< ᏉᎳ ᎶᎻ ᎠᏁᎯ ᏧᏬᏪᎳᏁᎸᎯ 10 >

1 ᎢᏓᎵᏅᏟ, ᎠᎩᎾᏫᏱ ᎢᏴᏛ ᎠᏆᏚᎵᎭ, ᎠᎴ ᏥᏯᏓᏙᎵᏍᏓᏁᎭ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎢᏏᎵ ᎤᎬᏩᎵ, ᎾᏍᎩ ᎨᏥᏍᏕᎸᏗᏱ.
Abale, chokhumba cha mtima wanga ndi pemphero langa kwa Mulungu ndi chakuti Aisraeli apulumutsidwe.
2 ᎦᏥᏲᎢᏳᏓᏁᎯᏰᏃ ᎾᏍᎩ ᎤᏣᏘ ᎤᎾᏚᎵᏍᎬ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎪᎱᏍᏗ ᎤᎾᏛᏁᏗᏱ; ᎠᏎᏃ ᎥᏝ ᎠᎦᏙᎮᎯᏍᏗ ᎨᏒ ᏯᏅᏗᎭ.
Popeza ndiwachitira umboni kuti ndi achangu pa zinthu za Mulungu koma osati mwachidziwitso.
3 ᎾᏂᎦᏔᎲᎾᏰᏃ ᎨᏒ ᏄᏍᏛ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏓᏚᏓᎴᏍᏙᏗ ᎨᏒᎢ, ᎠᎴ ᎠᎾᏟᏂᎬᏁᎲ ᎤᏂᏍᏓᏱᏗᏍᏗᏱ ᎤᏅᏒ ᎤᎾᏤᎵ ᎤᎾᏚᏓᎴᏍᏙᏗ ᎨᏒᎢ, ᎥᏝ ᏧᎾᏓᏲᎯᏎᎸᎯ ᏱᎩ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏓᏚᏓᎴᏍᏙᏗ ᎨᏒᎢ.
Pakuti sanadziwe chilungamo chochokera kwa Mulungu ndipo anafuna kukhazikitsa chawochawo. Iwo sanagonjere chilungamo cha Mulungu.
4 ᏗᎧᎿᎭᏩᏛᏍᏗᏰᏃ ᎤᎬᏩᎴ ᎦᎶᏁᏛ ᎤᎾᏚᏓᎴᏍᏙᏗᏱ ᎾᏂᎥ ᎠᏃᎯᏳᎲᏍᎩ.
Khristu ndiye mathero amalamulo kuti aliyense amene akhulupirira akhale olungama pamaso pa Mulungu.
5 ᎼᏏᏰᏃ ᎧᏃᎮᎭ ᏄᏍᏛ ᎤᏓᏚᏓᎴᏍᏙᏗ ᎨᏒ ᏗᎧᎿᎭᏩᏛᏍᏗ, ᎯᎠ ᏥᏂᎦᏪᎭ, ᎩᎶ ᏴᏫ ᎾᏍᎩ ᎾᏛᏁᎮᏍᏗ ᎬᏂᏛ ᎠᏩᏛᏗᏍᎨᏍᏗ.
Mose akulemba motere zachilungamo cha malamulo, “Munthu amene achita zinthu izi adzakhala ndi moyo pozichita.”
6 ᎪᎯᏳᏗᏍᎩᏂ ᎠᏚᏓᎴᏍᏙᏗ ᎨᏒ ᎯᎠ ᏂᎦᏪᎭ, ᏞᏍᏗ ᏣᎾᏫᏱ ᎯᎠ ᏱᏂᏪᏍᎨᏍᏗ, ᎦᎪ ᎦᎸᎶᎢ ᏓᏰᏏ? ( ᎾᏍᎩ ᎦᎶᏁᏛ ᎠᎦᏠᎥᏙᏗᏱ; )
Koma chilungamo cha chikhulupiriro chikuti, “Usanene mu mtima mwako kuti, ‘Kodi ndani amene akwere kumwamba?’” (ndiko, kukatsitsa Khristu)
7 ᎠᎴ ᎦᎪ ᎠᏍᏛᎩ ᎨᏒ ᏮᏓᎦᎶᏏ? ( ᎾᏍᎩ ᎦᎶᏁᏛ ᎤᏲᎱᏒ ᏧᎴᏙᏗᏱ; ) (Abyssos g12)
“kapena ‘Ndani adzatsikira ku dziko la anthu akufa?’” (ndiko, kukamutenga Khristu kwa akufa). (Abyssos g12)
8 ᎠᏎᏃ ᎦᏙ ᎠᏗᎭ? ᎧᏃᎮᏛ ᎮᎲ ᎾᎥᏂᏳ ᏄᏍᏗᏕᎦ, ᎾᏍᎩ ᎯᎰᎵᏉ, ᎠᎴ ᏣᎾᏫᏱᏉ ᎡᎭ; ᎾᏍᎩ ᎯᎠ ᎧᏃᎮᏛ ᎪᎯᏳᏗ ᎨᏒ ᎧᏃᎮᏍᎩ, ᎾᏍᎩ ᎠᏴ ᏦᏣᎵᏥᏙᎲᏍᎦ;
Nanga akuti chiyani? “Mawu ali pafupi ndi inu. Ali mʼkamwa mwanu ndi mu mtima mwanu.” Ndiwo mawu achikhulupiriro amene ife tikuwalalikira,
9 ᎾᏍᎩ ᎢᏳᏃ ᎯᎰᎵ ᏱᏨᏔᏅ ᎬᏂᎨᏒ ᏱᏂᏴᏁᎸ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᏥᏌ, ᎠᎴ ᏣᎾᏫᏱ ᎢᏴᏛ ᏱᏦᎯᏳᏅ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᏕᎤᎴᏔᏅ ᎤᏲᎱᏒᎢ, ᎠᏎ ᎡᏣᏍᏕᎸᏗ ᎨᏎᏍᏗ.
