< ᏉᎳ ᎡᏈᏌ ᎠᏁᎯ ᏧᏬᏪᎳᏁᎸᎯ 6 >

1 ᏗᏥᏲᎵ, ᏕᏦᎯᏳᏎᏍᏗ ᏗᏥᎦᏴᎵᎨᎢ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎨᏒ ᏅᏗᎦᎵᏍᏙᏗᏍᎨᏍᏗ; ᏚᏳᎪᏗᏰᏃ ᎾᏍᎩ ᎯᎠ.
Inu ana, mverani makolo anu mwa Ambuye, pakuti zimenezi ndi zoyenera.
2 ᎯᎸᏉᏕᏍᏗ ᏣᏙᏓ ᎠᎴ ᏣᏥ, ᎾᏍᎩ ᎢᎬᏱᏱ ᎤᎵᏁᏨ ᏥᎩ ᏧᎵᏠᏯᏍᏗ ᎠᏚᎢᏍᏛᎢ,
“Lemekeza abambo ndi amayi ako.” Limeneli ndi lamulo loyamba lokhala ndi lonjezo.
3 ᎾᏍᎩ ᎣᏏᏳ ᎢᎨᏣᎵᏍᏓᏁᏗ ᏱᎩ, ᎠᎴ ᎪᎯᏗᏳ ᎨᏣᎴᏂᏓᏍᏗ ᏱᎩ ᎡᎶᎯ.
Ngati ulemekeza abambo ako ndi amayi ako, “zinthu zidzakuyendera bwino ndipo udzasangalala ndi moyo wautali pa dziko lapansi.”
4 ᎠᎴ ᏂᎯ ᎢᏥᎦᏴᎵᎨᎢ, ᏞᏍᏗ ᏱᏗᏥᎿᎭᎸᏍᏗᏍᎨᏍᏗ ᏗᏤᏥ; ᏕᏣᏛᎯᏍᏗᏍᎨᏍᏗᏍᎩᏂ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎤᏤᎵ ᏗᏕᏲᏗ ᎨᏒ ᎠᎴ ᎨᏯᏙᎥᎯᏍᏗ ᎨᏒᎢ.
Abambo musakwiyitse ana anu; mʼmalo mwake, muwalere mʼchiphunzitso ndi mʼchilangizo cha Ambuye.
5 ᎡᏥᏅᏏᏓᏍᏗ, ᏕᏦᎯᏳᏎᏍᏗ ᎾᏍᎩ ᎨᏥᏅᏏᏙᎯ ᎠᏂ ᎤᏇᏓᎵ, ᎨᏒᎢ, ᎢᏥᎾᏰᏍᎨᏍᏗ ᎠᎴ ᏕᏥᎾᏫᏍᎨᏍᏗ, ᎣᏏᏳ ᎢᏥᏰᎸᎯ ᎨᏎᏍᏗ ᏗᏥᎾᏫᏱ, ᎦᎶᏁᏛ ᏥᏁᏣᏛᏁᎰ ᎾᏍᎩᏯᎢ.
Inu antchito, mverani mabwana anu mwaulemu ndi mwamantha ndi moona mtima, monga momwe mungamvere Khristu.
6 ᎥᏝ ᏥᏛᏓᏗᎧᏃ ᎢᏳᏍᏗ, ᏴᏫᏉ ᎣᏏᏳ ᎤᏂᏰᎸᏗ; ᎦᎶᏁᏛᏍᎩᏂ ᏧᏅᏏᏓᏍᏗ ᎢᏳᎾᏛᏁᏗ, ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎣᏏᏳ ᎤᏰᎸᏗ ᏂᏣᏛᏁᎲᎢ, ᏗᏥᎾᏫᏱ ᏨᏗᏓᎴᎲᏍᎪᎢ;
Musawamvere pamene akukuonani kuti akukomereni mtima, koma ngati akapolo a Khristu ochita chifuniro cha Mulungu kuchokera mu mtima mwanu.
7 ᎣᏏᏳ ᎢᏥᏰᎸᎯ ᎪᎱᏍᏗ ᎢᏣᏛᏁᎲ, ᎤᎬᏫᏳᎯ ᏥᏁᏣᏛᏁᎰ ᎾᏍᎩᏯᎢ, ᎥᏝᏃ ᏴᏫᏉ ᏥᏂᏕᏣᏛᏁᎰ ᎾᏍᎩᏯᎢ;
Tumikirani ndi mtima wonse, ngati kuti mukutumikira Ambuye, osati anthu.
