< Lucas 24 +

1 Y o brotoboro e dramia chaláron muy de clarico al sepulchro, lliguerando o bue, sos terelaban quinado.
Pa tsiku loyamba la Sabata, mmamawa kwambiri, amayi anatenga zonunkhira napita ku manda.
2 Y alacháron a bar revueltisarada del sepulchro.
Anaona mwala wa pa manda utagubuduzika
3 Y chalando enrún, na alacháron o trupos e Erañoró Jesus,
ndipo atalowamo sanapeze mtembo wa Ambuye Yesu.
4 Y anacó, que sinando perelales de dal por ocono, he acoi dui gachés, sos se mequeláron dicar sunparal á siras sat coneles resplandecientes.
Pamene iwo ankadabwa za zimenezi, mwadzidzidzi, amuna awiri ovala zovala zonyezimira kwambiri anayimirira pambali pawo.
5 Y sasta sinaban medrosas, y voltisaraban a chiche ostely al chiquen, les penáron: ¿Presas orotais enrun os mules al que vivisarela?
Ndi mantha, amayiwo anaweramitsa nkhope zawo pansi, koma amunawo anawawuza kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukufuna wamoyo pakati pa akufa?
6 Na sinela acoi, presas se ha ardiñado: ojaraos de ma penó á sangue, sinando aun andré Galiléa,
Iye sali muno ayi. Wauka! Kumbukirani zimene anakuwuzani pamene anali nanu ku Galileya:
7 Penando: Jomte que o Chaboro e manu sinele entreguisarado andré bastes es manuces chores, y que sinele trijulado, y ardiñele al trincho chibes.
‘Mwana wa Munthu ayenera kuperekedwa mʼmanja mwa anthu ochimwa, napachikidwa ndipo tsiku lachitatu adzaukitsidwanso.’”
8 Entonces se ojaráron de las vardas de ó.
Ndipo anakumbukira mawu ake.
9 Y chalando abrí del sepulchro, se guilláron á penar saro ocono á os once, y á sares os averes.
Atabwerera kuchokera ku mandako, anafotokoza zinthu zonse kwa khumi ndi mmodziwo ndi kwa ena onse.
10 Y siras sos laneláron á os Apóstoles oconas buchias sinaban Maria Magdalena, y Juana, y Maria Dai de Santiago, y as averes sos sinaban sat siras.
Amayi anali Mariya Magadalena, Yohana, Mariya amayi a Yakobo, ndi ena anali nawo amene anawuza atumwi.
11 Y junos tereláron por chichi oconas vardas, y na las pachibeláron.
Koma iwo sanawakhulupirire amayiwa, chifukwa mawu awo amaoneka kwa iwo ngati opanda nzeru.
12 Tami Pedro ardiñandose, se guilló al sepulchro, y bajandose, dicó solo á os dicles, sos sinaban chibados oté, y se chaló zibando enré sí ma habia anacado.
Komabe Petro anayimirira ndi kuthamangira ku manda. Atasuzumira, anaona nsalu zimene anamukulungira zija zili pa zokha, ndipo iye anachoka, akudabwa ndi zimene zinachitikazo.
13 Y dui de janos ocola matejo chibes, chalaban á yeque gau araquerado Emmaus, dur de Jerusalém sasta de zoi millas.
Ndipo tsiku lomwelo, awiri a iwo ankapita ku mudzi wotchedwa Emau, pafupifupi makilomita khumi ndi imodzi kuchokera ku Yerusalemu.
14 Y junos chalában chamuliando enré si de sarias oconas buchias sos habian anacado.
Iwo ankayankhulana za zonse zimene zinachitikazo.
15 Y sasta sinaban penando y chamuliando o yeque sat o aver, bigoreó á junos o matejo Jesus, y piraba sat junos.
Pamenepo Yesu mwini wake anabwera ndi kuyenda nawo pamodzi;
16 Tami as aquias de junos sinaban ucharadas, somia que na le pincharasen.
koma iwo sanamuzindikire.
17 Y les penó: ¿Qué vardas sinelan oconas, sos chamulais enré sangue pirando? Y presas sinelais charavares?
Iye anawafunsa kuti, “Kodi mukukambirana zotani mʼnjira muno?” Iwo anayima ndi nkhope zakugwa.
18 Y rudelando yeque de junos, arquerado Cleóphas, le penó: ¿Tucue gringó andré Jerusalém: y na chanelas ma ha anacado oté oconas chibéses.
Mmodzi wa iwo wotchedwa Kaliyopa anamufunsa kuti, “Kodi ndiwe wekha wokhala mu Yerusalemu amene sukudziwa zinthu zimene zachitika mʼmasiku awa?”
