< ᎣᏍᏛ ᎧᏃᎮᏛ ᏣᏂ ᎤᏬᏪᎳᏅᎯ 1 >

1 ᏗᏓᎴᏂᏍᎬ ᎧᏃᎮᏛ ᎡᎮᎢ, ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᎧᏃᎮᏛ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎢᏧᎳᎭ ᎠᏁᎮᎢ, ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᎧᏃᎮᏛ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎨᏎᎢ.
Pachiyambi panali Mawu, ndipo Mawu anali kwa Mulungu, ndipo Mawu ndiye Mulungu.
2 ᏗᏓᎴᏂᏍᎬᎢ ᎾᏍᎩ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎢᏧᎳᎭ ᎠᏁᎮᎢ.
Mawuwa anali ndi Mulungu pachiyambi.
3 ᏂᎦᎥ ᎪᎱᏍᏗ ᎾᏍᎩ ᎤᏬᏢᏁᎢ, ᎠᎴ ᏂᎦᎥ ᎪᏢᏅᎯ ᏥᎩ ᎥᏝ ᎪᎱᏍᏗ ᎾᏍᎩ ᏄᏬᏢᏅᎾ ᏱᎩ.
Zinthu zonse zinalengedwa ndi Iye; ndipo popanda Iye sikukanakhala kanthu kalikonse kolengedwa.
4 ᎾᏍᎩ [ ᎧᏃᎮᏛ ] ᎬᏂᏛ ᎤᏪᎮᎢ; ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᎬᏂᏛ ᏴᏫ ᎢᎦ ᎤᎾᏘᏍᏓᏁᎯ ᎨᏎᎢ.
Mwa Iye munali moyo, ndipo moyowo unali kuwunika kwa anthu.
5 ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᎢᎦ-ᎦᏘᏍᏗᏍᎩ ᎤᎵᏏᎬ ᏚᎸᏌᏕᎢ, ᎤᎵᏏᎩᏃ ᎥᏝ ᏱᏚᏓᏂᎸᏤᎢ.
Kuwunika kunawala mu mdima, koma mdimawo sunakuzindikire.
6 ᎩᎶ ᎢᏳᏍᏗ ᎠᏍᎦᏯ ᎡᎲᎩ ᏣᏂ ᏧᏙᎢᏛ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᏅᏓᏳᏅᏏᏛ ᎨᏒᎩ.
Kunabwera munthu amene anatumizidwa kuchokera kwa Mulungu; Iyeyo dzina lake linali Yohane.
7 ᎾᏍᎩ ᎤᎷᏨᎩ ᎧᏃᎮᏍᎩ ᎨᏒᎩ, ᎾᏍᎩ ᎢᎦ-ᎦᏘ ᎤᏃᎮᏗᏱ, ᎾᏍᎩ ᎢᏳᏩᏂᏐᏗᏱ ᎾᏂᎥ ᎤᏃᎯᏳᏗᏱ.
Iye anabwera ngati mboni kudzachitira umboni kuwunikako kuti kudzera mwa iye anthu onse akhulupirire.
8 ᎥᏝ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᎢᎦ-ᎦᏘ ᏱᎨᏎᎢ, ᎧᏃᎮᏍᎩᏉᏍᎩᏂ ᎨᏒᎩ ᎾᏍᎩ ᎢᎦ-ᎦᏘ.
Iyeyu sanali kuwunika; koma anabwera ngati mboni ya kuwunika.
9 ᎾᏍᎩᏍᎩᏂ Ꮎ ᎧᏃᎮᏛ ᎤᏙᎯᏳᏒ ᎢᎦ-ᎦᏘ ᎨᏒᎩ; ᎾᏍᎩ ᎡᎶᎯ ᏧᎷᏨ, ᎢᎦ ᏥᏕᎠᏘᏍᏓᏁ ᎾᏂᎥ ᏴᏫ.
Kuwunika koona kumene kuwunikira munthu aliyense kunabwera ku dziko lapansi.
