< ᎨᏥᏅᏏᏛ ᏄᎾᏛᏁᎵᏙᎸᎢ 7 >

1 ᏄᎬᏫᏳᏒᏃ ᎠᏥᎸ-ᎨᎶᎯ ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎢ; ᎾᏍᎩᏍᎪ ᎤᏃᎯᏳᎯ ᏄᏍᏗ?
Kenaka mkulu wa ansembe anafunsa Stefano kuti, “Kodi zimene akukunenerazi ndi zoona?”
2 [ ᏍᏗᏫᏃ ] ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎢ; ᎢᏥᏍᎦᏯ ᎢᏓᏓᏅᏟ ᎠᎴ ᏗᎩᏙᏓ, ᎢᏣᏛᏓᏍᏓ. ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎠᏥᎸᏉᏗ ᎬᏂᎨᏒ ᏄᏛᏁᎴ ᎢᎩᏙᏓ ᎡᏆᎭᎻ ᎾᏍᎩ ᎾᎯᏳ ᎺᏌᏆᏕᎻ ᏤᎮᎢ, ᎠᏏᏉ ᎨᎳᏂ ᎾᏁᎳᏗᏍᎬᎾ ᏥᎨᏎᎢ;
Stefano anayankha kuti, “Abale ndi makolo, tamverani! Mulungu waulemerero anaoneka kwa kholo lathu Abrahamu pamene ankakhala ku Mesopotamiya, asanakakhale ku Harani.
3 ᎯᎠᏃ ᏄᏪᏎᎴᎢ; ᏣᏤᎵᎪᎯ ᎯᏄᎪᎢ ᎠᎴ ᎪᎱᏍᏗ ᏗᏨᎿᎭ ᎠᎴ ᎾᎿᎭᎦᏙᎯ ᎬᏯᏎᎮᏗ ᎨᏒ ᏫᎷᎩ.
Mulungu anati, ‘Tuluka mʼdziko lako, siya abale ako, ndipo pita ku dziko limene ndidzakusonyeza.’
4 ᎿᎭᏉᏃ ᎤᏓᏅᏎ ᎠᏂᎦᎵᏗ ᎤᎾᏤᎵᎪᎯ, ᎨᎳᏂᏃ ᎤᏁᎳᏕᎢ, ᎾᎿᎭᏃ ᏗᎤᏓᏅᏒ, ᎤᏙᏓ ᎤᏲᎱᏒ, ᎡᏍᎦᏂ ᎤᎷᏤᎴᎢ ᎾᏍᎩ ᎠᏂ ᎪᎯ ᏥᏤᎭ.
“Ndipo iye anatulukadi mʼdziko la Akaldeya ndi kukakhala ku Harani. Atamwalira abambo ake, Mulungu anamuchotsa kumeneko ndi kumubweretsa mʼdziko lino limene inu mukukhalamo tsopano.
5 ᎠᎴ ᎥᏝ ᎦᏓ ᎠᏂ ᏳᏁᎴᎢ ᏂᎤᏟᏍᏕ ᏏᎳᏏᏅᎯᏉ ᎢᎩᏛ, ᎠᏎᏃ ᎤᏚᎢᏍᏓᏁᎴ ᎾᏍᎩ ᎤᏤᎵ ᎢᏳᏩᏁᏗᏱ ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᎤᏁᏢᏔᏅᏛ ᎨᏒ ᎠᏏᏉ ᎤᏪᏥ ᏁᎲᎾ ᎨᏎᎢ.
Mulungu sanamupatse cholowa kuno, ngakhale kadera kakangʼono kadziko. Koma Mulungu anamulonjeza kuti adzapereka dziko lino kwa iye ndi kwa zidzukulu zake, ngakhale kuti pa nthawi imeneyi analibe mwana.
6 ᎤᏁᎳᏅᎯᏃ ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎢ; “ᏣᏁᏢᏔᏅᏛ ᎠᏁᏙᎯ ᎨᏎᏍᏗ ᎾᎿᎭᎤᎾᏤ-ᎵᎪᎯ ᏂᎨᏒᎾ ᎨᏒᎢ, ᎠᎴ ᎾᎿᎭᎠᏁᎯ ᏙᏓᎬᏩᏂᎾᏢᏂ ᎠᎴ ᎤᏲ ᏅᏓᎬᏩᏅᏁᎵ ᏅᎩᏧᏈ ᏧᏕᏘᏴᏛ.
Mulungu anayankhula motere kwa iye: ‘Zidzukulu zako zidzakhala alendo mʼdziko lachilendo, ndipo zidzakhala akapolo ndi kuzunzidwa zaka 400.’
7 ᎾᏍᎩᏃ ᏑᎾᏓᎴᎩ ᏴᏫ ᏗᎬᏩᏂᎾᏢᏅᎯ ᏙᏓᎦᏥᏳᎪᏓᏁᎵ, ᎣᏂᏃ ᎤᏂᎾᏄᎪᎢᏍᏗ ᎨᏎᏍᏗ ᎠᎴ ᎠᏂ ᎪᎱᏍᏗ ᎬᏆᏛᏁᏗ ᎨᏎᏍᏗ,” ᎤᏛᏁ ᎤᏁᎳᏅᎯ.
