< Lucas 23 >

1 Y se ardiñó sari ocola sueti, y lo lligueráron á Pilato.
Kenaka gulu lonse la anthuwo linayimirira ndi kumutengera kwa Pilato.
2 Y se chitáron á acusarle, penando: A ocona terelamos alachado pervirtiendo á amari sueti, y vedando platisarar jayere á Cæsar, y penando que ó sinela Christo Crallis.
Ndipo iwo anayamba kumuneneza nati, “Ife tinapeza munthu uyu akusokoneza anthu a mtundu wathu ndipo amatsutsa zopereka msonkho kwa Kaisara komanso amati ndi Khristu, Mfumu.”
3 Y Pilato le puchabó, y penó: ¿Sinelas tucue o Crallis es Chuti? Y ó le rudeló penando: Tucue lo penelas.
Pamenepo Pilato anamufunsa Yesu kuti, “Kodi Iwe ndiwe Mfumu ya Ayuda?” Yesu anayankha kuti, “Mwatero ndinu.”
4 Penó Pilato á os Manclayes es Erajais, y á la sueti: Chichi, sos sinela choro alachelo andré ocona manu.
Kenaka Pilato anawawuza akulu a ansembe ndi gulu la anthu, “Ine sindikumupeza cholakwa munthuyu.”
5 Tami junos insistian, penando: Terela alborotado a sueti sat la beda, sos chibela por sari la Judéa, comenzando desde o chim de Galiléa, disde acoi.
Koma iwo analimbikirabe kuti, “Iyeyu amasokoneza anthu ku Yudeya konse ndi chiphunzitso chake, Iyeyu anayambira ku Galileya ndipo wayenda mtunda wonse mpaka kuno.”
6 Pilato, sos juneló penar Galiléa, puchabó si sinaba de Galiléa.
Pakumva zimenezi, Pilato anafunsa ngati munthuyo ndi Mgalileya.
7 Y pur chaneló, que sinaba e jurisdicion de Herodes, lo bichabó á Herodes: sos al chiros socababa tambien andré Jerusalém.
Iye atamva kuti Yesu anali pansi pa ulamuliro wa Herode, anamutumiza kwa Herodeyo, amene pa nthawi imeneyo analinso mu Yerusalemu.
8 Y Herodes pur dicó á Jesus, se alendó baribu. Presas de baribu chiros le terelaba camelado dicar, presas habia junelado penar de ó barias buchias, y fronsaperaba dicarle querelar alguno zibo.
Herode ataona Yesu, anakondwa kwambiri, chifukwa kwa nthawi yayitali, ankafunitsitsa atamuona. Kuchokera pa zimene anamva za Iye, anayembekezera kuti achita zodabwitsa.
9 Le quereló pues baribustrias preguntas: Tami ó le rudelaba chichi.
Iye anamufunsa mafunso ambiri, koma Yesu sanayankhe.
10 Y sinaban os Manclayes es erajais, y os Libanes acusandole silamente.
Akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, anayimirira pamenepo ndi kumuneneza kwambiri.
11 Y Herodes sat desqueres jundunáres ó despreció: y caquerandole le quereló chitar yeque conel parno, y aver begai o limbidió á Pilato.
Pamenepo Herode ndi asilikali ake anamuseka ndi kumunyoza Iye. Atamuveka mkanjo wonyezimira, anamutumizanso kwa Pilato.
12 Y ocola chibes se quereláron monres Herodes y Pilato; presas palal sinaban daschmanuces entre sí.
Tsiku limenelo, Herode ndi Pilato anakhala abwenzi. Zisanachitike izi anali adani.
13 Pilato pues araqueró á os Manclayes es erajais, y á os Barandéres, y á la sueti.
Pilato anasonkhanitsa akulu a ansembe, oweruza ndi anthu,
14 Y les penó: Terelais lanelado á mangue ocona manu, sasta pervertidor e sueti; y diquelad que puchabándole menda anglal de sangue, na alaché andré ocona manu yeque de ocolas buchias chorias de que o acusais.
ndipo anawawuza kuti, “Munabweretsa munthuyu kwa ine ngati ndiye amawuza anthu kuti awukire. Ine ndamufunsa pamaso panu ndipo sindinapeze chomuyimbira mlandu.
