< ᏉᎳ ᏕᏏᎶᏂᎦ ᎠᏁᎯ ᎢᎬᏱᏱ ᏧᏬᏪᎳᏁᎸᎯ 5 >

1 ᎾᎯᏳᏍᎩᏂ ᎨᏒᎢ ᎠᎴ ᎾᎯᏳ ᏕᎨᏌᏗᏒᎢ, ᎢᏓᎵᏅᏟ, ᎥᏝ ᎤᏚᎸᏗ ᏱᏂᏣᎵᏍᏓᏁᎭ ᎢᏨᏲᏪᎳᏁᏗᏱ.
Tsono abale, za nthawi ndi nyengo yake nʼkosafunikira kuti tikulembereni,
2 ᎢᏨᏒᏰᏃ ᎣᏏᏳ ᎢᏥᎦᏔ ᎾᏍᎩ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎤᏤᎵ ᎢᎦ ᎤᎵᏰᎢᎶᎯᏍᏗ ᎨᏒ ᎾᏍᎩᏯ ᎦᏃᏍᎩᏍᎩ ᏒᏃᏱ ᏥᎦᎷᎪᎢ.
chifukwa mukudziwa bwino lomwe kuti tsiku la Ambuye lidzafika ngati mbala usiku.
3 ᎾᎯᏳᏰᏃ ᏅᏩᏙᎯᏯᏛ ᎠᎴ ᏄᎾᏰᎯᏍᏛᎾ ᎠᎾᏗᏍᎨᏍᏗ, ᎿᎭᏉ ᏄᏰᎶᎢᏍᏔᏅᏛ ᎠᏓᏛᏗᏍᎩ ᎤᏂᎷᏤᏗ ᎨᏎᏍᏗ, ᎾᏍᎩᏯ ᎠᎩᎵᏯ ᏧᎷᏤᎰ ᎠᎨᏴ ᎦᏁᎵᏛ; ᎠᎴ ᎥᏝ ᎤᎾᏗᏫᏎᏗ ᏱᎨᏎᏍᏗ.
Pamene anthu akunena kuti, “Mtendere ndi chitetezo,” chiwonongeko chidzafika pa iwo mwadzidzidzi, monga zowawa za amayi pobereka, ndipo sadzathawa.
4 ᏂᎯᏍᎩᏂ, ᎢᏓᎵᏅᏟ, ᎥᏝ ᎤᎵᏏᎬ ᏱᏤᎭ, ᎾᏍᎩ Ꮎ ᎾᎯᏳ ᎢᎦ ᎨᏣᏢᏔᏍᏗ ᎢᏳᎵᏍᏙᏗᏱ ᎾᏍᎩᏯ ᎦᏃᏍᎩᏍᎩ ᏧᏢᏔᏍᎪᎢ.
Koma inu abale, simuli mu mdima kuti tsiku limeneli lidzakudzidzimutseni ngati mbala.
5 ᏂᏥᎥᎢ ᎢᎦ-ᎦᏘ ᏧᏪᏥ, ᎠᎴ ᎢᎦ ᏧᏪᏥ; ᎥᏝ ᏒᏃᏱ ᎠᎴ ᎤᎵᏏᎬ ᎢᏕᎯ ᏱᎩ.
Nonse ndinu ana a kuwunika ndi ana a usana. Sindife anthu a usiku kapena mdima.
6 ᎾᏍᎩ ᎢᏳᏍᏗ ᏞᏍᏗ ᏱᏗᎵᎮᏍᏗ, ᎾᏍᎩᏯ ᎠᏂᏐᎢ ᎾᎾᏛᏁᎲᎢ; ᎢᏗᏯᏫᏍᎨᏍᏗᏍᎩᏂ ᎠᎴ ᏂᏗᎩᏴᏍᏕᏍᎬᎾ ᎨᏎᏍᏗ.
Chomwecho tsono, tisafanane ndi ena amene akugona koma tikhale maso ndi odzisunga.
7 ᎠᏂᎵᎯᏰᏃ, ᏒᏃᏱ ᏓᏂᎵᎰᎢ; ᎠᎴ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᏧᏂᏴᏍᏕᏍᎩ, ᏒᏃᏱ ᏚᏂᏴᏍᏕᏍᎪᎢ.
Pakuti amene akugona, amagona usiku, ndi amene amaledzera, amaledzera usiku.
8 ᎠᏴᏍᎩᏂ ᎢᎦ ᎢᏕᎯ ᏥᎩ ᏂᏗᎩᏴᏍᏕᏍᎬᎾ ᎨᏎᏍᏗ, ᎠᏓᏁᏣᏍᏚᎶ ᎪᎯᏳᏗ ᎨᏒ ᎠᎴ ᎠᏓᎨᏳᏗ ᎨᏒ ᎢᏓᏓᏁᏥᏍᏚᎶᏗᏍᎨᏍᏗ, ᎡᎩᏍᏕᎸᏗᏱᏃ ᎨᏒ ᎤᏚᎩ ᎢᎬᏒ ᎢᎦᎵᏍᏚᎶᏕᏍᏗ.