Mulungu anati, ‘Ine ndidzalanga dziko limene zidzukulu zako zidzagwireko ukapolo, ndipo pambuyo pake akadzatuluka mʼdzikolo adzandipembedza Ine pamalo pano.’
8 ᏗᎧᎿᎭᏩᏛᏍᏗᏃ ᎤᏁᎴ ᎠᎱᏍᏕᏍᏗ ᎨᏒ ᎤᎬᏩᎵ; ᎡᏆᎭᎻᏃ ᎤᏕᏁᎴ ᎡᏏᎩ, ᎤᎱᏍᏕᏎᎴᏃ ᏧᏁᎵᏁ ᎢᎦ, ᎡᏏᎩᏃ ᏤᎦᏈ, ᏤᎦᏈᏃ ᏔᎳᏚ ᎢᏯᏂᏛ ᏗᎩᎦᏴᎵᎨᎢ.
Kenaka Mulungu anachita pangano la mdulidwe ndi Abrahamu. Ndipo Abrahamu, anabereka Isake, namudula ali ndi masiku asanu ndi atatu. Ndipo Isake anabereka Yakobo, Yakobo anabereka makolo khumi ndi awiri aja.
9 ᏗᎩᎦᏴᎵᎨᏃ ᎠᏅᏳᏤᎲ ᏅᏗᎤᎵᏍᏙᏔᏁ ᎤᏂᎾᏗᏅᏎ ᏦᏩ ᎢᏥᏈᏱ ᏩᎦᏘᏅᏍᏙᏗᏱ; ᎠᏎᏃ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᏚᎧᎿᎭᏩᏗᏙᎮᎢ,
“Makolo athu anachita nsanje ndi Yosefe ndipo anamugulitsa kuti akakhale kapolo ku Igupto. Koma Mulungu anali naye
10 ᎠᎴ ᎤᏭᏓᎴᏍᎨ ᏂᎦᏛ ᎤᏲ ᏄᎵᏍᏓᏁᎵᏕᎬᎢ, ᎠᎴ ᎤᏁᎴ ᎣᏏᏳ ᎠᎦᏓᏅᏖᏗᏱ ᎠᎴ ᎠᎦᏔᎿᎭᎢᏳ ᎨᏒ ᎠᎦᏔᎲ ᏇᎵᏲ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎢᏥᏈᏱ, ᎠᎴ ᏄᎬᏫᏳᏌᏕᎩ ᏄᏩᏁᎴ ᎢᏥᏈᏱ, ᎠᎴ ᏂᎦᏛ ᎦᏁᎸᎢ.
ndipo anamupulumutsa iye kumasautso ake onse. Mulungu anamupatsa Yosefe nzeru ndi chisomo pamaso pa Farao mfumu ya ku Igupto, kotero mfumuyo inamuyika iye kukhala nduna yayikulu ya dziko la Igupto ndiponso nyumba yake yonse yaufumu.
11 ᏂᎬᎾᏛᏃ ᎢᏥᏈᏱ ᎠᎴ ᎨᎾᏂ ᏚᎪᏄᎶᏎᎢ, ᎠᎴ ᎤᏣᏘ ᎠᎩᎵᏯ ᏄᎵᏍᏔᏁᎢ, ᏗᎩᎦᏴᎵᎨᏃ ᎤᎾᏠᎨ ᎤᎾᎵᏍᏓᏴᏗ.
“Kenaka munalowa njala mʼdziko la Kanaani, kotero kuti anthu anavutika kwambiri, ndipo makolo athu sanathe kupeza chakudya.
12 ᏤᎦᏈᏃ ᎤᏛᎦᏅ ᎤᏣᎴᏍᏗ ᎡᎲ ᎢᏥᏈᏱ, ᏕᎤᏅᏎ ᏗᎩᎦᏴᎵᎨ ᎩᎳ ᎾᎨᏎᎢ.
Pamene Yakobo anamva kuti ku Igupto kunali tirigu, iye anatuma makolo athu ulendo woyamba.
13 ᏔᎵᏁᏃ ᏦᏩ ᎠᎾᎵᏅᏟ ᎬᏬᎵᏤᎢ, ᎠᎴ ᏇᎵᏲ ᏕᎤᎦᏙᎥᏎ ᏦᏩ ᎪᎱᏍᏗ ᏧᏩᎿᎭ
Pa ulendo wawo wachiwiri, Yosefe anadziwulula kwa abale akewo ndipo Farao anadziwa za banja la Yosefe.
14 ᏦᏩᏃ ᎤᏓᏅᏎ ᏭᏯᏅᎮ ᎤᏙᏓ ᏤᎦᏈ ᎠᎴ ᏂᎦᏛ ᎤᏩᏒ ᎪᎱᏍᏗ ᏧᏩᎿᎭ ᎾᏍᎩ ᎦᎵᏆᏍᎪᎯ ᎯᏍᎩᎦᎵ ᎢᏯᏂᎢ.