10 ᎾᏍᎩ ᎡᎶᎯ ᎡᎲᎩ, ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᎡᎶᎯ ᎤᏬᏢᏅᎯ ᎨᏒᎩ, ᎠᎴ ᎡᎶᎯ ᎥᏝ ᏳᏬᎵᏤᎢ.
Iye anali mʼdziko lapansi, ndipo ngakhale kuti dziko lapansi linalengedwa ndi Iye, dziko lapansilo silinamuzindikire Iye.
11 ᎤᏤᎵᎪᎯ ᎤᎷᏨᎩ, ᎠᏎᏃ ᏧᏤᎵ ᎥᏝ ᏱᏗᎬᏩᏓᏂᎸᏤᎢ.
Iye anabwera kwa iwo amene anali akeake, koma akewo sanamulandire Iye.
12 ᎾᏂᎥᏍᎩᏂ ᏗᎬᏩᏓᏂᎸᏨᎯ ᏕᎤᎵᏍᎪᎸᏓᏁᎸᎩ ᎤᏁᎳᏅ Ꭿ ᏧᏪᏥ ᎢᏳᎾᎵᏍᏙᏗᏱ; ᎾᏍᎩ ᏕᎤᏙᎥ ᎠᏃᎯᏳᎲᏍᎩ;
Koma kwa onse amene anamulandira Iye, kwa amene anakhulupirira mʼdzina lake, Iye anawapatsa mphamvu yokhala ana a Mulungu;
13 ᎾᏍᎩ ᎩᎬ ᏧᎾᏄᎪᏫᏒᎯ ᏂᎨᏒᎾ, ᎠᎴ ᎤᏇᏓᎵ ᎠᏓᏅᏖᏍᎬ ᏧᎾᏄᎪᏫᏒᎯ ᏂᎨᏒᎾ, ᎠᎴ ᏴᏫ ᎠᏓᏅᏖᏍᎬ ᏧᎾᏄᎪᏫᏒᎯ ᏂᎨᏒᎾ, ᎤᏁᎳᏅᎯᏍᎩᏂ ᏧᎾᏄᎪᏫᏒᎯ.
ana wobadwa osati monga mwachilengedwe, kapena chisankho cha munthu, kapena chifuniro cha mwamuna koma wobadwa mwa Mulungu.
14 ᎠᎴ ᎧᏃᎮᏛ ᎤᏇᏓᎵ ᏄᎵᏍᏔᏅᎩ, ᎠᎴ ᎢᏕᎲ ᎤᎴᏂᏙᎸᎩ, ᎤᎧᎵᏨᎯ ᎨᏒᎩ ᎤᏓᏙᎵᏣᏛ ᎠᎴ ᏚᏳᎪᏛᎢ; ᎠᎴ ᎢᏗᎪᏩᏘᏍᎬᎩ ᎤᏤᎵᎦ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᎨᏒᎢ, ᎾᏍᎩ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᎨᏒ ᎠᎦᏴᎵᎨ ᎤᏩᏒᎯᏳ ᎤᏕᏁᎸᎯ ᎤᏤᎵᎦ ᎾᏍᎩᏯ ᎨᏒᎩ.
Mawu anasandulika thupi ndipo anakhala pakati pathu. Ife tinaona ulemerero wake, ulemerero wa Iye amene ndi Mwana mmodzi yekhayo wa Atate, wodzaza ndi chisomo ndi choonadi.
15 ᏣᏂ ᎧᏃᎮᏍᎬᎩ ᎾᏍᎩ [ ᎧᏃᎮᏛ, ] ᎠᎴ ᎤᏪᎷᏅᎩ ᎯᎠ ᏄᏪᏒᎩ; ᎯᎠ ᎾᏍᎩ ᏥᏥᏃᎮᏍᎬᎩ, ᎯᎠ ᏥᏂᏥᏪᏍᎬᎩ, ᎣᏂ ᏨᏓᏯᎢ ᎢᎬᏱ ᎠᎦᎴᏗ, ᎾᏍᎩᏰᏃ ᎡᎲᎩ ᎠᏏ ᏂᎨᎥᎾ ᏥᎨᏒᎩ.
