< ᎪᎵᏂᏗᏱ ᎠᏁᎯ ᏔᎵᏁ ᎨᎪᏪᎳᏁᎸᎯ 11 >

1 ᏲᎯᏉ ᎤᏍᏗᎩᏛ ᎤᏁᎳᎩ ᎨᏍᎩᏰᎵᏎᏗ ᏱᎩ ᎠᎩᏁᎫ ᎨᏒᎢ; ᎠᎴ ᎤᏙᎯᏳᎯ ᎤᏁᎳᎩ ᏍᎩᏰᎵᏏ.
Ndikukhulupirira kuti mupirira nako pangʼono kupusa kwanga. Chonde tandipirirani!
2 ᏕᏨᏰᎷᎦᏰᏃ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᏗᎬᏩᏓ ᏂᎸᎢᏍᏗ ᎠᏛᏳᎨᏗ ᎨᏒ ᎬᏗᎭ; ᏌᏉᏰᏃ ᎠᏍᎦᏯ ᏗᏣᏨᏍᏗᏱ ᏂᏨᏴᏁᎸ, ᎾᏍᎩ ᎤᎵᏏᎾᎯᏍᏗ ᎠᏛ ᎢᎦᎦᏛ ᎦᎶᏁᏛ ᏫᏗᏨᏲᎯᏎᏗᏱ.
Nsanje imene ndimakuchitirani ndi yofanana ndi ya Mulungu. Ndinakulonjezani mwamuna mmodzi yekha, mwamunayo ndiye Khristu, kuti ndidzakuperekeni inuyo kwa Iyeyo monga namwali wangwiro.
3 ᎠᏎᏃ ᏥᎾᏰᏍᎦ, ᎾᏍᎩᏯ Ꮎ ᎢᎾᏛ ᏧᎶᏄᎮᎴ ᎢᏫ ᎠᏏᎾᏌᏅ ᏥᎬᏗᏍᎨᎢ, ᎾᏍᎩᏯ ᏕᏣᏓᏅᏛ ᏱᏓᎪᎸᎾ ᏗᏥᏲᎯᏍᏗᏱ ᏱᏂᎬᎦ ᏄᏠᎾᏍᏛᎾ ᎨᏒ ᎦᎶᏁᏛ ᎤᏤᎵᎦ.
Koma ndikuopa kuti monga Hava ananyengedwa ndi kuchenjera kwa njoka, mitima yanunso ingasocheretsedwe kuleka nʼkudzipereka moona mtima ndi modzipereka kwenikweni kwa Khristu.
4 ᎩᎶᏰᏃ ᎢᏥᎷᏤᎯ ᏅᏩᏓᎴ ᏥᏌ ᎠᎵᏥᏙᎲᏍᎨᏍᏗ, ᎾᏍᎩ Ꮎ ᎠᏴ ᎣᏣᎵᏥᏙᏅᎯ ᏂᎨᏒᎾ, ᎢᏳ ᎠᎴ ᏅᏩᏓᎴ ᎠᏓᏅᏙ ᏙᏣᏓᏂᎸᏨᎭ, ᎾᏍᎩ Ꮎ ᏗᏣᏓᏂᎸᏨᎯ ᏂᎨᏒᎾ, ᎠᎴ ᏅᏩᏓᎴ ᎣᏍᏛ ᎧᏃᎮᏛ, ᎾᏍᎩ Ꮎ ᏗᏣᏓᏂᎸᏨᎯ ᏂᎨᏒᎾ, ᎣᏏᏳᏉ ᎤᏁᎳᎩ ᏱᏤᎵᏒ.
Pakuti ngati wina abwera kwa inu nalalikira Yesu wina wosiyana ndi Yesu amene tinamulalikira, kapena ngati mulandira mzimu wina wosiyana ndi Mzimu amene munalandira, kapena uthenga wabwino wina wosiyana ndi umene munawuvomereza, inuyo mumangolandira mosavuta.
5 ᎦᏓᏅᏖᏍᎬᏰᏃ ᎥᏝ ᎤᏍᏗ ᎤᏅ ᎡᏍᎦ ᏱᎦᏥᏲᎠᏍᎦ ᏄᏂᎬᏫᏳᏒ ᎨᏥᏅᏏᏛ ᎨᏒᎢ.