Izi zinachitika, Yosefe anayitanitsa abambo ake Yakobo ndi banja lonse, onse pamodzi analipo 75.
15 ᏤᎦᏈᏃ ᎢᏥᏈᏱ ᏭᎶᏎᎢ, ᎤᏲᎱᏎᏃ, ᎠᎴ ᎾᏍᏉ ᏗᎩᎦᏴᎵᎨᎢ.
Motero Yakobo anapita ku Igupto, kumene iye ndiponso makolo athu anamwalira.
16 ᏌᎩᎻᏃ ᏫᏗᎨᏥᏅᏍᏔᏁᎢ ᎠᎴ ᏕᎨᏥᏂᏌᏁ ᎠᏤᎵᏍᏛ ᎾᏍᎩ ᎡᏆᎭᎻ ᎠᏕᎸ ᏧᎫᏴᏔᏁ ᏥᏚᏩᏎᎴ ᎡᎹ ᏧᏪᏥ, ᎾᏍᎩ ᏌᎩᎻ ᎤᏙᏓ.
Mitembo yawo anayinyamula ndi kupita nayo ku Sekemu kumene inayikidwa mʼmanda amene Abrahamu anagula kochokera kwa ana a Hamori ku Sekemuko.
17 ᎠᏚᎢᏍᏛᏃ ᎤᏍᏆᎸᎯᏗᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏎᎵᏔᏅᎯ ᏧᏁᏤᎴ ᎡᏆᎭᎻ, ᎾᏍᎩ ᎤᏂᏁᏉᏤ ᏴᏫ ᎠᎴ ᎤᏂᏣᏔᏅᎯ ᏄᎾᎵᏍᏔᏁ ᎢᏥᏈᏱ.
“Nthawi itayandikira yakuti Mulungu achite zimene analonjeza kwa Abrahamu, mtundu wathu unakula ndi kuchuluka kwambiri mu Igupto.
18 ᎬᏂ ᏅᏩᏓᎴ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎤᎾᏄᎪᏨ ᎾᏍᎩ ᏄᎦᏔᎲᎾ ᏦᏩ.
Pambuyo pake mfumu yatsopano imene sinkamudziwa Yosefe, inayamba kulamulira dziko la Igupto.
19 ᎾᏍᎩ ᏓᏏᎾᏌᏅᏤᎮ ᎪᎱᏍᏗ ᏗᎬᎿᎭ ᎠᎴ ᎤᏲ ᏂᏚᏩᏁᎴ ᏗᎩᎦᏴᎵᎨᎢ, ᎾᏍᎩ ᏗᎨᎦᏓᎢᏅᏗᏱ ᏧᎾᏍᏗ ᏧᏁᏥ, ᏗᎬᏩᎾᏛᎯᏍᏗ ᏂᎨᏒᎾ ᎢᏳᎵᏍᏙᏗᏱ.
Mfumuyo inachita mwachinyengo ndi mtundu wathu ndi kuwazunza kuti ataye ana awo akhanda kuti afe.
20 ᎾᎯᏳ ᎼᏏ ᎤᏕᏁᎢ, ᎠᎴ ᎤᏩᏔᏅᎯ ᎤᏬᏚᎯᏳ ᎨᏎᎢ, ᎠᎴ ᎠᏥᏍᏆᏂᎪᏔᏁ ᎤᏙᏓ ᎦᏁᎸᎢ ᏦᎢ ᎢᏯᏅᏙ.
“Pa nthawi imeneyo Mose anabadwa, ndipo anali wokongola kwambiri. Iye analeredwa mʼnyumba ya abambo ake kwa miyezi itatu.
21 ᎠᎦᏓᎢᏅᏃ ᏇᎵᏲ ᎤᏪᏥ ᎠᎨᏴ ᎤᏁᏎᎢ, ᎠᎴ ᎤᏍᏆᏂᎪᏔᏁᎢ ᎤᏩᏒ ᎤᏪᏥ ᎤᏰᎸᏁᎢ.
Atakamutaya, mwana wamkazi wa Farao anamutola nakamulera ngati mwana wake.
22 ᏱᏏᏃ ᎠᎨᏲᏅᎯ ᎨᏎ ᏂᎦᎥ ᎠᏂᎦᏔᎿᎭᎢᏳ ᎨᏒ ᎢᏥᏈᏱ ᎠᏁᎯ, ᎠᎴ ᎤᎵᏂᎩᏗᏳ ᎨᏎ ᎤᏁᎢᏍᏗᏱ ᎠᎴ ᏧᎸᏫᏍᏓᏁᏗᏱ.
Mose anaphunzira nzeru zonse za Aigupto, ndipo anali wamphamvu mʼmawu ndi ntchito zake.
23 ᏅᎦᏍᎪᎯᏃ ᎢᏳᏕᏘᏴᏛ ᏄᎵᏍᏔᏅ, ᎤᏓᏅᏖᎴ ᏧᏩᏛᎲᏍᏗᏱ ᎠᎾᎵᏅᏟ ᎢᏏᎵ ᏧᏪᏥ.
“Mose ali ndi zaka makumi anayi, anaganizira zokayendera abale ake Aisraeli.
