< San Lucas 13 >

1 YA mangaegue güije na tiempo taotao sija, ni masangane güe pot y Galileo sija, ni si Pilatos janadaña y jâgâñija yan y inefresenñija.
Nthawi yomweyo panali ena amene analipo omwe amamuwuza Yesu za Agalileya amene magazi awo Pilato anawasakaniza ndi nsembe zawo.
2 Ya si Jesus manope ya ilegña nu sija: Jinasonmiyo na este sija na Galileo, mas manisao qui todo Galileo sija na japadese ayo sija?
Yesu anayankha kuti, “Kodi mukuganiza kuti Agalileya amenewa anali ochimwa kwambiri kuposa Agalileya ena onse chifukwa anavutika mʼnjira iyi?
3 Jusangane jamyo na aje; sa yanguin ti manmañotsot jamyo, manparejoja jamyo manáchamalingo.
Ine ndikuti, ayi! Koma ngati inu simutembenuka mtima, inunso mudzawonongeka nonse.
4 Pat ayo sija y diesiocho ni y podong y tore gui jiloñija guiya Siloe ya manpinino, jinasonmiyo na mas manisao ayo sija qui todo y taotao ni y mañasaga Jerusalem?
Kapena anthu 18 aja amene anafa nsanja ya Siloamu itawagwera, kodi mukuganiza kuti iwo aja anali ochimwa kwambiri kuposa onse amene amakhala mu Yerusalemu?
5 Jusangane jamyo na aje; sa yanguin ti manmañotsot jamyo, manparejoja jamyo manáchamalingo.
Ine ndikuti, ayi! Koma ngati inu simutembenuka mtima, inunso mudzawonongeka nonse.”
6 Ya jasangan este na acomparasion: Un taotao guaja y trongcon igos na matanme gui fangualuanña; ya anae mato para uegaga cao guaja tinegchaña, ti mañoda.
Kenaka Iye anawawuza fanizo kuti, “Munthu wina anali ndi mtengo wamkuyu, umene anadzala mʼmunda wamphesa, ndipo Iye anapita kukayangʼana zipatso, koma sanazipeze.
7 Ya ilegña ni y lancheruña: Esta guaja tres años ni matoyo güine na trongcon igos, manegagayo tinegcha, ya taya nae mañodayo; utut papa; para jafa na jaocucupa y tano?
Tsono kwa munthu amene amasamalira munda wamphesawo anati, ‘Kwa zaka zitatu tsopano ndakhala ndikubwera kudzafuna chipatso pa mtengo uwu ndipo sindinachipeze. Udule! Nʼchifukwa chiyani ukuwononga nthaka?’
8 Ya manope ilelegña nu güiya: Señot, polo pago na año ya juguadog y oriyaña, ya junaye estietcot:
“Munthuyo anayankha kuti, ‘Bwana, tawusiyani kwa chaka chimodzi chokha ndipo ine ndikumba ngalande mozungulira ndi kuthira manyowa.
9 Ya yanguin ufanogcha, mauleg; yanguin aje, siempre, unutut.
Ngati udzabale zipatso chaka chamawa, zili bwino! Koma ngati sudzabala, pamenepo mudzawudule.’”
10 Ya estaba na mamananagüe gui un sinagoga, gui sabado na jaane.
Pa Sabata Yesu ankaphunzitsa mʼsunagoge ina,
11 Ya estagüe un palaoan, na guaja un espiritun malango guiya güiya esta diesiocho años, ya esta ninaojlo, ya tisiña tumacho.
ndipo momwemo munali mayi amene anali ndi mzimu woyipa umene unamudwalitsa zaka 18. Iye anali wokhota msana ndipo samatha kuweramuka ndi pangʼono pomwe.
12 Ya anae linie as Jesus, inagang ya ilegña nu güiya: Palaoan, libre jao gui malangumo.
Yesu atamuona anamuyitana kutsogolo ndipo anati kwa iye, “Amayi, mwamasulidwa ku mavuto.”
13 Ya japolo y canaeña gui jiloña; ya enseguidas ninatunas, ya jaalaba si Yuus.
Kenaka anasanjika manja ake pa iye, ndipo nthawi yomweyo anawongoka nayamika Mulungu.
