the Hariphite;
6 Elikana, Isiya, Azareli, Yowezeri ndi Yasobeamu a ku banja la Kora;
Elkanah, and Isshiah, and Azarel, and Joezer, and Jashobeam, the Korahites;
7 ndi Yowela ndi Zebadiya ana a Yerohamu wa ku Gedori.
and Joelah, and Zebadiah, the sons of Jeroham of the troop.
8 Asilikali ena a fuko la Gadi anathawira kwa Davide ku linga lake ku chipululu. Iwo anali asilikali olimba mtima, okonzekera nkhondo ndipo amadziwa kugwiritsa ntchito chishango ndi mkondo. Iwowo anali woopsa ngati mikango ndipo anali aliwiro ngati ngoma zamʼmapiri.
And of the Gadites there separated themselves unto David to the stronghold in the wilderness, mighty men of valour, men trained for war, that could handle shield and spear; whose faces were like the faces of lions, and they were as swift as the roes upon the mountains;
9 Mtsogoleri wawo anali Ezeri, wotsatana naye anali Obadiya, wachitatu anali Eliabu,
Ezer the chief, Obadiah the second, Eliab the third;
10 wachinayi anali Misimana, Yeremiya anali wachisanu,
Mashmannah the fourth, Jeremiah the fifth;
11 wachisanu ndi chimodzi anali Atai, Elieli anali wachisanu ndi chiwiri,
Attai the sixth, Eliel the seventh;
12 wachisanu ndi chitatu anali Yohanani, Elizabadi anali wachisanu ndi chinayi,
Johanan the eighth, Elzabad the ninth;
13 wakhumi anali Yeremiya ndipo Makibanai anali wa 11.
Jeremiah the tenth, Machbannai the eleventh.
14 Anthu a fuko la Gadi amenewa anali atsogoleri; angʼonoangʼono amalamulira anthu 100 pamene akuluakulu amalamulira anthu 1,000.
These of the sons of Gad were captains of the host; he that was least was equal to a hundred, and the greatest to a thousand.
15 Awa ndi amene anawoloka Yorodani mwezi woyamba pamene mtsinje unali utasefukira mbali zonse, ndipo anathamangitsa aliyense amene amakhala mʼchigwa, mbali ya kumadzulo ndi kummawa.
These are they that went over the Jordan in the first month, when it had overflown all its banks; and they put to flight all them of the valleys, both toward the east, and toward the west.
16 Anthu ena a fuko la Benjamini ndi ena ochokera ku Yuda anabweranso kwa Davide pamene anali ku linga lake.
And there came of the children of Benjamin and Judah to the stronghold unto David.
17 Davide anapita kukakumana nawo ndipo anati, “Ngati mwabwera kwa ine mwamtendere, kuti mundithandize, ndakonzeka kugwirizana nanu. Koma ngati mwabwera kudzandipereka kwa adani anga, ngakhale kuti sindinalakwe, Mulungu wa makolo anthu aone izi ndipo akuweruzeni.”
And David went out to meet them, and answered and said unto them: 'If ye be come peaceably unto me to help me, my heart shall be knit unto you; but if ye be come to betray me to mine adversaries, seeing there is no wrong in my hands, the God of our fathers look thereon, and give judgment.'
18 Kenaka Mzimu anabwera pa Amasai, mtsogoleri wa anthu makumi atatu aja ndipo anati: “Inu Davide, ife ndife anu! Tili nanu limodzi, inu mwana wa Yese! Kupambana, Kupambana kwa inu, ndiponso kupambana kukhale kwa iwo amene akukuthandizani pakuti Mulungu wanu adzakuthandizani.” Kotero Davide anawalandira ndipo anawayika kukhala atsogoleri a magulu ake a ankhondo.
Then the spirit clothed Amasai, who was chief of the captains: Thine are we, David, and on thy side, thou son of Jesse; peace, peace be unto thee, and peace be to thy helpers; for thy God helpeth thee. Then David received them, and made them captains of the band.
19 Anthu ena a fuko la Manase anathawira kwa Davide pamene anapita ndi Afilisti kukamenyana ndi Sauli. (Iye ndi anthu ake sanathandize Afilisti chifukwa, atsogoleri awo atakambirana, anamubweza Davide. Iwo anati, “Ife tidzawonongedwa ngati uyu adzabwerera kwa mbuye wake Sauli).”
Of Manasseh also there fell away some to David, when he came with the Philistines against Saul to battle, but they helped them not; for the lords of the Philistines upon advisement sent him away, saying: 'He will fall away to his master Saul to the jeopardy of our heads.'
20 Davide atapita ku Zikilagi, anthu a fuko la Manase amene anathawira kwa iye anali awa: Adina, Yozabadi, Yediaeli, Mikayeli, Yozabadi, Elihu ndi Ziletai; atsogoleri a magulu a anthu 1,000 a ku Manase.
As he went to Ziklag, there fell to him of Manasseh, Adnah, and Jozabad, and Jediael, and Michael, and Jozabad, and Elihu, and Zillethai, captains of thousands that were of Manasseh.
21 Iwowa anathandiza Davide kulimbana ndi magulu achifwamba, pakuti onsewa anali asilikali olimba mtima ndipo anali atsogoleri mʼgulu lake la ankhondo.
And they helped David against the troop, for they were all mighty men of valour, and were captains in the host.