kuti ngati udzavomereza ndi pakamwa pako kuti, “Yesu ndiye Ambuye,” ndi kukhulupirira mu mtima mwako kuti Mulungu anamuukitsa kwa akufa, udzapulumuka.
10 ᎣᎾᏫᏰᏃ ᎬᏗ ᎠᎪᎯᏳᎲᏍᎪ ᎣᏚᏓᎴᏍᏗ ᏂᎦᎵᏍᏔᏂᎦ; ᎠᎴ ᎥᎰᎵ ᎬᏗ ᎬᏂᎨᏒ ᎾᎬᏁᎰ ᎥᏓᏗᏍᏕᎸᏗ ᏂᎦᎵᏍᏔᏂᎦ.
Pakuti ndi mtima wanu mukhulupirira ndi kulungamitsidwa, ndipo ndi pakamwa panu muvomereza ndi kupulumutsidwa.
11 ᎪᏪᎵᏰᏃ ᎯᎠ ᏂᎦᏪᎭ, ᎩᎶ ᎾᏍᎩ ᎪᎯᏳᎲᏍᎨᏍᏗ ᎥᏝ ᎤᏕᎰᎯᏍᏗ ᏱᎨᏎᏍᏗ.
Pakuti Malemba akuti, “Aliyense amene akhulupirira Iye, sadzachititsidwa manyazi.”
12 ᎥᏝᏰᏃ ᏱᏚᎾᏓᎴᎾᎠ ᎠᏂᏧᏏ ᎠᏃ ᎠᏂᎪᎢ; ᎾᏍᎩᏉᏰᏃ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎾᏂᎥ ᎤᎾᏤᎵᎦ ᎤᏣᏘ ᎤᏪᎿᎭᎢᏳ ᏧᏍᏕᎸᏗᏱ ᎾᏂᎥ ᎬᏩᏓᏙᎵᏍᏓᏁᎯ.
Pakuti palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi a mitundu ina, pakuti Ambuye mmodzi yemweyo ndi Ambuye wa onse ndipo amadalitsa mochuluka onse amene ayitana pa Iye
13 ᎾᏂᎥᏉᏰᏃ ᎩᎶ ᎠᎾᏓᏙᎵᏍᏗᏍᎨᏍᏗ ᏚᏙᎥ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎠᏂᏁᎢᏍᏗᏍᎨᏍᏗ ᎨᏥᏍᏕᎸᏗ ᎨᏎᏍᏗ.
pakuti, “Aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka.”
14 ᎦᏙᏃ ᏱᎦᎵᏍᏙᏓ ᏯᎾᏓᏙᎵᏍᏓᏏ ᎩᎶ ᏄᏃᎯᏳᏒᎾ ᏱᎩ ᎡᎲᎢ? ᎠᎴ ᎦᏙ ᏱᎦᎵᏍᏙᏓ ᏯᏃᎯᏳᎲᎦ ᎩᎶ ᎡᎲ ᎾᏍᎩ ᎤᎾᏛᎦᏅᎯ ᏂᎨᏒᎾ ᏱᎩ ᎡᎲᎢ? ᎠᎴ ᎦᏙ ᏱᎦᎵᏍᏙᏓ ᏯᎾᏛᎬᎦ ᎩᎶ ᎠᎵᏥᏙᎲᏍᎩ ᏄᏁᎲᎾ ᏱᎩ?
Kodi adzayitana bwanji amene sanamukhulupirire? Ndipo adzakhulupirira bwanji asanamve za Iye? Ndipo adzamva bwanji popanda wina kulalikira kwa iwo?
15 ᎠᎴ ᎦᏙ ᏱᎦᎵᏍᏙᏓ ᏯᎾᎵᏥᏙᎲᎦ ᎢᏳᏃ ᏂᎨᏥᏅᏒᎾ ᏱᎩ? ᎾᏍᎩᏯ ᎯᎠ ᏥᏂᎬᏅ ᏥᎪᏪᎳ, ᏂᏚᏬᏚᎭ ᏧᎾᎳᏏᏕᏂ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᎣᏍᏛ ᎧᏃᎮᏛ ᏅᏩᏙᎯᏯᏛ ᎠᏓᏁᎯ ᎠᎾᎵᏥᏙᎲᏍᎩ, ᎣᏍᏛ ᎧᏃᎮᏛ ᎠᎾᎵᏥᏙᎲᏍᎩ ᎾᏍᎩ ᎣᏍᏛ ᎤᎬᏩᎵ ᎨᏒᎢ.
