< ᎣᏍᏛ ᎧᏃᎮᏛ ᏣᏂ ᎤᏬᏪᎳᏅᎯ 8 >

1 ᏥᏌᏃ ᎤᎵᏩᏲᎢ ᎣᏓᎸ ᏬᎶᏒᎩ.
Koma Yesu anapita ku phiri la Olivi.
2 ᏑᎾᎴᏉᏃ ᏔᎵᏁ ᎤᏛᏅ-ᏗᎦᎳᏫᎢᏍᏗᏱ ᎤᎷᏨᎩ; ᎠᎴ ᏂᎦᏛ ᏴᏫ ᎥᎬᏩᎷᏤᎸᎩ; ᎤᏪᏅᏃ ᏑᏪᏲᏅᎩ.
Mmamawa Iye anaonekeranso ku Nyumba ya Mulungu kumene anthu onse anamuzungulira ndipo Iye anakhala pansi nawaphunzitsa.
3 ᏗᏃᏪᎵᏍᎩᏃ ᎠᎴ ᎠᏂᏆᎵᏏ ᎬᏩᏘᏃᎮᎸᎩ ᎠᎨᏴ ᎠᏓᏲᏁᎲ ᎠᏥᏂᏴᏛ; ᎠᏰᎵᏃ ᎤᏂᎧᏅ,
Aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi anabweretsa mkazi amene anagwidwa akuchita chigololo. Iwo anamuyimiritsa patsogolo pa anthu ndipo
4 ᎯᎠ ᏂᎬᏩᏪᏎᎸᎩ; ᏔᏕᏲᎲᏍᎩ, ᎯᎠ ᎠᎨᏴ ᎠᏓᏲᏁᎲ ᏕᎦᏅᎬᎢ ᎠᏥᏂᏴᎲᎩ.
anati kwa Yesu, “Aphunzitsi, mkazi uyu tinamugwira akuchita chigololo.
5 Ꭷ, ᎼᏏ ᎣᎩᏁᏤᎸᎩ ᏗᎧᎿᎭᏩᏛᏍᏗᏱ ᎾᏍᎩ ᎢᏳᎾᏍᏗ ᏅᏯ ᏗᎨᎬᏂᏍᏙᏗᏱ; ᎠᏎᏃ ᏂᎯ ᎦᏙ ᎭᏗᎭ?
Mʼmalamulo a Mose anatilamulira kuti akazi otere tiwagende ndi miyala. Tsopano Inu mukuti chiyani?”
6 ᎾᏍᎩ ᎯᎠ ᏄᏂᏪᏒᎩ ᎠᏂᏌᏛᎥᏍᎬᎩ, ᎤᏄᎯᏍᏙᏗᏱᏉ ᎤᏂᏰᎸᏒᎩ. ᎠᏎᏃ ᏥᏌ ᎤᏗᏌᏓᏛᎩ, ᎦᏰᏌᏛᏃ ᎤᏩᏔᏅᎩ ᎤᏬᏪᎳᏅᎩ ᎦᏙᎯ.
Iwo anagwiritsa ntchito funsoli ngati msampha, ndi cholinga choti apeze chifukwa cha kumuneneza Iye. Koma Yesu anawerama pansi ndi kuyamba kulemba pa dothi ndi chala chake.
7 ᎠᏏᏉᏃ ᎠᏂᏱᎵᏒ ᎬᏩᏛᏛᎲᏍᎬ ᎤᏓᏥᏃᎯᏍᏔᏅᎩ ᎯᎠ ᏂᏚᏪᏎᎸᎩ; ᎩᎶ ᎤᏓᏑᏰᏍᏗ ᎤᏍᎦᏅᏨᎯ ᏂᎨᏒᎾ ᎾᏍᎩ ᎢᎬᏱ ᏫᏓᏓᎴᏅᏓ ᏅᏯ ᏫᎬᏂᏍᏓ.
Pamene iwo anapitirira kumufunsa, Iye anaweramuka ndipo anawawuza kuti, “Ngati wina wa inu alipo wopanda tchimo, ayambe iyeyo kumugenda ndi miyala mkaziyu.”
8 ᏔᎵᏁᏃ ᎤᏗᏌᏓᏛ, ᎦᏙᎯ ᎤᏬᏪᎳᏅᎩ.
Iye anaweramanso pansi ndi kulemba pa dothi.
9 ᎾᏍᎩᏃ ᎤᎾᏛᎦᏅ, ᎠᎴ ᏧᎾᏓᏅᏙ ᎬᏩᏄᎯᏍᏔᏅ, ᎤᏂᏄᎪᏨᎩ ᏌᏉ ᎤᏛᏂᏛ ᎤᏓᏂᎵᎨ ᏚᏓᎴᏅᏔᏅᎩ, ᎣᏂᏱ ᏫᎬᏩᏛᏅᎩ; ᏥᏌᏃ ᎤᏩᏒ ᏄᎵᏍᏔᏅᎩ, ᎠᎨᏴᏃ ᎠᏰᎵ ᎦᏙᎬᎩ.
