< ᏉᎳ ᎶᎻ ᎠᏁᎯ ᏧᏬᏪᎳᏁᎸᎯ 12 >

1 ᎾᏍᎩ ᎢᏳᏍᏗ, ᎢᏓᎵᏅᏟ, ᎢᏨᏍᏗᏰᏗᎭ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏓᏙᎵᏣᏘᏳ ᎨᏒ ᎢᏳᏍᏗ, ᎾᏍᎩ ᏗᏥᏰᎸ ᏗᏣᎵᏍᎪᎸᏙᏗᏱ ᎬᏃᏛ ᎠᏥᎸ ᎨᎳᏍᏗ, ᎪᎱᏍᏗ ᏄᏍᏛᎾ, ᏗᎬᏩᏓᏂᎸᎢᏍᏗ ᎤᏁᎳᏅᎯ, ᏕᏣᏓᏅᏛ ᎬᏗ ᎪᎱᏍᏗ ᎡᏣᏛᏁᎲᎢ.
Nʼchifukwa chake ine ndikukupemphani abale, mwa chifundo cha Mulungu, kuti mupereke matupi anu monga nsembe yamoyo, yopatulika ndi yokondweretsa Mulungu. Nsembeyi ndiye kupembedza kwanu kwa uzimu.
2 ᎠᎴ ᏞᏍᏗ ᎡᎶᎯ ᎠᏁᎯ ᏄᎾᏍᏛ ᏱᏂᏨᏍᏕᏍᏗ; ᏗᏣᏓᏁᏟᏴᏛᏍᎩᏂ ᎨᏎᏍᏗ ᏗᏤ ᎢᏗᎬᏁᎸᎯ ᎨᏒ ᏕᏣᏓᏅᏛᎢ, ᎾᏍᎩ ᎨᏥᎪᎵᏰᏗ ᎢᏳᎵᏍᏙᏗᏱ ᏄᏍᏛ ᎤᏚᎵᏍᎬ ᎤᏁᎳᏅᎯ, ᎾᏍᎩ ᎣᏍᏛ ᎨᏒᎢ, ᎠᎴ ᏗᎬᏩᏓᏂᎸᎢᏍᏗ ᎨᏒᎢ, ᎠᎴ ᎠᎧᎵᎢ ᎨᏒᎢ. (aiōn g165)
Musafanizidwenso ndi makhalidwe a dziko lino koma musandulike pokonzanso maganizo anu. Ndipo mudzadziwa ndi kuzindikira chifuniro chabwino cha Mulungu chomwe ndi chokondweretsa ndi changwiro. (aiōn g165)
3 ᎬᏩᎦᏘᏯᏰᏃ ᎤᏓᏙᎵᏍᏗ ᎨᏒ ᎬᏗᏍᎬ, ᎾᏍᎩ ᎥᎩᏁᎸᎯ ᏥᎩ, ᎯᎠ ᏂᎦᏥᏪᏎᎭ ᎾᏂᎥᏉ ᏥᎨᏣᏓᏑᏯ; ᏞᏍᏗᏉ ᏯᏂᎶᏒᏍᏗᏍᎨᏍᏗ ᎠᎾᏓᏅᏖᏍᎬ ᎾᏍᎩ ᏥᏚᏳᎪᏗ ᎤᎾᏓᏅᏖᏗᏱ, ᎤᎾᎵᏏᎾᎯᏍᏗᏍᎩᏂ ᎨᏎᏍᏗ ᎠᎾᏓᏅᏖᏍᎬᎢ, ᎾᏍᎩᏯ ᏄᏍᏛ ᎪᎯᏳᏗ ᎨᏒ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᏚᏟᎶᎡᎸ ᎠᏂᏏᏴᏫᎭᎢ.
Chifukwa cha chisomo chopatsidwa kwa ine, ndinena kwa aliyense wa inu kuti musadziyenereze nokha kuposa mmene mulili. Koma mudziganizire nokha modzichepetsa, molingana ndi muyeso wa chikhulupiriro chimene Mulungu wakupatsani.
