< ᎣᏍᏛ ᎧᏃᎮᏛ ᎹᎦ ᎤᏬᏪᎳᏅᎯ 16 >

1 ᎤᎾᏙᏓᏆᏍᎬᏃ ᎤᎶᏐᏅ, ᎺᎵ ᎹᎩᏕᎵ ᎡᎯ, ᎠᎴ ᎺᎵ ᏥᎻ ᎤᏥ ᎠᎴ ᏌᎶᎻ ᎤᏂᏩᏒᎯ ᎨᏎ ᎤᎦᎾᏍᏛ ᎦᏩᏒᎩ, ᎤᏂᎷᎯᏍᏗᏱ ᎤᏂᏰᎸᏎ ᎠᎴ ᎬᏩᎶᏁᏗᏱ.
Litapita tsiku la Sabata, Mariya Magadalena, ndi amayi ake a Yakobo, ndi Salome anagula zonunkhiritsa ndi cholinga chakuti apite akadzoze thupi la Yesu.
2 ᏑᎾᎴᎢᏳᏃ ᎢᎬᏱᏱ ᎢᎦ ᏑᎾᏙᏓᏆᏍᏗ ᎨᏒᎢ, ᎤᏂᎷᏤ ᎠᏤᎵᏍᏛ ᏨᏗᎧᎸᎪᏉ.
Mmamawa, tsiku loyamba la Sabata, dzuwa litangotuluka kumene, anali pa ulendo wopita ku manda
3 ᎯᎠᏃ ᏂᏚᎾᏓᏪᏎᎴᎢ, ᎦᎪ ᏓᎩᎲᎡᎵ ᏅᏯ ᎠᏤᎵᏍᏛ ᎦᎶᎯᏍᏗᏱ ᎠᎲᎢ?
ndipo anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi akatikugudubuzira mwala pa khomo la manda ndani?”
4 ᏫᏚᎾᎧᎿᎭᏅᏃ ᎤᏂᎪᎮ ᏅᏯ ᎠᎲᏛ ᎨᏒᎢ, ᎤᏣᏘᏰᏃ ᎡᏉᎯᏳ ᎨᏎᎢ.
Koma atakweza maso awo, anaona kuti mwala umene unali waukulu kwambiri wagubuduzidwa kale.
5 ᏭᏂᏴᎸᏃ ᎠᏤᎵᏍᏛᎢ, ᎤᏂᎪᎮ ᎠᏫᏴ ᎠᎦᏘᏏᏗᏢ ᎤᏬᎴᎢ, ᎤᏄᏪ ᎦᏅᎯᏛ ᎤᏁᎬ ᎠᏄᏬ; ᎠᏂᏍᎦᎢᎮᏃ.
Atalowa mʼmanda, anaona mnyamata atavala mwinjiro woyera atakhala ku mbali ya kumanja, ndipo iwo anachita mantha.
6 ᎯᎠᏃ ᏂᏚᏪᏎᎴᎢ, ᏞᏍᏗ ᏱᏥᏍᎦᎢᎮᏍᏗ; ᏥᏌ ᎾᏎᎵᏗ ᎡᎯ ᎡᏥᏲᎭ, ᎾᏍᎩ ᏣᎦᏛᎥᏍᎬᎩ; ᏚᎴᎯᏌᏅ; ᎥᏝ ᎠᏂ ᏱᎦᏅ; ᏗᏣᎧᏅᎦ Ꭰ ᎤᏂᏅᏅᎢ.
Iye anati, “Musaope. Kodi mukufuna Yesu wa ku Nazareti, amene anapachikidwa? Wauka! Sali muno. Onani malo amene anamugonekapo.
7 ᎠᏎᏃ ᏥᏤᎾ, ᎠᎴ ᏫᏗᏥᏃᎲᏏ ᎬᏩᏍᏓᏩᏗᏙᎯ ᎠᎴ ᏈᏓ ᎾᏍᎩ ᎢᎬᏱ ᏫᏚᎶᎯᏎᏗᏱ ᎨᎵᎵ; ᎾᎿᎭᏓᏰᏥᎪᎢ, ᎾᏍᎩᏯ ᏂᏥᏪᏎᎸᎢ.
Koma pitani, kawuzeni ophunzira ake ndi Petro kuti, ‘Iye watsogola kupita ku Galileya. Kumeneko mukamuona Iye monga momwe anakuwuzirani.’”