Iwo atamva izi anayamba kuchoka mmodzimmodzi, akuluakulu poyamba, mpaka Yesu anatsala yekha ndi mkaziyo atayimirira pomwepo.
10 ᏥᏌᏃ ᎤᏓᏥᏃᎯᏍᏔᏅ, ᎠᎴ ᎠᎨᏴᏉ ᎤᏩᏒ ᎤᎪᎲ, ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎸᎩ; ᎯᎨᏴ, ᎭᏢ Ꮎ ᎨᏧᎯᏍᏗᏍᎩ? ᏝᏍᎪ ᎩᎶ ᏣᏍᎦᏅᏨᎢ ᏱᏕᎫᎪᏓ?
Yesu anaweramuka ndipo anamufunsa iye kuti, “Akuluakulu aja ali kuti? Kodi palibe amene wakutsutsa?”
11 ᎯᎠ ᏄᏪᏒᎩ; ᎥᏝ ᎩᎶ, ᏣᎬᏫᏳᎯ. ᏥᏌᏃ ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎸᎩ; ᎥᏝ ᎾᏍᏉ ᎠᏴ ᏣᏍᎦᏅᏨ ᏱᏗᎫᎪᏗᎭ. ᏥᎮᎾ, ᎠᎴ ᏞᏍᏗ ᎢᎸᎯᏳ ᎿᎭᏉ ᏱᏣᏍᎦᏅᏤᏍᏗ.
Iye anati, “Ambuye, palibe ndi mmodzi yemwe.” “Inenso sindikukutsutsa iwe. Pita kuyambira tsopano usakachimwenso.”
12 ᎠᎴᏬ ᏥᏐ ᏚᏬᏁᏔᏅᎩ, ᎯᎠ ᏂᏚᏪᏎᎸᎩ; ᎠᏴ ᎡᎶᎯ ᎢᎦ ᏥᏯᏘᏍᏓᏁᎯ; ᎩᎶ ᎠᎩᏍᏓᏩᏕᎨᏍᏗ ᎥᏝ ᎤᎵᏏᎬ ᏱᎦᏰᏙᎮᏍᏗ; ᎠᏛᏂᏗᏍᏙᏗᏍᎩᏂ ᎢᎦ ᎤᏤᎵᎦ ᎨᏎᏍᏗ.
Yesu atayankhulanso kwa anthu, anati, “Ine ndine kuwunika kwa dziko lapansi. Aliyense amene anditsata Ine sadzayenda mu mdima, koma adzakhala ndi kuwala kotsogolera anthu ku moyo.”
13 ᎿᎭᏉᏃ ᎠᏂᏆᎵᏏ ᎯᎠ ᏅᎬᏩᏪᏎᎸᎩ; ᏨᏒᏉ ᎭᏓᏃᎮᎭ, ᎯᏃᎮᏍᎬ ᎥᏝ ᏳᏙᎯᏳᎭ.
Afarisi anamutsutsa Iye nati, “Iwe ukudzichitira umboni wa Iwe mwini, umboni wako siwoona.”
14 ᏥᏌ ᎤᏁᏨᎩ, ᎯᎠ ᏂᏚᏪᏎᎸᎩ; ᎠᏋᏒᏉ ᎾᏍᏉ ᏱᎦᏓᏃᎮᎭ, ᎠᏎ ᏥᏃᎮᏍᎬ ᎤᏙᎯᏳᎭ; ᏥᎦᏔᎭᏰᏃ ᏗᏆᏓᎴᏅᎢ ᎠᎴ ᏫᏥᎦᏛᎢ. ᏂᎯᏍᎩᏂ ᎥᏝ ᏱᏥᎦᏔᎭ ᏗᏆᏓᎴᏅᎢ ᎠᎴ ᏫᏥᎦᏛᎢ.
Yesu anayankha kuti, “Ngakhale Ine ndidzichitire umboni, umboni wangawu ndi woona, pakuti Ine ndikudziwa kumene ndinachokera ndi kumene ndikupita. Koma inu simukudziwa ndi pangʼono pomwe kumene ndinachokera kapena kumene ndikupita.
15 ᏂᎯ ᏕᏧᎪᏗᏍᎪ ᎤᏇᏓᎵᏉ ᏧᏬᎪᏙᏗ ᎨᏒᎢ; ᎠᏴ ᎥᏝ ᎩᎶ ᏱᏗᏥᏳᎪᏓᏁᎰᎢ.
Inu mumaweruza potsata maganizo a anthu chabe. Ine sindiweruza munthu wina aliyense.
16 ᎠᏎᏃ ᎾᏍᏉ ᏱᏗᎫᎪᏗᎭ, ᏓᏇᎪᏔᏅ ᏑᏳᎪᏛ ᏱᎩ. ᎥᏝᏰᏃ ᎠᏋᏒᏉ ᏱᎩ, ᎠᎦᏴᎵᎨᏰᏃ ᏅᏛᎩᏅᏏᏛ ᎣᎩᎾᎵᎪᎭ.