19 O les penó: ¿Que buchí? Y rudeláron: De Jesus Nazareno, sos sinaba yeque gacho Propheta, silnó andré obras y andré vardas anglal de Debél y de sari a sueti;
Iye anafunsa kuti, “Zinthu zotani?” Iwo anayankha nati, “Za Yesu wa ku Nazareti, Iye anali mneneri, wamphamvu mʼmawu ndi mu zochita pamaso pa Mulungu ndi anthu onse.
20 Y sasta le entreguisaráron os Pontesquerés y amáres Manclayes á condenacion de meripen, y o trijuláron:
Akulu a ansembe ndi oweruza anamupereka Iye kuti aphedwe, ndipo anamupachika Iye;
21 Tami mu fronsaperabamos, que ó sinaba sos terelaba de diñar mestepé á Israel; o mas choro sinela, que sejonia sinela o trincho chibés, que oconas buchias han anacado.
koma ife tinkayembekezera kuti Iye ndiye amene akanawombola Israeli. Ndipo kuwonjeza apo, lero ndi tsiku lachitatu chichitikireni izi.
22 Aunque yeques cadchias de amarias nos han querelado darañar; siras anglal e clarico chaláron al sepulchro.
Kuwonjezanso apo, ena mwa amayi athu atidabwitsa ife. Iwo anapita ku manda mmamawa
23 Y na terelando alachado desquero trupo, limbidiáron, penando que habian dicado oté vision de Manfarieles, sos penelan que ó vivisarela.
koma sanakapeze mtembo wake. Iwo anabwera ndi kudzatiwuza ife kuti anaona masomphenya a angelo amene anati Yesu ali moyo.
24 Y yeques de amares plalores chaláron al sepulchro, y lo alacháron andiar sasta as cadchias lo habian penado; tami á ó na lo alacháron.
Kenaka ena mwa anzathu anapita ku manda ndipo anakapeza monga momwe amayiwo ananenera, koma Iye sanamuone.”
25 Y Jesus penó á junos: ¡O dinelés y tardos de carlochin, para pachibelar o saro sos os Prophetas han penado!
Iye anawawuza kuti, “Inu ndinu anthu opusa, osafuna kukhulupirira msanga zonse zimene aneneri ananena!
26 ¿Na jomte, que o Christo urjiyase oconas buchias, y que andiar chalase enré desquero chimusolano?
Kodi Khristu sanayenera kumva zowawa izi ndipo kenaka ndi kulowa mu ulemerero wake?”
27 Y se chitó á penar desde Moysés y de sarés os Prophetas, chibando en dundun as randiñipenes sos chamulian de ó.
Ndipo kuyambira ndi Mose ndi aneneri onse Iye anawafotokozera zimene zinalembedwa mʼmalemba wonse zokhudzana ndi Iye mwini.
28 Y bigoreáron al gau, á duque chalaban: Y ó diñó simaches de chalar mas dur.
Atayandikira mudzi omwe amapitako, Yesu anachita ngati akupitirira.
29 Tami o detereláron sat sila, penando: Queda tucue sat amangue, presas tasata sinela, y o cam ha chalado ostely. Y chaló andré sat junós.
Koma iwo anamupempha Iye kwambiri kuti, “Mukhale ndi ife, popeza kwatsala pangʼono kuda, ndipo dzuwa lili pafupi kulowa.” Ndipo Iye anapita kukakhala nawo.
30 Y sinando bejelado sat junos á la mensalli, ustiló o tato, y o majarificó: y terelando asparabado, se lo diñaba.
Iye ali pa tebulo pamodzi nawo, anatenga buledi ndipo anayamika, nanyema nayamba kuwagawira.
31 Y sináron despandadas as aquias de junós, y lo pincharáron; y ó entonces se najó de desquerias aquias.
Kenaka maso awo anatsekuka ndipo anamuzindikira Iye, ndipo anachoka pakati pawo.
32 Y penáron yeque á aver: ¿Pre baji na bucharaba amaro carlochin enrún amangue, pur andré o drun chamuliaba sat amangue, chibando en dundun as randiñipenes?
Iwo anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi mitima yathu sinali kutentha mʼkati mwathu pamene Iye ankayankhulana nafe pa njira ndi mmene anatitsekulira malemba?”
33 Y ardiñandose andré a mateja ocána, limbidiáron á Jerusalém: y alacháron catanés á os once, y á junos sos sinaban sat junós,
Nthawi yomweyo iwo anayimirira ndi kubwerera ku Yerusalemu. Iwo anapeza khumi ndi mmodziwo ndi ena anali nawo nasonkhana pamodzi
34 Sos penáron; Chachipen, ha ardiñado o Erañó, y se ha diado á Simón.
ndipo anati, “Ndi zoonadi! Ambuye auka ndipo anaonekera kwa Simoni.”