4 ᎤᏣᏘᏰᏃ ᏥᏕᎦᎯᏞᏫᏒ ᏌᏉ ᎠᏰᎸ ᎨᏒᎢ, ᎠᎴ ᎾᎦᏛ ᏕᎦᎯᏞᏫᏒ ᎤᏠᏱ ᏂᎨᏒᎾ ᏥᎩ ᎪᎱᏍᏗ ᎬᏔᏂᏓᏍᏗ ᎨᏒᎢ;
Pakuti monga aliyense wa ife ali ndi thupi limodzi koma ziwalo zambiri, ziwalozi sizili ndi ntchito yofanana.
5 ᎾᏍᎩᏯ ᎾᏍᏉ ᎠᏴ, ᎢᎩᏣᏘ ᏥᎩ, ᏌᏉᏉ ᎠᏰᎸ ᏂᏓᎵᏍᏗᎭ ᎦᎶᏁᏛ ᏕᏓᏁᎶᏛᎢ, ᎠᎴ ᏂᏗᎥ ᎢᏗᏏᏴᏫᎭ ᎢᎦᏚᏓᏕᏫᏒ.
Momwemonso mwa Khristu ife amene tili ambiri tipanga thupi limodzi ndipo chiwalo chilichonse ndi cholumikizika ku chinzake.
6 ᎾᏍᎩᏃ ᏧᏓᎴᎿᎭᎢ ᎡᎩᏁᎸᏅᎯ ᏥᎩ ᎾᏍᎩᏯ ᎬᏩᎦᏘᏯ ᎤᏓᏙᎵᏍᏗ ᎨᏒ ᎢᎩᏁᎸᎢ, ᎢᏳᏃ ᎠᏙᎴᎰᎯᏍᏗ ᏱᎩ, ᎾᏍᎩᏯ ᎪᎯᏳᏗ ᎨᏒ ᎡᎦᏟᎶᎡᎸ ᎢᏛᏗᏍᎨᏍᏗ [ ᎢᏓᏙᎴᎰᏍᎨᏍᏗ; ]
Ife tili ndi mphatso zosiyana, molingana ndi chisomo chopatsidwa kwa ife. Ngati mphatso ya munthu ndi kunenera, musiyeni ayigwiritse ntchito molingana ndi chikhulupiriro chake.
7 ᎢᏳ ᎠᎴ ᎢᏗᏯᏙᎯᎮᏍᏗ, ᎢᏗᏯᏙᎯᎲᏉ ᏕᎩᎸᏫᏍᏓᏁᎮᏍᏗ; ᎠᎴ ᎩᎶ ᏓᏕᏲᎲᏍᎨᏍᏗ, ᏗᏕᏲᏗᏉ ᎨᏒ ᏚᎸᏫᏍᏓᏁᎮᏍᏗ;
Ngati ndi kutumikira, musiyeni atumikire. Ngati ndi kuphunzitsa, musiyeni aphunzitse.
8 ᎠᎴ ᎩᎶ ᏗᎦᏬᏁᏗᏍᎩ ᎨᏎᏍᏗ, ᏗᎦᏬᏁᏙᏗᏉ ᎨᏒ ᏚᎸᏫᏍᏓᏁᎮᏍᏗ; ᎠᎴ ᎩᎶ ᏓᏯᏙᎮᎮᏍᏗ, ᏄᎨᏳᎲᏍᎬᎾ ᎾᏍᎩ ᎾᏛᏁᎮᏍᏗ; ᎩᎶ ᏣᎦᏁᎶᏗ ᎨᏎᏍᏗ, ᎣᏍᏛ ᎤᎦᏌᏯᏍᏗ ᎨᏎᏍᏗ; ᎩᎶ ᎠᏓᏙᎵᎨᏍᏗ, ᎤᎧᎵᏍᏗ ᎤᏓᏅᏛ ᎾᏍᎩ ᎾᏛᏁᎮᏍᏗ.