24 ᎤᎪᎲᏃ ᎠᏏᏴᏫ ᎦᏰᏥᏐᏢᏛᎢ, ᎤᏍᏕᎸᎮᎢ, ᎠᎴ ᎤᏞᏤᎴ ᎤᏲ ᎢᏯᎬᏁᎸᎯ, ᎠᎴ ᎤᎴ ᎢᏥᏈᏱ ᎡᎯ.
Iye ataona mmodzi wa iwo akuzunzidwa ndi Mwigupto, anatchinjiriza Mwisraeliyo, namupha Mwiguptoyo.
25 ᎠᎴ ᎯᎠ ᏁᎵᏍᎨᎢ, ᏛᏃᎵᏥ ᎣᏣᎵᏅᏟ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎠᏴ ᎠᏉᏰᏂ ᏗᎬᏔᏂᏒ ᏙᏗᏍᏕᎸᎯᏒᎢ; ᎠᏎᏃ ᎥᏝ ᏳᏃᎵᏤᎢ.
Mose anaganiza kuti abale ake adzazindikira kuti Mulungu anamuyika kuti awapulumutse koma iwo sanazindikire.
26 ᎤᎩᏨᏛᏃ ᏚᎾᏄᎪᏤᎴ ᎠᎾᎵᎲᎢ, ᎠᎴ ᎦᎪᎯᏍᏓᏁᎮ ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎢ; “ᎢᏍᏗᏍᎦᏯ, ᏗᏍᏓᏓᏅᏟᏉ; ᎦᏙᏃ ᎤᏲ ᏂᏙᏍᏓᏓᏛᏁᎭ?”
Mmawa mwake Mose anaona Aisraeli awiri akukangana. Iye anayesa kuwayanjanitsa ponena kuti, ‘Amuna inu, ndinu abale; chifukwa chiyani mukufuna kupwetekana?’
27 ᎠᏎᏃ ᎤᏣᏘᏂ ᎢᏳᏛᏁᎸᎯ ᎾᎥ ᎢᏧᎾᏓᎳ ᏗᎤᏪᏌᏙᏰᏉ, ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎢ; ᎦᎪ ᏂᏣᎬᏫᏳᏌᏕᎩ ᎠᎴ ᏗᏍᎩᏳᎪᏓᏁᎯ ᎢᏣᎧᏅ ᏂᎯ?
“Koma munthu amene amavutitsa mnzakeyo anakankha Mose ndipo anati, ‘Ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza.
28 ᏥᎪ ᎠᏴ ᎾᏍᏉ ᏣᏚᎵ ᏍᎩᎯᏍᏗᏱ ᎾᏍᎩᏯ ᎤᏒᎯ ᏥᎸᎩ ᎢᏥᏈᏱ ᎡᎯ?
Kodi ukufuna kundipha monga momwe unaphera Mwigupto uja dzulo?’
29 ᎾᏍᎩᏃ ᏄᏪᏒ ᎼᏏ ᎤᎵᏘᏎᎢ, ᎠᎴ ᎻᏗᏂ ᎦᏓ ᎠᎲ ᎡᏙᎯ ᏄᎵᏍᏔᏁᎢ, ᎾᎿᎭᏃ ᎠᏂᏔᎵ ᎠᏂᏍᎦᏯ ᏧᏪᏥ ᎬᏩᏕᏁᎴᎢ.
Mose atamva mawu awa anathawira ku Midiyani, kumene anakhala mlendo ndipo anabereka ana amuna awiri.
30 ᏅᎦᏍᎪᎯᏃ ᏄᏕᏘᏴᎲ ᏗᎧᎿᎭᏩᏗᏙᎯ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎤᏤᎵᎦ ᎬᏂᎨᏒ ᏄᏛᏁᎴ ᎢᎾᎨ ᏌᎾᏱ ᎣᏓᎸ ᎤᏪᏲᏓᏛ ᎠᏓᏪᎵᎩᏍᎬᎢ.
“Ndipo patapita zaka makumi anayi mngelo anaonekera kwa Mose mʼmalawi amoto pa chitsamba mʼchipululu pafupi ndi Phiri la Sinai.
31 ᎼᏏᏃ ᎤᎪᎲ ᎤᏍᏆᏂᎪᏎ ᏄᏍᏛ ᎠᎪᏩᏘᏍᎬᎢ. ᎤᎪᎵᏰᏗᏱᏃ ᎤᏰᎸᏅ ᎾᎥ ᏭᎷᏨ ᏗᎪᎵᏰᏎᎢ, ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎧᏁᎬ ᎤᏛᎦᏁ [ ᎯᎠ ᏂᎦᏪᏍᎨᎢ; ]
Iye ataona zimenezi, anadabwa. Akupita kuti akaonetsetse pafupi, Mose anamva mawu a Ambuye:
32 “ᎠᏴ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᏗᏣᎦᏴᎵᎨ ᎤᎾᏤᎵᎦ, ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎡᏆᎭᎻ ᎤᏤᎵᎦ, ᎠᎴ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎡᏏᎩ ᎤᏤᎵᎦ, ᎠᎴ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᏤᎦᏈ ᏅᏤᎵᎦ.” ᎣᏏᏃ ᎤᏪᎿᎭᏪᎢ, ᎠᎴ ᎤᏍᎦᎴ ᎤᎪᎵᏰᏗᏱ.