15 Ni Herodes Crallis: presas sangue bichabé á ó, y he acoi que se ha probisarado chichi, sos merezca meripen.
Herodenso sanapeze chifukwa pakuti wamutumizanso kwa ife monga mmene mukuoneramu. Iyeyu sanachite chinthu chakuti aphedwe.
16 Y andiar le despandaré despues de terelar curado.
Nʼchifukwa chake, ine ndingomulanga, nʼkumumasula.”
17 Y debisaraba despandarles yeque estardo andré o chibes e fiesta.
(Pa nthawi yachikondwerero cha Paska iye ankayenera kumasula munthu mmodzi).
18 Y sari a sueti diñó goles catanés, penando: Querelad merar a ocona, y despandanos á Barrabás.
Onse pamodzi anafuwula kuti, “Muchotseni munthuyu! Timasulireni Baraba!”
19 Ocona habia sinado bucharado andré l’estaripel por yeque sedicion ardiñada andré o foros, y por yeque mordipen.
(Baraba anaponyedwa mʼndende chifukwa choyambitsa chipolowe mu mzinda ndi kupha).
20 Y Pilato les chamulió de nuevo, camelando despandar á Jesus.
Pofuna kumumasula Yesu, Pilato anawadandaulira iwo.
21 Tami junos limbidiaban á diñar goles, penando: A la trijul con ó, A la trijul con ó.
Koma iwo anapitirirabe kufuwula kuti, “Mpachikeni! Mpachikeni!”
22 Y ó a trincha begai les penó: ¿Pues qué choro ha querdi ocona? Menda na alachelo andré ó necautia causa de meripen: le curelaré pues y le despandaré.
Kachitatu anawafunsanso iwo kuti, “Chifukwa chiyani? Kodi munthu uyu wachita choyipa chanji? Ine sindinapeze cholakwa mwa Iye chakuti aphedwe choncho ndingomukwapula ndi kumumasula.”
23 Tami junos insistian mangando á goles bares, que sinase trijulado, y ardiñaban butér sus goles.
Koma ndi mawu ofuwulitsa, analimbikirabe kuti Iye apachikidwe, ndipo kufuwulako kunapitirira.
24 Y Pilato penchabó, que se querelara ma junos mangaban.
Choncho Pilato anatsimikiza kuchita zofuna zawozo.
25 Y les despandó á ó sos por sedicion, y mordipen habia sinado bucharado andré l’estaripel, al sos habian mangado: y entregisaró á Jesus á las bastes de junos.
Iye anawamasulira munthu amene anaponyedwa mʼndende chifukwa choyambitsa chipolowe ndi kupha, amene ankamufunayo, ndipo anawapatsa Yesu mwakufuna kwawo.
26 Y pur lo lligueráron, ustiláron yeque manu de Cyrene, sos se hetó Simón, sos abillaba de yeque cosque: y le carguisaráron la trijul, somia que la lliguerase palal de Jesus.
Ndipo pamene ankapita naye, anagwira Simoni wa ku Kurene, amene ankachokera ku munda, namusenzetsa mtanda namuyendetsa pambuyo pa Yesu.
27 Y le plastañaban yeque plastañi bari de sueti, y de cadchias, sos le plañian y orobaban.
Gulu lalikulu la anthu linamutsata Iye, kuphatikiza amayi amene ankabuma ndi kumulirira.
28 Tami Jesus? límbidiandose hacia siras, les penó: Dugidas de Jerusalém, na orobeis opré mangue; antes orobad opré jirias matejas, ta opré jires chaborés.
Yesu anatembenuka nati kwa iwo, “Ana aakazi a Yerusalemu, musandilirire Ine; dzililireni nokha ndi ana anu.