Koma popeza ndife a usana, tikhale odzisunga, titavala chikhulupiriro ndi chikondi ngati chovala pachifuwa, ndi chiyembekezo cha chipulumutso ngati chipewa.
9 ᎤᏁᎳᏅᎯᏰᏃ ᎥᏝ ᏱᎦᏑᏰᏒ ᎤᏔᎳᏬᎯᏍᏗ ᎨᏒ ᎢᎩᎷᏤᏗᏱ; ᎠᎵᏍᏕᎸᏙᏗᏍᎩᏂ ᎢᎩᏩᏛᏗᏱ ᎢᎦᏤᎵ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᏥᏌ ᎦᎶᏁᏛ ᎢᏳᏩᏂᏌᏛ;
Pakuti Mulungu sanatisankhe kuti tikavutike ndi mkwiyo koma kuti tilandire chipulumutso kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu.
10 ᎾᏍᎩ ᏥᎩᏲᎱᎯᏎᎴᎢ, ᎾᏍᎩ ᎾᏍᏉ ᏱᏗᎵᎭ ᎠᎴ ᏂᏗᎵᎲᎾ ᏱᎩ, ᎾᏍᎩ ᎢᏧᎳᎭ ᏫᎦᏕᏗᏱ ᎢᏳᎵᏍᏙᏗᏱ.
Iye anatifera ndi cholinga chakuti, kaya tili ndi moyo kapena tagona, tikhale naye pamodzi.
11 ᎾᏍᎩ ᎢᏳᏍᏗ, ᏕᏣᏓᎦᎵᏍᏓᏗᏍᎨᏍᏗ, ᎠᎴ ᏕᏣᏓᎵᏂᎪᎯᏍᏗᏍᎨᏍᏗ, ᎾᏍᎩᏯ ᏥᏂᏣᏛᏁᎭ.
Choncho limbikitsanani wina ndi mnzake ndi kuthandizana kukula mu mzimu, monga momwe mukuchitira.
12 ᎠᎴ ᎢᏨᏔᏲᏎᎭ, ᎢᏓᎵᏅᏟ, ᎾᏍᎩ ᏗᏥᎦᏔᎯ ᎢᏳᎵᏍᏙᏗᏱ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᏧᏂᎸᏫᏍᏓᏁᎯ ᎢᏤᎲᎢ, ᎠᎴ ᏗᎨᏣᏁᎶᏗ ᏥᎩ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᏕᏣᏁᎶᏛᎢ, ᎠᎴ ᏥᎨᏣᏅᏓᏗᏍᏗᎭ;
Tsopano tikukupemphani abale kuti muziwalemekeza amene akugwira ntchito pakati panu, amene amakuyangʼanirani mwa Ambuye ndi amene amakulimbikitsani.
13 ᎠᎴ ᎤᏣᏘ ᏗᏥᎸᏉᏗᏳ ᎢᏳᎵᏍᏙᏗᏱ ᎠᏓᎨᏳᏗ ᎬᏗ ᏅᏗᎦᎵᏍᏙᏗᏍᎨᏍᏗ ᏚᏂᎸᏫᏍᏓᏁᎲᎢ. ᎠᎴ ᏙᎯᏱ ᏂᏨᏁᏍᏗ ᎢᏨᏒ ᎢᏤᎲᎢ.
Muziwachitira ulemu kwambiri mwachikondi chifukwa cha ntchito yawo. Mukhale pa mtendere wina ndi mnzake.
14 ᎠᎴ ᎢᏨᏔᏲᏎᎭ, ᎢᏓᎵᏅᏟ, ᏕᏤᏯᏔᎲᏍᎨᏍᏗ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᏄᎾᏁᎸᎾ, ᏕᏥᎦᎵᏍᏓᏗᏍᎨᏍᏗ ᏗᏩᎾᎦᎳ ᏧᎾᏓᏅᏘ, ᏕᏥᏂᏴᏎᏍᏗ ᏗᏂᏩᎾᎦᎳᎢ, ᏗᏨᏂᏗᏳ ᎨᏎᏍᏗ ᎾᏂᎥ [ ᎤᏣᏘᏂ ᏂᎨᏣᏛᏁᎲᎢ.]
Ndipo tikukupemphani abale, muwachenjeze amene akungokhala osagwira ntchito, alimbikitseni amanyazi, thandizani ofowoka ndipo muzilezera mtima aliyense.
15 ᏞᏍᏗ ᎩᎶ ᎤᏲ ᎾᎬᏁᎸ ᏳᏞᎨᏍᏗ ᎤᏲ ᏱᎾᏓᏛᏁᎮᏍᏗ; ᎢᏥᏍᏓᏩᏕᎨᏍᏗᏍᎩᏂ ᏂᎪᎯᎸ ᎾᏍᎩ ᎣᏍᏛ ᎨᏒᎢ, ᎾᏍᏉ ᎢᏨᏒ ᎪᎱᏍᏗ ᏕᏣᏓᏛᏗᏍᎬ, ᎠᎴ ᎾᏂᎥᏉ.
Onetsetsani kuti wina asabwezere choyipa kwa omuchitira choyipa koma nthawi zonse yesetsani kukhala okoma mtima kwa wina ndi mnzake; ndiponso ndi kwa anthu ena onse.