‘Ine ndine Mulungu wa makolo ako, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo.’ Mose ananjenjemera chifukwa cha mantha ndipo sanalimbe mtima kuyangʼananso.
33 ᎤᎬᏫᏳᎯᏃ ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎴᎢ; “ᏔᎳᏑᎳᎩ, ᎾᎿᎭᏰᏃ ᏥᏙᎦ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᎦᏙᎯ.
“Ndipo Ambuye anati kwa Mose, ‘Vula nsapato zako, pakuti malo amene wayimapo ndi opatulika.
34 ᎤᏙᎯᏳᎯᏯ ᎠᎩᎪᎲ ᎤᏲ ᏄᎾᎵᏍᏓᏁᎵᏕᎬ ᏴᏫ ᏗᏆᏤᎵ ᎢᏥᏈᏱ ᏣᏁᎭ, ᎠᎴ ᎠᏆᏛᎦᏅ ᏚᏂᎵᏰᏗᏍᎬᎢ, ᎠᎴ ᎠᏆᏠᎣᏏᎸ ᏕᎫᏓᎴᏏᎸ; Ꭷ ᎿᎭᏉ ᏓᎬᏅᏏ ᎢᏥᏈᏱ.”
Ine ndaona ndithu mazunzo a anthu anga amene ali ku Igupto. Ndamva kulira kwawo choncho ndabwera kuti ndiwapulumutse. Tsopano tiye ndikutume ku Igupto.’
35 ᎾᏍᎩ ᎯᎠ ᎼᏏ ᏧᏂᏲᎢᏎᎴ ᎯᎠ ᏥᏄᏂᏪᏎᎢ, ᎦᎪ ᏂᏣᎬᏫᏳᏌᏕᎩ ᎠᎴ ᏚᎪᏗᏍᎩ ᏣᎧᏅ, ᎾᏍᎩ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏅᏎ ᏄᎬᏫᏳᏌᏕᎩ ᎠᎴ ᎤᏄᏓᎴᏍᎩ ᏄᏩᏁᎴ ᎤᏩᏔᏁ ᏗᎧᎿᎭᏩᏗᏙᎯ ᎬᏂᎨᏒ ᎢᏳᏛᏁᎸᎯ ᎤᏪᏲᏓᏛᎢ.
“Uyu ndi Mose yemwe uja amene Aisraeli anamukana ndi kunena kuti, ‘Ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza?’ Iyeyo anatumidwa ndi Mulungu mwini kuti akakhale wowalamulira ndiponso mpulumutsi, mothandizidwa ndi mngelo amene anamuonekera pa chitsamba.
36 ᎾᏍᎩ ᏚᏘᎿᎭᏫᏛᎮᎢ ᏂᏚᎸᏫᏍᏓᏁᎶ ᎤᏍᏆᏂᎪᏗ ᎠᎴ ᎤᏰᎸᏛ ᎢᏥᏈᏱ ᎠᎴ ᎠᎹ-ᎩᎦᎨᏍᏛᏱ ᎠᎴ ᎢᎾᎨ ᏅᎦᏍᎪᎯ ᏧᏕᏘᏴᏛ.
Iye anawatulutsa mu Igupto ndipo anachita zodabwitsa ndi zizindikiro zozizwitsa mu Igupto, pa Nyanja Yofiira, ndiponso mʼchipululu kwa zaka makumi anayi.
37 ᎯᎠ ᎾᏍᎩ ᎼᏏ ᎾᏍᎩ ᎯᎠ ᏥᏂᏚᏪᏎᎴ ᎢᏏᎵ ᏧᏪᏥ; ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎢᏣᏁᎳᏅᎯ ᏓᏥᎾᏄᎪᏫᏎᎵ ᎠᏙᎴᎰᏍᎩ ᎢᏣᎵᏅᏟ ᎨᏒ ᏓᎦᎾᏄᎪᏥ ᎠᏴ ᎾᏍᎩᏯᎢ; ᎾᏍᎩ ᏓᏰᏣᏛᎦᏁᎵ.
“Uyu ndi Mose uja amene anati kwa Aisraeli, ‘Mulungu adzawutsa pakati pa abale anu mneneri ngati ine.’
38 ᎯᎠ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᏥᎨᎳᏗᏙᎮ ᎤᎾᏓᏡᏩᏕᎬ ᎢᎾᎨᎢ, ᏔᎵ ᏧᏛᏗᏕᎨ ᏗᎧᎿᎭᏩᏗᏙᎯ ᎾᏍᎩ ᏧᏁᏤᎴ ᎣᏓᎸ ᏌᎾᏱ, ᏥᎨᎳᏗᏙᎮ ᎠᏁᏙᎲ ᏗᎩᎦᏴᎵᎨᎢ, ᎾᏍᎩ ᎾᏍᏉ ᏥᏓᏥᏲᎯᏎᎴ ᎠᏛᏂᏗᏍᏙᏗ ᎧᏃᎮᏛ ᎠᏴ ᎢᎩᏁᏗ.
