< ᎪᎵᏂᏗᏱ ᎠᏁᎯ ᏔᎵᏁ ᎨᎪᏪᎳᏁᎸᎯ 3 >

1 ᏥᎪ ᏔᎵᏁ ᎣᏣᎴᏂ ᎣᎬᏒ ᎣᏣᏓᎸᏉᏗᎭ? ᏥᎪᎨ ᎠᏎ ᏫᏗᏨᏃᎮᏗ ᏃᎦᎵᏍᏓᏁᎭ, ᎪᏪᎵ ᎣᎩᎸᏉᏗᏍᎩ ᎩᎶ ᏥᏄᎾᎵᏍᏓᏁᎰᎢ, ᎠᎴ ᏂᎯ ᏗᏍᎩᏅᏁᎸᎯ ᏍᎩᎸᏉᏗᏍᎩ?
Kodi tayambanso kudzichitira umboni tokha? Kapena kodi ifenso tikufuna makalata otivomereza kwa inu, kapena ochokera kwa inu monga anthu ena?
2 ᏂᎯ ᎪᏪᎵ ᎣᎦᏤᎵᎦ, ᏥᎪᏪᎳ ᏦᎩᎾᏫᎯ, ᎾᏂᎥ ᏴᏫ ᏣᏂᎦᏔᎭ ᎠᎴ ᏣᏂᎪᎵᏰᎠ.
Inu ndinu kalata yathu, yolembedwa pa mitima yathu, yodziwika ndi yowerengedwa ndi aliyense.
3 ᎬᏂᎨᏒᎢᏳ ᎢᏰᏨᏁᎸᎯ ᏂᎯ ᎦᎶᏁᏛ ᎤᏤᎵ ᎪᏪᎵ ᎨᏒᎢ, ᎠᏴ ᏦᎩᎸᏫᏍᏓᏁᎸᎯ, ᎪᏪᎳᏅᎯ ᎪᏪᎶᏗ ᎬᏔᏅᎯ ᏂᎨᏒᎾ, ᎠᏓᏅᏙᏍᎩᏂ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎬᏂᏛ ᎤᏤᎵ ᎬᏔᏅᎯ; ᎥᏝ ᏅᏲᎯ ᏗᎪᏪᎶᏗᏱ ᏗᎪᏪᎳᏅᎯ ᏱᎩ, ᎤᏇᏓᎵᏍᎩᏂ ᎨᏒ ᏗᎪᏪᎶᏗᏱ ᎣᎾᏫᏱ.
Inu mukuonetsa kuti ndinu kalata yochokera kwa Khristu, zotsatira za utumiki wathu, osati yolembedwa ndi inki koma ndi Mzimu wa Mulungu wamoyo, osati pa miyala yosemedwa koma mʼmitima ya anthu.
4 ᎾᏍᎩᏃ ᏄᏍᏗ ᏱᏣᎵᏍᎦᏍᏙᏛ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎦᎶᏁᏛ ᎢᏳᏩᏂᏌᏛ.
Kulimba mtima kumeneku tili nako pamaso pa Mulungu kudzera mwa Khristu.
5 ᎥᏝᏍᎩᏂᏃᏅ ᎣᎬᏒ ᎨᏒ ᏰᎵ ᎦᏲᎦᏓᏅᏖᏗ ᏱᎩ ᎪᎱᏍᏗ ᎣᎬᏒᏉ ᎨᏒ ᏅᏛᏓᎴᎲᏍᎩ, ᏰᎵᏉᏍᎩᏂ ᎢᎦᏲᎦᏛᏁᏗ ᎨᏒ ᎤᏁᎳᏅᎯᏱ ᏗᏓᎴᎲᏍᎦ.
Sikuti mwa ife muli kanthu kotiganizitsa kuti tingathe kugwira ntchitoyi patokha, koma kulimba mtima kwathu kumachokera kwa Mulungu.
6 ᎾᏍᎩ ᎾᏍᏉ ᏰᎵ ᎢᎦᏲᎦᏛᏁᏗ ᏥᏃᎬᏁᎸ ᏦᎩᎸᏫᏍᏓᏁᏗᏱ ᎾᎿᎭᎢᏤ ᎧᏃᎮᏛ ᏓᏠᎯᏍᏛᎢ; ᎥᏝ ᎠᏗᎾ ᏄᏍᏛ ᎪᏪᎸᎢ, ᎠᏓᏅᏙᏍᎩᏂ ᏓᏕᏲᎲᏍᎬᎢ; ᏄᏍᏛᏰᏃ ᎪᏪᎸ ᎠᏓᎯᎰᏉ, ᎠᏓᏅᏙᏍᎩᏂ ᎠᏓᏛᏂᏗᏍᎪᎢ.