14 Lao y magas sinagoga lalalo sa si Jesus, numanajomlo gui sabado na jaane, ya manope ilegña nu y linajyan taotao sija: Guaja saes na jaane para ufanmachocho y taotao sija: ya este nae mauleg mato para numajomlo; lao ti y sabado na jaane.
Chifukwa cha kuyipidwa kuti Yesu anachiritsa pa Sabata, wolamulira sunagoge anati kwa anthu, “Pali masiku asanu ndi limodzi ogwira ntchito. Choncho bwerani kuti mudzachiritsidwe masiku amenewo osati pa Sabata.”
15 Ayonae inepe ni y Señot, ya ilegña: Hipocrita jamyo, ada ti siña cada uno guiya jamyo upula y gaña guaca, pat asno gui pesebre, ya ucone ya unaguimen gui sabado na jaane?
Ambuye anamuyankha kuti, “Iwe wachiphamaso! Kodi nonsenu simumasula pa Sabata ngʼombe zanu kapena bulu kumuchotsa mʼkhola ndi kupita naye kukamupatsa madzi?
16 Ya ti siña este na palaoan, ni y jagan Abraham, ni guinede as Satanas diesiocho años, manalibre gui magodeña, gui sabado na jaane?
Nanga mayiyu, amene ndi mwana wa Abrahamu, ndipo anamangidwa ndi Satana zaka 18, kodi siwoyenera kuti amasulidwe msinga imeneyi pa tsiku la Sabata?”
17 Ya anae jasangan estesija, todo y enemiguña ninafan mamajlao; ya todo y taotao sija ninafanmagof, pot todo y sennamagof na güinaja ni y machogüe pot güiya.
Atanena izi, onse omutsutsa anachititsidwa manyazi, koma anthu anakondwera ndi zodabwitsa zonse zimene Iye anazichita.
18 Pot enao ilegña: Jafa parejuña y raenon Yuus? yan jafa nae juacompara?
Kenaka Yesu anafunsa kuti, “Kodi ufumu wa Mulungu uli ngati chiyani? Kodi Ine ndingawufanizire ndi chiyani?
19 Parejo yan y granon y semiyan mustasa, ni y jachule y taotao, ya jatanme gui jalom jardinña; ya docó, ya jumuyong trongcon jayo; ya esta y pajaro sija gui langet mañaga gui ramasña.
Uli ngati mbewu ya mpiru, imene munthu anatenga ndi kudzala mʼmunda mwake. Inakula, nʼkukhala mtengo, ndipo mbalame zamlengalenga zinakhala mʼnthambi zake.”
20 Ya ilegña talo: Jafa nae juacompara y raenon Yuus.
Iye anafunsanso kuti, “Kodi ufumu wa Mulungu ndingawufanizire ndi chiyani?
21 Parejo yan y libadura, ni jachule un palaoan, ya janaatog gui tres medidan arina, asta qui todo manespongja.
Uli ngati yisiti amene mayi anatenga ndi kusakaniza ndi ufa wambiri mpaka anafufumitsa ufawo.”
22 Ya jumajanao gin chalaña, malag y siuda sija, yan y sengsong mamananagüe, ya jumajananao para Jerusalem.
Ndipo Yesu anayendayenda mʼmizinda ndi mʼmidzi, kumaphunzitsa pamene Iye ankapita ku Yerusalemu.
23 Ya ilegña uno nu güiya: Señot, didide manmasatba? si Jesus ilegña nu sija,
Wina anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi ndi anthu ochepa okha amene adzapulumutsidwe?” Iye anawawuza kuti,
24 Guefprocura mangejalom gui maiot na potta; sa jusangane jamyo na megae prumocucura mangejalom, lao ti mansiña.
“Yesetsani kulowa pa khomo lopapatiza, chifukwa ndikukuwuzani kuti ambiri adzafuna kulowa koma sadzatha kutero.
25 Yanguin y magas y guima jayasja cajulo ya jajuchom y petta, ya intitujon jamyo manmanojgue gui sumanjiyong ya inyajo y petta, ya ilegmi miyo: Señot, babayejam: ya ufanope ya ualog nu jamyo: Ti jutungo manguinemano jamyo:
Nthawi yomwe mwini nyumba adzayimirira ndi kutseka chitseko, inu mudzayima kunja kugogoda ndi kudandaula kuti, ‘Bwana, tatitsekulirani khomo.’ “Koma Iye adzayankha kuti, ‘Ine sindikukudziwani ndipo sindikudziwanso kumene mwachokera.’