35 Y junos penáron ma les terelaba anacado andré o drun y sasta le habian pincherado al asparabar o tato.
Kenaka awiriwo anawawuza zimene zinachitika pa njira, ndi mmene iwo anamudziwira Yesu, Iye atanyema buledi.
36 Y sinando chamuliando oconas buchias, se chitó Jesus en medio de junos, y les penó: Paz á sangue: menda sinelo, na darañeleis.
Akufotokoza zimenezi, Yesu mwini wake anayimirira pakati pawo ndipo anati, “Mukhale ndi mtendere.”
37 Presas junos perelales de dal, y canguelo, penchababan que diquelaban yeque barbalé.
Koma chifukwa choti anathedwa nzeru ndi kuchita mantha, ankaganiza kuti akuona mzukwa.
38 Y les penó: ¿Presás terelais dal, y costunelan pensamientos á jirés carlochines?
Iye anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukuvutika? Nʼchifukwa chiyani mukukayika mu mtima mwanu?
39 Diquelad minrias bastes y minrés pindrés, que menda matejo sinelo: pajabelad y diquelad, presas yeque barbalé na terela brinza ta cocális, sasta diquelais que terelo menda.
Taonani manja anga ndi mapazi anga. Ine ndine amene! Khudzeni kuti muone. Mzukwa ulibe mnofu ndi mafupa monga mukuonera ndili nazo.”
40 Y penado ocono, les dió as bastes y os pindrés.
Iye atanena izi anawaonetsa manja ake ndi mapazi ake.
41 Tami sasta aun na astisirasen creer, sinando maravillados de pesquital, les penó: ¿Terelais acoi buchi que jamar?
Ndipo pamene iwo samakhulupirirabe, chifukwa cha chimwemwe ndi kudabwa, Iye anawafunsa kuti, “Kodi muli ndi chakudya chilichonse pano?”
42 Y junos le laneláron yeque arecata de macho querabado, y yeque frimita de anguin.
Iwo anamupatsa Iye kachidutswa ka nsomba yophika.
43 Y habiendo jamado anglal de junos, ustiló as sobras, y se les diñó.
Iye anakatenga ndi kukadya iwo akuona.
44 Y les penó: Oconas sinelan as vardas sos pené á sangue, sinando aun con-a-sangue, que jomte que se perele o saro ma sinela libanado de mangue andré a Eschastra de Moysés, y andré os Prophetas, y andré os Psalmes.
Iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene ndinakuwuzani pamene ndinali nanu: chilichonse chiyenera kukwaniritsidwa chimene chinalembedwa cha Ine mʼbuku la Malamulo a Mose, Aneneri ndi Masalimo.”
45 Entonces les despandó a suncai, somia que jabillasen as randiñapenes.
Kenaka anawatsekula maganizo kuti azindikire Malemba.
46 Y les penó: Andiar sinela libanado, y andiar jomte que o Christo urjiyaráse, y ardiñáse al trincho chibes de enrún os mulés:
Iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene zinalembedwa: Khristu adzazunzika ndipo adzauka kwa akufa tsiku lachitatu.
47 Y que se chamuliase andré desquero nao penitencia y mecos de grecos á sari a sueti, y brotoboro á Jerusalém.
Ndipo kutembenuka mtima ndi kukhululukidwa kwa machimo zidzalalikidwa mu dzina lake kwa anthu amitundu yonse kuyambira mu Yerusalemu.
48 Y sangue marchirés sinelais de ocónas buchias.
Inu ndinu mboni za zimenezi.
49 Y menda bichabelo opré sangue á la buchi prometida de minrio Dada: Tami sangue permaneced acoi andré o foros, disde que sinelais perelalés de la sila e udscho.
Ine ndidzakutumizirani chimene Atate anga analonjeza. Koma khalani mu mzinda muno mpaka mutavekedwa mphamvu yochokera kumwamba.”
50 Y os sicabó abrí disde Bethania: y ardiñando desqueres hastes os majarificó.
Iye atawatengera kunja kwa mzindawo mpaka ku Betaniya, anakweza manja ake ndi kuwadalitsa.
51 Y anacó, que o chiros que os majarificaba, se najó de junos, y sinaba lliguerado al Tarpe.
Iye akuwadalitsa, anawasiya ndipo anatengedwa kupita kumwamba.
52 Y junos despues de buchararse al chiquen y querelarle adoracion, se limbidiáron á Jerusalém sat bari pesquital.
Pamenepo anamulambira Iye ndipo anabwerera ku Yerusalemu ndi chimwemwe chachikulu.
53 Y sinaban deltó andré a cangrí loando ta majarificando á Debél. Unga. Saboca Enrecar Debel Ererio. Chachipè.
Ndipo iwo anakhalabe ku Nyumba ya Mulungu, akulemekeza Mulungu.

< Lucas 24 +