Ngati ndi kulimbikitsa, musiyeni alimbikitse. Ngati ndi kupereka kuthandiza osowa, musiyeni apereke mowolowamanja. Ngati ndi utsogoleri, musiyeni alamulire mosamala. Ngati ndi kuonetsa chifundo, musiyeni achite mosangalala.
9 ᎠᏓᎨᏳᏗ ᎨᏒ ᏄᏠᎾᏍᏛᎾ ᎨᏎᏍᏗ. ᎢᏥᏂᏆᏘᎮᏍᏗ Ꮎ ᎤᏲ ᎨᏒᎢ; ᏕᏥᏂᏴᏎᏍᏗ ᎣᏍᏛ ᎨᏒᎢ.
Chikondi chikhale chopanda chinyengo. Dana nacho choyipa; gwiritsitsa chabwino.
10 ᎠᎾᎵᏅᏟ ᏧᎾᏓᎨᏳᏗ ᎨᏒ ᎬᏗ ᎣᏍᏛ ᏕᏣᏓᎨᏳᏎᏍᏗ; ᏗᏓᎸᏉᏙᏗ ᎨᏒ ᎢᏨᏗᏍᎬ ᏕᏣᏓᎬᏫᏳᏗᏍᎨᏍᏗ.
Mukondane kwathunthu monga abale. Lemekezanani wina ndi mnzake kuposa inu eni.
11 ᏕᏥᎸᏫᏍᏓᏁᎲ ᏞᏍᏗ ᎢᏣᏓᏄᎸᏗ ᏱᎨᏎᏍᏗ; ᎤᎵᏂᎩᏛ ᏕᏣᏓᏅᏖᏍᏗ; ᎪᎱᏍᏗ ᎡᏣᏛᏁᎮᏍᏗ ᎤᎬᏫᏳᎯ.
Musakhale aulesi mʼmachitidwe anu. Khalani achangu mu mzimu ndipo tumikirani Ambuye.
12 ᎤᏚᎩ ᎢᏨᏒ ᎢᏣᎵᎮᎵᎨᏍᏗ; ᏗᏨᏂᏗᏳ ᎨᏎᏍᏗ ᎢᏥᎩᎵᏲᎬᎢ; ᎢᏣᏓᏙᎵᏍᏗᏍᎨᏍᏗ ᏂᎪᎯᎸᎢ;
Kondwerani mʼchiyembekezo, pirirani mʼmasautso ndiponso khulupirikani mʼpemphero.
13 ᎤᎾᏓᏅᏘ ᎤᏂᏂᎬᏎᎲ ᏕᏥᏯᏙᎮᎮᏍᏗ; ᎢᏥᎦᎵᏱᏳ ᎨᏎᏍᏗ ᏗᏣᏓᏍᏆᏂᎪᏙᏗᏱ.
Gawanani ndi anthu a Mulungu amene ali ndi chosowa. Cherezani alendo.
14 ᎣᏍᏛ ᏕᏥᏁᏤᎮᏍᏗ ᎤᏲ ᎢᎨᏨᎿᎭᏕᎩ; ᎣᏍᏛᏉ ᏕᏥᏁᏤᎮᏍᏗ, ᎠᎴ ᏞᏍᏗ ᏱᏗᏥᏍᎩᏅᏗᏍᎨᏍᏗ.
Adalitseni amene akuzunzani. Adalitseni ndipo musawatemberere.
15 ᎾᏍᎩ Ꮎ ᎠᎾᎵᎮᎵᎩ ᎢᏧᎳᎭ ᎢᏣᎵᎮᎵᎨᏍᏗ, ᎠᎴ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᏗᎾᏠᏱᎯ ᎢᏧᎳᎭ ᏕᏣᏠᏱᎮᏍᏗ.
Kondwani pamodzi ndi amene akukondwa ndipo lirani ndi amene akulira.
16 ᎤᏠᏱᎭᏉ ᎨᏎᏍᏗ ᏕᏣᏓᏓᏅᏖᏍᎬᎢ. ᏞᏍᏗ ᏱᏣᎦᏌᏯᏍᏕᏍᏗ ᎪᎱᏍᏗ ᎦᎸᏉᏗ ᎨᏒᎢ, ᏕᏤᎳᏗᏙᎮᏍᏗᏍᎩᏂ ᎤᎾᏓᏙᎵᏍᏗ. ᏞᏍᏗ ᎢᏥᎦᏔᎾᎢ ᏱᏣᏓᏰᎸᏎᏍᏗ.