Koma Ine ndikati ndiweruze, ndimaweruza molondola, chifukwa Ine sindili ndekha koma ndili ndi Atate amene anandituma.
17 ᎠᎴ ᎾᏍᏉ ᎪᏪᎳ ᏗᏥᎧᎿᎭᏩᏛᏍᏗᏱ ᎾᏍᎩ ᎠᏂᏔᎵ ᎤᏂᏃᎮᎸᎯ ᎨᏒ ᎤᏙᎯᏳᎯᏯ ᎨᏒᎢ.
Mʼmalamulo anu munalembedwa kuti umboni wa anthu awiri ndi wovomerezeka.
18 ᎠᏴ ᎠᏋᏒ ᎦᏓᏃᎮᏍᎩ, ᎠᎦᏴᎵᎨᏃ ᏅᏛᎩᏅᏏᏛ ᎾᏍᏉ ᎠᏴ ᎠᎩᏃᎮᎭ.
Ine ndikudzichitira ndekha umboni; ndipo mboni inanso ndi Atate amene anandituma.”
19 ᎿᎭᏉ ᎯᎠ ᏅᎬᏩᏪᏎᎸᎩ, ᎭᏢ ᏣᏙᏓ? ᏥᏌ ᎯᎠ ᏂᏚᏪᏎᎸᎩ; ᎥᏝ ᎠᏴ ᏱᏍᎩᎦᏔᎭ, ᎠᎴ ᎥᏝ ᏰᏥᎦᏔᎭ ᎡᏙᏓ. ᎢᏳᏃ ᎠᏴ ᏱᏍᎩᎦᏔᎮᎢ, ᎾᏍᏉ ᏰᏥᎦᏔᎮ ᎡᏙᏓ.
Kenaka iwo anamufunsa Iye kuti, “Kodi Atate anuwo ali kuti?” Yesu anayankha kuti, “Inu simundidziwa Ine. Atate anganso simuwadziwa. Mukanandidziwa Ine, mukanawadziwanso Atate anga.”
20 ᎾᏍᎩ ᎯᎠ ᏄᏪᏒᎩ ᏥᏌ ᎠᏕᎸ ᏗᏍᏆᏂᎪᏗᏱ, ᎾᎯᏳ ᏓᏕᏲᎲᏍᎬ ᎤᏛᎤ-ᏗᎦᎳᏫᎢᏍᏗᏱ; ᎠᎴ ᎥᏝ ᎩᎶ ᏳᏂᏴᎮᎢ, ᎥᏝᏰᏃ ᎠᏏ ᏳᏍᏆᎸᎡᎮᎢ.
Iye anayankhula mawu awa pamene amaphunzitsa Nyumba ya Mulungu pafupi ndi malo amene amaponyapo zopereka. Komabe palibe amene anamugwira Iye, chifukwa nthawi yake inali isanakwane.
21 ᎿᎭᏉᏃ ᏥᏌ ᏔᎵᏁ ᎯᎠ ᏂᏚᏪᏎᎸᎩ; ᏓᎦᏓᏅᏏ, ᏂᎯᏃ ᏍᎩᏲᎮᏍᏗ, ᎠᎴ ᎠᏎ ᎠᏍᎦᏂ ᎨᏒ ᏙᏓᏥᏲᎱᏏ, ᎠᎴ ᏫᏥᎦᏛ ᎥᏝ ᏫᏴᎨᏥᎷᎩ.
Kenakanso Yesu anawawuza kuti, “Ine ndikupita, ndipo mudzandifunafuna, koma mudzafa muli mʼmachimo anu. Kumene ndikupita, inu simungabwereko.”
22 ᎿᎭᏉᏃ ᎠᏂᏧᏏ ᎯᎠ ᏄᏂᏪᏒᎩ, ᏥᎪ ᎤᏩᏒ ᏛᏓᎵ? ᎯᎠ ᏥᏂᎦᏪᎭ; ᏫᏥᎦᏛ ᎥᏝ ᏫᏴᎨᏥᎷᎩ.
Izi zinachititsa Ayuda kufunsa kuti, “Kodi adzadzipha yekha? Kodi ndicho chifukwa chake akuti, ‘Kumene ndikupita, inu simungabwereko?’”
23 ᎯᎠᏃ ᏂᏚᏪᏎᎸᎩ; ᏂᎯ ᎡᎳᏗ ᎢᏣᏓᎴᏅᎯ; ᎠᏴ ᎦᎸᎳᏗ ᏅᏛᏆᏓᎴᏅᎯ. ᏂᎯ ᎠᏂ ᎡᎶᎯ ᎢᏣᏓᎴᏅᎯ; ᎠᏴ ᎥᏝ ᎠᏂ ᎡᎶᎯ ᎠᏆᏓᎴᏅᎯ ᏱᎩ.
Koma Iye anapitiriza kuti, “Inu ndi ochokera pansi pano. Ine ndine wochokera kumwamba. Inu ndinu anthu a dziko la pansi. Ine sindine wa dziko lapansi lino.