Yohane achitira umboni za Iye. Iye akufuwula kuti, “Uyu ndi Iye amene ndinati, ‘Iye amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa, Iyeyo analipo ine ndisanabadwe.’”
16 ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᎤᎧᎵᏨᎯ ᎨᏒ ᏂᏗᎥ ᎡᎩᏁᎸᎯ, ᎬᏩᎦᏘᏯᏰᏃ ᎤᏓᏙᎵᏍᏗ ᎨᏒ ᎤᎶᏏᎶᏛ ᎡᎩᏁᎸ.
Kuchokera mʼkuchuluka kwa chisomo chake ife tonse talandira madalitso pamwamba pa madalitso.
17 ᏗᎧᎿᎭᏩᏛᏍᏗᏰᏃ ᎼᏏ ᎬᏂᎨᏒ ᎢᏳᏩᏁᎸᎯ ᎨᏒᎩ, ᎤᏓᏙᎵᏣᏛᏍᎩᏂ ᎠᎴ ᏚᏳᎪᏛᎢ ᏥᏌ ᎦᎶᏁᏛ ᏂᏙᏓᏳᎵᏍᎪᎸᏔᏅᎯ.
Pakuti lamulo linapatsidwa kudzera mwa Mose; chisomo ndi choonadi zinabwera kudzera mwa Yesu Khristu.
18 ᎥᏝ ᎩᎶ ᎢᎸᎯᏳ ᏱᎬᏩᎪᎰ ᎤᏁᎳᏅᎯ; ᎤᏩᏒᎯᏳ ᎤᏕᏁᎸᎯ ᎤᏪᏥ, ᎠᎦᏴᎵᎨ ᎦᏁᏥᎢ ᎡᎯ, ᎾᏍᎩ ᎬᏂᎨᏒ ᏄᏩᏁᎸ.
Palibe munthu amene anaona Mulungu, koma Mwana mmodzi yekhayo amene ali wa pamtima pa Atate, ndiye anafotokoza za Iye.
19 ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᎯᎠ ᏣᏂ ᎤᏃᎮᎸᎯ, ᎾᎯᏳ ᎠᏂᏧᏏ ᏥᎷᏏᎵᎻ ᏙᏧᏂᏅᏒ ᎠᏥᎸ-ᎠᏁᎶᎯ ᎠᎴ ᎠᏂᎵᏫ ᎬᏩᏛᏛᏗᏱ, ᎯᎠ ᎢᏳᏂᏪᏍᏗᏱ; ᎦᎪ ᏂᎯ?
Tsopano uwu ndi umboni wa Yohane pamene Ayuda a ku Yerusalemu anatumiza ansembe ndi Alevi kudzamufunsa kuti iye anali yani.
20 ᎠᎴ Ꭴ’ᏃᏅᎩ, ᎠᎴ ᎥᏝ ᏳᏓᏱᎴᎢ, Ꭴ’ᏃᏅᏉᏍᎩᏂ ᎯᎠ ᏄᏪᏒᎩ; ᎥᏝ ᎠᏴ ᎦᎶᏁᏛ ᏱᎩ.
Iye sanalephere kuvomereza, koma iye anavomereza momasuka kuti, “Ine sindine Khristu.”
21 ᎠᎴ ᎥᎬᏩᏛᏛᏅᎩ ᎯᎠ ᏄᏂᏪᏒᎩ; ᎦᎪᎨ? ᎢᎳᏯᏍᎪ ᏂᎯ? ᎯᎠᏃ ᏄᏪᏒᎩ; ᎥᏝ. ᏥᎪᎨ Ꮎ ᎠᏙᎴᎰᏍᎩ ᏂᎯ? ᎥᏝ, ᎤᏛᏅᎩ.