8 ᎢᏥᎦᏔᎲ ᎾᏍᎩ ᏂᎦᎥ ᎪᎱᏍᏗ ᎣᏍᏛ ᏚᎸᏫᏍᏓᏁᎲ ᎩᎶᎢ, ᎾᏍᎩᏯ ᎢᏳᏍᏗ ᎤᏁᏗ ᎨᏒ ᎤᎬᏫᏳᎯ, ᎾᏍᏉ ᎠᏥᎾᏝᎢ ᏱᎩ, ᎠᎴ ᎾᏥᎾᏝᎥᎾ ᏱᎩ.
Inu mukudziwa kuti Ambuye adzamupatsa munthu aliyense mphotho chifukwa cha ntchito yake yabwino imene anagwira, kaya munthuyo ndi kapolo kapena mfulu.
9 ᎠᎴ ᏂᎯ ᏗᏣᏓᏅᏏᏙᎯ, ᎾᏍᎩᏯ ᎤᏠᏱ ᎾᏍᎩ ᏂᏕᏣᏛᏁᎮᏍᏗ, ᎤᏁᎳᎩ ᎢᏤᎵᏎᏍᏗ ᏕᏥᎾᏰᏓᏁᎲᎢ, ᏥᏥᎦᏔᎭ ᎾᏍᎩ ᏂᎯ ᎾᏍᏉ ᎢᏥᏅᏏᏙᎯ ᎦᎸᎶᎢ ᎡᎲᎢ; ᎥᏝ ᎠᎴ ᏱᏚᏑᏰᏍᏗ ᏴᏫ ᏗᎬᏩᎸᏉᏙᏗ ᎨᏒᎢ.
Ndipo inu mabwana, muziwachitiranso chimodzimodzi antchito anu. Musamawaopseze, popeza mukudziwa kuti Mbuye wawo ndi wanunso, nonse Mbuye wanu ali kumwamba, ndipo Iyeyo alibe tsankho.
10 ᎤᎵᏍᏆᎸᏗᏃ ᎨᏒᎢ, ᎢᏓᎵᏅᏟ, ᏗᏣᎵᏂᎩᏗᏳ ᎨᏎᏍᏗ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎡᏣᎵᏍᎦᏍᏙᏛᎢ, ᎠᎴ ᎢᏣᎵᏍᎦᏍᏙᏛ ᎤᏣᏔᏅᎯ ᎤᎵᏂᎩᏗᏳ ᎨᏒᎢ.
Potsiriza ndikuti, dzilimbitseni mwa Ambuye ndi mwa mphamvu zake zazikulu.
11 ᏂᎦᏛ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏤᎵᎦ ᎠᎵᏍᎦᏍᏙᏙ ᎢᏣᏣᏅᏓ, ᎾᏍᎩ ᏰᎵ ᎨᏣᎴᏗ ᎢᏳᎵᏍᏙᏗᏱ ᎠᏍᎩᎾ ᎠᏏᎾᏌᏅ ᏕᏥᎦᏘᎸᏍᏗᏍᎬᎢ.
Valani zida zonse za Mulungu kuti muthe kuyima ndi kukana machenjerero a Satana.
12 ᎥᏝᏰᏃ ᏱᏗᎦᏟᏴᎭ ᎤᏇᏓᎵ ᎨᏒ ᎠᎴ ᎩᎬ, ᎤᏂᎬᏫᏳᎯᏍᎩᏂ, ᎠᎴ ᏧᎾᎵᏂᎩᏛ, ᎠᎴ ᏄᏂᎬᏫᏳᏌᏕᎩ ᎠᏂ ᎡᎶᎯ ᎤᎵᏏᎩ ᎨᏒᎢ, ᏗᏓᏅᏙ ᎤᏂᏁᎫᏥᏛ ᎦᎸᎶ ᏄᎾᏛᎿᎭᏕᎬᎢ. (aiōn g165)
Pakuti sitikulimbana ndi thupi ndi magazi, koma tikulimbana ndi maufumu, maulamuliro, mphamvu za dziko la mdima, ndi mphamvu zoyipa kwambiri zauzimu zamlengalenga. (aiōn g165)
13 ᎾᏍᎩ ᎢᏳᏍᏗ ᎢᏣᎩ ᏂᎦᏛ ᎠᎵ ᏍᎦᏍᏙᏙ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏤᎵᎦ, ᎾᏍᎩ ᏰᎵ ᏗᎨᏣᏟᏴᏗ ᎢᏳᎵᏍᏙᏗᏱ ᎾᎯᏳ ᎤᏲᎢᏳ ᎢᎦ ᎨᏎᏍᏗ, ᎾᏍᎩᏃ ᏂᎦᏛ ᎢᏣᏛᏁᎸᎯ ᎨᏎᏍᏗ, ᎨᏣᎴᏗ ᎢᏳᎵᏍᏙᏗᏱ.
