< Y Checho Y Apostoles Sija 21 >

1 YA anae susede na manadingojam, manmaudaejam gui batco, ya manmatojam gui tinas na chalan para Coos, ya y inagpaña na jaane manmatojam Rodas, ya desde ayo asta Pátara.
Titalawirana nawo, tinachoka kumeneko mʼsitima ya pamadzi, ndipo tinayenda molunjika mpaka kufika ku Kosi. Mmawa mwake tinapita ku Rode, kuchokera kumeneko tinapita ku Patara.
2 Ya inseda un batco na jumajanao para Finesia, ya manmaudaejam, ya manjanaojam.
Kumeneko tinapeza sitima yapamadzi yopita ku Foinike. Choncho tinalowamo nʼkunyamuka.
3 Ya anae intutujon lumie Chipre inpelo gui acagüe, ya manjanaojam asta Siria, ya manmatojam Tiro: sa para umadescatga güije y batco.
Tinaona chilumba cha Kupro ndipo tinadutsa kummwera kwake nʼkupita ku Siriya. Tinakayima ku Turo chifukwa sitima yathuyo imayenera kusiya katundu kumeneko.
4 Ya anae manmañodajam güije disipulo, mañagajam siete na jaane; ya ilegñija as Pablo pot y Espiritu, na chaña jumajanao julo Jerusalem.
Tinafunafuna ophunzira kumeneko, ndipo titawapeza tinakhala nawo masiku asanu ndi awiri. Iwowa, mwa Mzimu Woyera anakakamiza Paulo kuti asapite ku Yerusalemu.
5 Ya anae inquimple todo esta ayo sija na jaane, manjanaojam ya insigue y jinanaomame, ya manmaosgaejonjam ni y asaguanñija yan y famaguonñija, asta qui manjuyongjam gui siuda: ya mandimojam gui oriyan tase ya manmanayuyutjam.
Koma nthawi yathu itatha, tinachokako ndi kupitiriza ulendo wathu. Ophunzira onse pamodzi ndi akazi awo ndi ana anatiperekeza mpaka kunja kwa mzinda. Ndipo kumeneko tinagwada mʼmbali mwa nyanja ndi kupemphera.
6 Ya, anae manadingojam, uno y otro, manmaudaejam gui batco, ya sija manalo guato guiya sija.
Titatsanzikana, tinalowa mʼsitima ija, iwowo anabwerera ku nyumba zawo.
7 Ya anae inquimple y jinanaomame desde Tiro, manmatojam Tolemaida, ya insaluda y mañelo, ya mañagajam güije yan sija un jaane.
Ife tinapitiriza ulendo wathu wochokera ku Turo mpaka tinafika ku Ptolemayi. Kumeneko tinalonjera abale ndi kukhala nawo tsiku limodzi.
8 Ya y inagpaña, jame ni y mangachong Pablo, manjanaojam, ya manmatojam Sesarea; ya manjalomjam gui guima Felipe y ebangelista ni y uno gui siete, ya mañagajam güije yan güiya.
Tinachoka mmawa mwake, mpaka tinakafika ku Kaisareya. Tinapita kukakhala mʼnyumba ya mlaliki Filipo, amene anali mmodzi mwa atumiki a mpingo asanu ndi awiri aja.
9 Ya ayo na taotao, guaja cuatro jagaña na vitgen na manmanprofetisa.
Iye anali ndi ana aakazi anayi osakwatiwa amene anali ndi mphatso ya uneneri.
10 Ya mientras mañagajam güije megae na jaane, mato papa guinin Judea un profeta na y naanña Agabo.
Titakhala kumeneko masiku ambiri, kunabwera mneneri wina wochokera ku Yudeya dzina lake Agabu.
11 Ya anae mato guiya jame, jachule y senturon Pablo, ya jagode güe canaeña yan y adengña, ya ilegña: Taegüine ilegña y Espiritu Santo: Taegüineja magodeña y gaeiyo este na senturon, ni y Judios ni mangaegue Jerusalem, ya umaentrega gui canae Gentiles.