Komatu sindikuganiza kuti ndine wotsika kwambiri kwa “atumwi apamwamba.”
6 ᎤᏁᎳᎩ ᏅᏇᏲᏅᎾ ᏱᎩ ᎠᎩᏬᏂᎯᏍᏗᏱ, ᎠᏎᏃ ᎥᏝ ᎾᏍᎩ ᏱᏄᏍᏗ ᏥᎦᏔᎾᎥᎢ; ᏂᎦᎥᏉᏍᎩᏂ ᏃᎦᏍᏛ ᎬᏂᎨᏒ ᏃᎦᎵᏍᏔᏅ ᎾᏂᎥ ᎠᏂᎦᏔᎲ ᏂᎯ ᎢᏤᎲᎢ.
Mwina ndikhoza kukhala wosaphunzitsidwa kayankhulidwe, koma ndili ndi chidziwitso. Izi tinakufotokozerani momveka bwinobwino.
7 ᏥᎪ ᏥᏍᎦᏅᎩ ᎡᎳᏗ ᏥᎾᏆᏓᏛᏁᎸ, ᏂᎯ ᎡᏥᏌᎳᏙᏗᏱ, ᎾᏍᎩ ᏂᏗᏨᎬᏩᎶᏓᏁᎸᎾ ᏥᎩ ᎣᏍᏛ ᎧᏃᎮᏛ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏤᎵᎦ ᎢᏨᏯᎵᏥᏙᏁᎸᎢ?
Kodi linali tchimo kwa ine kudzichepetsa nʼcholinga chakuti ndikukwezeni pamene ndinkalalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu kwa inu mwaulere?
8 ᏕᎦᏥᎾᏌᏅ ᏅᏩᎾᏓᎴ ᏧᎾᏁᎶᏗ ᏚᎾᏓᏡᏩᏗᏒᎢ, ᏥᎩᏍᎬᎩ ᎬᏆᎫᏴᎡᎲᎢ, ᏂᎯ ᎪᎱᏍᏗ ᎢᏨᏯᏛᏁᏗᏱ.
Ndinkalanda mipingo ina pomalandira thandizo kwa iwo kuti ndikutumikireni.
9 ᎠᎴ ᎾᎯᏳ ᏥᏨᏰᎳᏗᏙᎲᎩ ᎠᎴ ᎠᏆᏚᎸᎲᎥᎦ, ᎥᏝ ᎩᎶ ᏯᏆᎫᏱᏍᎨᎢ; ᎾᏍᎩᏰᏃ ᎠᎩᏂᎬᏎᎲᎢ, ᎣᏣᎵᏅᏟ ᎹᏏᏙᏂ ᏅᏓᏳᏂᎶᏒᎯ ᎬᎩᏁᎲᎩ; ᎠᎴ ᏂᎦᎥᏉ ᎠᏆᏟᏂᎬᏁᎸ ᎢᏨᏐᏈᎸᏗᏱ ᏂᎨᏒᎾ, ᎠᎴ ᎠᏏᏉ ᎾᏍᎩ ᏂᎦᏛᏁᎮᏍᏗ.
Ndipo pamene ndinali pakati panu, nditasowa kanthu, sindinalemetse munthu aliyense, pakuti abale ena amene anachokera ku Makedoniya anandipatsa zonse zimene ndinkazisowa. Ndayesetsa kuti ndisakhale cholemetsa kwa inu mʼnjira ina iliyonse, ndipo ndidzapitiriza kutero.
10 ᎾᏍᎩᏯ ᎦᎶᏁᏛ ᎤᏤᎵ ᎦᏰᎪᎩ ᏂᎨᏒᎾ ᎨᏒ ᏣᎩᏯᎠ, ᎥᏝ ᎥᎩᏲᎯᏍᏓᏁᏗ ᏱᎨᏎᏍᏗ ᎯᎠ ᎾᏍᎩ ᎦᏢᏈᏍᎬ ᎡᎧᏯ ᏂᎬᎾᏛᎢ.
Kunena moona mtima molingana ndi chilungamo cha Khristu chimene chili mwa ine, palibe amene angandiletse kudzitamandira mʼzigawo za ku Akaya.
11 ᎦᏙᏃ? ᏥᎪ ᏂᏨᎨᏳᏒᎾ ᎨᏒ ᎢᏳᏍᏗ? ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎠᎦᏔᎭ.