24 ᎾᏍᎩ ᎢᏳᏍᏗ ᎯᎠ ᏂᏨᏪᏏ; ᎠᏎ ᎨᏥᏍᎦᏂᏉ ᎨᏒ ᏙᏓᏥᏲᎱᏏ; ᎢᏳᏰᏃ ᏂᏦᎯᏳᎲᏍᎬᎾ ᎢᎨᏎᏍᏗ ᎠᏴ ᎾᏍᎩ ᎨᏒᎢ, ᎠᏎ ᎨᏥᏍᎦᏂ ᎨᏒ ᏙᏓᏥᏲᎱᏏ.
Ine ndinakuwuzani kuti mudzafera mʼmachimo anu ngati simukhulupirira kuti Ine Ndine. Ndithu inu mudzafera mʼmachimo anu.”
25 ᎿᎭᏉᏃ ᎯᎠ ᏅᎬᏩᏪᏎᎸᎩ; ᎦᎪᏂᎯ? ᏥᏌᏃ ᎯᎠ ᏂᏚᏪᏎᎸᎩ; ᎾᏍᎩᏉ ᏥᏨᏲᏎᎰᎢ, ᎤᏙᎯᏳᎯᏯ ᎾᏍᎩᏉ.
Iwo anafunsa kuti, “Ndinu ndani?” Yesu anayankha kuti, “Monga Ine ndakhala ndikunena nthawi yonseyi,
26 ᎤᏣᏘ ᎪᎱᏍᏗ ᎠᎩᎭ ᎢᏨᏲᏎᏗ, ᎠᎴ ᏗᏨᏳᎪᏓᏁᏗ; ᎠᏎᏃ ᏅᏛᎩᏅᏏᏛ ᏚᏳᎪᏛᎢ; ᎠᏴᏃ ᎡᎶᎯ ᏥᏃᎮᎮᎭ ᎾᏍᎩ ᏄᏍᏛ ᏥᏯᏛᎦᏁᎸᎢ.
ndili ndi zambiri zoti ndinene zoweruza inu. Koma Iye amene anandituma ndi woona, ndipo chimene Ine ndamva kuchokera kwa Iye, ndi chimene ndimaliwuza dziko lapansi.”
27 ᎥᏝ ᏳᏃᎵᏤ ᎠᎦᏴᎵᎨ ᎦᏛᎬ ᎾᏍᎩ ᏕᎦᏬᏁᏗᏍᎬᎢ.
Iwo sanazindikire kuti Iye amawawuza za Atate ake.
28 ᎾᏍᎩ ᎢᏳᏍᏗ ᏥᏌ ᎯᎠ ᏂᏚᏪᏎᎸᎩ; ᏴᏫ ᎤᏪᏥ ᎡᏥᏌᎳᏓᏅᎭ, ᎿᎭᏉ ᏓᏣᏙᎴᎰᏏ ᎠᏴ ᎾᏍᎩ ᎨᏒᎢ, ᎠᎴ ᎠᏋᏒᏉ ᎠᏆᏓᏅᏖᏛ ᎪᎱᏍᏗ ᏂᏓᎩᎸᏫᏍᏓᏁᎲᎾ ᎨᏒᎢ, ᎡᏙᏓᏉᏍᎩᏂ ᎠᏇᏲᏅ ᎾᏍᎩ ᏥᏃᎮᏍᎬᎢ.
Choncho Yesu anati, “Inu mukadzapachika Mwana wa Munthu, pamenepo mudzadziwa kuti Ine Ndine. Mudzadziwa kuti sindichita kalikonse pa Ine ndekha koma ndimayankhula zokhazo zimene Atate anandiphunzitsa.
29 ᏅᏛᎩᏅᏏᏛ ᎣᎩᎾᎵᎪᎭ; ᎠᎦᏴᎵᎨ ᎥᏝ ᏯᏋᏕᏨ, ᏂᎪᎯᎸᏰᏃ ᏓᎩᎸᏫᏍᏓᏁᎰ ᎣᏍᏛ ᎤᏰᎸᏗ.
Iye amene anandituma Ine ali nane pamodzi. Iye sanandisiye ndekha popeza nthawi zonse ndimachita zomwe zimamukondweretsa Iye.”
30 ᎠᏏᏉ ᎾᏍᎩ ᎯᎠ ᏂᎦᏪᏍᎬᎩ, ᎤᏂᏣᏛ ᎬᏬᎯᏳᏅᎩ.
Pamene Iye ankayankhula zimenezi, ambiri anamukhulupirira.
31 ᎿᎭᏉ ᏥᏌ ᎯᎠ ᏂᏚᏪᏎᎸᎩ ᎠᏂᏧᏏ ᎬᏬᎯᏳᎲᏍᎩ; ᎢᏳᏃ ᏕᏥᎧᎿᎭᏩᏗᏎᏍᏗ ᎠᎩᏁᏨᎢ, ᎤᏙᎯᏳᎯᏯ ᏍᎩᏍᏓᏩᏗᏙᎯ ᎨᏎᏍᏗ.