16 ᎢᏣᎵᎮᎵᎨᏍᏗ ᏂᎪᎯᎸᎢ;
Kondwerani nthawi zonse.
17 ᏂᏥᏲᎯᏍᏗᏍᎬᎾ ᎢᏣᏓᏙᎵᏍᏗᏍᎨᏍᏗ;
Pempherani kosalekeza.
18 ᏂᎦᎥᏉ ᏂᏣᎵᏍᏓᏁᎵᏕᎬ ᎡᏣᎵᎡᎵᏤᎮᏍᏗ [ ᎤᏁᎳᏅᎯ; ] ᎯᎠᏰᏃ ᎾᏍᎩ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎢᏣᏓᏅᏖᎮᎲ ᏥᏌ ᎦᎶᏁᏛ ᏕᏣᏁᎶᏛ ᎢᏳᏍᏗ.
Yamikani mu zonse, pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu kwa inu mwa Khristu Yesu.
19 ᎠᏓᏅᏙ ᎠᏓᏪᎵᎩᏍᎬ ᏞᏍᏗ ᏴᏝᏗᏍᎨᏍᏗ.
Musazimitse moto wa Mzimu Woyera.
20 ᏞᏍᏗ ᎠᏎᏉ ᏱᏥᏰᎸᏍᎨᏍᏗ ᎠᏙᎴᎰᎯᏍᏗ ᎨᏒᎢ.
Musanyoze mawu a uneneri.
21 ᏄᏓᎴᏒ ᎪᎱᏍᏗ ᎢᏥᎪᎵᏰᏍᎨᏍᏗ; ᎠᏍᏓᏯ ᏕᏥᏂᏴᏎᏍᏗ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᎣᏍᏛ ᎨᏒᎢ.
Yesani zinthu zonse. Gwiritsitsani chimene ndi chabwino.
22 ᎢᏣᏓᏅᎡᎮᏍᏗ ᏂᎦᎥ ᏄᏓᎴᏒ ᎤᏲᎢ.
Mupewe choyipa cha mtundu wina uliwonse.
23 ᎤᏁᎳᏅᎯᏃ ᎤᏩᏒ ᏅᏩᏙᎯᏯᏛ ᎠᏓᏁᎯ ᏂᎦᎷᎶᎬᎾ ᎢᏥᏅᎦᎸᏗ ᎨᏎᏍᏗ; ᎠᎴ ᏂᎬ ᎢᏣᏓᏅᏖᏗᏱ ᎠᎴ ᏗᏣᏓᏅᏙ ᎠᎴ ᏗᏥᏰᎸᎢ ᏤᏥᏍᏆᏂᎪᏓᏁᏗ ᎨᏎᏍᏗ, ᏂᏚᏚᎯᏍᏛᎾ ᎢᏣᎵᏍᏙᏗᏱ ᎢᎦᏤᎵ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᏥᏌ ᎦᎶᏁᏛ ᎦᎷᏨ ᎢᏳᎢ.
Mulungu mwini, Mulungu wamtendere, akuyeretseni kotheratu. Mzimu wanu wonse, moyo ndi thupi zisungidwe zopanda cholakwa mpaka kubwera kwa Ambuye athu Yesu Khristu.
24 ᏄᏓᎵᏓᏍᏛᎾ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᎢᏣᏯᏅᏛ, ᎾᏍᏉ ᎾᏍᎩ ᎠᏎ ᏥᏅᏛᏛᏁᎵ.
Amene anakuyitanani ndi wokhulupirika ndipo Iye adzachita zimenezi.
25 ᎢᏓᎵᏅᏟ ᏍᎩᏯᏅᏓᏗᏍᎨᏍᏗ ᎢᏣᏓᏙᎵᏍᏗᏍᎬᎢ.
Abale, mutipempherere.
26 ᏂᎦᏛ ᎠᎾᎵᏅᏟ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᏗᏓᏙᏪᏙᎥᏍᏗ ᏕᏥᏲᎵᏍᏗᏍᎨᏍᏗ.
Perekani moni wachikondi kwa onse.
27 ᎢᏨᏁᏤᎭ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎢᏨᏁᎢᏍᏓᏁᎭ, ᎯᎠ ᎾᏍᎩ ᎪᏪᎵ ᎨᏥᎪᎵᏰᏗᏱ ᎾᏂᎥ ᎤᎾᏓᏅᏘ ᎠᎾᎵᏅᏟ.
Pamaso pa Ambuye ndikulamula kuti kalatayi iwerengedwe kwa abale onse.
28 ᎢᎦᏤᎵ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᏥᏌ ᎦᎶᏁᏛ ᎬᏩᎦᏘᏯ ᎤᏓᏙᎵᏍᏗ ᎨᏒ ᏕᏥᎧᎿᎭᏩᏗᏙᎮᏍᏗ. ᎡᎺᏅ.
Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale nanu.

< ᏉᎳ ᏕᏏᎶᏂᎦ ᎠᏁᎯ ᎢᎬᏱᏱ ᏧᏬᏪᎳᏁᎸᎯ 5 >