Iwo anamufunsa kuti, “Nanga iwe ndiwe yani? Kodi ndiwe Eliya?” Iye anati, “Sindine.” “Kodi ndiwe Mneneri?” Iye anayankha kuti, “Ayi.”
22 ᎿᎭᏉᏃ ᎯᎠ ᏅᎬᏩᏪᏎᎸᎩ; ᎦᎪ ᏂᎯ? ᏫᏙᏥᏃᏁᏗᏱᏰᏃ ᏅᏓᎪᎩᏅᏒᎯ; ᎦᏙ ᎭᏗᎭ ᏨᏒ ᎭᏓᏃᎮᏍᎬᎢ?
Pomaliza iwo anati, “Ndiwe yani? Tipatse yankho kuti tipite nalo kwa amene anatituma. Kodi iwe ukuti chiyani za iwe mwini?”
23 ᎯᎠ ᏄᏪᏒᎩ; ᎠᏴ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᎤᏪᎷᎩ ᎯᎠ ᏥᏂᎦᏪ ᎢᎾᎨᎢ; ᎢᏥᏥᏃᎯᏍᏓ ᏅᏃᎯ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎤᏤᎵᎦ; ᎾᏍᎩ ᏄᏪᏒ ᎢᏌᏯ ᎠᏙᎴᎰᏍᎩ.
Yohane anayankha ndi mawu a mneneri Yesaya kuti, “Ine ndi mawu a wofuwula mʼchipululu, ‘Wongolani njira ya Ambuye.’”
24 ᎾᏍᎩᏃ Ꮎ ᏅᏓᎨᏥᏅᏏᏛ ᎠᏂᏆᎵᏏᏱ ᎤᎾᎵᎪᎯ ᎨᏒᎩ.
Tsopano Afarisi ena amene anatumidwa
25 ᎬᏩᏛᏛᏅᎩᏃ ᎯᎠ ᏂᎬᏩᏪᏎᎸᎩ; ᎦᏙᏃ ᏥᏕᎭᏓᏬᏍᎦ, ᎢᏳᏃ ᏂᎯ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᎦᎶᏁᏛ ᎠᎴ ᎢᎳᏯ ᎠᎴ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᎠᏙᎴᎰᏍᎩ ᏂᎨᏒᎾ ᏱᎩ?
anamufunsa Iye kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani, umabatiza ngati iwe si Khristu, kapena Eliya, kapena Mneneri?”
26 ᏣᏂ ᏚᏁᏤᎸᎩ, ᎯᎠ ᏄᏪᏒᎩ, ᎠᏴ ᎠᎹ ᏕᎦᏓᏬᏍᏗᎭ; ᎠᏎᏃ ᎦᏙᎦ ᎩᎶ ᎢᏥᏙᎾᎥ ᎤᏓᏑᏯ ᎾᏍᎩ ᏁᏥᎦᏔᎲᎾ;
Yohane anayankha kuti, “Ine ndimabatiza ndi madzi, koma pakati panu payima amene simukumudziwa.
27 ᎾᏍᎩᏍᎩᏂ Ꮎ ᎣᏂ ᏨᏓᏯᎢ, ᎢᎬᏱ ᏣᎦᎴᏗ; ᎾᏍᎩ ᏧᎳᏑᎶ ᏕᎪᎸᏌᏛ ᎥᏝ ᏰᎵ ᏱᏂᎪᎢ ᏗᏍᎩᎧᏁᏴᏗᏱ.
Iye ndi amene akubwera pambuyo panga, ine siwoyenera kumasula zingwe za nsapato zake.”
28 ᎾᏍᎩ ᎯᎠ ᏄᎵᏍᏔᏂᏙᎸᎩ ᏗᎦᏐᎯᏍᏗᏱ ᏦᏓᏂ ᏍᎪᏂᏗᏢ ᎾᎿᎭᏣᏂ ᏓᏓᏬᏍᎬᎢ.
Zonsezi zinachitika ku Betaniya kutsidya lina la mtsinje wa Yorodani, kumene Yohane ankabatizira.
