< San Marcos 8 >

1 AYO sija na jaane, anae guaja talo un dangculon linajyan taotao ya taya jafa nañija, si Jesus jaagang y disipuluña sija, ya ilegña nu sija:
Mʼmasiku amenewo gulu lina lalikulu la anthu linasonkhana. Popeza iwo analibe chakudya, Yesu anayitana ophunzira ake nati kwa iwo,
2 Maase yo ni linajyan taotao sa esta tres jaane na manjame; ya taya jafa nañija.
“Ndili ndi chifundo ndi anthu awa; akhala ali ndi Ine masiku atatuwa ndipo alibe chakudya.
3 Yaguin junafanjanao sin mañocho para iyasija, ufanlalango gui chalan; sa palo guiya sija manmato guine y chago.
Ngati nditawawuza kuti apite kwawo ali ndi njala, iwo adzakomoka mʼnjira chifukwa ena a iwo achokera kutali.”
4 Ya y disipuluña sija, maope güe: Guine mano nae siña manafanjaspog este taotao sija pan, güine gui desierto?
Ophunzira ake anayankha nati, “Kodi ndi kuti kuthengo kuno kumene munthu angapeze buledi okwanira kuwadyetsa?”
5 Guiya jafaesen sija: Cuanto na pan guaja jamyo? Ylegñija, siete.
Yesu anafunsa kuti, “Muli ndi malofu a buledi angati?” Iwo anayankha kuti, “Asanu ndi awiri.”
6 Ayo nae jatago y linajyan taotao na ufanason gui jilo oda; ya jachule y siete na pan, ya janae Yuus maase ya jaipe, ya janae y disipuluña sija para ujaplanta gui menanñija; ya sija japlanta gui menan y linajyan taotao.
Iye anawuza gulu la anthu kuti likhale pansi. Atatenga malofu a buledi asanu ndi awiri, anayamika, nawanyema ndipo anapatsa ophunzira ake kuti agawire anthu, ndipo iwo anatero.
7 Yan guaja locue palo mandiquique na güijan sija; ya anae jabendise, jatago na ujaplanta locue gui menanñija.
Analinso ndi tinsomba tochepa; Iye anayamikanso chifukwa cha nsombazo. Ndipo anawuza ophunzira kuti awagawire.
8 Pues mañocho, ya manjaspog; ya majatsa y pidaso sija ni sebbla, siete canastra.
Anthu anadya ndipo anakhuta. Atamaliza, ophunzira anatola buledi ndi nsomba zotsalira ndi kudzaza madengu asanu ndi awiri.
9 Ya y mañocho sija, buente cuatro mit; ya jadespide.
Panali amuna pafupifupi 4,000. Ndipo atawawuza kuti apite kwawo,
10 Ya enseguidas jumalom gui batco yan y disipuluña sija, ya manmato gui oriyan Dalmanuta.
analowa mʼbwato pamodzi ndi ophunzira ake napita ku dera la Dalamanuta.
11 Ya manmato y Fariseo sija, ya matutujon manafaesen yan güiya, manmanaliligao guiya güiya un señat guine y langet, matietienta güe.
Afarisi anabwera nayamba kumufunsa Yesu. Pomuyesa Iye, anamufunsa za chizindikiro chochokera kumwamba.
12 Ya sumospiros gostadong gui espirituña, ya ilegña: Jafa na mangagagao señat este na generasion? Magajet jusangane jamyo, na ti umanae señat este na generasion.
Ndipo anatsitsa moyo nati, “Nʼchifukwa chiyani mʼbado uno ukufuna chizindikiro chodabwitsa? Zoonadi, ndikuwuzani kuti palibe chizindikiro chidzapatsidwa kwa iwo.”
13 Ya jadingo sija, ya jumalom talo gui batco, ya mapos para y otro banda.
Ndipo anawasiya, nalowanso mʼbwato ndi kuwolokera tsidya lina.
14 Ya manmalefa ti manmañule pan, ya taya na unoja na pan gui batco.
Ophunzira anayiwala kutenga buledi, kupatula buledi mmodzi yekha amene anali naye mʼbwato.
