< 1 Mbiri 11 >

1 Aisraeli onse anasonkhana pamaso pa Davide ku Hebroni ndipo anati, “Ife ndife abale anu.
Tout Israël s’assembla et vint auprès de David à Hébron, pour lui dire: "Nous sommes ta chair et ton sang.
2 Kale lija, ngakhale pamene Sauli anali mfumu, inu ndinu amene munkatsogolera Aisraeli pa nkhondo zawo. Ndipo Yehova Mulungu wanu anakuwuzani kuti, ‘Iwe udzaweta anthu anga Aisraeli, ndipo udzakhala mfumu yawo.’”
Déjà hier, déjà avant-hier, alors que Saül était roi, c’est toi qui dirigeais toutes les expéditions d’Israël. C’Est toi, t’avait dit l’Eternel, ton Dieu, qui gouverneras Israël, mon peuple, toi qui seras son chef."
3 Akuluakulu onse a Israeli atafika kwa Mfumu Davide ku Hebroni, iye anachita nawo pangano pamaso pa Yehova, ndipo anamudzoza Davide kukhala mfumu ya Israeli, monga momwe Yehova analonjezera kudzera mwa Samueli.
Tous les Anciens d’Israël vinrent donc trouver le roi à Hébron; le roi David fit un pacte avec eux à Hébron devant l’Eternel, et ils le sacrèrent comme roi d’Israël, selon la parole de l’Eternel à Samuel.
4 Davide ndi Aisraeli onse anapita ku Yerusalemu (ku Yebusi). Ayebusi amene ankakhala kumeneko
David et tous les Israélites marchèrent sur Jérusalem, qui s’appelait Jébus. Là étaient les Jébuséens, qui occupaient le pays.
5 anamuwuza Davide kuti, “Simulowa muno.” Komabe Davide analanda linga la Ziyoni, limene ndi mzinda wa Davide.
Mais ceux-ci dirent à David: "Tu n’entreras pas ici." Toutefois, David s’empara de la forteresse de Sion, qui est la Cité de David.
6 Davide anali atanena kuti “Aliyense amene adzatsogolere kukathira nkhondo Ayebusi adzakhala mkulu wa asilikali.” Yowabu mwana wa Zeruya ndiye anayamba kupita, motero anakhala mkulu wa asilikali.
David avait dit: "Celui qui battra les Jébuséens en premier deviendra chef et prince." Ce fut Joab, fils de Cerouya, qui monta le premier, et il devint chef.
7 Tsono Davide anakhazikika mu lingamo, ndipo mzindawu anawutcha Mzinda wa Davide.
David s’établit dans la forteresse, qu’on nomma pour cette raison Cité de David.
8 Iye anamanga malo onse ozungulira, kuyambira ku matsitso ozungulira khoma. Ndipo Yowabu anakonzanso mbali ina ya mzindawu.
Il ajouta des constructions à la ronde, sur le pourtour du Millo. Quant à Joab, il restaura le reste de la ville.
9 Ndipo mphamvu za Davide zinkakulirakulira chifukwa anali ndi Yehova Wamphamvuzonse.
David alla grandissant de plus en plus, assisté par l’Eternel-Cebaot.
10 Awa ndiye anali atsogoleri amphamvu a Davide. Iwo pamodzi ndi Aisraeli onse, anathandiza kulimbikitsa ufumu wake kuti ukwanire madera onse, monga momwe Yehova analonjezera.
Voici les chefs des vaillants guerriers de David, qui l’aidèrent, avec tout Israël, à conquérir le trône et le firent régner selon la parole de l’Eternel, adressée à Israël.
11 Nawa mayina a ankhondo amphamvu a Davide: Yasobeamu Mhakimoni anali mkulu wa atsogoleri. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300 nthawi imodzi.
Et voici la liste des vaillants guerriers de David: Yachobam, fils de Hakhmoni, chef de la garde. C’Est lui qui, en une seule rencontre, brandit la lance, faisant trois cents cadavres.
12 Wotsatana naye anali Eliezara mwana wa Dodo Mwahohi, mmodzi mwa ankhondo atatu amphamvu.
Après lui, Eléazar, fils de Dodo, l’Ahohite, l’un des trois héros,
13 Iye anali ndi Davide ku Pasi-Damimu pamene Afilisti anasonkhana kudzachita nkhondo. Ankhondo anathawa Afilistiwo pamalo pamene panali munda wodzaza ndi barele.
assista David à Pass-Dammim. Là s’étaient assemblés les Philistins pour la bataille. Il s’y trouvait une pièce de terre pleine d’orge, et le peuple fuyait devant les Philistins.