29 Presas abillarán chibeses andré que penarán: Majaradas as estériles, y as porias, sos na concibiéron, y as chuchai sos na diñáron de mamisarar.
Pakuti nthawi idzabwera imene inu mudzati, ‘Ndi odala amayi osabereka, mimba zimene sizinabereke ndi mawere amene sanayamwitse!’
30 Entonces se chibarán á penar á as playas: Perad opré amangue: y á os bures: Ucharadnos.
Kenaka, “adzawuza mapiri kuti tigwereni ife; zitunda kuti tiphimbeni ife.
31 Presas si andré carschta bardry querelan ocono, ¿andré a seca, que se querelará?
Chifukwa ngati anthu akuchita izi pa mtengo wauwisi, chidzachitike nʼchiyani ndi wowuma?”
32 Y lligueraban tambien sat ó dui averes, sos sinaban chores, somia mulabarlos.
Amuna ena awiri, onsewo achifwamba, anatengedwanso pamodzi ndi Yesu kukaphedwa.
33 Y pur bigoreáron á o stano, sos se heta de la Calavéra, le trijuláron oté; y os dui randés, yeque á la bastari, y aver á la can.
Pamene anafika pamalo otchedwa Bade, anamupachika Iye pamodzi ndi achifwambawo, mmodzi kudzanja lake lamanja ndi winayo la ku lamazere.
34 Tami Jesus penaba: Dada, ojabesalos: presas na chanelan, ma querelan. Y dividiendo desqueres talalorés, bucháron sustirias.
Yesu anati, “Atate, akhululukireni, pakuti sakudziwa chimene akuchita.” Ndipo anagawana malaya ake mochita maere.
35 Y a sueti sinaba dicando, y os Manclayes catanamente sat junos o denostabelaban, y penaban: A averes chibó lacho, listrabese á sí matejo, si ocona sinela o Christo, o camelado de Debél.
Anthu anayimirira nʼkumaonerera, ngakhalenso akuluakulu ankamulalatira Iye. Iwo anati, “Iye anapulumutsa ena; adzipulumutse yekha ngati ndi Khristu wa Mulungu, Wosankhidwayo.”
36 Le caqueraban tambien os jundunares, chalando sunparal á ó, y chitandole anglal vinagre.
Asilikalinso anabwera ndi kumunyoza Iye. Iwo anamupatsa vinyo wosasa,
37 Y penando: Si tucue sinelas o Crallis es Chuti, listrabelate á tun matejo.
ndipo anati, “Ngati ndiwe Mfumu ya Ayuda, dzipulumutse wekha.”
38 Y sinaba opré ó yeque titulo libanado andré letras Griegas, Latinas y Ybuchias: Ocona sinela o Crallis es Chuti.
Ndipo panalembedwa chikwangwani pamwamba pake chimene chinati: uyu ndi mfumu ya ayuda.
39 Y yeque de ocolas randes, sos sinaban luanados, o injuriaba, penando: Si tucue sinelas o Christo, listrabela á tun matejo, y á amangue.
Mmodzi wa achifwambawo, amene anapachikidwa, anamunenera Iye zamwano nati, “Kodi sindiwe Khristu? Dzipulumutse wekha ndi ifenso!”
40 Tami o aver rudelando, le chingaró, penando: Ni aun tucue canguelas á Debél, sinando andré a mateja corypény?
Koma wachifwamba winayo anamudzudzula iye nati, “Suopa Mulungu, iwenso ukulandira chilango chomwechi?
41 Aromali amangue urgiyamos por amaro grecos, presas ustilamos ma merecen amarias obras: tami ocona chichi choro ha querdi.
Ife tikulangidwa mwachilungamo, pakuti ife tikulandira monga mwa ntchito zathu. Koma munthu uyu sanachimwe kanthu.”
42 Y penába á Jesus: Erañó, enjallate de mangue pur abillares á tun chim.
Kenaka anati, “Yesu, mundikumbukire ine pamene mulowa mu ufumu wanu.”