Nʼchifukwa chiyani ndikutero? Kodi nʼchifukwa choti sindikukondani? Mulungu akudziwa kuti ndimakukondani!
12 ᎠᏎᏃ ᏂᎦᏛᏁᎲ ᎾᏍᎩ ᏂᎦᎦᏛᏁᎮᏍᏗ, ᎾᏍᎩ ᎦᏥᏲᏍᏙᏓᏁᏗᏱ ᎤᎾᏜᏓᏅᏓᏕᏗᏱ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᏧᎾᏚᎵᎭ ᎤᎾᏜᏓᏅᏓᏕᏗᏱ; ᎾᏍᎩ ᎾᎿᎭᎠᎾᏢᏈᏍᎬ ᎾᏍᎩ ᎠᏴ ᏃᎦᏍᏛ ᎾᏍᎩᏯ ᏄᎾᏍᏛ ᎬᏂᎨᏒ ᏱᏂᎦᎵᏍᏓ.
Ndipo ndipitiriza kuchita zomwe ndikuchitazi nʼcholinga chakuti ndisapereke mpata kwa amene akufuna kupezera mwayi woti afanane nafe pa zinthu zimene iwowo amadzitamandira.
13 ᎯᎠᏰᏃ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᎤᎾᏠᎾᏍᎩ ᎨᏥᏅᏏᏛ, ᎤᎾᏓᎵᏓᏍᏗ ᏧᏂᎸᏫᏍᏓᏁᎯ, ᎦᎶᏁᏛ ᏧᏤᎵ ᎨᏥᏅᏏᏛ ᎠᎾᏤᎸᏍᎩ.
Pakuti anthu oterewa ndi atumwi onama, antchito achinyengo, odzizimbayitsa ngati atumwi a Khristu.
14 ᎥᏝ ᎠᎴ ᏳᏍᏆᏂᎪᏗ; ᏎᏓᏂᏰᏃ ᎤᏩᏒ ᏗᎧᎿᎭᏩᏗᏙᎯ ᎢᎦ-ᎦᏛ ᎡᎯ ᎠᏤᎸᏍᎪᎢ.
Sizododometsa zimenezi, pakuti Satana mwini amadzizimbayitsa kuoneka ngati mngelo wowunikira anthu.
15 ᎾᏍᎩ ᎢᏳᏍᏗ ᎥᏝ ᎤᏣᏘ ᎤᏍᏆᏂᎪᏗᏳ ᏱᎩ ᎾᏍᏉ ᎾᏍᎩ ᏧᏅᏏᏓᏍᏗ ᏚᏳᎪᏛ ᎨᏒ ᎨᏥᏅᏏᏓᏍᏗ ᏯᎾᏤᎸᏍᎦ; ᎾᏍᎩ ᎤᎵᏍᏆᎸᏗ ᎢᏳᎾᎵᏍᏓᏁᏗ ᎨᏒ ᎾᏍᎩᏯ ᏚᏂᎸᏫᏍᏓᏁᎸ ᎨᏎᏍᏗ.
Nʼzosadabwitsa tsono ngati atumiki ake akudzizimbayitsa ngati otumikira chilungamo. Matsiriziro awo adzalandira zoyenerana ndi ntchito zawo.
16 ᏔᎵᏁ ᎯᎠ ᏂᏥᏪᎭ, ᏞᏍᏗ ᎩᎶ ᎤᏁᎫ ᏯᏇᎵᏎᎮᏍᏗ; ᎢᏳ ᎠᏗᎾ ᎾᏍᎩ ᏄᏍᏕᏍᏗ, ᎠᏎ ᎠᎩᏁᎫ ᎾᏍᎩᏯ ᏗᏍᎩᏯᏓᏂᎸᎩ, ᎾᏍᎩ ᎠᏴ ᎤᏍᏗ ᎠᏆᏢᏈᏍᏗᏱ.
Ndibwereze kunena kuti, wina aliyense asandiyese chitsiru. Koma ngati mutero, mundilandire monga mmene mukhoza kulandirira chitsiru, kuti ndinyadirepo pangʼono.