29 ᎠᎴ ᎤᎩᏨᏛ ᏣᏂ ᏭᎪᎲᎩ ᏥᏌ ᎦᏙᎬ ᎢᏗᏢ ᏛᎦᏛᎩ, ᎠᎴ ᎯᎠ ᏄᏪᏒᎩ; ᏤᏣᎦᏅᎦ ᎠᏫ-ᎠᎩᎾ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏤᎵᎦ, ᎾᏍᎩ ᎠᎲᏍᎩ ᎡᎶᎯ ᎤᏂᏍᎦᏅᏨᎢ.
Pa tsiku lotsatira Yohane anaona Yesu akubwera kwa iye ndipo anati, “Taonani, Mwana Wankhosa wa Mulungu, amene achotsa tchimo la dziko lapansi!
30 ᎾᏍᎩᏍᎩᏂ ᎯᎠ Ꮎ ᏥᏥᏁᎢᏍᏗᏍᎬᎩ; ᎣᏂ ᏓᏯᎢ ᎢᎬᏱ ᎠᎦᎴᏗ ᏥᎦᏗᏍᎬᎩ, ᎾᏍᎩᏰᏃ ᎡᎲᎩ ᎠᏏ ᏂᎨᎥᎾ ᏥᎨᏒᎢ.
Uyu ndi amene ndimatanthauza pamene ndinanena kuti, ‘Munthu amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa analipo ine ndisanabadwe.’
31 ᎠᎴ ᎠᏴ ᎥᏝ ᏱᏥᎦᏔᎮᎢ; ᎠᏎᏃ ᎾᏍᎩ ᎢᏏᎵ ᎨᏥᎾᏄᎪᏫᏎᏗᏱ ᏅᏧᎵᏍᏙᏔᏅ ᎠᎩᎷᏨ ᎠᎹ ᏕᎦᏓᏬᏍᏗᎭ.
Ine mwini sindinamudziwe Iye, koma ndinabwera kubatiza ndi madzi kuti Iye adziwike mu Israeli.”
32 ᎠᎴ ᏣᏂ ᎤᏃᎮᎸᎩ ᎯᎠ ᏄᏪᏒᎩ; ᎠᎩᎪᎲᎩ ᎠᏓᏅᏙ ᎫᎴ-ᏗᏍᎪᏂᎯ ᎾᏍᎩᏯ ᏓᏳᏁᏡᏅᎩ ᎦᎸᎳᏗ, ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᏚᎩᎸᏨᎩ.
Kenaka Yohane anapereka umboni uwu: “Ine ndinaona Mzimu Woyera ngati nkhunda kuchokera kumwamba nakhala pa Iye.
33 ᎠᎴ ᎠᏴ ᎥᏝ ᏱᏥᎦᏔᎮᎢ; ᎠᏎᏃ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᏅᏛᎩᏅᏏᏛ ᎠᎹ ᏗᏆᏓᏬᏍᏙᏗᏱ ᎾᏍᎩ ᎯᎠ ᎾᎩᏪᏎᎸᎩ; ᎩᎶ ᎯᎪᎥᎭ ᎠᏓᏅᏙ ᎠᏁᏡᎲᏍᎬᎢ ᏚᎩᎸᏨᎭ, ᎾᏍᎩ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᎠᏓᏅᏙ ᏗᏓᏬᏍᏗᏍᎩ.
Ine sindikanamudziwa Iye, koma kuti amene anandituma ine kudzabatiza ndi madzi anati kwa ine, ‘Munthu amene udzaona Mzimu Woyera akutsika nakhazikika pa Iye ndi amene adzabatize ndi Mzimu Woyera.’
34 ᎠᎩᎪᎲᎩᏃ ᎠᎴ ᎠᎩᏃᎮᎸᎩ ᎾᏍᎩ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏪᏥ ᎨᏒᎢ.
Ine ndaona ndipo ndikuchitira umboni kuti uyu ndi Mwana wa Mulungu.”