8 ᎤᎵᏍᏗᏃ ᎤᏂᏄᎪᏨ ᏚᎾᎵᏖᏎ ᎠᏤᎵᏍᏛᎢ; ᏚᏂᎾᏫᏍᎨᏰᏃ ᎠᎴ ᎤᏂᏍᏆᏂᎪᏍᎨᎢ; ᎥᏝ ᎠᎴ ᎩᎶ ᎪᎱᏍᏗ ᏳᏃᏎᎴᎢ; ᎠᏂᏍᎦᎢᎮᏰᏃ.
Akunjenjemera ndi kudabwa, amayiwo anatuluka ndipo anathawa ku mandako. Sananene china chilichonse kwa aliyense, chifukwa anachita mantha.
9 (note: The most reliable and earliest manuscripts do not include Mark 16:9-20.) ᏥᏌᏃ ᏚᎴᎯᏌᏅ ᏑᎾᎴᎢᏳ ᎢᎬᏱᏱ ᎢᎦ ᏑᎾᏙᏓᏆᏍᏗ ᎨᏒᎢ, ᎢᎬᏱ ᎬᏂᎨᏒ ᏄᏛᏁᎴ ᎺᎵ ᎹᎩᏕᎵ ᎡᎯ, ᎾᏍᎩ ᎦᎵᏉᎩ ᎠᏂᏍᎩᎾ ᏥᏚᏄᎪᏫᏎᎴᎢ.
(note: The most reliable and earliest manuscripts do not include Mark 16:9-20.) Yesu atauka kwa akufa mmawa pa tsiku loyamba la Sabata, anayamba kuonekera kwa Mariya Magadalena, amene anatulutsa mwa iye ziwanda zisanu ndi ziwiri.
10 ᎾᏍᎩᏃ ᎤᏪᏅ ᎤᏁᏙᎸᎯ ᏫᏚᏃᏁᎴ ᎤᏲ ᏚᎾᏓᏅᏛᎢ ᎠᎴ ᏓᎾᏠᏱᎲᎢ.
Iye anapita ndi kukawawuza amene anali ndi Yesu, amene ankakhuza maliro ndi kulira.
11 ᎾᏍᎩᏃ ᎤᎾᏛᎦᏅ ᎬᏅᎢ, ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᎤᎪᎲᎢ, ᎥᏝ ᏳᏃᎯᏳᏁᎢ.
Atamva kuti Yesu ali moyo ndikuti amuona, iwo sanakhulupirire.
12 ᎣᏂᏃ ᏅᏩᏓᎴ ᏄᏍᏕ ᎬᏂᎨᏒ ᏂᏚᏛᏁᎴ ᎠᏂᏔᎵ ᎾᎿᎭᎠᏁᎳ ᎠᎾᎢᏎᎢ, ᏙᏗᎦᎶᎨᏒ ᏩᏂᎦᏖᎢ.
Zitatha izi Yesu anaonekera mʼmaonekedwe ena kwa awiri a iwo amene anali ku dera la ku mudzi.
13 ᎾᏍᎩᏃ ᎤᏁᏅ ᏫᏚᏂᏃᏁᎴ ᎠᏂᏐᎢ; ᎾᏍᏉ ᎥᏝ ᏱᏚᏃᎯᏳᏁ ᎾᏍᎩ.
Iwo anabwerera ndi kudzawawuza enawo; koma iwo sanakhulupirirebe.
14 ᎣᏂᏃ ᎬᏂᎨᏒ ᏂᏚᏛᏁᎴ ᏌᏚ ᎢᏯᏂᏛ ᎠᎾᎵᏍᏓᏴᎲᏍᎬᎢ, ᎠᎴ ᏚᎬᏍᎪᎸᏁ ᏂᎦᎵᏍᏙᏗᏍᎨ ᏄᏃᎯᏳᏒᎾ ᎨᏒ ᎠᎴ ᏗᏍᏓᏱᏳ ᎨᏒ ᏧᏂᎾᏫ, ᏂᏚᏃᎯᏳᏅᎾ ᎨᏒ ᎢᏳᏍᏗ ᎾᏍᎩ ᎬᏩᎪᎲᎯ ᏧᎴᎯᏌᏅᎯ ᏂᎨᏎᎢ.
Pambuyo pake Yesu anaonekera kwa khumi ndi mmodziwo pamene ankadya; anawadzudzula chifukwa chopanda chikhulupiriro ndi kukanitsitsa kwawo kuti akhulupirire amene anamuona Iye atauka.
