< Lucas 21 >

1 Y sinando diando, dicó os balbales sos bucharaban desquerias ofrendas andré a jestari e manchin.
Yesu atayangʼana, anaona olemera akuyika mphatso zawo mu chosungira ndalama za mʼNyumba ya Mulungu.
2 Y dicó tambien yeque piuli chorori, sos chibelaba dui cales chinores.
Iye anaonanso mkazi wamasiye wosauka akuyikamo timakopala tiwiri.
3 Y penó: Aromali sangue penelo, que ocona chorori piuli ha chibado butér que sares os avéres.
Iye anati, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mkazi wamasiye wosaukayu wapereka zambiri kuposa ena onsewa.
4 Presas sares ocolas terelan bucharado somía ofrendas de Debél, de ma les sobresarela: Tami ocona de desqueri erdicha terela chibado saro o jayere sos terelaba.
Anthu onsewa atapa mphatso zawo kuchokera pa zochuluka zimene ali nazo; koma uyu, mwa umphawi wake, wapereka zonse zimene ali nazo.”
5 Y rudeló á yeques, sos penaban de la cangri, que sinaba chiti de barias pacuarias, y de diñipenes:
Ena mwa ophunzira ake ankachita ndemanga za mmene Nyumba ya Mulungu anayikongoletsera ndi miyala yokongola ndiponso zinthu zina zomwe anthu anapereka kwa Mulungu. Koma Yesu anati,
6 Oconas buchias sos diquelais, abillarán chibeses, pur na sinará mequelada bar opré bar, sos na sinará demolida.
“Koma zimene mukuziona panozi, nthawi idzafika pamene ngakhale mwala umodzi omwe sudzakhala pa unzake; uliwonse udzagwetsedwa pansi.”
7 Y le puchabáron, y penáron: ¿Duquendio, pur sinará ocono? y que simache sinará, pur ocono comenzáre á sinar?
Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, kodi zonsezi zidzachitika liti? Ndipo tidzaonera chiyani kuti zili pafupi kuchitika?”
8 O penó: Diquelad, que na sineleis jongabados: presas baribustres abillarán andré minrio nao, penando: Menda sinelo, y o chiros sinela sunparal: garabelaos pues de chalar palal de junos.
Iye anayankha kuti, “Chenjerani kuti musanyengedwe. Pakuti ambiri adzabwera mʼdzina langa nadzati ‘Ine ndine Iye’ ndi kuti ‘Nthawi yayandikira.’ Musadzawatsate iwo.
9 Y pur junelareis chingaripenes y jestias, sangue na cangueleis: presas jomte que ocono anaquele brotoboro, tami na sinará yescotria a anda.
Mukadzamva zankhondo ndi zipolowe, musadzachite mantha. Zinthu izi ziyenera kuchitika poyamba, koma chimaliziro sichidzafika nthawi yomweyo.”
10 Entonces les penaba: Se ardiñará sueti contra sueti, y chim contra chim.
Kenaka anawawuza kuti, “Mtundu wa anthu udzawukirana ndi mtundu wina, ndi ufumu kuwukira ufumu wina.
11 Y sinará bares jolili-motos por os gaues, y salipénes, y boquises y sinará buchias espantosas, y barias simaches e Charos.
Kudzakhala zivomerezi zazikulu, njala ndi miliri mʼmalo osiyanasiyana, ndi zinthu zoopsa ndi zizindikiro zamphamvu kuchokera kumwamba.
12 Tami anglal de saro ocono sangue ustilarán, y plastañarán, entregisarando sangue á as Synagogas, y á os estaripeles, y lliguerarán sangue á os Crallises, y á os Poresqueres, por minrio nao:
“Koma zonsezi zisanachitike, adzakugwirani ndi kukuzunzani. Adzakuperekani ku masunagoge ndi ku ndende, ndipo adzakutengerani pamaso pa mafumu ndi olamulira, ndipo zonsezi zidzachitika chifukwa cha dzina langa.
13 Y ocono sinará sasta machiria á sangue.
Umenewu udzakhala mwayi wanu ochitira umboni.
14 Terelad yeque buchi silni andré jires carlés, o na penchabar anglal ma terelais de rudelar.
Koma tsimikizani mtima kuti musadzade nkhawa za momwe mudzadzitchinjirizire.
15 Presas menda diñaré sangue mui y chaneleria, al que n’astisarelarán resistir, ni contrapenar sares jires daschmanuces:
Pakuti Ine ndidzakupatsani mawu ndi nzeru kotero kuti palibe mmodzi wa adani anu adzathe kuwakana kapena kuwatsutsa.
16 Y sinareis entregados de jires batuces, y plalores, y rati, y monrés, y querelarán merar a yéques de sangue.
Inu mudzaperekedwa ndi makolo anu, abale, anansi ndi abwenzi anu ndipo ena mwa inu adzakuphani.
17 Y sares aborrecerán á sangue pre minrio nao.
Anthu onse adzakudani chifukwa cha Ine.
18 Tami na se najabará yeque bal de jires jerés.
Koma palibe tsitsi limodzi la mʼmutu mwanu lidzawonongeke.
19 Sat jiri paciencia listrabareis jirias ochias.
Mukadzalimbikira ndiye mudzapeze moyo.
20 Pues pur dicáreis á Jerusalém pandada al crugos de jundunares, entonces chanelad que sun najipen sinela sunparal.
“Mukadzaona Yerusalemu atazingidwa ndi magulu ankhondo, inu mudzadziwe kuti kuwonongeka kwake kuli pafupi.