43 Y Jesus le penó; Aromali te penelo, que achibes sinarás con-a-mangue andré o Paraiso.
Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, ndikukuwuza kuti lero lino udzakhala ndi Ine mʼparadaiso.”
44 Y sinaba ya casi a ocana zobia, y sari a chiquen se ucharó de tinieblas disde a ocana nubia.
Linali tsopano pafupi ora lachisanu ndi chimodzi, ndipo mdima unagwa pa dziko lonse mpaka ora lachisanu ndi chinayi,
45 Y se chitó oruné o Cam: y o velo e cangri se asparabó pré medio.
pakuti dzuwa linaleka kuwala. Ndipo chinsalu cha mʼNyumba ya Mulungu chinangʼambika pakati.
46 Y Jesus diñando yeque gole baro, penó: Dada: andré tirias bastes encomiendo minrio ylo: y penando ocono, espiró.
Yesu anafuwula ndi mawu okweza kuti, “Atate, ndikupereka mzimu wanga mʼmanja mwanu.” Atanena zimenezi, anamwalira.
47 Y pur dicó o Centurion ma habia anacado, diñó chimusolano á Debél, penando: Aromali, ocona manu sinaba lacho.
Kenturiyo, ataona zimene zinachitikazi, analemekeza Mulungu ndipo anati, “Zoonadi, uyu anali munthu wolungama.”
48 Y sari a sueti sos sunparal sinaba, pur dicaba ma anacaba, se limbidiaba curandose andré os chepés.
Anthu onse amene anasonkhana kudzaonerera izi, ataona zinachitikazo, anadziguguda pachifuwa ndipo anachoka.
49 Y sares os pincherados de Jesus, y as cadchias sos le habian plastañado de Galiléa, sinaban dicando oconas buchias de dur.
Koma onse amene anamudziwa Iye, kuphatikiza amayi amene anamutsatira kuchokera ku Galileya, anayimirira akuona zinthu izi.
50 Y he acoi yeque gacho araquerado Joseph, sos sinaba Barander, gacho lachó ta justo:
Ndipo taonani panali munthu wina wotchedwa Yosefe, mmodzi wa gulu loweruza, munthu wabwino ndi wolungama.
51 Sos na habia consentido andré o consejo, ni andré os hechos de junos, de Arimathéa, foros e Judéa, sos ujaraba o chim de Debél.
Iye sanavomereze zimene anzake abwalo anagwirizana ndi kuchita. Iye ankachokera ku mudzi wa Arimateyu wa ku Yudeya ndipo ankayembekezera ufumu wa Mulungu.
52 Ocona bigoreó á Pilato, y le mangó o trupos de Jesus.
Atapita kwa Pilato, iye anakapempha mtembo wa Yesu.
53 Y habiendole nicabado, lo involvisaró andré yeque sabana parni, y lo childó andré yeque sepulchro querdi andré un bur, anduque cayque disde entonces habia sinado childado.
Ndipo anawutsitsa, nawukulunga nsalu yabafuta nawuyika mʼmanda wosemedwa mʼmwala, amene panalibe wina amene anayikidwamo.
54 Y sinaba o chibes de Parasceve, y sunparal sinaba a Canché.
Linali tsiku lokonzekera ndipo Sabata linatsala pangʼono kuyamba.
55 Y abillando tambien as cadchias sos habian plastañado á Jesus desde Galiléa, dicáron o sepulchro, y a beda en que sinaba childado desquero trupos.
Amayi amene anabwera ndi Yesu kuchokera ku Galileya, anatsata Yosefe ndipo anaona manda ndi momwe mtembo wake anawuyikira.
56 Y limbidiandose, quináron bus ta unguentes; y reposáron a Canché sasta mandisarela a Eschastra.
Kenaka anapita ku mudzi ndi kukakonza mafuta onunkhira. Koma anapuma pa tsiku la Sabata pomvera malamulo.

< Lucas 23 >