Kwa Ayuda amene anamukhulupirira, Yesu anati, “Ngati inu mutsatira chiphunzitso changa, ndithu ndinu ophunzira anga.
32 ᎠᎴ ᏓᏥᎦᏙᎥᏏ ᏚᏳᎪᏛᎢ, ᏚᏳᎪᏛᏃ ᏂᏕᏥᎾᏝᎥᎾ ᏅᏓᏨᏁᎵ.
Tsono mudzadziwa choonadi, ndipo choonadicho chidzakumasulani.”
33 ᎬᏩᏁᏤᎸ ᎯᎠ ᏂᎬᏩᏪᏎᎸᎩ; ᎠᏴ ᎡᏆᎭᎻ ᎤᏁᏢᏔᏅᏛ, ᎠᎴ ᎥᏝ ᎢᎸᎯᏳ ᎩᎶ ᏱᏙᎩᎾᏢᏃᎢ, ᎦᏙᏃ ᏂᏕᏥᎾᏝᎥᎾ ᏅᏓᏰᏨᏁᎵ, ᏣᏗᎭ?
Iwo anamuyankha Iye kuti, “Ife ndife zidzukulu za Abrahamu ndipo sitinakhalepo akapolo a wina aliyense. Kodi mukunena bwanji kuti, ‘Ife tidzamasulidwa?’”
34 ᏥᏌ ᏚᏁᏤᎸ ᎯᎠ ᏂᏚᏪᏎᎸᎩ; ᎤᏙᎯᏳᎯᏯ ᎤᏙᎯᏳᎯᏯ ᎯᎠ ᏂᏨᏪᏎᎭ; ᎩᎶ ᏣᏍᎦᏅᎪᎢ ᎠᏍᎦᏂ ᎤᎾᏝᎢ ᎨᏐᎢ.
Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense wochita tchimo ndi kapolo wa tchimolo.
35 ᎠᏥᎾᏝᎢᏃ ᎥᏝ ᎠᏓᏁᎸ ᏂᎪᎯᎸ ᎡᎯ ᏱᎨᏐᎢ; ᎠᎦᏅᎩᏍᎩᏂ ᏂᎪᎯᎸ ᎡᎰᎢ. (aiōn g165)
Pajatu kapolo alibe malo wokhazikika mʼbanja, koma mwana ndi wa mʼbanjamo nthawi zonse. (aiōn g165)
36 ᎾᏍᎩ ᎢᏳᏍᏗ ᎢᏳᏃ ᎠᎦᏅᎩ ᏂᏕᏥᎾᏝᎥᎾ ᏱᏂᏨᏁᎸ ᎤᏙᎯᏳᏒ ᏂᏕᏥᎾᏝᎥᎾ ᏱᎩ.
Nʼchifukwa chake ngati Mwana adzakumasulani, mudzakhala mfulu ndithu.
37 ᏥᎦᏔᎭ ᏂᎯ ᎡᏆᎭᎻ ᎤᏁᏢᏔᏅᏛ ᎨᏒᎢ; ᎠᏎᏃ ᎢᏣᏚᎵ ᏍᎩᎢᏍᏗᏱ, ᏅᏗᎦᎵᏍᏙᏗᎭ ᏥᏁᎬ ᏕᏣᏓᏅᏛ ᏫᎾᏴᎯᎲᎾ ᎨᏒᎢ.
Ine ndikudziwa kuti inu ndinu zidzukulu za Abrahamu. Chonsecho inu mwakonzeka kundipha Ine, chifukwa mawu anga alibe malo mwa inu.
38 ᏄᏍᏛ ᎠᎩᎪᎲ ᎡᏙᏙᏱ ᎾᏍᎩ ᏥᏁᎪᎢ; ᏂᎯᏃ ᏄᏍᏛ ᎢᏥᎪᎲ ᎢᏥᏙᏙᏱ ᎾᏍᎩ ᏂᏣᏛᏁᎰᎢ.
Ine ndikukuwuzani zimene ndaziona pamaso pa Atate, ndipo inu mukuchita zimene mwazimva kwa abambo anu.”
39 ᎤᏂᏁᏨ ᎯᎠ ᏅᎬᏩᏪᏎᎸᎩ; ᎡᏆᎭᎻ ᎣᎩᏙᏓ. ᏥᏌ ᎯᎠ ᏂᏚᏪᏎᎸᎩ; ᎢᏳᏃ ᏂᎯ ᎡᏆᎭᎻ ᏧᏪᏥ ᏱᎩ, ᎡᏆᎭᎻ ᏧᎸᏫᏍᏓᏁᏗ ᎨᏒ ᏱᏗᏥᎸᏫᏍᏓᏁᎭ.
Iwo anayankha kuti, “Ife abambo athu ndi Abrahamu.” Yesu anati, “Inu mukanakhala ana a Abrahamu, bwenzi mukuchita zinthu zimene Abrahamuyo ankachita.