Choncho valani zida zonse za Mulungu, kuti pamene tsiku loyipa kwambiri lifika, mudzathe kuyima chilili, ndipo mutatha kuchita zonse, mudzayimabe mwamphamvu.
14 ᎾᏍᎩ ᎢᏳᏍᏗ ᏕᏥᏙᎨᏍᏗ, ᏕᏣᏓᏠᏍᏕᏍᏗ ᎦᏰᎪᎩ ᏂᎨᏒᎾ ᎨᏒᎢ, ᎠᎴ ᏚᏳᎪᏛ ᎨᏒ ᏕᏣᏓᏁᏣᏍᏚᎶᏕᏍᏗ;
Tsono imani mwamphamvu, mutamangira choonadi ngati lamba mʼchiwuno mwanu, mutavala chilungamo ngati chitsulo chotchinjiriza pa chifuwa.
15 ᏗᏣᎳᏏᏕᏂᏃ ᏕᏣᎳᏑᎶᏕᏍᏗ ᎠᏛᏅᎢᏍᏔᏅᎯ ᎨᏒ ᎣᏍᏛ ᎧᏃᎮᏛ ᏅᏩᏙᎯᏯᏛ ᎠᏓᏁᎯ;
Valani Uthenga Wabwino wamtendere ku mapazi anu ngati nsapato.
16 ᎠᏎᏃ ᎾᏍᏉ ᎪᎯᏳᏗ ᎨᏒ ᎢᏣᎵᎬᏑᎶᏓ, ᎾᏍᎩ ᎢᏨᏗᏍᎬ ᏰᎵᏉ ᏗᎨᏨᏜᏓᏕᏗ ᎢᏳᎵᏍᏙᏗᏱ ᏧᏥᏍᏟ ᎦᏂ ᎠᏍᎩᎾ ᏧᏤᎵᎦ.
Kuwonjezera pa zonsezi, nyamulani chishango cha chikhulupiriro, ndipo ndi chimenechi mudzatha kuzimitsa mivi yonse yoyaka moto ya oyipayo.
17 ᎠᎵᏍᏕᎸᏙᏗᏃ ᎠᎵᏍᏚᎶ ᎢᏥᎾᎩ, ᎠᎴ ᎠᏰᎳᏍᏗ-ᎦᏅᎯᏛ ᎠᏓᏅᏙ ᎤᏤᎵᎦ, ᎾᏍᎩ ᎧᏃᎮᏛ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏤᎵ ᏥᎩ;
Valani chipewa cha chipulumutso ndi kutenga lupanga la mzimu, limene ndi Mawu a Mulungu.
18 ᏂᎪᎯᎸ ᎢᏣᏓᏙᎵᏍᏗᏍᎨᏍᏗ ᏄᏓᎴᏒ ᎠᏓᏙᎵᏍᏗ ᎨᏒ, ᎠᎴ ᎠᏔᏲᏍᏗ ᎨᏒ ᎠᏓᏅᏙ ᎬᏗ, ᎠᎴ ᎢᏥᏯᏫᏍᎨᏍᏗ ᎾᎿᎭᏂ ᎢᏨᏗᏍᎨᏍᏗ ᏗᏯᏪᎢᏍᏗ ᏂᎨᏒᎾ, ᎠᎴ ᎠᏔᏲᏍᏗ ᎨᏒ ᎨᏥᏍᏕᎸᏗᏱ ᎤᎾᏓᏅᏘ ᎾᏂᎥᎢ.
Ndipo mupemphere mwa Mzimu nthawi zonse, mʼmitundu yonse ya mapemphero ndi zopempha. Ndipo pozindikira izi, khalani achangu kupempherera oyera mtima nthawi zonse.