14 Koma awiriwo anayima pakati pa mundawo. Iwo anawuteteza, nakantha Afilistiwo ndipo Yehova anawapambanitsa koposa.
Mais lui prit position au milieu du champ, le défendit et battit les Philistins; le Seigneur opéra ainsi une grande délivrance.
15 Atatu mwa atsogoleri makumi atatu aja anabwera kwa Davide ku thanthwe ku phanga la Adulamu pamene gulu la Afilisti linali litamanga misasa mʼchigwa cha Refaimu.
Trois des trente chefs descendirent sur le roc auprès de David, du côté de la caverne d’Adoullam; un corps de Philistins se trouvait campé dans la vallée de Rephaïm.
16 Nthawi imeneyo Davide anali mu linga, ndipo boma la Afilisti linali ku Betelehemu.
David était alors dans la forteresse, et les Philistins avaient une garnison à Bethléem.
17 Davide analakalaka madzi ndipo anati, “Haa, pakanapezeka munthu wokanditungira madzi a mʼchitsime chomwe chili pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu!”
David eut un désir et dit: "Ah! si on pouvait me faire boire de l’eau de la citerne qui est à la porte de Bethléem!"
18 Choncho anthu atatuwa anadutsa mizere ya Afilisti, natunga madzi amene anali mʼchitsime chomwe chinali pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu nabwera nawo kwa Davide. Koma iye anakana kumwa. Mʼmalo mwake anathira pansi pamaso pa Yehova.
Les trois guerriers s’ouvrirent un passage par le camp des Philistins, puisèrent de l’eau à la citerne qui est à la porte de Bethléem et l’apportèrent à David; mais celui-ci ne voulut pas la boire et en fit une libation à l’Eternel,
19 Iye anati, “Inu Mulungu, musalole kuti ine ndichite chinthu ichi! Kodi ndimwe magazi a anthu amene anayika miyoyo yawo pachiswe?” Chifukwa iwo anayika miyoyo yawo pachiswe kuti abweretse madziwo, Davide sanamwe. Zimenezi ndi zimene anachita anthu amphamvu atatuwo.
en disant: "Mon Dieu me préserve de faire pareille chose! Boirais-je le sang de ces hommes qui ont risqué leur vie, car ils l’ont apportée au péril de leur vie!" Il refusa donc de boire. Voilà ce que firent ces trois guerriers.
20 Abisai mʼbale wa Yowabu ndiye anali mtsogoleri wa anthu atatuwa. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300. Choncho iyeyo anali wotchuka pakati pa anthu atatu aja.
Puis Abchaï, frère de Joab, le chef des trois: il brandit un jour sa lance sur trois cents ennemis qu’il immola, et se fit un nom parmi les Trois.
21 Iye analandira ulemu woposa atatuwo. Kotero anakhala mtsogoleri wawo ngakhale kuti iyeyo sanali mʼgulu la anthu atatu aja.
Il fut plus estimé que les Trente, de la deuxième série, car il devint leur chef, cependant il n’arriva pas jusqu’aux Trois.
22 Benaya mwana wa Yehoyada wa ku Kabizeeli anali munthu wolimba mtima amene anachita zinthu zamphamvu. Iye anakantha ankhondo awiri otchuka a ku Mowabu. Tsiku lina kukuzizira kwambiri, iye analowa mʼdzenje ndi kuphamo mkango.
Puis Benaïa, fils de Joïada, d’un vaillant aux nombreux exploits, originaire de Kabceël; ce fut lui qui triompha des deux Arïel de Moab; ce fut lui aussi qui descendit et tua un lion dans une fosse par un jour de neige.
23 Ndipo iye anakanthanso Mwigupto amene anali wotalika mamita awiri ndi theka. Ngakhale kuti Mwiguptoyo anali ndi mkondo wofanana ndi ndodo yowombera nsalu mʼdzanja mwake, Benaya anapita kukamenyana naye ali ndi chibonga chokha mʼmanja. Iye analanda mkondo mʼdzanja la Mwiguptoyo ndi kumupha ndi mkondo wake womwe.
Il tua aussi un Egyptien, homme de grande taille, haut de cinq coudées, et, dans la main de l’Egyptien, il y avait une lance, grande comme une ensouple de tisserand; il descendit vers lui avec un bâton, arracha la lance de la main de l’Egyptien et le tua avec sa lance.