40 ᎠᏎᏃ ᎢᏣᏚᎵ ᏍᎩᎢᏍᏗᏱ ᎠᏴ ᏚᏳᎪᏛ ᎢᏨᏃᏁᎸᎯ, ᎾᏍᎩ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᏥᏯᏛᎦᏁᎸᎯ ᎨᏒᎢ; ᎥᏝ ᎾᏍᎩ ᏱᎾᏛᏁᎮ ᎡᏆᎭᎻ.
Koma mmene zililimu, inu mwatsimikiza kundipha Ine, munthu amene ndinakuwuzani choonadi chimene Ine ndinachimva kuchokera kwa Mulungu. Abrahamu sanachite zinthu zoterezi.
41 ᎢᏥᏙᏓ ᏧᎸᏫᏍᏓᏁᏗ ᎨᏒ ᏕᏥᎸᏫᏍᏓᏁᎰᎢ. ᎿᎭᏉᏃ ᎯᎠ ᏅᎬᏩᏪᏎᎸᎩ; ᎥᏝ ᎤᏕᎵᏛ ᏗᏂᏏᏅᎯ ᎣᎩᎾᏄᎪᏨᎯ ᏱᎩ; ᏌᏉ ᎡᎭ ᎣᎩᏙᏓ-ᎾᏍᎩ ᎤᏁᎳᏅᎯ.
Inu mukuchita zinthu zimene abambo anu amachita.” Iwo anatsutsa kuti, “Ife si ana amʼchigololo, Atate amene tili nawo ndi Mulungu yekha.”
42 ᏥᏌ ᎯᎠ ᏂᏚᏪᏎᎸᎩ; ᎢᏳᏃ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎢᏥᏙᏓ ᏱᎩ, ᏍᎩᎨᏳᎢᏳ ᏱᎩ; ᎤᏁᎳᏅᎯᏱᏰᏃ ᏗᏆᏓᎴᏅ ᎠᎩᎷᏥᎸ; ᎠᎴ ᎥᏝ ᎠᏋᏒᏉ ᎠᏆᏓᏅᏖᏛᏯᎩᎷᏥᎸ, ᏗᎩᏅᏒᏍᎩᏂ.
Yesu anawawuza kuti, “Mulungu akanakhala Atate anu, inu mukanandikonda Ine, pakuti Ine ndinachokera kwa Mulungu ndipo tsopano ndili pano. Ine sindinabwere mwa Ine ndekha.
43 ᎦᏙᏃ Ꮭ ᏱᏦᎵᎦ ᏥᏬᏂᏍᎬᎢ? ᏅᏗᎦᎵᏍᏙᏗᏍᎩᏂ ᏥᏁᎬ ᏰᎵ ᎨᏣᏛᎪᏗ ᏂᎨᏒᎾ ᎨᏒᎢ.
Nʼchifukwa chiyani simukumvetsetsa mawu anga? Chifukwa chake nʼchakuti simungathe kumva zoyankhula zanga.
44 ᎢᏥᏙᏓ ᎠᏍᎩᎾ ᏅᏓᏣᏓᎴᏅᎯ ᏂᎯ, ᎠᎴ ᎢᏥᏙᏓ ᎤᏲ ᏚᎸᏫᏍᏓᏁᎲ ᎢᏣᏛᏁᏗᏱ ᎢᏣᏚᎵᎭ. ᎾᏍᎩ ᏴᏫ ᏗᎯᎯ ᏂᎨᏐ ᏗᏓᎴᏂᏍᎬᎢ, ᎠᎴ ᎤᏙᎯᏳᎯ ᎨᏒ ᎥᏝ ᏱᏚᎧᎿᎭᏩᏛᏎᎢ, ᎥᏝᏰᏃ ᎤᏙᎯᏳᎯ ᎨᏒ ᏳᏪᎭ. ᎦᏰᎪᎩ ᎧᏁᎩ ᎤᏤᎵᎦᏉ ᎧᏁᎪᎢ; ᎦᏰᎪᎩᏰᏃ ᎾᏍᎩ, ᎠᎴ ᎤᎦᏴᎵᎨ ᎦᏰᎪᎩ ᎨᏒᎢ.
Inu ndinu ana a mdierekezi. Iye ndiye abambo anu ndipo mukufuna kuchita zimene abambo anuwo amakhumba. Iye anali wakupha kuyambira pachiyambi, sanasunge choonadi, pakuti mwa iye mulibe choonadi. Pamene Iye anena bodza, amayankhula chiyankhulo chobadwa nacho, popeza ndi wabodza ndipo ndi bambo wa mabodza.
45 ᎠᏎᏃ ᏚᏳᎪᏛ ᏥᏁᎬ ᏅᏗᎦᎵᏍᏙᏗᎭ ᎥᏝ ᏱᏍᎩᏲᎢᏳᎲᏍᎦ.
Koma chifukwa ndikuwuzani choonadi, inu simukundikhulupirira Ine!