19 ᎠᎴ ᎠᏴ ᎥᎩᏍᏕᎸᏗᏱ, ᎾᏍᎩ ᎥᏆᎵᏍᎪᎸᏓᏁᏗᏱ ᎠᎩᏬᏂᎯᏍᏗᏱ, ᎠᎩᏍᏚᎢᏍᏗᏱ ᏥᎣᎵ ᏂᏥᏍᎦᎢᎲᎾ, ᎬᏂᎨᏒ ᎢᏯᏋᏁᏗᏱ ᎤᏕᎵᏛ ᎨᏒ ᎣᏍᏛ ᎧᏁᎮᏛ;
Mundipempherere inenso, kuti nthawi iliyonse pamene nditsekula pakamwa panga, andipatse mawu kuti ndiwulule zinsinsi za Uthenga Wabwino mopanda mantha.
20 ᎾᏍᎩ [ ᎣᏍᏛ ᎧᏃᎮᏛ ] ᏥᏅᏗᎦᎵᏍᏙᏗᎭ ᎠᏴ ᎥᎩᏅᏏᏛ ᎥᏆᎸᎢᏛ ᏥᎩ; ᎾᏍᎩ ᎢᏳᏩᏂᏐᏗᏱ ᎾᎿᎭᏂ ᏂᏥᏍᎦᎢᎲᎾ ᎠᎩᏁᎢᏍᏗᏱ, ᎾᏍᎩᏯ ᎢᏯᎩᏪᏍᏗᏱ ᏥᏚᏳᎪᏗ.
Ndine kazembe wa Uthenga Wabwinowu ngakhale ndili womangidwa mʼndende. Pempherani kuti ndilalikire mopanda mantha, monga ndiyenera.
21 ᎾᏍᎩᏃ ᎢᏥᎦᏙᎥᎯᏍᏗᏱ ᎾᏍᏉ ᎠᏴ ᎾᏆᎵᏍᏓᏁᎵᏕᎬ ᎠᎴ ᎾᏆᏛᎿᎭᏕᎬᎢ, ᏗᎩᎦ, ᎣᏥᎨᏳᎢ ᎣᏣᎵᏅᏟ ᎠᎴ ᎣᏍᏛ ᎢᏯᏛᏁᎯ ᏧᎸᏫᏍᏓᏁᎯ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎤᏤᎵ ᎤᎬᏩᎵ, ᎬᏂᎨᏒ ᏅᏓᏨᏁᎵ ᏄᏓᎴᏒ ᎪᎱᏍᏗ;
Tukiko, mʼbale wanga wokondedwa ndi mtumiki wokhulupirika mwa Ambuye, adzakuwuzani zonse kuti inunso mudziwe mmene ndilili ndi zimene ndikuchita.
22 ᎾᏍᎩ ᏥᏅᎵ ᏗᏤᎲᎢ ᎾᏍᎩᏉ ᎤᎬᏩᎵ, ᎾᏍᎩ ᎢᏥᎦᏙᎥᎯᏍᏗᏱ ᏃᎦᎵᏍᏓᏁᎵᏕᎬᎢ, ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᏧᎦᎵᏍᏓᏗᏍᏗᏱ ᏗᏥᎾᏫ.
Ine ndikumutumiza kwa inu, kuti mudziwe za moyo wathu, ndi kuti akulimbikitseni.
23 ᎤᏩᏙᎯᏯᏛ ᏚᏂᎧᎿᎭᏩᏗᏙᎮᏍᏗ ᎠᎾᎵᏅᏟ, ᎠᎴ ᎠᏓᎨᏳᏗ ᎨᏒ ᎤᎵᏠᏯᏍᏕᏍᏗ ᎪᎯᏳᏗ ᎨᏒᎢ, ᏅᏓᏳᎾᎵᏍᎪᎸᏔᏅᎯ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎠᎦᏴᎵᎨᎢ, ᎠᎴ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᏥᏌ ᎦᎶᏁᏛ.
Mtendere, chikondi pamodzi ndi chikhulupiriro kuchokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi abale onse.
24 ᎬᏩᎦᏘᏯ ᎤᏓᏙᎵᏍᏗ ᎨᏒ ᏚᏂᎧᎿᎭᏩᏗᏙᎮᏍᏗ ᎾᏂᎥ ᏄᎾᏠᎾᏍᏛᎾ ᎤᏂᎨᏳᎯ ᎢᎦᏤᎵ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᏥᏌ ᎦᎶᏁᏛ. ᎡᎺᏅ.
Chisomo kwa onse amene amakonda Ambuye athu Yesu Khristu ndi chikondi chosatha.

< ᏉᎳ ᎡᏈᏌ ᎠᏁᎯ ᏧᏬᏪᎳᏁᎸᎯ 6 >