Iyeyu anali mʼgulu la Aisraeli mʼchipululu pamodzi ndi mngelo amene anamuyankhula pa phiri la Sinai ndiponso makolo athu; ndipo Mose analandira mawu amoyo kuti atipatse ife.
39 ᎾᏍᎩ ᏗᎩᎦᏴᎵᎨ ᎥᏝ ᏳᎾᏚᎵᏍᎨ ᎤᏃᎯᏳᏗᏱ, ᎢᏴᏛᏉᏍᎩᏂ ᏄᏅᏁᏔᏁᎢ, ᎠᎴ ᏚᎾᏓᏅᏛ ᎢᏥᏈᏱᏉ ᏫᏂᏚᏅᏁᎢ,
“Koma makolo athu anakana kumumvera iye. Iwo anamukana iye ndipo mʼmitima mwawo anatembenukira ku Igupto.
40 ᎯᎠ ᏄᏂᏪᏎᎴ ᎡᎳᏂ; ᏗᏍᎩᏲᏢᎾᏏ ᏦᎦᏁᎳᏅᎯ ᏗᎪᎦᏘᏂᏙᎯ, ᎯᎠᏰᏃ ᎼᏏ ᎢᏥᏈᏱ ᏂᏙᏓᏲᎦᏘᏅᏍᏔᏅᎯ ᎥᏝ ᏲᏥᎦᏔᎭ ᏄᎵᏍᏓᏁᎸᎢ.
Iwo anati kwa Aaroni, ‘Bwera utipangire milungu imene idzititsogolera. Kunena za Mose amene anatitsogolera kutuluka mʼdziko la Igupto, sitikudziwa chimene chamuchitikira.
41 ᎾᎯᏳᏃ ᎤᏃᏢᏁ ᏩᎦ ᎠᎩᎾ, ᎾᏍᎩᏃ ᏗᏟᎶᏍᏔᏅᎯ ᎠᏥᎸ-ᎨᎳᏍᏗ ᎤᏂᏲᎮᎴᎢ, ᎠᎴ ᎤᎾᎵᎮᎵᏤᎴ ᎤᏅᏒ ᏧᏃᏰᏂ ᏧᏅᏔᏅᎯ ᎤᏃᏢᏅᎯ.
Iyi ndi nthawi imene anapanga fano la mwana wangʼombe. Anapereka nsembe kwa fanoli nachita chikondwerero kulemekeza ntchito ya manja awo.
42 ᎿᎭᏉᏃ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᎦᏔᎲᏎᎢ, ᎠᎴ ᎤᎾᏁᎳᎩ ᏫᏓᏂᎸᏉᏓ ᎤᏂᏣᏘ ᎦᎸᎶ ᎠᏁᎯ ᏚᏪᎵᏎᎴᎢ, ᎾᏍᎩᏯ ᎯᎠ ᏥᏂᎬᏅ ᏥᎪᏪᎳ ᎠᎾᏙᎴᎰᏍᎩ ᏧᏃᏪᎳᏅᎯ; “ᏂᎯ ᎢᏏᎵ ᏏᏓᏁᎸᎯ ᎨᏒᎢ, ᏥᎪ ᏕᏍᎩᏃᎮᎸ ᏗᎸᎯ ᎦᎾᏝᎢ ᎠᎴ ᎠᏥᎸ-ᎨᎳᏍᏗ ᏅᎦᏍᎪᎯ ᏥᎾᏕᏘᏴ ᎢᎾᎨᎢ?
Koma Mulungu anawafulatira, nawapereka kuti apembedze zolengedwa zakumwamba. Zimenezi zikugwirizana ndi zimene zinalembedwa mʼbuku la aneneri kuti, “‘Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?’
43 ᎢᏥᎲᏒᏰᏃ ᎦᎵᏦᏙᏗ ᎼᎳᎩ ᎤᏤᎵᎦ ᎠᎴ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎢᏥᏰᎸᎯ ᎴᎻᏈᏂ ᎤᏤᎵᎦ ᏃᏈᏏ, ᏗᏟᎶᏍᏔᏅᎯ ᎾᏍᎩ ᏗᏦᏢᏅᎯ ᏗᏣᏓᏙᎵᏍᏓᏁᏗ; ᏓᏗᎶᏂᏃ ᎤᏗᏗᏢ ᏫᏙᏓᏨᏯᎧᏂ.”
Ayi, inu mwanyamula tenti ya Moloki ndi nyenyezi ya mulungu wanu Refani, mafano amene munapanga kuti muziwapembedza. Chifukwa chake, Ine ndidzakutumizani kutali, kupitirira dziko la Babuloni.
44 ᏗᎩᎦᏴᎵᎨ ᎢᎾᎨ ᎤᏂᎮ ᎦᎵᏦᏛ ᎠᏙᎴᎰᎯᏍᏙᏗ, ᎾᏍᎩᏯ ᎤᏁᏨᎢ ᎼᏏ ᏧᏁᏤᎴ ᎤᏬᏢᏗᏱ ᏧᏟᎶᏍᏙᏗᏱ ᏄᏍᏛ ᎤᎪᎲᎢ.