Muyanjane wina ndi mnzake. Musakhale onyada, koma lolani kuyanjana ndi anthu wamba. Musaganize kuti mumadziwa zonse.
17 ᎤᏐᏅ ᏂᏨᏁᎮᏍᏗ ᎩᎶ ᏞᏍᏗ ᏱᏣᏞᎨᏍᏗ ᎤᏐᏅ ᏱᏁᏨᏁᎮᏍᏗ. ᎢᎬᏱ ᏂᏣᏓᏅᏖᏍᎨᏍᏗ ᎣᏍᏛ ᎢᏣᏛᏁᎵᏓᏍᏗ ᎨᏒ ᏂᎦᏛ ᎠᏂᎦᏔᎲᎢ.
Musabwezere choyipa ndi choyipa kwa aliyense. Samalitsani kuchita chabwino pamaso pa aliyense.
18 ᎢᏳᏃ ᏰᎵ ᎨᏎᏍᏗ ᏂᎦᎥ ᎢᎨᏣᏛᏁᏗ ᎨᏒ ᎢᏣᏟᏂᎬᏁᎮᏍᏗ ᏙᎯᏱ ᎢᏣᏕᏗᏱ ᎾᏂᎥ ᏴᏫ.
Ngati nʼkotheka, khalani mwamtendere ndi aliyense monga momwe mungathere.
19 ᎢᏨᎨᏳᎢ, ᏞᏍᏗ ᏱᏣᏞᎨᏍᏗ, ᎢᏥᎳᏅᏓᏕᎮᏍᏗᏍᎩᏂ ᎤᏔᎳᏬᎯᏍᏗ ᎨᏒᎢ; ᎯᎠᏰᏃ ᏂᎬᏅ ᎪᏪᎳ, ᎠᏞᎢᏍᏗ ᎨᏒ ᎠᏴ ᎠᏆᏤᎵᎦ; ᎠᏴ ᏓᎦᎫᏴᎯ, ᎠᏗᎭ ᏱᎰᏩ.
Okondedwa anga, musabwezere choyipa, koma lekerani Mulungu. Pakuti kwalembedwa, “Kubwezera chilango nʼkwanga. Ndidzawalanga ndine,” akutero Ambuye.
20 ᎾᏍᎩ ᎢᏳᏍᏗ, ᎢᏳᏃ ᏣᏍᎦᎩ ᎠᎪᏄ ᎤᏲᏏᏍᎨᏍᏗ, ᎯᏰᎶᎮᏍᏗ; ᎢᏳᏃ ᎤᏔᏕᎩᏍᎨᏍᏗ, ᎯᎤᎥᏍᎨᏍᏗ; ᎾᏍᎩᏰᏃ ᎿᎭᏛᏁᎲ ᏥᏃᏍᎦ ᏧᏥᏍᏟ ᏕᎯᏡᏍᎨᏍᏗ ᎠᏍᎪᎵ.
Koma, “Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya. Ngati ali ndi ludzu, mupatse kanthu kakumwa. Pochita ichi, udzamuwunjikira makala amoto pamutu pake.”
21 ᏞᏍᏗ ᎤᏐᏅ ᏁᏨᏁᎸ ᏱᏣᏓᎵᏁᎯᏕᎴᏍᏗ, ᎤᏐᏅᏍᎩᏂ ᏁᏨᏁᎸ ᎯᏯᏓᎵᏁᎯᏕᎮᏍᏗ ᎣᏍᏛ ᎿᎭᏛᏁᎲᎢ.
Musagonjetsedwe ndi choyipa, koma gonjetsani choyipa pochita chabwino.

< ᏉᎳ ᎶᎻ ᎠᏁᎯ ᏧᏬᏪᎳᏁᎸᎯ 12 >