15 Ya jaencatga sija, ilegña: Atan, adaje jamyo ni lebaduran y Fariseo sija, yan y lebaduran Herodes.
Yesu anawachenjeza kuti, “Samalani ndipo onetsetsani yisiti wa Afarisi ndi wa Herode.”
16 Ya manafaesen gui entalo sija, ilegña: Pot y taya panta.
Iwo anakambirana wina ndi mnzake ndipo anati, “Ndi chifukwa choti tilibe buledi.”
17 Ya anae jatungo si Jesus ilegña nu sija: Jafa manafaesen gui entalomiyo pot y taya panmiyo? Ti injaso ni ti intingo? Majejetogja trabia y corasonmiyo?
Yesu atadziwa zokambirana zawo anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukukambirana kuti mulibe buledi? Kodi inu simukuonabe kapena kuzindikira? Kodi mitima yanu ndi yowumitsidwa?
18 Guaja atadogmiyo, lao ti manmanlilie jamyo? Guaja talanganmiyo, ya ti manmanjujungogja jamyo? Ya ti injajasoja?
Kodi muli ndi maso ndipo simukuona, ndi makutu ndipo mukulephera kumva? Kodi simukukumbukira?
19 Anae juipe y sinco na pan sija entalo y sinco mit, cuanto na canastra injatsa bula ni pidaso sija ni sebbla? Ylegñija: Dose.
Pamene ndinagawa malofu asanu a buledi kwa anthu 5,000, ndi madengu angati amene munatoleramo buledi ndi nsomba zotsalira?” Iwo anayankha kuti, “Khumi ndi awiri.”
20 Ya anae y siete na pan sija entalo y cuatro mit, cuanto na canastra injatsa bula ni pidaso sija ni sebbla? Ylegñija: Siete.
“Ndipo pamene ndinagawa malofu asanu ndi awiri a buledi, kwa anthu 4,000, ndi madengu angati amene munatoleramo buledi ndi nsomba zotsalira?” Iwo anayankha kuti, “Asanu ndi awiri.”
21 Güiya ilegña nu sija: Ti intingo asta pago?
Iye anawafunsa kuti, “Kodi simumvetsetsabe?”
22 Ya mato guiya Betsaida; ya maconie güe guato un bachet, ya matayuyut güe na upacha güe.
Iwo anafika ku Betisaida, ndipo anthu ena anabweretsa munthu wosaona ndipo anamupempha Yesu kuti amukhudze.
23 Ayo nae jamantiene y canae y bachet, ya jacone asta y jiyong y siuda; ya anae jatolae y atadogña, japolo y canaeña gui jiloña, ya jafaesen: Unlie jafa?
Iye anagwira dzanja la munthu wosaonayo napita naye kunja kwa mudzi. Atalavulira mʼmaso a munthuyo ndi kumusanjika manja, Yesu anafunsa kuti, “Kodi ukuona kalikonse?”
24 Ya güiya manatan ya, ilegña: Julie taotao sija; lao julie sija calang trongconjayo na manmamómocat.
Iye anakweza maso nati, “Ndikuona anthu; akuoneka ngati mitengo imene ikuyendayenda.”
25 Entonses japolo ya canaeña talo gui atadogña ya jaguefatan; ya jomlo, ya manlie claro todo.
Kenakanso Yesu anayika manja ake mʼmaso a munthuyo. Ndipo maso ake anatsekuka, naonanso, ndipo anaona zonse bwinobwino.
26 Ya jatago para iyasija, ilegña: Chamo jumajalom gui sengsong (ni usangane jaye gui siuda).
Yesu anamuwuza kuti apite kwawo nati, “Usapite mʼmudzimo.”
27 Ya mapos si Jesus yan y disipuluña sija gui sensong sija y Cesarean Felipe: ya y chalan jafaesen y disipuluña sija, ilegña nu sija: Jaye ilegñija y taotao sija nu guajo?