21 Entonces junos sos sinelan andré la Judéa, najalelen á os bures: y junos en medio de siró se sicobelen abrí; y junos andré os bures na chalen andré de siró.
Pamenepo amene ali ku Yudeya adzathawire ku mapiri, amene ali mu mzinda adzatulukemo, ndi amene ali ku midzi asadzalowe mu mzinda.
22 Presas oconas sinelan chibeses de venganza, somia se perelalen sarias as buchias, sos sinelan libanadas.
Pakuti iyi ndi nthawi yachilango pokwaniritsa zonse zimene zinalembedwa.
23 Tami ysna de las cambrias, y de ocolas sos diñelan de mamisarar andré ocolas chibeses! Presas sinará bari apretura opré a pu, y ira para ocona sueti.
Zidzakhala zoopsa nthawi imenewo kwa amayi oyembekezera ndi amayi oyamwitsa! Kudzakhala masautso aakulu mʼdziko ndipo anthu onse adzawakwiyira.
24 Y perarán á filo e estuche: y sinarán lliguerados utildes á sares os chimes, y Jerusalém sinará hollada de los Busnés: disde que se perele o chiros es Busnes.
Iwo adzaphedwa ndi lupanga ndi kutengedwa ukapolo kupita ku mayiko wonse. Yerusalemu adzaponderezedwa ndi anthu a mitundu ina mpaka nthawi ya a mitundu ina itakwaniritsidwa.
25 Y terelará simáches Cam, y andré a Chimutra, y andré as cherdillas; y andré la pu tráqui es manuces pre a confusion sos querelara a chumas e moros, y de sus panias.
“Padzakhala zizindikiro zodabwitsa pa dzuwa, mwezi ndi nyenyezi. Pa dziko lapansi, mitundu ya anthu idzakhala mʼmasautso ndipo idzathedwa nzeru pakumva mkokomo ndi mafunde a mʼnyanja.
26 Sinando os manuces yertos por o dal y canguelo es buchias, sos opre abillaran á sari a sueti: presas as silas e Tarpe sinarán conmovidas:
Anthu adzakomoka chifukwa cha mantha, akadzamva za zimene zikubwera pa dziko lapansi, pakuti zinthu zamlengalenga zidzagwedezeka.
27 Entonces diquelarán al Chaboro e manu abíllar opré yeque paros sat ezor baro y chimusolano.
Nthawi imeneyo adzaona Mwana wa Munthu akubwera ndi mitambo, mphamvu ndi ulemerero waukulu.
28 Pur comenzaren pues á perelarse oconas buchias, diquelad, y ardiñelad jires jeres; presas sunparal sinela jire mestepé.
Zinthu izi zikadzayamba kuchitika, mudzayimirire ndi kutukula mitu yanu, chifukwa chipulumutso chanu chayandikira.”
29 Y les penó yeque semejanza: Diquelad a carschta-heila, y sarias as carschtas.
Iye anawawuza fanizo ili, “Taonani mtengo wamkuyu ndi mitengo ina yonse.
30 Pur bucharelan ya abrí de sí o mibao, jabillais que sunparal sinela o canriano.
Ikamatulutsa masamba, mumakhoza kudzionera nokha ndi kudziwa kuti dzinja lili pafupi.
31 Andiar tambien sangue, pur dicalareis querelarse oconas buchias, chanelad que sunparal sinela o chim de Debél.
Chimodzimodzinso, mukadzaona zinthu zonsezi, dziwani kuti ufumu wa Mulungu uli pafupi.
32 Aromali sangue penelo, que na nacará ocona generacion, disde que sarias oconas buchias sinarán quereladas.
“Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mʼbado uno sudzatha mpaka zinthu zonsezi zitachitika.
33 O Charos y la pu nacabarán: tami minrias vardas na nacarán.
Kumwamba ndi dziko lapansi zidzatha, koma mawu anga sadzatha.”
34 Diquelad pues por sangue, na sinele que jires carlés se carguisarelen de glotoneria y de matipen, y de las gramias de ocona chipen: y que abillele de repente opré sangue ocola chibes.
“Samalani, kuti mitima yanu ingalemetsedwe ndi maphwando, kuledzera ndi kudera nkhawa za moyo uno, ndi kuti tsiku ilo lingadzakupezeni modzidzimutsa ngati msampha.
35 Presas andiar sasta yeque maluno abillará opré sares sos sinelan opré a chichi de sari a jolili.
Pakuti lidzafika pa onse okhala pa dziko lonse lapansi.
36 Pues sinelad de vela manguelando á Un-debél andré saro chiros, somia que sineleis cabalicos de najar sarias oconas buchias, sos jomte sinar, y de sinar andre pindré, anglal e Chaboro e manu.
Khalani tcheru nthawi zonse ndi kupemphera kuti inu mudzathe kuthawa zonse zimene zili pafupi kuchitika, ndi kuti mudzathe kuyima pamaso pa Mwana wa Munthu.”
37 Y sinaba bedando andré a cangri: ta arachis chalaba abrí, y lo nacaba andré o bur, araquerado e Urucal.
Tsiku lililonse Yesu amaphunzitsa ku Nyumba ya Mulungu, ndi madzulo ali wonse Iye amachoka kukakhala pa phiri la Olivi usiku wonse.
38 Y sari a sueti se ardiñeló de clarico, somia abillar, a junarle andré a cangri.
Ndipo anthu onse amabwera mmamawa kudzamumva Iye ku Nyumba ya Mulungu.

< Lucas 21 >