“Makolo athu anali ndi tenti ya msonkhano pakati pawo mʼchipululu. Anayipanga monga momwe Mulungu anawuzira Mose, molingana ndi chithunzi chimene Mose anachiona.
45 ᎾᏍᎩ ᎾᏍᏉ ᏗᎩᎦᏴᎵᎨ ᏗᎨᏥᏲᎯᏎᎸᎯ ᎨᏒ ᏦᏑᏩ ᏧᎾᏖᏉᎶᏎ ᏧᏂᏲᎴ ᏧᎾᏓᎴᏅᏛ ᏴᏫ ᎤᎾᏤᎵᎪᎯ ᎾᏍᎩ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᏥᏚᎨᎯᏕᎴ ᏗᎩᎦᏴᎵᎨ ᏕᏫ ᏤᎮ ᎢᏯᏍᏗ.
Makolo athu, atayilandira Tentiyo, anabwera nayo motsogozedwa ndi Yoswa pamene analanda dziko la mitundu imene Mulungu anayipirikitsa pamaso pawo. Tentiyo inakhala mʼdzikomo mpaka nthawi ya Davide,
46 ᎾᏍᎩ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎣᏏᏳ ᎤᏓᏅᏖᏍᎩ ᏄᎵᏍᏔᏁᎢ, ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᎤᏔᏲᎴ ᎤᏩᏛᏗᏱ ᎤᏁᎳᏗᏍᏗᏱ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᏤᎦᏈ ᎤᏤᎵᎦ.
amene anapeza chisomo pamaso pa Mulungu ndipo anapempha kuti amʼmangire nyumba Mulungu wa Yakobo.
47 ᎠᏎᏃ ᏐᎵᎹᏅ ᎤᏁᏍᎨᎴᎢ.
Koma anali Solomoni amene anamanga nyumbayo.
48 ᎥᏝᏍᎩᏂᏃᏅ ᏩᏍᏛ ᎦᎸᎳᏗᏳ ᎡᎯ ᏱᎦᏁᎸ ᏓᏓᏁᎸ ᎩᎶ ᏧᏃᏰᏂ ᏧᏅᏔᏅᎯ ᏧᎾᏁᏍᎨᎲᎯ, ᎾᏍᎩᏯ ᎠᏙᎴᎰᏍᎩ ᎯᎠ ᏥᏂᎦᏪᎠ;
“Komatu, Wammwambamwambayo sakhala mʼnyumba zomangidwa ndi anthu. Monga mneneri akunena kuti,
49 “ᎦᎸᎳᏗ ᎠᎩᏗᏱ ᎡᎶᎯᏃ ᏗᏆᎳᏏᏗᏱ. ᎦᏙ ᎤᏍᏕᏍᏗ ᎦᎵᏦᏕ ᏓᏍᎩᏯᏁᏍᎨᎵ? ᎠᏗᎭ ᎤᎬᏫᏳᎯ; ᎠᎴ ᎭᏢ ᎠᏆᎵᏙᎯᏍᏙᏗᏱ;
“‘Kumwamba ndi mpando wanga waufumu, ndipo dziko lapansi ndi chopondapo mapazi anga. Kodi mudzandimangira nyumba yotani? Akutero Ambuye. Kapena malo opumuliramo Ine ali kuti?
50 ᏝᏍᎪ ᎠᏉᏰᏂ ᎠᏋᏔᏅᎯ ᎠᏉᏢᏅᎯ ᏱᎩ ᎯᎠ ᏂᎦᏛ ᏥᏄᏍᏗᏓᎾ?”
Kodi si dzanja langa linapanga zonsezi?’
51 ᏧᏩᏗᏔᏯ ᏗᏥᎩᎵᎨᏂ, ᎠᎴ ᏂᏕᏥᎤᏍᏕᏎᎸᎾ ᏗᏥᎾᏫ ᎠᎴ ᏕᏥᎵᎷᎬᎢ, ᏂᎪᎯᎸ ᎡᏣᏡᏗᏍᎪ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᎠᏓᏅᏙ; ᏗᏥᎦᏴᎵᎨ ᏄᎾᏛᏁᎸ ᎾᏍᎩᏯ ᏂᎯ ᏂᏣᏛᏁᎰᎢ.
“Anthu wokanika inu, osachita mdulidwe wa mu mtima ndi a makutu ogontha! Inu ofanana ndi makolo anu. Nthawi zonse mumakana kumvera Mzimu Woyera:
52 ᎦᏙ ᎤᏍᏗ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᎠᎾᏙᎴᎰᏍᎩ ᎨᏒ ᏗᏥᎦᏴᎵᎨ ᎥᏝ ᎤᏲ ᎢᏳᏅᏁᎸᎯ ᏱᎩ? ᎠᎴ ᏕᎤᏂᎸ ᎤᎾᏙᎴᎰᏒᎯ ᎬᏂᎨᏒ ᎢᏳᏅᏁᎸᎯ ᎤᎷᎯᏍᏗᏱ ᎾᏍᎦᏅᎾ ᎾᏍᎩ ᏂᎯ ᎡᏥᎶᏄᎡᎸᎯ ᎠᎴ ᎡᏥᎸᎯ ᏥᏄᎵᏍᏔᏅ;
Kodi analipo mneneri amene makolo anu sanamuzunze? Iwo anapha ngakhale amene ananeneratu za kubwera kwa Wolungamayo. Ndipo tsopano inu munamupereka ndi kumupha Iye.