46 ᎦᎪ ᎤᏓᏑᏯ ᎯᎠ ᏥᏂᏣᏛᏅ ᎬᏂᎨᏒ ᎢᎬᏩᏁᏗ ᎠᎩᏍᎦᏅᏨᎯ ᎨᏒᎢ? ᎢᏳᏃ ᏚᏳᎪᏛ ᏱᏥᏁᎦ, ᎦᏙᏃ Ꮭ ᏱᏍᎩᏲᎢᏳᎲᏍᎦ?
Ndani mwa inu angatsimikize kuti ndine wochimwa? Ngati Ine ndikunena choonadi, nʼchifukwa chiyani simukundikhulupirira?
47 ᎾᏍᎩ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᏅᏓᏳᏓᎴᏅᎯ ᎨᏒ ᎾᏍᎩ ᎠᏛᎩᏍᎪ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎧᏁᎬᎢ; ᏂᎯ ᏂᏣᏛᎩᏍᎬᎾ ᏥᎩ ᏅᏗᎦᎵᏍᏙᏗ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᏅᏓᏣᏓᎴᏅᎯ ᏂᎨᏒᎾ ᎨᏒᎢ.
Munthu wochokera kwa Mulungu amamva zimene Mulungu amanena. Chifukwa chimene simumvera nʼchakuti, inuyo sindinu ochokera kwa Mulungu.”
48 ᎿᎭᏉᏃ ᎠᏂᏧᏏ ᎤᏂᏁᏨᎩ, ᎯᎠ ᏄᏂᏪᏎᎸᎩ; ᏝᏍᎪ ᏚᏳᎪᏛ ᏲᏥᏁᎦ, ᏌᎺᎵᏱ ᎮᎯ ᎠᎴ ᎠᏍᎩᎾ ᏣᏯᎢ, ᏥᏨᏲᏎᎭ?
Ayuda anamuyankha Iye kuti, “Kodi ife sitikulondola ponena kuti Inu ndi Msamariya ndi wogwidwa ndi chiwanda?”
49 ᏥᏌ ᎯᎠ ᏂᏚᏪᏎᎸᎩ; ᎥᏝ ᎠᏍᎩᎾ ᏯᎩᏯᎠ, ᏥᎸᏉᏗᏉᏍᎩᏂ ᎡᏙᏓ; ᏂᎯᏃ ᎠᏴ ᎨᏍᎩᏐᏢᎢᏍᏗᎭ.
Yesu anati, “Ine sindinagwidwe ndi chiwanda, koma ndimalemekeza Atate anga, koma inu mukundinyoza.
50 ᎠᏎᏃ ᎥᏝ ᏯᎩᏲᎭ ᎠᏋᏒ ᎥᎩᎸᏉᏗᏱ; ᎡᎭ ᎤᏲᎯ ᎠᎴ ᏗᎫᎪᏗᏍᎩ.
Ine sindidzifunira ndekha ulemu; koma alipo wina amene amandifunira, ndipo Iyeyo ndiye woweruza.
51 ᎤᏙᎯᏳᎯᏯ ᎤᏙᎯᏳᎯᏯ ᎯᎠ ᏂᏨᏪᏎᎭ, ᎢᏳᏃ ᎩᎶ ᎠᏍᏆᏂᎪᏗᏍᎨᏍᏗ ᏥᏁᎬᎢ, ᎾᏍᎩ ᎥᏝ ᎢᎸᎯᏳ ᎠᏲᎱᎯᏍᏗ ᎨᏒ ᎤᎪᏩᏛᏗ ᏱᎨᏎᏍᏗ. (aiōn g165)
Ine ndikukuwuzani choonadi, munthu akasunga mawu anga, sadzafa konse.” (aiōn g165)
52 ᎿᎭᏉᏃ ᎠᏂᏧᏏ ᎯᎠ ᏅᎬᏩᏪᏎᎸᎩ; ᎿᎭᏉ ᎣᏣᏙᎴᎰᎯ ᎠᏍᎩᎾ ᏣᏯᎥᎢ. ᎡᏆᎭᎻ ᎤᏲᎱᏒ, ᎠᎴ ᎠᎾᏙᎴᎰᏍᎩ, ᏂᎯᏃ ᎯᎠ ᏂᎯᏪᎭ; ᎢᏳᏃ ᎩᎶ ᎠᏍᏆᏂᎪᏗᏍᎨᏍᏗ ᏥᏁᎬᎢ, ᎾᏍᎩ ᎥᏝ ᎢᎸᎯᏳ ᎠᏲᎱᎯᏍᏗ ᎨᏒ ᎤᏙᎴᎰᏍᏗ ᏱᎨᏎᏍᏗ. (aiōn g165)
Pamenepo Ayuda anafuwula kuti, “Tsopano ife tadziwadi kuti Inu ndi wogwidwa ndi chiwanda! Abrahamu anafa ndiponso aneneri, koma Inu mukunena kuti, ‘Ngati munthu asunga mawu anga, sadzafa.’ (aiōn g165)
53 ᏥᎪ ᏂᎯ ᎤᏟ ᎡᏣᎸᏉᏗᏳ ᎡᏍᎦᏉ ᎡᏆᎭᎻ ᎣᎩᏙᏓ, ᏧᏲᎱᏒ? ᎠᎴ ᎾᏍᏉ ᎠᎾᏙᎴᎰᏍᎩ ᏚᏂᏲᎱᏒ. ᎦᎪ ᏂᎯ ᎭᏤᎸᏍᎦ?