17 ᎾᏍᎩ ᎯᎠ ᏂᏥᏪᏍᎬ ᏥᏁᎬ ᎥᏝ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎢᏳᏪᏍᏗ ᏱᏥᏁᎦ, ᎠᎩᏁᎫᏍᎩᏂ ᎾᏍᎩᏯ ᏥᏁᎦ, ᎯᎠ ᎾᏍᎩ ᏂᏥᎾᏰᏍᎬᎾ ᎨᏒ ᏥᎬᏗᎭ ᏥᎦᏢᏆᏍᎦ.
Kudzinyadira kwangaku, sindikuyankhula monga mmene Ambuye akufunira koma ngati chitsiru.
18 ᎾᏍᎩᏃ ᏧᏂᏣᏔ ᏣᎾᏢᏈᏍᎦ ᎤᏇᏓᎵ ᎬᏙᏗ ᎨᏒᎢ, ᎠᏴ ᎾᏍᏉ ᏓᎦᏢᏆᏏ.
Popeza ambiri akudzitama monga dziko lapansi limachitira, inenso ndidzitamanso.
19 ᎤᏂᏁᎫᏰᏃ ᎤᎾᏁᎳᎩ ᏙᏤᎵᏎᎭ ᎣᏏᏳ ᎢᏥᏰᎸᎭ, ᏂᎯ ᎢᏥᎦᏔᎾᎢ ᎨᏒ ᎢᏳᏍᏗ.
Inu mumalolera kukhala ndi zitsiru mokondwera chifukwa mumati ndinu anzeru!
20 ᎤᏁᎳᎩᏰᏃ ᎢᏤᎵᏍᎪ ᎢᏳᏃ ᎩᎶ ᏱᏗᏥᎾᏢᏅ, ᎢᏳᏃ ᎩᎶ ᎠᏒᎭ ᏱᏂᏨᏁᎸ, ᎢᏳᏃ ᎩᎶ [ ᎪᎱᏍᏗ ᎢᏥᎲ ] ᏱᏥᎩᎡᎸ, ᎢᏳᏃ ᎩᎶ ᎤᏩᏒ ᏳᏓᎵᏌᎳᏓᏅ, ᎢᏳᏃ ᎩᎶ ᏕᏣᎧᏛ ᏱᏨᏂᎸ.
Kunena zoona mumangololera aliyense; amene amakusandutsani akapolo, kapena amene amakudyerani masuku pamutu, kapena amene amakupezererani, kapena amene amadzitukumula, kapena amene amakumenyani khofi.
21 ᎤᏕᎰᎯᏍᏗ ᎨᏒ ᎤᎬᏩᎵ ᏥᏁᎦ, ᎾᏍᎩ ᏦᏥᏩᎾᎦᎳ ᎪᎪᏎᎲᎢ. ᎾᎿᎭᏍᎩᏂᏃᏅ ᎩᎶ ᎬᏩᎾᏰᎯᏍᏗ ᏂᎨᏒᎾ ᎨᏒ ( ᎤᏁᎫ ᎤᏁᎢᏍᏗ ᏥᏁᎦ, ) ᎠᏴ ᎾᏍᏉ ᏂᏥᎾᏰᏍᎬᎾ.
Ndikuvomera mwamanyazi kuti ife sitinali olimba mtima kuti nʼkuchita zinthu zimenezi. Ndikuyankhula ngati chitsiru kuti chimene wina aliyense akhoza kudzitama nacho, Inenso ndikhoza kudzitama nachonso.
22 ᏥᎪ ᎢᎾᏈᎷ ᎾᏍᎩ? ᎠᏴ ᎾᏍᏉ. ᏥᎪ ᎠᏂᎢᏏᎵ? ᎠᏴ ᎾᏍᏉ. ᎡᏆᎭᎻᏍᎪ ᏧᏁᏢᏔᏅᏛ ᎾᏍᎩ? ᎠᏴ ᎾᏍᏉ.
Kodi iwo ndi Ahebri? Inenso ndine Mhebri. Kodi iwo ndi Aisraeli? Inenso ndine Mwisraeli. Kodi iwo ndi zidzukulu za Abrahamu? Inenso ndine mdzukulu wa Abrahamu.