53 ᏤᏥᏲᎯᏎᎸᎩ ᏗᎧᎿᎭᏩᏛᏍᏗ ᏗᏂᎧᎿᎭᏩᏗᏙᎯ ᎣᏍᏛ ᏄᏅᎿᎭᏕᎬᎢ ᎠᏎᏃ ᎥᏝ ᎢᏥᏍᏆᏂᎪᏔᏅᎯ ᏱᎩ.
Inu amene munalandira Malamulo amene anaperekedwa ndi angelo ndipo simunawamvere.”
54 ᎾᏍᎩᏃ ᎤᎾᏛᎦᏅ ᏚᏂᏘᎴ ᏧᏂᎾᏫᏱ, ᎠᎴ ᏗᏂᏄᏙᎬ ᏕᎬᏩᏄᏓᎨᎴᎢ.
Atamva zimenezi, iwo anakwiya kwambiri ndipo anamukukutira mano.
55 ᎠᏎᏃ ᎤᎧᎵᏨᎯ ᎨᏎ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᎠᏓᏅᏙ ᎤᏯᏅᏒᎯ ᎦᎸᎳᏗ ᏫᏚᎧᎿᎭᏁᎢ, ᎠᎴ ᏭᎪᎮ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᎨᏒ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏤᎵᎦ, ᎠᎴ ᏥᏌ ᎦᏙᎨ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎠᎦᏘᏏᏗᏢ;
Koma Stefano, wodzaza ndi Mzimu Woyera, anayangʼana kumwamba ndipo anaona ulemerero wa Mulungu ndiponso Yesu atayimirira ku dzanja lamanja la Mulungu.
56 ᎯᎠᏃ ᏄᏪᏎᎢ; ᎬᏂᏳᏉ ᎦᎸᎳᏗ ᎤᎵᏍᏚᎢᏛ ᏥᎪᏩᏘᎭ, ᎠᎴ ᏴᏫ ᎤᏪᏥ ᎦᏙᎦ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎠᎦᏘᏏᏗᏢ.
Stefano anati, “Taonani, ndikuona kumwamba kotsekuka ndiponso Mwana wa Munthu atayimirira ku dzanja la manja la Mulungu.”
57 ᎠᏍᏓᏯᏃ ᎤᏁᎷᏅ ᏗᏏᎴᏂ ᏚᏂᏍᏚᏁᎢ, ᎠᎴ ᎤᎴᏃᏅᎯ ᎤᎾᏁᎷᎩᎡᎴᎢ;
Koma iwo anatseka mʼmakutu mwawo, ndipo anafuwula kolimba, onse anathamangira kwa iye,
58 ᎦᏚᎲᏃ ᎤᏂᏄᎪᏫᏒ ᏅᏯ ᏚᏅᏂᏍᏔᏁᎢ. ᎠᏂᎦᏔᎯᏃ ᏧᎾᏅᏬ ᏚᏂᏅᏁ ᏚᎳᏍᎬ ᎾᎥ ᎠᏫᏅ ᏐᎳ ᏧᏙᎢᏛ.
anamukokera kunja kwa mzinda ndipo anayamba kumugenda miyala. Mboni zinasungitsa zovala zawo kwa mnyamata otchedwa Saulo.
59 ᏅᏯᏃ ᏚᏅᏂᏍᏔᏁ ᏍᏗᏫ ᎠᏓᏙᎵᏍᏗᏍᎨᎢ, ᎯᎠ ᏂᎦᏪᏍᎨᎢ; ᏣᎬᏫᏳᎯ, ᏥᏌ, ᏔᏓᏂᎸᎩ ᎠᏆᏓᏅᏙᎩ.
Akumugenda miyala, Stefano anapemphera kuti, “Ambuye Yesu, landirani mzimu wanga.”
60 ᏚᎵᏂᏆᏅᏅᏃ ᎠᏍᏓᏯ ᎤᏪᎷᏁᎢ, ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎢ; ᏣᎬᏫᏳᎯ, ᏞᏍᏗ ᎯᎠ ᎤᏂᏍᎦᏅᏨ ᏱᎦᎯᏍᏔᏁᏍᏗ. ᎾᏍᎩᏃ ᏄᏪᏒ ᎤᎸᏁᎢ.
Ndipo anagwada pansi nafuwula mwamphamvu kuti, “Ambuye musawawerengere tchimoli.” Atanena mawu amenewa anamwalira.

< ᎨᏥᏅᏏᏛ ᏄᎾᏛᏁᎵᏙᎸᎢ 7 >