Atafika kwa ife, anatenga lamba wa Paulo, nadzimanga naye manja ake ndi mapazi ake ndipo anati, “Mzimu Woyera akuti, ‘Mwini lambayu, Ayuda adzamumanga chomwechi ku Yerusalemu, ndipo adzamupereka mʼmanja mwa anthu a mitundu ina.’”
12 Ya anae injingog este sija, parejoja jame yan ayo y mañasaga güije na lugat, matayuyut güe na chaña jumajanao julo Jerusalem.
Titamva zimenezi, ife pamodzi ndi anthu kumeneko tinamudandaulira Paulo kuti asapite ku Yerusalemu.
13 Ayonae manope si Pablo ilegña: Jafa na manatanges jamyo, ya inyamag y corasonjo? sa esta listoyo ti para jumagodeja, lao asta jumatae guiya Jerusalem, pot y naan Jesucristo.
Koma Paulo anayankha kuti, “Chifukwa chiyani mukulira ndi kunditayitsa mtima? Ndine wokonzeka osati kumangidwa kokha ayi, komanso kufa ku Yerusalemu chifukwa cha dzina la Ambuye Yesu.”
14 Ya anae timalago manamañaña, manbastajam ilegmame: Y minalago y Señot umafatinas.
Titalephera kumuletsa tinamuleka ndipo tinati, “Chifuniro cha Ambuye chichitike.”
15 Ya despues di ayo sija na jaane, inchile y güinajanmame ya manjanaojam papa Jerusalem.
Pambuyo pake, ife tinakonzeka ndi kunyamuka kumapita ku Yerusalemu.
16 Ya manjame locue yan palo disipulon Sesarea, ya manmangongone un Mnason iya Chipre, y bijo na disipulo ya infanjame mañaga.
Ena mwa ophunzira a ku Kaisareya anatiperekeza mpaka kukatifikitsa ku nyumba ya Mnasoni, kumene tinakonza kuti tizikhalako. Iye anali wa ku Kupro ndiponso mmodzi wa ophunzira oyambirira.
17 Ya anae manmatojam Jerusalem, mangosmagof y mañelo jaresibejam.
Titafika ku Yerusalemu, abale anatilandira mwachimwemwe.
18 Ya y inagpaña, manjanaojam yan si Pablo para as Santiago: ya todo y manamco manestaba.
Mmawa mwake Paulo pamodzi ndi ife tonse tinapita kwa Yakobo, ndipo akulu onse a mpingo anali komweko.
19 Ya anae munjayan jasaluda sija, jasanganen adumidide ni y finatinas Yuus gui entalo Gentiles pot y chechoña.
Paulo anawalonjera ndi kuwafotokozera mwatsatanetsatane zimene Mulungu anachita pakati pa anthu a mitundu ina kudzera mu utumiki wake.
20 Ya anae jajungog sija, maalaba y Señot, ya ilegñija nu güiya: Unlie chelujo cuantos miles na Judios y manmanjonggue, yan maneggo ni y tinago:
Atamva zimenezi, iwo anayamika Mulungu. Kenaka anawuza Paulo kuti, “Mʼbale, ukuona kuti pali Ayuda ambirimbiri amene anakhulupirira, ndipo ndi okhulupirika potsatira Malamulo a Mose.
21 Ya matungo guinin jago, na unfanagüe todo y Judios ni y mangaegue gui Gentiles, na ujafañuja gui as Moises, ilegmo, na munga manmasirconsida y famaguonñija, ni ujadalalag y costumbre.
Iwo anawuzidwa kuti iwe umaphunzitsa Ayuda onse amene akukhala pakati pa anthu a mitundu ina kuti asiye kutsatira Mose, kuti asamachite mdulidwe kapena kutsatira miyambo.