24 Izi ndi zamphamvu zimene Benaya mwana wa Yehoyada anachita. Iyeyo analinso wotchuka ngati anthu atatu amphamvu aja.
Voilà ce que fit Benaïahou, fils de Joïada, renommé parmi les trois héros.
25 Iye ankalemekezedwa kuposa wina aliyense mwa anthu makumi atatu, koma sanali mʼgulu la anthu atatu aja. Ndipo Davide anamuyika kukhala woyangʼanira asilikali omuteteza.
Il fut plus estimé que les Trente, mais il n’arriva pas jusqu’aux Trois. David l’admit dans son conseil.
26 Ankhondo amphamvuwa anali: Asaheli mʼbale wa Yowabu, Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,
Puis d’autres héroïques guerriers: Assahel, frère de Joab; Elhanân, fils de Dodo, de Bethléem;
27 Samoti Mharori, Helezi Mpeloni.
Chammot, le Harorite, Hêleç, le Pelonite;
28 Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa, Abiezeri wa ku Anatoti,
Ira, fils d’Ikkech, de Tekoa; Abiézer, d’Anatot;
29 Sibekai Mhusati, Ilai Mwahohi,
Sibbekhaï, le Houchatite; Ilaï, l’Ahohite;
30 Maharai Mnetofa, Heledi mwana wa Baana Mnetofa,
Maharaï, de Netofa; Hêled, fils de Baana, de Netofa;
31 Itai mwana wa Ribai wa ku Gibeya ku Benjamini, Benaya Mpiratoni,
Itaï, fils de Ribaï, de Ghibea des Benjaminites; Benaïa, de Piratôn
32 Hurai wa ku zigwa za Gaasi, Abieli Mwaribati,
Houraï, de Nahalê-Gaach; Abiël, l’Arbatite;
33 Azimaveti Mbaharumi, Eliyahiba Msaaliboni,
Azmaveth, le Baharoumite; Elyahba, le Chaalbonite;
34 ana a Hasemu Mgizoni, Yonatani mwana wa Sage Mharari,
des fils de Hachêm le Ghizonite; Jonathan, fils de Chaghê, le Hararite;
35 Ahiamu mwana wa Sakari Mharari, Elifali mwana wa Uri,
Ahïâm, fils de Sakhar, le Hararite; Elifal, fils d’Our;
36 Heferi Mmekerati, Ahiya Mpeloni,
Hêfer, le Mekhératite; Ahiya, le Pelonite;
37 Heziro wa ku Karimeli Naara mwana wa Ezibai,
Heçro, le Carmélite; Naaraï, fils d’Ezbaï;
38 Yoweli mʼbale wa Natani, Mibihari mwana wa Hagiri,
Joël, frère de Nathan; Mibhar, fils du Hagrite;
39 Zeleki Mwamoni, Naharai wa ku Beeroti, mnyamata wonyamula zida za Yowabu mwana wa Zeruya.
Célek, l’Ammonite; Nahraï, le Bêrotite, écuyer de Joab, fils de Cerouya;
40 Ira Mwitiri, Garebu Mwitiri,
Ira, le Yithrite; Garêb, le Yithrite;
41 Uriya Mhiti, Zabadi mwana wa Ahilai,
Urie, le Héthéen; Zabad, fils d’Ahlaï;
42 Adina mwana wa Siza Mrubeni, amene anali mtsogoleri wa Arubeni ndi anthu makumi atatu pamodzi naye,
Adina, fils de Chiza, le Rubénite, chef rubénite, commandant à trente;
43 Hanani mwana wa Maaka, Yehosafati Mmitini,
Hanân, fils de Maakha; Josaphat, le Mitnite;
44 Uziya Mwasiterati, Sama ndi Yeiyeli ana a Hotamu Mwaroeri,
Ouzzia, l’Achteratite; Chama et Yeïêl, fils de Hotam, d’Aroër;
45 Yediaeli mwana wa Simiri, ndi Yoha Mtizi mʼbale wake,
Yedïaêl, fils de Chimri; Yoha, son frère, le Tiçite;
46 Elieli Mhavati, Yeribai ndi Yosaviya ana a Elinaamu, Itima Mmowabu,
Eliël, de Mahavïm; Yeribaï et Yochavia, fils d’Elnaam; Yitma, le Moabite;
47 Elieli, Obedi ndi Yaasieli Mmeobai.
Eliël, Obed et Yaassïêl, de Meçobaïa.

< 1 Mbiri 11 >