Kodi ndinu wa mkulu kuposa abambo athu Abrahamu? Iye anafa, ndiponso aneneri onse. Inu mukuganiza kuti ndinu yani?”
54 ᏥᏌ ᎯᎠ ᏂᏚᏪᏎᎸᎩ; ᎢᏳᏃ ᎠᏋᏒ ᏱᎦᏓᎸᏉᏗᎭ, ᎥᎩᎸᏉᏗᏳ ᎠᏎᏉᏉ ᏱᎩ; ᎡᏙᏓᏍᎩᏂ ᎠᎩᎸᏉᏗᏍᎩ, ᎾᏍᎩ ᎠᏴ ᎣᎦᏁᎳᏅᎯ ᏥᏣᏗᎭ.
Yesu anayankha kuti, “Ngati Ine ndidzilemekeza ndekha, ulemu wangawo ndi wosatanthauza kanthu. Atate anga amene inu mukuti ndi Mulungu wanu, ndiye amene amandilemekeza Ine.
55 ᎠᏎᏃ ᎥᏝ ᏰᏥᎦᏔᎭ, ᎠᏴᏍᎩᏂ ᏥᎦᏔᎭ; ᎢᏳᏃ ᎥᏝ ᏱᏥᎦᏔᎭ ᏱᏚᏗᎭ ᏥᏰᎪᎩᏉ ᏱᎩ, ᏂᎯ ᏥᏂᏣᏍᏗ ᎾᏍᎩᏯᎢ; ᎠᏎᏃ ᏥᎦᏔᎭ, ᎠᎴ ᎤᏁᏨ ᎠᎩᏍᏆᏂᎪᏗ.
Ngakhale kuti inuyo simukumudziwa, Ineyo ndikumudziwa. Ngati Ine nditanena kuti sindikumudziwa, Ineyo nditha kukhala wabodza ngati inuyo, koma Ine ndimamudziwa ndipo ndimasunga mawu ake.
56 ᎢᏥᏙᏓ ᎡᏆᎭᎻ ᎠᎵᎮᎵᏍᏗ ᎤᏚᎩ ᎤᏩᏒ ᎤᎪᏩᏛᏗᏱ ᎪᎯ ᎨᏒ ᎠᏴ ᎨᎥᎢ, ᎠᎴ ᎤᎪᎲᎩ ᎠᎴ ᎣᏏᏳ ᎤᏓᏅᏓᏛᎩ.
Abambo anu Abrahamu anakondwera poyembekezera kubwera kwanga. Iwo anandiona ndipo anasangalala.”
57 ᎿᎭᏉᏃ ᎠᏂᏧᏏ ᎯᎠ ᏅᎬᏪᏎᎸᎩ; ᎥᏝ ᎠᏏ ᎯᏍᎩᏍᎪᎯ ᎢᏣᏕᏘᏴᏛ ᏱᎩ; ᏥᏌᏃ ᎯᎪᎥᎯ ᎢᎩ ᎡᏆᎭᎻ?
Ayuda anati kwa Iye, “Inu sumunafike nʼkomwe zaka makumi asanu, ndipo mukuti munamuona Abrahamu!”
58 ᏥᏌ ᎯᎠ ᏂᏚᏪᏎᎸᎩ; ᎤᏙᎯᏳᎯᏯ ᎤᏙᎯᏳᎯᏯ ᎯᎠ ᏂᏨᏪᏎᎭ; ᎠᏏᏉ ᎡᏆᎭᎻ ᏁᎲᎾ ᏥᎨᏒᎩ, ᎠᏴ ᏂᎨᎣᎢ.
Yesu anayankha kuti, “Ine ndikukuwuzani choonadi, Abrahamu asanabadwe, Ine Ndine!”
59 ᎿᎭᏉᏃ ᏅᏯ ᏚᏂᎩᏒᎩ, ᏗᎬᏩᏂᏍᏙᏗ, ᎠᏎᏃ ᏥᏌ ᎤᏗᏍᎦᎳᏅᎩ, ᎠᎴ ᎤᏛᏅ-ᏗᎦᎳᏫᎢᏍᏗᏱ ᎤᏄᎪᏨᎩ, ᎠᏰᎵ ᎠᏂᏙᎾᎥ ᎤᎦᏛᎴᏒᏍᏔᏅᎩ, ᎠᎴ ᎤᎶᏐᏅᎩ.
Pamenepo iwo anatola miyala kuti amugende, koma Yesu anabisala, nachoka mozemba mʼNyumba ya Mulungu.

< ᎣᏍᏛ ᎧᏃᎮᏛ ᏣᏂ ᎤᏬᏪᎳᏅᎯ 8 >