Iye watipatsa kulimba mtima kuti tikhale atumiki a pangano latsopano, osati malamulo olembedwa koma a Mzimu; pakuti malamulo olembedwa amapha koma Mzimu amapereka moyo.
7 ᎢᏳᏃ ᏗᎦᎸᏫᏍᏓᏁᏗ ᎠᏓᎯᎯ ᎨᏒ ᎤᎬᏩᎵ ᏥᎪᏪᎴ ᏣᏰᎶᎴ ᏅᏲᎯ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᏥᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎢᏏᎵ ᏧᏪᏥ ᎪᎯᏛ ᏗᎬᏩᎾᎧᏃᏗ ᏂᎨᏒᎾ ᏥᎨᏎ ᎼᏏ ᎤᎧᏛᎢ, ᏥᏅᏗᎦᎵᏍᏙᏗᏍᎨ ᏗᎬᏩᎸᏌᏛ ᎨᏒ ᎤᎧᏛᎢ; ᎾᏍᎩ ᎠᎲᏍᏗᏉ ᏥᎨᏎᎢ;
Koma ngati utumiki umene unabweretsa imfa uja, wolembedwa ndi malemba pa mwalawu, unabwera ndi ulemerero mwakuti Aisraeli sanathe kuyangʼanitsitsa nkhope ya Mose chifukwa cha ulemerero wa pa nkhopeyo, ngakhale kuti unali kunka nuzilala,
8 ᏝᏍᎪ Ꮀ ᏳᎬᏫᏳᏎᏍᏗ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᏱᎨᏎᏍᏗ ᎠᏓᏅᏙ ᎤᎬᏩᎵ ᎨᏒ ᏗᎦᎸᏫᏍᏓᏁᏗ?
kodi nanga utumiki wa Mzimu sudzaposa apa?
9 ᎢᏳᏰᏃ ᏗᎦᎸᏫᏍᏓᏁᏗ ᏗᏓᏚᎪᏓᏁᎯ ᎨᏒ ᎦᎾᏄᏫᏍᎩ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᏱᎩ, Ꮀ ᎤᎬᏫᏳᎭ ᎤᏓᎪᎾᏛᏗ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᎠᏓᏚᏓᎴᏍᎩ ᎨᏒ ᏗᎦᎸᏫᏍᏓᏁᏗ.
Ngati utumiki umene umatsutsa anthu unali ndi ulemerero, nanga koposa kotani ulemerero wa utumiki wobweretsa chilungamo!
10 ᎾᏍᎩᏰᏃ ᎾᏍᏉ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᎢᎬᏁᎸᎯ ᏥᎨᏎ ᎥᏝ ᎰᏩ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᏱᎨᏎᎢ, ᏅᏗᎦᎵᏍᏙᏗᏍᎨ ᎬᏩᏓᎪᎾᏛᏛ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᎨᏒ ᏐᎢ.
Pakuti zimene zinali ndi ulemerero, tsopano zilibenso ulemerero pofananitsa ndi ulemerero wopambanawo.
11 ᎢᏳᏰᏃ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᎠᎲᏛ ᏥᎩ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᏱᎨᏎᎢ, ᎤᏟᎯᏳ ᏭᏓᎪᎾᏛᏗ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᏥᏅᏩᏍᏗᏉ.
Ndipo ngati zosakhalitsa zinabwera ndi ulemerero, koposa kotani ulemerero wamuyayawo!
12 ᎾᏍᎩᏃ Ꮎ ᏥᏄᏍᏗ ᎤᏚᎩ ᏦᎬᎭ, ᎤᏣᏘ ᎠᎯᏗᏳ ᎦᎪᎵᏍᏗ ᎣᏥᏬᏂᎭ;
Choncho, popeza tili ndi chiyembekezo chotere, ndife olimba mtima kwambiri.