23 ᏥᎪ ᎦᎶᏁᏛ ᏧᏅᏏᏓᏍᏗ ᎾᏍᎩ? ( ᎤᏁᎫ ᎤᏁᎢᏍᏗ ᏥᏁᎦ, ) ᎠᏴ ᎤᏟᎢ; ᏓᎩᎸᏫᏍᏓᏁᎲ ᎤᏟ ᎢᎦᎢ; ᎥᎩᎵᎥᏂᎸ ᎤᏟᎯᏳ ᎢᎦᎢ; ᏗᎦᏍᏚᏗᏱ ᎥᎩᏴᏔᏅᎢ ᎤᏟ ᎢᎦᎢ; ᎠᎩᏲᎱᏏᏕᎾ ᎨᏒ ᏯᏃᏉ;
Kodi iwo ndi atumiki a Khristu? Ndikuyankhula ngati wamisala. Ine ndine woposa iwowo. Ndagwira ntchito kwambiri kupambana iwo, ndakhala ndikuyikidwa mʼndende kawirikawiri, ndakwapulidwapo kwambiri, kawirikawiri ndinali pafupi kufa.
24 ᎠᏂᏧᏏ ᎯᏍᎩ ᏂᎬᎩᎵᎥᏂᎸᎩ ᎢᏳᏍᏗᎭ ᏌᏉ ᎦᎷᎶᎩ ᏅᎦᏍᎪᎯ ᎢᎬᏋᏂᏍᏗᏱ;
Andikwapulapo kasanu zikoti zija za Ayuda, makumi anayi kuchotsapo chimodzi.
25 ᏦᎢ ᎢᏳᏩᎫᏗ ᎦᎾᏍᏓ ᏕᎬᎩᎵᎥᏂᏍᏔᏅᎩ; ᏌᏉ ᏅᏯ ᏂᏕᎬᏋᏂᏍᏔᏅᎩ; ᏦᎢ ᎢᏳᏩᎫᏗ ᏥᏳ ᎠᏆᏦᏛ ᎤᏲᏨᎩ; ᎤᎵᏨᏓᏆᏛ ᎠᎴ ᎤᏙᏓᏆᏛ ᎠᏍᏛᎬ ᎾᏆᏛᏅᎩ;
Katatu anandimenya ndi ndodo. Kamodzi anandigendapo miyala. Katatu sitima yathu ya panyanja inasweka, ndipo ndinakhala usiku ndi usana ndi kuyandama pa nyanja.
26 ᎨᏙᎲ ᏯᏃᏉ; ᎡᏉᏂ ᏕᎨᏴ ᎤᎾᏰᎯᏍᏗᏳ ᎨᏒᎢ; ᏗᎾᏓᎾᏌᎲᏍᎩ ᎤᏂᎾᏰᎯᏍᏗᏳ ᎨᏒᎢ; ᏗᏆᏤᎵ ᏴᏫ ᎤᏂᎾᏰᎯᏍᏗᏳ ᎨᏒᎢ; ᏧᎾᏓᎴᏅᏛ ᏴᏫ ᎤᏂᎾᏰᎯᏍᏗᏳ ᎨᏒᎢ; ᎦᏚᎲ ᎤᎾᏰᎯᏍᏗᏳ ᎨᏒᎢ; ᎢᎾᎨ ᎨᏒ ᎤᎾᏰᎯᏍᏗᏳ ᎨᏒᎢ; ᎠᎺᏉᎯ ᎤᎾᏰᎯᏍᏗᏳ ᎨᏒᎢ; ᎤᎾᏠᎾᏍᏗ ᎣᏣᎵᏅᏟ ᎤᏂᎾᏰᎯᏍᏗᏳ ᎨᏒᎢ;
Ndakhala ndikuyenda maulendo ataliatali. Moyo wanga wakhala ukukumana ndi zoopsa pa mitsinje, zoopsa za achifwamba, zoopsa zochokera kwa abale anga Ayuda, zoopsa zochokera kwa anthu akunja. Ndinakumana ndi zoopsa mʼmizinda, mʼmidzi, pa nyanja, ndi pakati pa abale onyenga.