Yesu ndi ophunzira ake anapita ku midzi yozungulira Kaisareya wa Filipo. Ali panjira, Iye anawafunsa kuti, “Kodi anthu amati ndine yani?”
28 Ya sija masangane güe, ilegñija: Si Juan Bautista; y palo ilegñija: Si Elias; y palo ilegñija: Uno gui profeta sija.
Iwo anayankha kuti, “Ena amati Yohane Mʼbatizi; ena amati Eliya; ndipo enanso amati ndinu mmodzi wa aneneri.”
29 Ayo nae jafaesen sija: Ya jamyo, jaye ilegmiyo nu guajo? Inepe as Pedro ilegña: Jago si Cristo jao.
Iye anafunsa kuti, “Koma nanga inu, mumati ndine yani?” Petro anayankha kuti, “Inu ndinu Khristu.”
30 Ya jaencatga sija na chañija sumangangane ni jaye pot güiya.
Yesu anawachenjeza kuti asawuze wina aliyense za Iye.
31 Ya jatutujon fumanagüe sija na y Lajin taotao janesesita upadese megae, ya umarechasa ni manamco sija, yan y prinsipen y mamale sija, yan y escriba sija, ya umapuno; ya ucajulo talo gui mina tres na jaane.
Iye anayamba kuwaphunzitsa kuti, “Mwana wa Munthu ayenera kumva zowawa zambiri ndi kukanidwa ndi akulu a ansembe, ndi aphunzitsi a malamulo, ndi kuti ayenera kuphedwa ndipo patatha masiku atatu adzaukanso.”
32 Ya claroja nae jasangan este na sinangan. Ayo nae si Pedro quinene güe, ya tinitujon güe rineprende.
Izi anaziyankhula momveka bwino, ndipo Petro anamutengera pambali ndipo anayamba kumudzudzula.
33 Lao anae jabira güe, ya jaatan y disipuluña sija, jalalatde si Pedro ilegña: Suja guiya guajo, Satanas; sa ti unadadaje y güinaja sija ni para si Yuus, na y güinajan taotao sija.
Koma Yesu atatembenuka ndi kuyangʼana ophunzira ake, anamudzudzula Petro nati, “Choka pamaso panga Satana! Suganizira zinthu za Mulungu koma za anthu.”
34 Ya jaagang y linajyan taotao yan y disipuluña sija, ya ilegña nu sija; Jaye y malago tumatiye yo, upune maesa güe, ya uchule y quiluusña ya udalalagyo.
Kenaka anayitana gulu la anthu pamodzi ndi ophunzira ake nati: “Ngati wina aliyense afuna kunditsata Ine, ayenera kudzikana yekha ndi kunyamula mtanda wake ndi kunditsata.
35 Sa y malago sumatba y linâlâña, ufinalingaeguan; lao y finalingaeguan ni linâlâña pot guajo, yan y ibangelio, este usatba y linâlâña.
Pakuti aliyense amene afuna kupulumutsa moyo wake adzawutaya, koma aliyense amene ataya moyo wake chifukwa cha Ine ndi cha Uthenga Wabwino, adzawupulumutsa.
36 Sa, jafa uaprobecha y taotao, yaguin jagana todo y tano, ya finalingaeguan ni linâlâña?
Kodi munthu adzapindulanji akalandira dziko lonse lapansi, koma ndi kutaya moyo wake?
37 Pat jafa na apas ufannae y taotao pot y linâlâña?
Kapena nʼchiyani chomwe munthu angapereke chosinthana ndi moyo wake?
38 Sa y mamajlao nu guajo yan y sinaganjo, gui sanmenan este y generasion ábale yan gaeisao, unimamajlaogüe locue ni Lajin taotao y tiempo nae mato gui minalag y Tataña, yan y mañantos na angjetña sija.
Ngati wina achita manyazi chifukwa cha Ine ndi mawu anga mu mʼbado uno wachigololo ndi wochimwa, Mwana wa Munthu adzachita naye manyazi pamene adzabwera mu ulemerero wa Atate ake pamodzi ndi angelo oyera.”

< San Marcos 8 >