15 ᎯᎠᏃ ᏂᏚᏪᏎᎴᎢ, ᎢᏤᏙᎾ ᎡᎶᎯ ᏂᎬᎾᏛᎢ, ᎠᎴ ᏫᏗᏣᎵᏥᏙᎲᏏ ᎣᏍᏛ ᎧᏃᎮᏛ ᎾᏂᎥ ᎨᎪᏢᏅᎯ.
Anati kwa iwo, “Pitani mʼdziko lonse lapansi ndipo mukalalikire Uthenga Wabwino kwa zolengedwa zonse.
16 ᎩᎶ ᎪᎯᏳᎲᏍᎨᏍᏗ ᎠᎴ ᎠᎦᏬᏍᎨᏍᏗ ᎠᏥᏍᏕᎸᏗ ᎨᏎᏍᏗ; ᏂᎪᎯᏳᎲᏍᎬᎾᏍᎩᏂ ᏣᎫᎪᏓᏁᏗ ᎨᏎᏍᏗ.
Aliyense amene akakhulupirire nabatizidwa adzapulumuka, koma amene sakakhulupirira adzalangidwa.
17 ᎯᎠᏃ ᎾᏍᎩ ᎤᏰᎸᏛ ᏗᎪᎵᏍᏙᏗ ᏔᎵ ᏚᏛᏗᏕᎨᏍᏗ ᎠᏃᎯᏳᎲᏍᎩ; ᎠᏴ ᏓᏆᏙᎥ ᎠᏅᏗᏍᎨᏍᏗ ᎠᏂᏍᎩᎾ ᏓᏂᏄᎪᏫᏍᎨᏍᏗ; ᏅᏩᎾᏓᎴ ᏧᏂᏬᏂᎯᏍᏗ ᏓᏂᏬᏂᏍᎨᏍᏗ;
Tsono zizindikiro izi zidzawatsata amene adzakhulupirira: Mʼdzina langa adzatulutsa ziwanda; adzayankhula malilime atsopano;
18 ᎢᎾᏛ ᏓᏂᏁᏍᎨᏍᏗ; ᎢᏳ ᎠᎴ ᎪᎱᏍᏗ ᎠᏓᎯᎯ ᏳᎾᏗᏔᎲ, ᎥᏝ ᎪᎱᏍᏗ ᏳᏅᏁᎮᏍᏗ; ᏧᏂᏢᎩ ᏓᎾᏏᏔᏗᏍᎨᏍᏗ, ᎠᎴ ᏚᎾᏗᏩᏍᎨᏍᏗ.
adzanyamula njoka ndi manja awo; ndipo pamene adzamwa mankhwala akupha, sadzawapweteka nʼpangʼonongʼono pomwe; adzasanjika manja awo pa anthu odwala ndipo odwalawo adzachira.”
19 ᎾᏍᎩᏃ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᏚᏬᏁᏔᏅ, ᎦᎸᎳᏗ ᏙᏣᏕᏓᏂᎸᏤᎢ, ᎠᎴ ᎠᎦᏘᏏ ᎢᏗᏢ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏬᎸ ᎤᏪᏁᎢ.
Ambuye Yesu atatha kuyankhulana nawo, anatengedwa kupita kumwamba ndipo anakhala kudzanja lamanja la Mulungu.
20 ᎤᏁᏅᏎᏃ ᎠᎴ ᏂᎬᎾᏛ ᎤᎾᎵᏥᏙᏂᏙᎴᎢ, ᎤᎬᏫᏳᎯ ᏔᎵ ᎤᏛᏗᏕᎨ ᏚᏂᎸᏫᏍᏓᏁᎲᎢ, ᎠᎴ ᎠᏂᏁᎬ ᎠᏍᏓᏱᏗᏍᏗᏍᎨ ᎤᏰᎸᏛ ᎤᎵᏠᏯᏍᏗᏕᎬᎢ. ᎡᎺᏅ.
Pamenepo ophunzira aja anapita ndi kukalalikira ponseponse, ndipo Ambuye anagwira nawo ntchito pamodzi, ndipo anatsimikizira mawuwo ndi zizindikiro zimene ankachita.

< ᎣᏍᏛ ᎧᏃᎮᏛ ᎹᎦ ᎤᏬᏪᎳᏅᎯ 16 >