26 Ya intitujon umalog: Guinin mañochojam yan manguimenjam gui menamo, yan mamanagüe jam gui cayenmame.
“Ndipo inu mudzati, tinkadya ndi kumwa ndi inu ndipo munkaphunzitsa mʼmisewu yathu.
27 Lao güiya ualog: Jusangane jamyo, na ti jutungo manguinemano jamyo: fañuja guiya guajo, todos jamyo ni y chumogüe y tinaelaye.
“Koma Iye adzayankha kuti, ‘Ine sindikukudziwani ndipo sindikudziwanso kumene mwachokera. Chokereni inu nonse ochita zoyipa!’
28 Ya ayonae uguaja cumasao, yan chegcheg nifen, yanguin inlie si Abraham, yan si Ysaac, yan si Jacob, yan todo y profeta sija, gui raenon Yuus; ya jamyo infanmachoneg juyong.
“Mudzalira ndi kukuta mano mukadzaona Abrahamu, Isake ndi Yakobo ndi aneneri onse ali mu ufumu wa Mulungu koma inuyo mutaponyedwa kunja.
29 Ya ufanmato manguinen y sancatan yan y sanlichan, yan y sanlago yan y sanjaya; ya ufanmatachong gui raenon Yuus.
Anthu adzachokera kummawa ndi kumadzulo, kumpoto ndi kummwera, kudzakhala pa phwando mu ufumu wa Mulungu.
30 Ya estagüe na guaja manuttimo ya ufanfinenana, y guaja manfinenana ya ufanuttimo.
Ndithudi otsirizira ndiye adzakhale oyambirira, ndipo oyambirira ndiye adzakhale otsirizira.”
31 Ya ayo na ora, manmato Fariseo sija ya ilegñija nu güiya: Janao ya unsuja güine; sa malago si Herodes na unpinino.
Pa nthawi imeneyo Afarisi anabwera kwa Yesu ndipo anati kwa Iye, “Chokani malo ano ndipo pitani kumalo ena aliwonse. Herode akufuna kukuphani.”
32 Ya ilegña nu sija: Janao, sangane ayo na sora, na estagüe, na juyute juyong y anite sija, yan manaamteyo pago na jaane yan agupa, ya y mina tres na jaane ufonjayanyo.
Iye anayankha kuti, “Pitani kawuzeni nkhandweyo, Ine ndikutulutsa ziwanda ndi kuchiritsa anthu lero ndi mawa ndipo tsiku lachitatu ndidzakwaniritsa cholinga changa.”
33 Lao nesesita jufamocat pago yan agupa yan y inagpaña, sa ti siña na ufalingo y profeta gui Jerusalem.
Mʼnjira ina iliyonse, Ine ndiyenera kupitirira ulendo wanga lero, mawa ndi mkuja. Zoona nʼzakuti mneneri sangafere kunja kwa Yerusalemu.
34 O Jerusalem! Jerusalem! ni y unpuno y profeta sija, yan unfagas ni acho ayo sija y manmatago para güiya! cuanto biaje malagoyo na junafandaña y famaguonmo, taegüije y ponidera janafandaña y poyitasña gui papa papaña, ya timalago jamyo!
Iwe Yerusalemu, Yerusalemu! Umapha aneneri ndi kuwagenda miyala anthu amene atumizidwa kwa iwe. Nthawi zambiri ndakhala ndikufuna kusonkhanitsa ana ako pamodzi, monga nkhuku imasonkhanitsira anapiye pansi pa mapiko ake, koma iwe sunafune!
35 Estagüe na manmapoluye jamyo ni y guimanmiyo taetaotao; ya jusangane jamyo: Ti inliiyo, asta qui mato ayo na tiempo anae inalog: Dichoso ayo y mamamaela ni y naan y Señot.
Taona, nyumba yako yasanduka bwinja. Ine ndikukuwuza kuti, sudzandionanso mpaka pamene udzati, “Wodala amene akubwera mʼdzina la Ambuye!”

< San Lucas 13 >