22 Tsiku ndi tsiku anthu amabwera kudzathandiza Davide, mpaka anakhala ndi gulu lalikulu la ankhondo, ngati gulu la ankhondo a Mulungu.
For from day to day men came to David to help him, until there was a great host, like the host of God.
23 Nachi chiwerengero cha magulu a anthu ankhondo amene anabwera kwa Davide ku Hebroni kudzapereka ufumu wa Sauli kwa iye, monga momwe ananenera Yehova:
And these are the numbers of the heads of them that were armed for war, who came to David to Hebron, to turn the kingdom of Saul to him, according to the word of the LORD.
24 Anthu a fuko la Yuda onyamula chishango ndi mkondo analipo 6,800;
The children of Judah that bore shield and spear were six thousand and eight hundred, armed for war.
25 Anthu a fuko la Simeoni, asilikali okonzekera nkhondo analipo 7,100;
Of the children of Simeon, mighty men of valour for the war, seven thousand and one hundred.
26 Anthu a fuko la Levi analipo 4,600,
Of the children of Levi four thousand and six hundred.
27 mtsogoleri Yehoyada wa banja la Aaroni anabweranso ndi anthu 3,700,
And Jehoiada was the leader of the house of Aaron, and with him were three thousand and seven hundred;
28 ndi Zadoki, mnyamata wankhondo wolimba mtima, anabwera ndi akuluakulu 22 ochokera mʼbanja lake;
and Zadok, a young man mighty of valour, and of his father's house twenty and two captains.
29 Anthu a fuko la Benjamini, abale ake a Sauli analipo 3,000 ndipo ambiri anali ndi Sauli ku nyumba yake pa nthawiyi;
And of the children of Benjamin, the brethren of Saul, three thousand; for hitherto the greatest part of them had kept their allegiance to the house of Saul.
30 Anthu a fuko la Efereimu, asilikali olimba mtima, otchuka pa mabanja awo analipo 20,800;
And of the children of Ephraim twenty thousand and eight hundred, mighty men of valour, famous men in their fathers' houses.
31 Anthu a fuko latheka la Manase amene anawayitana kuti adzakhazikitse nawo ufumu wa Davide analipo 18,000;
And of the half-tribe of Manasseh eighteen thousand, who were mentioned by name, to come and make David king.
32 Anthu a fuko la Isakara amene ankazindikira nthawi ndipo amadziwa zimene Israeli ankayenera kuchita, analipo atsogoleri 200 pamodzi ndi abale awo onse amene amawatsogolera.
And of the children of Issachar, men that had understanding of the times, to know what Israel ought to do; the heads of them were two hundred; and all their brethren were at their commandment.
33 Anthu a fuko la Zebuloni, analipo 5,000. Iwowa anali asilikali odziwa bwino nkhondo, okhala ndi zida za mtundu uliwonse, okonzekera kudzathandiza Davide ndi mtima umodzi.
Of Zebulun, such as were able to go out in the host, that could set the battle in array, with all manner of instruments of war, fifty thousand; and that could order the battle array, and were not of double heart.
34 Anthu a fuko la Nafutali, analipo atsogoleri 1,000 pamodzi ndi anthu 37,000 onyamula zishango ndi mikondo;
And of Naphtali a thousand captains, and with them with shield and spear thirty and seven thousand.
35 Anthu a fuko la Dani, okonzekera nkhondo analipo 28,600.
And of the Danites that could set the battle in array, twenty and eight thousand and six hundred.
36 Anthu a fuko la Aseri, asilikali odziwa bwino nkhondo, okonzekeradi nkhondo analipo 40,000;
And of Asher, such as were able to go out in the host, that could set the battle in array, forty thousand.
37 Ndipo kuchokera kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase, amene anali ndi zida za mtundu uliwonse analipo 120,000.
And on the other side of the Jordan, of the Reubenites, and the Gadites, and of the half-tribe of Manasseh, with all manner of instruments of war for the battle, a hundred and twenty thousand.
38 Onsewa anali anthu odziwa kumenya nkhondo amene anadzipereka ku magulu awo. Iwo anabwera ku Hebroni ali otsimikiza kudzamuyika Davide kukhala mfumu ya Aisraeli. Aisraeli ena onse anali ndi mtima umodzinso womuyika Davide kukhala mfumu.
All these, being men of war, that could order the battle array, came with a whole heart to Hebron, to make David king over all Israel; and all the rest also of Israel were of one heart to make David king.
39 Anthuwa anakhala ndi Davide masiku atatu akudya ndi kumwa pakuti mabanja awo anawapatsa zakudya.
And they were there with David three days, eating and drinking; for their brethren had made preparation for them.
40 Komanso anthu oyandikana nawo ochokera ku Isakara, Zebuloni ndi Nafutali anabweretsa zakudya pa abulu, ngamira, nyulu ndi ngʼombe. Panali ufa wambiri, makeke ankhuyu, ntchintchi za mphesa, vinyo, mafuta, ngʼombe, nkhosa ndi mbuzi, popeza munali chimwemwe mu Israeli.
Moreover they that were nigh unto them, even as far as Issachar and Zebulun and Naphtali, brought bread on asses, and on camels, and on mules, and on oxen, victual of meal, cakes of figs, and clusters of raisins, and wine, and oil, and oxen, and sheep in abundance; for there was joy in Israel.

< 1 Mbiri 12 >