< Lucas 16 >

1 Y penaba tambien á desqueres discipules: Sinaba manu balbalo, sos terelaba queresquero; y ocona sinaba acusado anglal de ó, de haber nicobado desquero parné.
Yesu anawuza ophunzira ake kuti, “Panali munthu wina wachuma amene kapitawo wake anzake anamuneneza kuti amawononga chuma chakecho.
2 Y le araqueró, y le penó: ¿Que sinela ma junelo penar de tucue? din pista de tiri queresqueria: presas acana n’astis que sineles queresquero de mangue butér.
Choncho anamuyitana ndi kumufunsa kuti, ‘Kodi nʼchiyani chimene ndikumva za iwe? Pereka tsatanetsatane wa ntchito yako, pakuti supitirizanso kukhala kapitawo wanga.’
3 Entonces penó o queresquero andré sí: ¿Que querelaré, presas minrio Erañó ustilela de mangue a queresqueria? Cavar na terelo silas, mangar terelo verguenza.
“Kapitawoyo analingalira kuti, ‘Kodi tsopano ndidzachita chiyani? Bwana wanga andichotsa ntchito. Ine ndilibe mphamvu zokwanira zolimira, komanso ine ndimachita manyazi kupempha.
4 Chanelo ma me jomte querelar, somia que pur sinare nicobada a queresqueria, ustilelen mangue andré desqueres queres.
Ine ndikudziwa chimene ndidzachita kotero kuti, pamene ntchito yanga yatha pano, anthu adzandilandire mʼnyumba zawo.’
5 Araqueró pues á cata yeque es deudores de desquero erañoró, y penó al brotoro: ¿Quanto debisarelas á minrio Erañoró?
“Choncho iye anayitana aliyense amene anali ndi ngongole kwa bwana wake. Iye anafunsa woyamba, ‘Kodi uli ndi ngongole yotani kwa bwana wanga?’
6 Y ocona le rudeló: Cien pigotes de ampio: y le penó: Ustilela tiro por: y bestelate yescotria, y libana cinquenta.
“Iye anayankha kuti, ‘Migolo yamafuta a olivi 800.’ “Kapitawo uja anamuwuza iye, ‘Tenga pamene unalemba ngongole yakoyo, khala pansi msanga ndipo lemba kuti ndi migolo 400.’
7 Despues penó á aver: ¿Y tucue quanto debisarelas? Y ó rudeló: Cien melales de gi. Penó: Ustilela tiri papiri, y libana ochenta.
“Kenaka iye anafunsa wachiwiri kuti, ‘Nanga iwe uli ndi ngongole yotani?’ “Iye ayankha kuti madengu a tirigu 1,000. “Iye anati, ‘Tenga pamene unalemba ngongole yakoyo ndipo ulembepo 800.’
8 Y loó ó erañó al queresquero choro, presas queró saro cuerdamente: presas os chai de ocona gré chanelan butér andré su beda, que os chai e dut. (aiōn g165)
“Bwana anayamikira kapitawo wosakhulupirikayo popeza anachita mochenjera. Pakuti anthu a dziko lino lapansi ndi ochenjera kwambiri akamachita zinthu ndi anthu ofanana nawo kuposa anthu a kuwunika. (aiōn g165)
9 Menda sangue penelo: Que quereleis monres es manchines e choripen; somia que pur perareis, ustilelen sangue andré eternos querés. (aiōnios g166)
Ine ndikukuwuzani inu, gwiritsani ntchito chuma cha dziko lapansi kuti mudzipezere nokha abwenzi, kuti pamene chatha mudzalandiridwe mʼmalo okhala amuyaya. (aiōnios g166)
10 O sos sinelo lacho andré o mendesquero, lo sinela tambien andré o mas baro; o sos sinela choro andré frimi, tambien sinela choro andré baribu.
“Amene akhulupirika pa zinthu zochepa akhoza kukhulupirikanso pa zinthu zambiri, ndipo amene sakhulupirika pa zinthu zochepa adzakhala wosakhulupirika pa zinthu zambiri.
11 Pues si andré manchines chores na sinasteis fieles: ¿coin á sangue fiará ma sinelo chirdino.
Ndipo ngati simunakhale okhulupirika pogwiritsa ntchito chuma cha dziko lapansi, ndani amene adzakusungitsani chuma chenicheni?
12 Y si na sinasteis fieles andré ma de aver: ¿ma sinela jire coin á sangue lo diñará.
Ndipo ngati simunakhale okhulupirika ndi chuma cha mwini wake, ndani amene adzakupatsani katundu wanuwanu?
13 Ningun lacró astisarela servir á dui erañés: presas el ó na camelará á yeque, y camelará al aver: ó a ocona bigorelará, y al aver despreciará: n’astis servir á Debél, y al jayere.
“Palibe wantchito amene angatumikire mabwana awiri. Mwina iye adzadana ndi wina ndi kukonda winayo, kapena adzakhala wodzipereka kwa wina ndi kumunyoza winayo. Inu simungathe kutumikira Mulungu komanso ndalama nthawi imodzi.”
14 Tami os Phariseyes, sos sinaban cascañés, junelando sarias oconas buchias, girelaban.
Afarisi amene ankakonda ndalama atamva zimenezi anamuseka Yesu.
15 Y les penó: Sangue sinelais junos sos os binelais por laches anglal es manuces: Tami Debél: pincharela jires carles: presas ma os manuces terelan por udscho, sinela choro anglal de Debél.
Yesu anawawuza kuti, “Inu ndi amene mumadzilungamitsa nokha pamaso pa anthu, koma Mulungu amadziwa mitima yanu. Zinthu zimene anthu amaziyesa zopambana, ndi zonyansa pamaso pa Mulungu.