Ndipo iwo adzalalikira bwanji osatumidwa? Kwalembedwa kuti, “Akongoladi mapazi a iwo amene amabweretsa Uthenga Wabwino!”
16 ᎠᏎᏃ ᎥᏝ ᎾᏂᎥ ᎤᏃᎯᏳᏅᎯ ᏱᎩ ᎣᏍᏛ ᎧᏃᎮᏛ. ᎢᏌᏯᏰᏃ ᎯᎠ ᏂᎦᏪᎭ, ᏱᎰᏩ, ᎦᎪ ᎤᏬᎯᏳᏅ ᎣᏥᏃᎮᏍᎬᎢ?
Koma si onse amene anavomereza Uthenga Wabwino. Pakuti Yesaya akuti, “Ambuye, ndani amene wakhulupirira uthenga wathu?”
17 ᎾᏍᎩᏃ ᎯᎠ ᏥᏄᏍᏗ ᎪᎯᏳᏗ ᎨᏒ ᎠᏛᎪᏗᏱ ᏗᏓᎴᎲᏍᎦ, ᎠᏛᎪᏗᏱᏃ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏤᎵ ᎧᏃᎮᏛ ᏗᏓᎴᎲᏍᎦ.
Motero, chikhulupiriro chimabwera pamene timva uthenga ndipo uthenga umamveka kuchokera ku mawu a Khristu.
18 ᎠᏎᏃ ᎠᏴ ᎯᎠ ᏂᏥᏪᎭ, ᏝᏍᎪ ᏳᎾᏛᎦᏅ? ᎥᎥ, ᎤᏙᎯᏳᎯ, ᎤᎾᏓᏃᏴᎵᏍᏛ ᏚᏰᎵᏒ ᎡᎳᏂᎬᎢ, ᎠᎴ ᎠᏂᏬᏂᏍᎬ ᎡᎶᎯ ᏩᏍᏛ ᎢᏴᏛ ᏚᏰᎵᏒ.
Koma ndikufunsa kuti kodi iwo anamva? Inde, iwo anamva kuti, “Liwu lawo linamveka ponseponse pa dziko lapansi. Mawu awo anafika ku malekezero a dziko lonse.”
19 ᎠᏎᏃ ᎠᏴ ᏂᏥᏪᎭ, ᏝᏍᎪ ᏯᏂᎦᏔᎮ ᎢᏏᎵ? ᎢᎬᏱ ᎨᏒ ᎼᏏ ᎯᎠ ᏂᎦᏪᎭ, ᎢᏣᏛᏳᎨᏗᏱ ᏅᏓᏨᏴᏁᎵ ᏓᎦᏥᏴᏔᏂ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᎠᏰᎵ ᎤᏃᏢᎯ ᏂᎨᏒᎾ ᎨᏒᎢ, ᎠᎴ ᏄᎾᏓᏅᏛᎾ ᏴᏫ ᎦᏥᏴᏗᏍᎬ ᏓᏨᎾᎸᏍᏔᏂ.
Ine ndifunsanso kuti, kodi Israeli sanazindikire? Poyamba Mose akuti, “Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake. Ine ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.”
20 ᎠᏎᏃ ᎢᏌᏯ ᏂᎦᎾᏰᏍᎬᎾ ᎯᎠ ᏂᎦᏪᎭ, ᎬᎩᏩᏛᎲᎩ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᏂᎬᎩᏲᎸᎾ ᎨᏒᎢ; ᎬᏂᎨᏒ ᏂᎬᏋᏁᎸᎩ ᎠᏁᎲ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᎾᎾᏛᏛᎲᏍᎬᎾ ᎨᏒ ᎨᎥᎢ.
Ndipo Yesaya molimba mtima akuti, “Anandipeza anthu amene sanali kundifunafuna. Ndinadzionetsera kwa amene sanafunse za Ine.”
21 ᎢᏏᎵᏍᎩᏂ ᎯᎠ ᏂᏕᎦᏪᏎᎭ, ᎤᏙᏓᏆᏛ ᏓᏆᏎᎵᏛᎩ ᎦᏥᏯᏂᏍᎬ ᏄᏃᎯᏳᏒᎾ ᎠᎴ ᎤᏂᎪᏁᎶᎯᏌᏘ ᏴᏫ.
Koma zokhudzana ndi Aisraeli akuti, “Tsiku lonse ndinatambasulira manja anga kwa anthu osandimvera ndi okanika.”

< ᏉᎳ ᎶᎻ ᎠᏁᎯ ᏧᏬᏪᎳᏁᎸᎯ 10 >