35 ᎠᎴᏬ ᎤᎩᏨᏛ ᏣᏂ ᎦᏙᎬᎩ, ᎠᎴ ᎠᏂᏔᎵ ᎬᏩᏍᏓᏩᏗᏙᎯ ᏓᏂᏙᎬᎩ.
Pa tsiku lotsatira Yohane analinso pamenepo pamodzi ndi awiri a ophunzira ake.
36 ᏚᎧᎿᎭᏅᏃ ᏥᏌ ᎠᎢᏒᎢ ᎯᎠ ᏄᏪᏒᎩ; ᏤᏣᎦᏅᎦ ᎠᏫ-ᎠᎩᎾ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏤᎵᎦ;
Iye ataona Yesu akudutsa anati, “Taonani Mwana Wankhosa wa Mulungu!”
37 ᎾᏍᎩᏃ Ꮎ ᎠᏂᏔᎵ ᎬᏩᏍᏓᏩᏗᏙᎯ ᎤᎾᏛᎦᏅᎩ ᎤᏁᏨ; ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᎤᏂᏍᏓᏩᏛᏒᎩ ᏥᏌ.
Ophunzira ake awiriwo atamva iye akunena izi, iwo anamutsatira Yesu.
38 ᏥᏌᏃ ᎤᎦᏔᎲᏒ, ᎠᎴ ᎬᏩᏍᏓᏩᏗᏒ ᏚᎪᎲ, ᎯᎠ ᏂᏚᏪᏎᎸᎩ; ᎦᏙ ᎢᏍᏗᏲᎭ? ᎯᎠᏃ ᏂᎬᏩᏪᏎᎸᎩ; ᏔᏈ-ᎾᏍᎩ ᎠᏁᏢᏔᏅᎯ ᎦᏛᎦ ᏔᏕᏲᎲᏍᎩ-ᎭᏢ ᏗᏤᏅ.
Atatembenuka, Yesu anaona iwo akumutsatira ndipo anawafunsa kuti, “Kodi mukufuna chiyani?” Iwo anati, “Rabi (kutanthauza kuti Aphunzitsi), kodi mukukhala kuti?”
39 ᎯᎠ ᏂᏚᏪᏎᎸᎩ; ᎢᏕᎾ, ᏫᏍᏓᎦᏔ. ᎤᏁᏅᏒᎩᏃ ᎠᎴ ᎤᎾᎦᏔᏅᎩ ᎦᏁᎸᎢ, ᎠᎴ ᎢᏧᎳᎭ ᎤᏁᏙᎸᎯ ᎾᎯᏳ ᎢᎦ; ᏅᎩᏁᏰᏃ ᎢᏳᏟᎶᏛ ᎧᎳᏩᏗᏒ ᎨᏒᎩ.
Iye anayankha kuti, “Bwerani mudzaone.” Choncho iwo anapita ndi kukaona kumene Iye amakhala, ndipo anakhala naye tsiku limenelo. Linali ngati pafupifupi ora la khumi.
40 ᎠᏏᏴᏫ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᎠᏂᏔᎵ ᏣᏂ ᎤᎾᏛᎦᏁᎸᎯ, ᎠᎴ [ ᏥᏌ ] ᎤᏂᏍᏓᏩᏛᏛ, ᎾᏍᎩ ᎡᏂᏗ ᎨᏒᎩ, ᏌᏩᏂ ᏈᏓ ᏗᎾᏓᏅᏟ.
Andreya mʼbale wake wa Simoni Petro, anali mmodzi wa awiriwo amene anamva zimene Yohane ananena ndiponso amene anamutsata Yesu.
41 ᎢᎬᏱ ᎤᏩᏛᎲᎩ ᎤᏤᎵ ᎤᏂᎵ ᏌᏩᏂ, ᎠᎴ ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎸᎩ; ᎣᏥᏩᏛᎲ ᎺᏌᏯ; ( ᎾᏍᎩ ᎠᏁᏢᏔᏅᎯ ᎦᎶᏁᏛ ᎦᏛᎦ.)