22 Ya jafa nae umafatinas? Magajet na ujajungog na mato jao.
Nanga pamenepa ife titani? Iwo adzamva ndithu kuti iwe wabwera,
23 Enao mina fatinas este y insangane jao: Guajajam cuatro na taotao na manmanpromesa;
tsono iwe chita zimene ife tikuwuze. Tili nawo amuna anayi pano amene anachita lumbiro kwa Mulungu.
24 Cone sija, ya unnagasgas jao yan sija, ya unfangata pot sija ya ufanmadasae ilunñija; ya todo utiningo na ayo sija y matungo pot jago taya guaja; lao jago locue dalalag jaftaemano y tinago, ya unadaje y lay.
Muwatenge anthu amenewa, ndipo muchite nawo mwambo wowayeretsa ndipo muwalipirire zoti apereke kuti amete tsitsi lawo. Kotero aliyense adzadziwa kuti palibe choonadi pa zimene anamva za inu, koma kuti inu mwini mumakhala moyo womvera Malamulo.
25 Ya pot y Gentiles ni y manmanjonggue, esta intigue na innafagpo, na chañija umadadaje ni uno güine; solo ujaadajeja sija güije na güinaja y manmaofrese y idolos, yan y jâgâ, y mamuno, yan y inábale.
Koma kunena za anthu a mitundu ina amene asandulika okhulupirira, ife tinawalembera zimene tinavomerezana zakuti asadye chakudya choperekedwa ku mafano, asadye magazi, asadye nyama yopotola ndiponso asachite zadama.”
26 Ayonae si Pablo jacone y taotao sija, ya y inagpaña na jaane janagasgas güe yan sija, jumalom gui templo para usangan y macumplen y jaanen y managasgas, asta qui ufanmaofrese y inefrese cada uno guiya sija.
Mmawa mwake Paulo anatenga amuna aja ndipo anachita mwambo wodziyeretsa. Kenaka anapita ku Nyumba ya Mulungu nakadziwitsa ansembe za tsiku limene adzatsiriza nthawi ya kudziyeretsa ndi kuperekera nsembe aliyense wa iwo.
27 Ya anae esta cana mamagpo y siete na jaane, ni Judios ni y mangaegue Asia, anae malie güe gui templo, janafangalamten todo y taotao contra güiya.
Ali pafupi kutsiriza masiku asanu ndi awiriwo, Ayuda ena ochokera ku Asiya anaona Paulo mʼNyumba ya Mulungu. Iwo anawutsa gulu lonse la anthu ndipo anamugwira Paulo,
28 Ya managang ilegñija: Taotao Israel, fanmanayuda: Estagüe yuje na taotao y jafananagüe todo y taotao manoja guato contra y pueblo, yan y lay, yan este na lugat: yan janafanjalom y Gentiles gui templo, ya janataelaye este na lugat.
akufuwula kuti, “Inu Aisraeli, tithandizeni! Ndi uyu munthu uja amaphunzitsa anthu onse ponseponse kuti azinyoza mtundu wathu ndiponso Malamulo athu ndi malo ano. Kuwonjezera pamenepo, walowetsa Agriki mʼbwalo la Nyumba ino ndipo wadetsa malo opatulika.”
29 (Sa guinin malie güe antes yan si Trófimo, un taotao Efeso, gui siuda, ya jinasoñija na si Pablo cumone jalom gui templo.)
Iwo ananena izi chifukwa anali ataona Trofimo wa ku Efeso ali ndi Paulo mu mzindamo ndipo iwo ankaganiza kuti Paulo anamulowetsa mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
30 Ya todo manatborotao y siuda, yan todo y taotao manmalago, ya macone si Pablo, ya manajuyong gui templo; ya enseguidas manmajuchom y petta.
Mzinda wonse unasokonezeka, ndipo anthu anabwera akuthamanga kuchokera kumbali zonse. Anamugwira Paulo, namukokera kunja kwa Nyumbayo, ndipo nthawi yomweyo anatseka zipata.