16 A Eschastra, y os Prophetas disde Juan: desde entonces sinela pucanado o chim de Debél: y os sares querelan sila contra ó.
“Malamulo ndi Aneneri zinagwira ntchito mpaka nthawi ya Yohane. Kuyambira nthawi imeneyo, Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ukulalikidwa, ndipo aliyense akuyesetsa mwamphamvu kuti alowemo.
17 Buchi facil butér najarse o Charos y a pu, que perar yeque buchi e Eschastra.
Nʼkwapafupi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zichoke kulekana ndi kuti kalemba kakangʼono kachoke mʼMalamulo.
18 Saro manu sos mequela desqueri romi, y ustilela aver, querela adulterio, y tambien ó sos se romandiñela con la sos bucharó o rom, querela adulterio.
“Aliyense amene asiya mkazi wake ndi kukakwatira mkazi wina akuchita chigololo, ndipo mwamuna amene akwatira mkazi wosiyidwayo akuchitanso chigololo.”
19 Sinaba manu balbalo, sos se vistió de lalané y de bostan lacho, lacho: y cata chibes terelaba jachipenes jucales.
“Panali munthu wachuma amene ankavala zovala zofiirira za mtengowapatali ndipo ankakhala moyo wachisangalalo tsiku lililonse.
20 Y sinaba oté yeque choro hetó Lazaro, sos yacia al bundal e balbalo; perdo de merdés.
Pa khomo la mpanda wake ankagonekapo munthu wopempha wotchedwa Lazaro, wazilonda thupi lonse
21 Camelando marar sun boquis de las bedoras, que peraban de la mensalle e balbalo, y cayque se las diñaba, tami abillaban os chuqueles, y le lamian as merdés.
ndipo ankafunitsitsa atadya zomwe zinkagwa pansi kuchokera pamene munthu wolemerayo amadyerapo. Agalu ankabweranso ndi kumanyambita zilonda zake.
22 Y anacó que pur meró ocola chororo lo lligueráron os Manfarieles al chepo de Abraham. Y meró tambien o balbalo, y sinaba bucharado andré benguistano.
“Nthawi inafika imene wopemphayo anamwalira ndipo angelo anamunyamula nakamuyika mʼmanja mwa Abrahamu. Munthu wolemerayo anamwaliranso ndipo anayikidwa mʼmanda.
23 Y ardiñelando as aquias, pur sinaba andré os jacháres, diqueló de muy dur á Abraham, y á Lazaro andré desquero chepo: (Hadēs g86)
Ali mʼgehena kuzunzika, anakweza maso ake ndipo anaona Abrahamu ali ndi Lazaro pambali pake. (Hadēs g86)
24 Y ó, á gole, gole, penó: Batico Abraham, terela canrea de mangue: y bichabela á Lazaro, que mojisarele o vuque de sun angusti en pani, somia jilar á minri chipe, presas sinelo jurepenado andré ocona yaque.
Ndipo anafuwula kwa iye kuti, ‘Abambo Abrahamu, mundimvere chisoni ine ndipo mutumeni Lazaroyo kuti aviyike msonga ya chala chake mʼmadzi kuti aziziritse lilime langa, chifukwa ndikumva ululu mʼmoto muno.’
25 Y Abraham le penó: Chaboro: terela en fácho, que ustilaste o lacho andré tun chipen, y Lazaro bastardo: pues acana terela ó acoi paratató, y tucue jurepénes.
“Koma Abrahamu anayankha kuti, ‘Mwanawe kumbukira kuti nthawi yamoyo wako unalandira zinthu zako zabwino, pamene Lazaro analandira zinthu zoyipa, koma tsopano akusangalatsidwa kuno ndipo iwe uli mʼmazunzo.
26 Fuera de que sinela butron baro entré amangue y sangue; de manera que junos sos camelaren nacar de acoi á sangue, n’astisarelan, ni de oté nacar acoi.
Ndipo kuwonjezera pa zonsezi, pakati pa inu ndi ife pali chiphompho chachikulu chimene chinayikidwa, kotero kuti amene akufuna kubwera kumeneko sangathe, kapena palibe amene angawoloke kuchokera kumeneko kudzafika kuno.’
27 Y penó: Pues te manguelo, batu, que lo bichobeles al quer de minrio batu.
“Iye anayankha kuti, ‘Ndipo ndikupemphani inu, abambo, mutumeni Lazaro ku nyumba ya abambo anga,
28 Presas terelo pansch plalores, somia que les díñele machiria, que na sinele que abillelen junos tambien a ocona sosimbo de jurepénes.
pakuti ine ndili ndi abale asanu. Lolani iye akawachenjeze kotero kuti asadzabwere kumalo ano amazunzo.’
29 Y Abraham le rudeló: Terelan á Moyses y á os Prophetas: junelenlos.
“Abrahamu anayankha kuti, ‘Ali ndi Mose ndi Aneneri; aleke amvere iwo.’
30 Tami o aver penó: Nanai, Dada Abraham; tami si yeque es mules chalare á junos, querelarán penitencia.
“Iye anati, ‘Ayi, bambo Abrahamu, koma ngati wina ochokera kwa akufa adzapita kwa iwo, adzatembenuka mtima.’
31 Y Abraham le penó: Si na junelan á Moyses y á os Prophetas: tampoco pachibelarán á yeque, aun pur se ardiñelare de enré os mulés.
“Anati kwa iye, ‘Ngati iwo samvera Mose ndi Aneneri, sadzakhulupirira ngakhale wina atauka kwa akufa.’”

< Lucas 16 >