27 ᏓᎩᏯᏪᏥᏙᎸ ᎠᎴ ᎡᎯᏍᏗ ᎾᏆᎵᏍᏓᏁᎸᎢ; ᏯᏃᎩᏳ ᏂᏥᎸᏍᎬᎾ ᎨᏒᎢ; ᎠᎪᏄ ᎠᎩᏲᏏᏍᎬᎢ ᎠᎴ ᎠᎩᏔᏕᎩᏍᎬᎢ; ᏯᏃᎩᏳ ᎠᎹᏟ ᎬᏍᎬᎢ; ᎤᏴᏢ ᎠᎴ ᎠᎩᏰᎸᎭ ᎨᏒᎢ.
Ndakhala ndikugwira ntchito molimbika ndipo kawirikawiri ndakhala ndikuchezera usiku wonse osagona. Ndakhala ndikumva njala ndi ludzu ndipo kawirikawiri ndakhala wopanda chakudya. Ndakhala ndi kuzizidwa ndi wosowa zovala.
28 ᏂᏓᏠᏯᏍᏛᎾ ᏧᏓᎴᏅᏛ, ᎾᏍᎩ ᏂᏚᎩᏨᏂᏒ ᏣᎩᎷᏤᎭ, ᎾᏍᎩ Ꮎ ᏗᏆᎦᏌᏯᏍᏙᏗᏱ ᏂᎦᏛ ᏧᎾᏁᎶᏗ ᏚᎾᏓᏡᏩᏗᏒᎢ.
Kuwonjezera pa zonsezi, tsiku ndi tsiku ndimakhala pa chipsinjo cha nkhawa ya mipingo yonse.
29 ᎦᎪ ᎠᏩᎾᎦᎶᎢ, ᎠᏴᏃ ᏂᏥᏩᏂᎦᎸᎾ ᎨᏐᎢ? ᎦᎪ ᏚᏬᏕᎯᎰᎢ, ᎠᏴᏃ ᏂᏥᎴᏴᏍᎬᎾ ᎨᏐᎢ?
Ndani ali wofowoka, ine wosakhala naye mʼkufowoka kwakeko? Ndani amene mnzake amuchimwitsa, ine wosavutika mu mtima?
30 ᎢᏳᏃ ᎠᏎ ᎠᏆᏢᏈᏍᏗ ᎨᏎᏍᏗ, ᏥᏩᎾᎦᎵᏳ ᎨᏒ ᎤᎬᏩᎵ ᏓᎦᏢᏆᏏ.
Ngati nʼkoyenera kudzitamandira, ndidzadzitamandira pa zinthu zimene zimaonetsa kufowoka kwanga.
31 ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎢᎦᏤᎵ ᏥᏌ ᎦᎶᏁᏛ ᎤᏤᎵ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎠᎴ ᎤᏙᏓ, ᎾᏍᎩ ᏂᎪᎯᎸ ᎦᎸᏉᏙᏗ ᏥᎩ, ᎠᎦᏔᎭ ᏂᎦᏥᎪᎥᏍᎬᎾ ᎨᏒᎢ. (aiōn g165)
Mulungu, Atate a Ambuye Yesu, amene tiyenera kumutamanda nthawi zonse, akudziwa kuti sindikunama. (aiōn g165)
32 ᏕᎹᏍᎦ ᏫᎨᏙᎲ ᏄᎬᏫᏳᏎᏕᎩ ᎡᎵᏓ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎤᏪᎧᏅᎯ, ᎠᏯᏫᏍᎬᎩ ᎠᏂᏕᎹᏍᎦ ᎤᏂᏚᎲᎢ ᎾᏍᎩ ᎤᏚᎵᏍᎬ ᎠᎩᏂᏴᏗᏱ;
Ku Damasiko, bwanamkubwa woyimira Mfumu Areta, anayika alonda kuzungulira mzinda wonse kuti andigwire.
33 ᎠᏦᎳᏅᏃ ᏓᎬᎩᏄᎪᏫᏒᎩ ᏔᎷᏣᎩᎯ ᎬᏆᏦᏗ ᎬᏆᏠᎥᏔᏅᎩ ᎠᏐᏳᎶᏗ, ᎠᎴ ᏥᏯᏗᏫᏎᎸᎩ.
Koma abale anandiyika mʼdengu nanditsitsira pa chipupa kudzera pa zenera la mpandawo, motero ndinapulumuka mʼmanja mwake.

< ᎪᎵᏂᏗᏱ ᎠᏁᎯ ᏔᎵᏁ ᎨᎪᏪᎳᏁᎸᎯ 11 >