31 Ya anae manjajanao para umapuno si Pablo, mato notisia gui magas y inetnon, na todo iya Jerusalem man atborotao.
Pamene anthuwo ankafuna kupha Paulo, nkhaniyi inamveka kwa mkulu wa magulu a asilikali a Aroma kuti mzinda wonse wa Yerusalemu wasokonezeka.
32 Ya enseguidas mangone sendalo sija yan capitan, ya manmalago guato guiya sija; ya anae malie y magas y inetnon yan y sendalo sija, manbasta masaulag si Pablo.
Nthawi yomweyo iye anatenga asilikali ndi atsogoleri a magulu a asilikali ndi kuthamangira kumene kunali anthuwo. Anthuwo ataona mkuluyo ndi asilikali ake analeka kumenya Paulo.
33 Ayonae y magas y inetnon jumijot, ya quinene güe, ya manago na umagode dos na cadena: ya mamaesen jaye güe, yan jafa finatinasña.
Mkulu wa asilikaliyo anabwera nagwira Paulo, ndipo analamula kuti amangidwe ndi maunyolo awiri. Kenaka iye anafunsa kuti ndi ndani ndipo wachita chiyani.
34 Ya palo manaagang un inagang, ya y palo, otro inagang, gui entre y linajyan taotao: ya anae ti siña tumungo y magajet pot y atboroto, manago na umacone guato gui castiyo.
Ena mʼgulumo anafuwula chinthu china ndi enanso chinanso. Tsono popeza mkulu wa asilikaliyo sanathe kudziwa choonadi chenicheni chifukwa cha phokoso, analamula kuti Paulo atengedwe kupita ku malo a asilikali.
35 Ya anae mato gui guaot, sa macocone ni y sendalo sija, pot y finijom y linajyan taotao;
Paulo atafika pa makwerero olowera ku malo a asilikaliwo, ananyamulidwa ndi asilikali chifukwa cha ukali wa anthuwo.
36 Sa manatateja y linajyan taotao, ya manaagangja ilegñija: Fañuja yan guiya.
Gulu la anthu limene linamutsatira linapitiriza kufuwula kuti, “Ameneyo aphedwe basi!”
37 Ya anae para umacone si Pablo gui castiyo, ilegña nu y magas inetnon: Siñajit cumuentos? ya ilegña: Untungo Griego?
Asilikali ali pafupi kulowa naye ku malo awo, iye anapempha mkulu wa asilikaliyo kuti, “Kodi mungandilole ndiyankhulepo?” Mkulu wa asilikaliyo anafunsa kuti, “Kodi umayankhula Chigriki?
38 Ti jago ayo y taotao Egipto, ni y antes di este sija na jaane unfatinas jatsamiento, ya uncone guato gui desierto cuatro mil na taotao ni y manpegno?
Kodi sindiwe Mwigupto uja amene masiku apitawo unayambitsa kuwukira ndi kutsogolera anthu 4,000 owukira aja nʼkupita nawo ku chipululu?”
39 Lao si Pablo ilegña: Guajo Judioyo, taotao Tarso, siuda Silisia—taotao un siuda ti diquique: ya jutayuyut jao na unpoloyo ya jucuentuse y taotao sija.
Paulo anayankha kuti, “Ine ndine Myuda, wa ku Tarisisi ku Kilikiya. Sindine nzika ya mzinda wamba. Chonde loleni ndiyankhule nawo anthuwa.”
40 Ya anae ninae lisensia, tumojgue si Pablo gui guaot, ya jaseñas y taotao sija ni y canaeña. Ya anae manmamatquilo jacuentuse sija ni cuentos Hebrea, ilegña:
Ataloledwa ndi mkulu wa asilikaliyo, Paulo anayimirira pa makwereropo nakweza dzanja lake kwa gulu la anthuwo. Onse atakhala chete, iye anayankhula nawo mʼChihebri.

< Y Checho Y Apostoles Sija 21 >