13 ᎢᏝᏃ ᎼᏏ ᏥᏄᏛᏁᎴ [ ᏱᏃᏣᏛᏁᎭ ] ᏧᎵᎬᏚᎳᏁ ᎾᏍᎩ ᎢᏏᎵ ᏧᏪᏥ ᏫᏗᎬᏩᎾᎧᏃᏗ ᏂᎨᏒᎾ ᎢᏳᎵᏍᏙᏗᏱ ᏩᏍᏛ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᎠᎲᏛ ᏥᎩ.
Ife sitili ngati Mose amene amaphimba nkhope yake kuopa kuti Aisraeli angaone kuti kunyezimira kwa nkhope yake kumazilala.
14 ᏚᎾᏓᏅᏛᏍᎩᏂ ᏧᏍᎦᏃᎵᏳ ᎨᏎᎢ; ᎪᎯᏰᏃ ᎢᏯᏍᏗ ᏅᏩᏍᏗᏉ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᎠᎵᎬᏚᎶ ᎠᎲᏛ ᏂᎨᏒᎾ ᎢᏳᏃ ᏓᏂᎪᎵᏯ ᎤᏪᏘ ᎧᏃᎮᏛ ᏓᏠᎯᏍᏛ ᎪᏪᎸᎢ; ᎦᎶᏁᏛᏰᏃ ᏂᎬᏂᏏᏍᎪ ᎠᎲᏛ ᏂᎨᏐᎢ.
Koma nzeru zawo zinawumitsidwa, pakuti mpaka lero chophimbira chomwecho chikanalipo pamene akuwerenga Chipangano Chakale. Sichinachotsedwebe, chifukwa chimachotsedwa ngati munthuyo ali mwa Khristu yekha.
15 ᎩᎳᎯᏳᏉᏍᎩᏂ ᎪᎯ ᎢᎦ ᎢᏯᏍᏗ ᎢᏳᏃ ᎼᏏ ᏓᏥᎪᎵᏯ ᎠᎵᎬᏚᎶ ᏧᏂᎾᏫ ᏚᏭᏢᏙᎢ.
Ngakhale lero lomwe lino akuwerenga mabuku a Mose pali chophimbabe mitima yawo.
16 ᎠᏎᏍᎩᏂᏃᏅ, ᎤᎬᏫᏳᎯᏱ ᏫᏓᎦᏔᎲᏍᏔᏅᎭ, ᎾᏍᎩ Ꮎ ᎠᎵᎬᏚᎶ ᎢᏴᏛ ᎢᎬᏁᏗ ᏅᏓᎦᎵᏍᏔᏂ.
Koma pamene aliyense atembenukira kwa Ambuye, “chophimbacho chimachotsedwa.”
17 ᎠᎴ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᎠᏓᏅᏙ; ᎢᎸᎯᏢᏃ ᏄᏛᎿᎭᏕᎬ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎤᏤᎵ ᎠᏓᏅᏙ, ᎾᎿᎭᎡᎭ ᎣᏩᏒ ᎣᏓᏤᎵᎦᏯ ᎨᏒᎢ.
Tsono Ambuye ndi Mzimu, ndipo pamene pali Mzimu wa Ambuye, pali ufulu.
18 ᎠᏴᏍᎩᏂ ᏂᏗᎥ ᏂᏗᎦᎵᎬᏚᎸᎾ ᎠᏓᎨᏗᏱ ᎾᏍᎩᏯ ᏕᏓᎧᏂᏍᎬ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᎨᏒ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎤᏤᎵᎦ, ᎢᏓᏓᏁᏟᏴᎭ ᎾᏍᎩᏯ ᏄᏍᏛ ᏂᏓᎵᏍᏗᎭ, ᎦᎸᏉᏗᏳ ᎨᏒ ᎢᎩᎲ ᎧᏁᏉᏤᎦ, ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎤᏓᏅᏙ ᎢᏳᏩᏂᏌᏛ ᎾᏍᎩᏯᎢ.
Ife tonse, amene ndi nkhope zosaphimba timaonetsera ulemerero wa Ambuye, tikusinthika kufanana ndi ulemerero wake, umene ukunka nuchulukirachulukira, wochokera kwa Ambuye, amene ndi Mzimu.

< ᎪᎵᏂᏗᏱ ᎠᏁᎯ ᏔᎵᏁ ᎨᎪᏪᎳᏁᎸᎯ 3 >