Choncho chimene Andreya anachita ndi kukapeza mʼbale wake Simoni ndipo anamuwuza kuti, “Ife tamupeza Mesiya,” (kutanthauza kuti Khristu).
42 ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᎤᏘᏃᎸᎩ ᏥᏌ ᎡᏙᎲᎢ. ᏥᏌᏃ ᏚᎧᎿᎭᏅ ᎯᎠ ᏄᏪᏒᎩ; ᏌᏩᏂ ᏂᎯ, ᏦᎾ ᎤᏪᏥ, ᏏᏆᏏ ᏕᏣᏙᎡᏍᏗ; ᎾᏍᎩ ᎠᏁᏢᏔᏅᎯ ᏈᏓ ᎦᏛᎦ.
Kenaka iye anabweretsa Simoni kwa Yesu, amene anamuyangʼana ndipo anati, “Iwe ndiwe Simoni, mwana wa Yohane. Udzatchedwa Kefa” (limene litanthauza kuti Petro).
43 ᎤᎩᏨᏛ ᏥᏌ ᎤᏚᎵᏍᎬᎩ ᎨᎵᎵ ᎤᏪᏅᏍᏗᏱ; ᏈᎵᎩᏃ ᎤᏩᏛᎲᎩ, ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎸᎩ; ᏍᎩᏍᏓᏩᏚᎦ.
Pa tsiku lotsatira Yesu anaganiza zopita ku Galileya. Atamupeza Filipo, anati kwa iye, “Nditsate.”
44 ᏈᎵᎩ ᏇᏣᏱᏗ ᎡᎯ ᎨᏒᎩ, ᎡᏂᏗ ᎠᎴ ᏈᏓ ᎤᏂᏚᎲᎢ.
Filipo monga Andreya ndi Petro, anali wochokera ku mzinda mudzi Betisaida.
45 ᏈᎵᏃ ᎤᏩᏛᎲᎩ ᏁᏓᏂᎵ, ᎠᎴ ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎸᎩ; ᎣᏥᏩᏛᎲ ᎾᏍᎩ ᎼᏏ ᎫᏬᏪᎳ ᏥᎧᏃᎮᎭ ᏗᎧᎿᎭᏩᏛᏍᏗ ᎪᏪᎵᎯ, ᎠᎴ ᎠᎾᏙᎴᎰᏍᎩ ᏣᏂᏃᎮᎭ, ᎾᏍᎩ ᏥᏌ ᎾᏎᎵᏗ ᎡᎯ ᏦᏩ ᎤᏪᏥ.
Filipo anakapeza Natanieli ndipo anamuwuza kuti, “Ife tapeza amene Mose analemba za Iye mʼmalamulo, ndi zimene aneneri analembanso za Iye, Yesu wa ku Nazareti, mwana wa Yosefe.”
46 ᏁᏓᏂᎵᏃ ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎸᎩ; ᏰᎵᏍᎪ ᎪᎱᏍᏗ ᎣᏍᏛ ᏅᏓᎬᏩᎾᏄᎪᎢᏍᏗ ᎾᏎᎵᏗ? ᏈᎵᎩ ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎸᎩ; ᎢᏁᎾ, ᏩᎦᏔ.
Natanieli anafunsa kuti, “Nazareti! Kodi kanthu kalikonse kabwino kangachokere kumeneko?” Filipo anati, “Bwera udzaone.”
47 ᏥᏌ ᏭᎪᎲᎩ ᏁᏓᏂᎵ, ᎦᏙᎬ ᎢᏗᏢ ᏛᎦᏛᎩ; ᎯᎠᏃ ᏄᏪᏒᎩ, ᎾᏍᎩ ᎤᏁᎢᏍᏔᏅᎩ; ᎬᏂᏳᏉ ᎤᏙᎯᏳᎯᏯ ᎢᏏᎵ ᎤᏪᏥ, ᎾᏍᎩ ᎦᎶᏄᎮᏛ ᏄᏓᏑᏴᎾ.
Yesu atamuona Natanieli akuyandikira, anati kwa iye, “Uyu ndi Mwisraeli weniweni, mwa iye mulibe chinyengo.”
48 ᏁᏓᏂᎵ ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎸᎩ; ᎦᏙ ᏗᎦᎵᏍᏙᏗ ᎢᏍᎩᎦᏔᎭ? ᏥᏌ ᎤᏁᏨ ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎸᎩ; ᎠᏏᏉ ᏈᎵᎩ ᏫᏂᏣᏯᏂᏍᎬᎾ ᏥᎨᏒᎩ, ᎡᎦᏔ-ᎢᏳᏍᏗ ᏡᎬᎢ ᎭᏫᏂᏗᏢ ᏥᏦᎸᎩ, ᏫᎬᎪᎥᎩ.
Natanieli anafunsa kuti, “Kodi mwandidziwa bwanji?” Yesu anayankha kuti, “Ine ndinakuona iwe utakhala pansi pamtengo wamkuyu Filipo asanakuyitane.”
49 ᏁᏓᏂᎵ ᎤᏅᏨ ᎯᎠ ᏄᏪᏒᎩ; ᏔᏕᏲᎲᏍᎩ, ᏂᎯ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏪᏥ; ᏂᎯ ᏣᎬᏫᏳᎯ ᎢᏏᎵ ᎤᎾᏤᎵᎦ.
Kenaka Natanieli ananena kuti, “Rabi, Inu ndinu Mwana wa Mulungu; Inu ndinu Mfumu ya Israeli.”
50 ᏥᏌ ᎤᏁᏨ ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎸᎩ; ᏥᎪ ᎯᎠ ᏥᏂᎬᏪᏏ, ᎬᎪᎥᎩ ᎭᏫᏂᏗᏢ ᏒᎦᏔ-ᎢᏳᏍᏗ ᏡᎬᎢ, ᎾᏍᎩ ᏅᏗᎦᎵᏍᏙᏗᎭ ᎰᎯᏳᎲᏍᎦ? ᎤᏟ ᎢᏳᏍᏆᏂᎪᏗ ᎯᎪᏩᏘᏍᎨᏍᏗ, ᎡᏍᎦᏉ ᎾᏍᎩ.
Yesu anati, “Ukukhulupirira chifukwa chakuti ndakuwuza kuti Ine ndinakuona iwe uli pansi pamtengo wamkuyu? Iwe udzaona zinthu zazikulu kuposa izo.”
51 ᎠᎴᏬ ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎸᎩ; ᎤᏙᎯᏳᎯᏩ ᎤᏙᎯᏳᎯᏯ ᎯᎠ ᏂᏨᏪᏎᎭ; ᎪᎯ ᎢᏳᏓᎴᏅᏛ ᎢᏥᎪᏩᏘᏍᎨᏍᏗ ᎦᎸᎳᏗ ᎤᎵᏍᏚᎢᏛ ᎨᏎᏍᏗ, ᎠᎴ ᏕᏥᎪᏩᏘᏍᎨᏍᏗ ᏗᏂᎧᎿᎭᏩᏗᏙᎯ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᏧᏤᎵᎦ ᎠᎾᎵᏌᎳᏗᏍᎨᏍᏗ ᎠᎴ ᎡᎳᏗ ᎾᎾᏛᏁᎮᏍᏗ ᎬᏩᎷᏤᎮᏍᏗ ᏴᏫ ᎤᏪᏥ.
Ndipo Iye anapitirira kuti, “Zoonadi, Ine ndikuwuza kuti iwe udzaona kumwamba, kutatsekuka ndi angelo a Mulungu akukwera ndi kutsika pa Mwana wa Munthu.”

< ᎣᏍᏛ ᎧᏃᎮᏛ ᏣᏂ ᎤᏬᏪᎳᏅᎯ 1 >